< Hezekiel 19 >

1 “Sen İsrail önderleri için şu ağıtı yak
“Imba nyimbo ya madandawulo, kuyimbira akalonga a ku Israeli.
2 ve de ki, “‘Annen neydi? Aslanlar arasında dişi bir aslan! Genç aslanlar arasında yatar, Yavrularını beslerdi.
Uzinena kuti, “‘Amayi ako anali ndani? Anali ngati mkango waukazi! Iwo unabwatama pakati pa mikango yayimuna; unkalera ana ake pakati pa misona.
3 Büyüttüğü yavrulardan biri Genç bir aslan oldu. Avını kapıp parçalamayı öğrendi, İnsan yiyen bir aslan oldu.
Unalera mmodzi mwa ana ake, ndipo mwanayo anasanduka mkango wamphamvu. Unaphunzira kugwira nyama, ndipo unayamba kudya anthu.
4 Haberi uluslar arasında duyuldu. Kurdukları tuzağa düştü, Onu çengellerle Mısır'a sürüklediler.
Anthu amitundu anamva za mkangowo, ndipo tsiku lina unagwa mʼmbuna mwawo. Iwo anawukoka ndi ngowe kupita nawo ku dziko la Igupto.
5 Dişi aslan bekledi, umudunun boşa çıktığını görünce, Yavrularından başka birini alıp Genç bir aslan olarak yetiştirdi.
“‘Amayi aja ataona kuti mwana ankamukhulupirira uja wagwidwa ndi kuti chiyembekezo chake chapita padera, amayiwo anatenganso mwana wina namusandutsa mkango wamphamvu.
6 Yavru aslanlar arasında dolaşmaya başladı, Genç bir aslan oldu. Avını kapıp parçalamayı öğrendi, İnsan yiyen bir aslan oldu.
Unkayendayenda pakati pa mikango inzake, pakuti tsopano unali mkango wamphamvu. Unaphunzira kugwira nyama ndipo unayamba kudya anthu.
7 Onların kalelerini yıktı, Kentlerini viraneye çevirdi. Ülkede yaşayan herkes Onun kükreyişinden dehşete düştü.
Unagwetsa malinga awo, ndikuwononga mizinda yawo. Onse a mʼdzikomo anachita mantha chifukwa cha kubangula kwake.
8 Çevredeki uluslar üzerine geldiler, Ağlarını gerdiler, Onu tuzağa düşürdüler.
Pamenepo mitundu ya anthu, makamaka ochokera madera ozungulira, inabwera kudzalimbana nawo. Anawutchera ukonde wawo, ndipo tsiku lina unagwera mʼmbuna mwawo.
9 Çengel takıp onu kafese koydular Ve Babil Kralı'na götürdüler. İsrail dağlarında kükreyişi bir daha duyulmasın diye Onu gözetim altında tuttular.
Anawukoka ndi ngowe nawuponya mʼchitatanga. Anabwera nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ndipo mfumuyo inawuponya mʼndende ndi cholinga choti liwu lake lisamamvekenso ku mapiri a Israeli.
10 “‘Annen su kıyısındaki bağında Dikilmiş bir asma gibiydi. Bol su sayesinde dal budak saldı, Ürün verdi.
“‘Amayi ako anali ngati mpesa mʼmunda wamphesa wodzalidwa mʼmbali mwa madzi. Unabereka bwino ndipo unali ndi nthambi zambiri chifukwa cha kuchuluka kwa madzi.
11 Dalları kral asası olacak kadar güçlendi. Asma boy attı, Bulutlara dek yükseldi. Yüksekliği ve dallarının çokluğu Herkesçe görüldü.
Nthambi zake zinali zolimba, zoyenera kupangira ndodo yaufumu. Unatalika nusomphoka pakati pa zomera zina. Unkaoneka bwino chifukwa cha kutalika kwake, ndi nthambi zake zambiri.
12 Ama onu öfkeyle kökünden söküp yere attılar. Doğu rüzgarı ürününü kuruttu. Güçlü dalları koparılıp kurudu, Ateş onları yakıp yok etti.
Koma unazulidwa mwaukali ndipo unagwetsedwa pansi. Unawuma ndi mphepo ya kummawa, zipatso zake zinayoyoka; nthambi zake zolimba zinafota ndipo moto unapsereza mtengo wonse.
13 Şimdi çöle, Kurak, susuz bir yere dikildi.
Ndipo tsopano anawuwokeranso ku chipululu, dziko lowuma ndi lopanda madzi.
14 Gövdesi ateş aldı, Filizini, ürününü yakıp yok etti. Kral asası olacak kadar güçlü dalı kalmadı.’ Bu bir ağıttır ve ağıt olarak kalacaktır.”
Moto unatulukanso mu mtengomo ndi kupsereza nthambi ndi zipatso zake. Palibe nthambi yolimba inatsala pa mtengowo yoyenera kupangira ndodo yaufumu. Imeneyi ndi nyimbo yachisoni ndipo yasanduka nyimbo ya pa maliro.’”

< Hezekiel 19 >