< Hezekiel 33 >
1 RAB bana şöyle seslendi:
Yehova anandiyankhula nati:
2 “İnsanoğlu, kendi halkına şöyle diyeceksin: ‘Bir ülkenin üzerine kılıç gönderdiğim, ülke halkı aralarından birini seçip bekçi atadığı,
“Iwe mwana wa munthu awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Paja zimati ndikatumiza nkhondo mʼdziko anthu a mʼdzikomo amasankha munthu mmodzi pakati pawo kuti akhale mlonda.
3 bekçi kılıcın ülkenin üzerine yaklaştığını görüp halkı uyarmak için boru çaldığı zaman;
Tsono iyeyo amati akaona nkhondo ikubwera amaliza lipenga kuti achenjeze anthuwo.
4 kim boru sesini işitip de uyarıyı dikkate almazsa, kılıç da gelip onu öldürürse, kanından kendisi sorumludur.
Wina aliyense akamva lipenga koma osasamala, mdani uja akabwera nʼkumupha, ndiye kuti wadziphetsa yekha.
5 Boru sesini duymuş, ama uyarıyı dikkate almamıştır; kanından kendisi sorumludur. Uyarıyı dikkate alsaydı, canını kurtaracaktı.
Iye anamva kulira kwa lipenga koma sanalabadire. Ndiye kuti wadziphetsa yekha. Akanasamala kuchenjeza kwa mlonda akanapulumuka.
6 Ne var ki, bekçi kılıcın ülkenin üzerine yaklaştığını görüp halkı uyarmak için boru çalmazsa, kılıç da gelip halktan birini öldürürse, o kişi kendi günahı içinde öldürülmüştür; kanından bekçiyi sorumlu tutacağım.’
Koma ngati mlondayo aona lupanga likubwera ndipo osawomba lipengalo kuchenjeza anthu, ndipo lupanga libwera ndi kuchotsa moyo wa mmodzi mwa iwo, munthu ameneyo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma ndidzamuyimba mlandu mlondayo chifukwa cha imfa ya mnzakeyo.’
7 “İnsanoğlu, seni İsrail halkına bekçi atadım. Benden bir söz duyar duymaz onları benim yerime uyaracaksın.
“Tsono iwe mwana wa munthu, ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Choncho imva mawu amene ndikuyankhula ndipo uwachenjeze.
8 Kötü kişiye, ‘Ey kötü kişi, kesinlikle öleceksin’ dediğim zaman, onu uyarmaz, kötü yolundan döndürmek için konuşmazsan, o kişi günahı içinde ölecek; ama onun kanından seni sorumlu tutacağım.
Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe munthu woyipa, udzafa ndithu,’ ndipo iwe osayankhula kumuchenjeza kuti aleke njira zake, munthu wochimwayo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
9 Ancak kötü kişiyi uyardığın halde yolundan dönmezse, o günahı içinde ölecek. Ama sen canını kurtarmış olacaksın.
Koma ngati uchenjeza munthu woyipa kuti aleke njira zake, ndipo iye osatero, adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
10 “İnsanoğlu, İsrail halkına de ki, ‘Siz şöyle diyorsunuz: İsyanlarımızla günahlarımız bizi çökertiyor, onlardan ötürü eriyip yok oluyoruz. Durum böyleyken nasıl yaşayabiliriz?’
“Iwe mwana wa munthu, akumbutse Aisraeli mawu awo akuti, ‘Ife talemedwa ndi zolakwa zathu ndi machimo athu, ndipo tikuwonda chifukwa cha zimene tachita. Kodi tingakhale ndi moyo bwanji?’”
11 Onlara de ki, ‘Varlığım hakkı için diyor Egemen RAB, ben kötü kişinin ölümünden sevinç duymam, ancak kötü kişinin kötü yollarından dönüp yaşamasından sevinç duyarım. Dönün! Kötü yollarınızdan dönün! Niçin ölesiniz, ey İsrail halkı!’
Uwawuze kuti, Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Pali Ine wamoyo, sindikondwera ndi imfa ya munthu woyipa. Ndimakondwera ndikamaona munthu woyipa akuleka zoyipa zake kuti akhale ndi moyo. Tembenukani! Tembenukani, siyani makhalidwe anu oyipa! Muferanji, Inu Aisraeli?
12 “Sen, ey insanoğlu, halkına de ki, ‘Doğru kişi Tanrı'ya başkaldırırsa, doğruluğu onu kurtarmaz. Kötü kişi kötülüğünden döndüğü zaman kötülüğü yıkımına neden olmaz. Doğru kişi Tanrı'ya başkaldırırsa, doğruluğu yaşamasını sağlamaz.’
“Tsono iwe mwana wa munthu, awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Ngati munthu wolungama achimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwino zija sizidzamupulutsa. Koma wochimwa akaleka ntchito zake zoyipazo, sadzalangidwa konse. Ndithu ngati munthu wolungama ayamba kuchimwa sadzatha kukhala ndi moyo chifukwa cha ntchito zake zabwino zija.’
13 Doğru kişi için, ‘Kesinlikle yaşayacak’ desem, ama o doğruluğuna güvenip de kötülük yapsa, yaptığı doğru işlerin hiçbiri anımsanmayacak. Yaptığı kötülükten ötürü ölecek.
Ngati ndiwuza munthu wolungama kuti adzafa ndithu, koma iyeyo nʼkumadalira ntchito zake zabwino zimene anachita kale ndi kuyamba kuchimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwinozo zidzayiwalika. Iye adzafa chifukwa cha machimo ake.
14 Kötü kişiye, ‘Kesinlikle öleceksin’ desem, ama o günahından dönüp adil ve doğru olanı yapsa,
Ndipo ngati ndiwuza munthu woyipa kuti, ‘Udzafa ndithu,’ tsono iye nʼkutembenuka kuleka machimo ake ndi kuyamba kuchita zimene Yehova afuna,
15 aldığı rehini geri verse, çaldığını ödese, yaşam veren kurallar uyarınca davranıp günah işlemese kesinlikle yaşayacak, ölmeyecektir.
monga kubweza chimene anatenga ngati chikole cha ngongole, kubweza chimene anaba, kutsatira malamulo omwe amapereka moyo ndi kuleka kuchita zoyipa, iye adzakhala ndithu ndi moyo; sadzafa.
16 İşlediği günahlardan hiçbiri ona karşı anımsanmayacaktır, adil ve doğru olanı yapmıştır; kesinlikle yaşayacaktır.
Ndidzakhululuka machimo ake onse anachita. Iye wachita zimene ndi zolungama ndi zoyenera ndipo iye adzakhala ndi moyo ndithu.
17 “Senin halkın, ‘Rab'bin yolu doğru değil’ diyor. Oysa doğru olmayan onların yolu.
“Komabe anthu a mtundu wako akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, koma makhalidwe awo ndiwo ali osalungama.
18 Doğru kişi doğruluğundan döner de kötülük yaparsa, yaptığı kötülüğün içinde ölecektir.
Ngati munthu wolungama atembenuka ndi kuleka ntchito zake zolungama ndi kuyamba kuchita zoyipa, adzafa nazo.
19 Kötü kişi yaptığı kötülükten döner de adil ve doğru olanı yaparsa, yaptığı bu işlerle yaşayacaktır.
Ndipo ngati munthu woyipa atembenuka ndi kuleka ntchito zake zoyipa ndi kuyamba kuchita zolungama ndi zoyenera, iye adzakhala ndi moyo pochita zimenezo.
20 Ey İsrail halkı, ‘Rab'bin yolu doğru değil’ diyorsun. Her birinizi kendi yoluna göre yargılayacağım.”
Koma Inu Aisraeli, mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, inu Aisraeli, Ine ndidzaweruza aliyense wa inu potsata ntchito zake.”
21 Sürgünlüğümüzün on ikinci yılı, onuncu ayın beşinci günü Yeruşalim'den kaçıp kurtulan biri yanıma gelip, “Kent düştü!” dedi.
Pa tsiku lachisanu la mwezi wakhumi, chaka chakhumi ndi chiwiri cha ukapolo wathu, munthu wina amene anapulumuka ku Yerusalemu anabwera kudzandiwuza kuti, “Mzinda wagwa!”
22 Akşam, Yeruşalim'den kaçıp kurtulan adam gelmeden önce, RAB'bin eli üzerimdeydi, konuşamıyordum. Sabah o yanıma gelmeden RAB dilimi çözdü. Dilim açıldı, artık konuşabilirdim.
Tsono madzulo ake munthuyo asanafike, dzanja la Yehova linali pa ine. Koma mmawa mwake munthuyo atabwera Yehova anatsekula pakamwa panga, motero kuti sindinakhalenso wosayankhula.
23 RAB bana şöyle seslendi:
Ndipo Yehova anandiyankhula kuti:
24 “İnsanoğlu, İsrail'in viran olmuş kentlerinde yaşayanlar, ‘İbrahim tek kişiyken ülkeyi miras almıştı. Oysa biz kalabalığız, ülke miras olarak bize verilmiştir’ diyorlar.
“Iwe mwana wa munthu, anthu amene akukhala mʼmizinda ya mabwinja ya dziko la Israeli akunena kuti, ‘Abrahamu anali munthu mmodzi yekha, ndipo anamupatsa dziko lonse. Koma ife tilipo ambiri, motero tsono dzikolo ndi lathu.’
25 Bu nedenle onlara de ki, ‘Egemen RAB şöyle diyor: Eti kanıyla yiyor, putlarınıza bel bağlıyor, kan döküyorsunuz. Yine de ülkeyi miras almayı mı umuyorsunuz?
Choncho iwe uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Inu mumadya nyama ili ndi magazi ake, ndipo mumapembedza mafano ndi kukhetsa magazi, kodi tsono inu nʼkulandira dzikoli?
26 Kılıcınıza güveniyor, iğrenç şeyler yapıyor, komşunuzun karısını kirletiyorsunuz. Yine de ülkeyi miras almayı mı umuyorsunuz?’
Mumadalira lupanga lanu, mumachita zinthu zonyansa, ndipo aliyense wa inu amachita chigololo ndi mkazi wa mnzake. Kodi inu nʼkulandira dzikoli?’
27 “Onlara de ki, ‘Egemen RAB şöyle diyor: Varlığım hakkı için, viran olmuş kentlerde yaşayanlar kılıçtan geçirilecek, kırda yaşayanları yem olarak yabanıl hayvanlara vereceğim, kalelerde, mağaralarda yaşayanlar salgın hastalıkla yok olacak.
“Uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Ndithu pali Ine wamoyo, anthu amene anatsala mʼmizinda ya mabwinja adzaphedwa ndi lupanga, amene ali ku midzi ndidzawapereka kuti adzadyedwe ndi zirombo zakuthengo, ndipo amene ali mʼmalinga ndi mʼmapanga adzafa ndi mliri.
28 Ülkeyi ıssız, kimsesiz bırakacağım, övündükleri güç son bulacak. İsrail dağları ıssız kalacak, oradan kimse geçmeyecek.
Ndidzalisandutsa chipululu dzikolo, ndipo mphamvu zake zimene amanyadira zidzatheratu, ndipo mapiri a Yerusalemu adzasanduka chipululu, kotero kuti palibe amene adzatha kudutsako.
29 Yaptıkları iğrenç şeylerden ötürü ülkeyi ıssız, kimsesiz bıraktığım zaman benim RAB olduğumu anlayacaklar.’
Ndikadzasandutsa dzikolo chipululu chifukwa cha zonyansa zimene ankachita, pamenepo ndiye adzadziwa kuti ndine Yehova.’
30 “Sen, ey insanoğlu, halkın duvar diplerinde, evlerin kapıları önünde senin hakkında konuşuyor. Birbirlerine, ‘Haydi, gidip RAB'den gelen sözün ne olduğunu duyalım’ diyorlar.
“Koma kunena za iwe, mwana wa munthu, anthu a mtundu wako akumayankhula za iwe akakhala pa makoma a mzinda ndi pa makomo a nyumba zawo. Akumawuzana kuti, ‘Tiyeni tikamve uthenga umene wachokera kwa Yehova.’
31 Halk her zamanki gibi sana geliyor. Benim halkım olarak önünde oturuyor, sözlerini dinliyor, ama dediklerini yapmıyorlar. Ağızlarıyla istekli olduklarını açıklıyorlar, ama yürekleri haksız kazanç peşinde.
Anthu anga amabwera kwa iwe, monga momwe amachitira nthawi zonse anthu anga, ndipo amakhala pansi pamaso pako kumvetsera mawu ako. Koma zimene akumvazo sazichita. Zokamba zawo zimaonetsa chikondi, koma mitima yawo imakhala pa phindu lawo.
32 Sen onlar için güzel sesle sevgi ezgileri okuyan, iyi çalgı çalan biri gibisin. Sözlerini dinliyor, ama dediklerini yapmıyorlar.
Kunena zoona, kwa iwowo sindiwe kanthu konse, ndiwe munthu wamba chabe womangoyimba nyimbo zachikondi ndi liwu lokoma poyimba zeze. Kumva amamva mawu ako koma sawagwiritsa ntchito.
33 “Bütün bunlar gerçekleşince –ki gerçekleşecek– aralarında bir peygamber bulunduğunu anlayacaklar.”
“Koma zonsezi zikadzachitika, ndipo zidzachitika ndithu, pamenepo adzadziwa kuti mneneri anali pakati pawo.”