< Hezekiel 6 >

1 RAB bana şöyle seslendi:
Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti,
2 “Ey insanoğlu, yüzünü İsrail dağlarına doğru çevir ve onlara karşı peygamberlik et.
“Iwe mwana wa munthu, yangʼana ku mapiri a Israeli; yankhula nawo modzudzula
3 De ki, ‘Ey İsrail dağları, Egemen RAB'bin sözünü dinleyin. Egemen RAB dağlara, tepelere, vadilere, derelere şöyle diyor: Üzerinize kılıç göndereceğim, tapınma yerlerinizi yıkacağım.
kuti, ‘Inu mapiri a ku Israeli, imvani mawu a Ambuye Yehova. Iye akuwuza mapiri, magomo, mitsinje ndi zigwa kuti: Ine ndizakuthirani nkhondo ndipo ndidzawononga nyumba zanu mʼmene mukupembedzeramo mafano.
4 Sunaklarınızı devirecek, buhur sunaklarınızı paramparça edeceğim. Kılıçtan geçirilmiş halkınızı putlarınızın önüne düşüreceğim.
Maguwa anu ansembe adzagumulidwa ndipo maguwa anu ofukizira lubani adzaphwanyidwa; ndipo ndidzapha anthu anu pamaso pa mafano anu.
5 İsrailliler'in cesetlerini putlarının önüne atacak, kemiklerini sunaklarının çevresine dağıtacağım.
Ine ndidzagoneka mitembo ya Aisraeli pamaso pa mafano awo, ndipo ndidzamwaza mafupa anu mozungulira maguwa anu ansembe.
6 Yaşadığınız her yerde kentleriniz yakılıp yıkılacak, tapınma yerleriniz yerle bir edilecek. Öyle ki, sunaklarınız devrilip yıkılsın, putlarınız ezilip paramparça olsun, buhur sunaklarınız yok edilsin, el emeğiniz boşa çıksın.
Konse kumene mumakhala, mizinda yanu idzasanduka bwinja. Nyumba zanu zopembedzera mafano zidzagumulidwa kotero kuti maguwa anu adzawonongedwa ndi kusakazidwa, mafano anu adzaphwanyidwa ndi kuwonongedwa. Maguwa anu ofukizirapo lubani adzagwetsedwa pansi ndipo zonse zimene munapanga zidzatheratu.
7 Halkınız her yerde öldürülecek. O zaman benim RAB olduğumu anlayacaksınız.
Anthu anu adzaphedwa pakati panu, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
8 “‘Birkaç kişiyi ölümden kurtaracağım. Ülkelere, uluslar arasına dağılan bazılarınız kılıçtan kurtulacak.
“Komabe ndidzasiya ena pangʼono opulumuka ku nkhondo. Iwowa ndidzawamwazira ku mayiko ena pakati pa anthu a mitundu ina.
9 Kurtulanlar tutsak alındıkları uluslarda beni anımsayacaklar. Benden dönen sadakatsiz yüreklerinden, putları ardınca şehvete sürükleyen gözlerinden derin acı duydum. Yaptıkları kötülükler ve iğrenç uygulamalar yüzünden kendilerinden tiksinecekler.
Pamenepo opulumuka mwa inu adzandikumbukira ku mayiko kumene anatengedwa ukapolo. Ndidzawamvetsa chisoni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo ndi kundipandukira kuja ndiponso chifukwa kuti anayika mtima wawo pa mafano. Choncho adzachita okha manyazi chifukwa cha zoyipa zimene ankachita ndi miyambo yonyansa imene ankatsata.
10 Benim RAB olduğumu, başlarına bu felaketi getireceğimi boşuna söylemediğimi anlayacaklar.
Ndipo iwo adzadziwa kuti ndine Yehova ndi kuti sindinkawaopseza chabe pamene ndinanena kuti ndidzawawononga.
11 “‘Egemen RAB şöyle diyor: Ellerini çırp, ayaklarını yere vur, İsrail halkının bütün kötü ve iğrenç uygulamalarından ötürü ah çek! Çünkü kılıçla, kıtlıkla, salgın hastalıkla yok olacaklar.
“Ambuye Yehova akuti: Womba mʼmanja mwako ndipo uponde mapazi ako pansi mwamphamvu ndipo ufuwule kuti, ‘Mayo!’ chifukwa cha zonyansa ndi zoyipa zonse zimene Aisraeli achita, pakuti adzaphedwa ndi lupanga, njala ndi mliri.
12 Uzaktakiler salgın hastalıktan ölecek, yakındakiler kılıçtan geçirilecek, kuşatma sırasında sağ kalanlar kıtlıktan ölecek. Böylece onlara duyduğum öfkeye son vereceğim.
Amene ali kutali adzafa ndi mliri, ndipo amene ali pafupi adzafa pa nkhondo, ndipo amene adzapulumuke ndi kusaphedwa adzafa ndi njala. Kotero ndidzakwaniritsa ukali wanga pa iwo.
13 Putlarının arasına, sunaklarının çevresine, her yüksek tepeye, dağ doruğuna, her yeşeren bol yapraklı ağacın altına cesetleri serilince, benim RAB olduğumu anlayacaklar. Oralarda putlarına güzel kokulu buhur sundular.
Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene anthu awo adzagona atafa pakati pa mafano awo mozungulira maguwa awo ansembe, pamwamba pa magomo ndi mapiri onse, pansi pa mtengo uliwonse watambalala ndi wa thundu uliwonse wamasamba ambiri, kumalo kumene ankapereka nsembe zonunkhira kwa mafano awo onse.
14 Elimi onlara karşı uzatacak, çölden Rivla'ya kadar yaşadıkları ülkeyi yerle bir edip ıssız bırakacağım. O zaman benim RAB olduğumu anlayacaklar.’”
Choncho ndidzawalanga ndi mkono wanga ndi kusandutsa dziko kukhala bwinja. Dziko lonse kumene akukhala kuyambira ku chipululu mpaka ku mzinda wa Ribula ndidzalisandutsa bwinja. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

< Hezekiel 6 >