< Hezekiel 18 >

1 RAB bana şöyle seslendi:
Yehova anandiyankhula nati:
2 “İsrail için, ‘Babalar koruk yedi, Çocukların dişleri kamaştı’ diyorsunuz. Bu deyişle ne demek istiyorsunuz?
“Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti: “‘Nkhuyu zodya akulu zimapota ndi ana omwe?’”
3 “Varlığım hakkı için diyor Egemen RAB, İsrail'de artık bu deyişi ağzınıza almayacaksınız.
“Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli.
4 Her yaşayan can benimdir. Babanın canı da, çocuğun canı da benimdir. Ölecek olan, günah işleyen candır.
Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.
5 “Diyelim ki, adil ve doğru olanı yapan doğru bir adam var.
“Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama amene amachita zolungama ndi zolondola.
6 Dağlarda putlara sunulan kurbandan yemez, İsrail halkının putlarına bel bağlamaz. Komşusunun karısını kirletmez, Âdet gören kadına yaklaşmaz.
Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo kapena kupembedza mafano a Aisraeli. Iye sayipitsa mkazi wa mnzake kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.
7 Kimseye haksızlık etmez, Rehin olarak aldığını geri verir, Soygunculuk etmez, Aç olana ekmeğini verir, Çıplağı giydirir.
Iye sapondereza munthu wina aliyense, koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake. Iye salanda zinthu za osauka, koma amapereka chakudya kwa anthu anjala, ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.
8 Faizle para vermez, Aşırı kâr gütmez. Elini kötülükten çeker, İki kişi arasında doğrulukla yargılar.
Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira, kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu. Amadziletsa kuchita zoyipa ndipo sakondera poweruza milandu.
9 Kurallarımı izler, İlkelerimi özenle uygular. İşte böyle biri doğru kişidir. O yaşayacaktır. Egemen RAB böyle diyor.
Iye amatsatira malangizo anga, ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika. Munthu ameneyo ndi wolungama; iye adzakhala ndithu ndi moyo, akutero Ambuye Yehova.
10 “Diyelim ki, bu adamın zorba, kan döken, Kardeşine bunlardan birini yapan bir oğlu var.
“Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere.
11 Babası bunlardan hiçbirini yapmazken, Oğul dağlarda putlara sunulan kurbandan yer, Komşusunun karısını kirletir.
Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo. “Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo. Amayipitsa mkazi wa mnzake.
12 Düşküne, yoksula haksızlık eder, Soygunculuk eder, Rehini geri vermez. Putlara bel bağlar, İğrenç şeyler yapar.
Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa. Amalanda zinthu za osauka. Sabweza chikole cha munthu wa ngongole. Iye amatembenukira ku mafano nachita zonyansa.
13 Faizle para verir, aşırı kâr güder. Böyle biri yaşayacak mı? Hayır, yaşamayacak! Bütün bu iğrençlikleri yapmıştır, öldürülecektir. Onun kanından kendisi sorumlu olacaktır.
Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu. Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.
14 “Diyelim ki, bu oğulun da bir oğlu olur ve babasının işlediği bütün günahları görür, Ama hiçbirini yapmaz;
“Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.
15 Dağlarda putlara sunulan kurbandan yemez, İsrail halkının putlarına bel bağlamaz, Komşusunun karısını kirletmez;
“Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo. Sapembedza mafano a ku Israeli. Sayipitsa mkazi wa mnzake.
16 Kimseye haksızlık etmez, Rehin almaz, Soygunculuk etmez, Aç olana ekmeğini verir, Çıplağı giydirir.
Sapondereza munthu wina aliyense. Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka. Salanda zinthu za munthu. Amapereka chakudya kwa anthu anjala. Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.
17 Böyle biri elini kötülükten çeker, Faiz almaz, aşırı kâr gütmez, Kurallarımı izler, İlkelerimi uygularsa, Babasının günahı yüzünden ölmeyecek, Kesinlikle yaşayacaktır.
Amadziletsa kuchita zoyipa. Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja. Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga. Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu.
18 Ama babası kendi günahı yüzünden ölecektir. Çünkü zorbalık etti, kardeşini soydu, Halkı arasında iyi olmayanı yaptı.
Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.
19 “Ama siz, ‘Oğul neden babasının işlediği suçlardan sorumlu tutulmasın?’ dersiniz. Bu oğul adil ve doğru olanı yapmış, bütün kurallarımı dikkatle izlemiştir. Böyle biri kesinlikle yaşayacaktır.
“Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse.
20 Ölecek olan günah işleyen kişidir. Oğul babasının suçundan sorumlu tutulamaz, baba da oğlunun suçundan sorumlu tutulamaz. Doğru kişi doğruluğunun, kötü kişi kötülüğünün karşılığını alacaktır.
Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.
21 “Kötü kişi işlediği bütün günahlardan döner, buyruklarıma uyar, adil ve doğru olanı yaparsa, kesinlikle yaşayacak, ölmeyecektir.
“‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi.
22 İşlediği günahlardan hiçbiri ona karşı anılmayacaktır. Doğruluğu sayesinde yaşayacaktır.
Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo.
23 Ben kötü kişinin ölümünden sevinç duymam, ancak kötü kişinin kötü yollarından dönüp yaşamasından sevinç duyarım. Egemen RAB böyle diyor.
Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.
24 “Doğru kişi doğruluğundan döner, günah işler, kötü kişinin yaptığı bütün iğrenç şeyleri yaparsa, yaşayacak mı? Onun yaptığı doğru işlerin hiçbiri anılmayacaktır. Sadakatsizliği yüzünden suçludur, günahları yüzünden ölecektir.
“‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.
25 “Siz yine de, ‘Rab'bin yolu doğru değil’ diyorsunuz. Ey İsrail halkı, dinle: Benim yolum mu doğru değil? Doğru olmayan sizin yollarınız değil mi?
“Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama?
26 Doğru kişi doğruluğundan döner de kötülük yaparsa, bu yüzden ölecek. Evet, işlediği günah yüzünden ölecektir.
Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo.
27 Ama kötü kişi, yaptığı kötülükten döner, adil ve doğru olanı yaparsa, canını kurtaracaktır.
Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake.
28 Çünkü isyanlarının farkına varıyor ve onlardan dönüyor. Böyle biri kesinlikle yaşayacak, ölmeyecektir.
Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa.
29 Öyleyken, İsrail halkı, ‘Rab'bin yolu doğru değil’ diyor. Ey İsrail halkı, benim yollarım mı doğru değil? Doğru olmayan sizin yollarınız değil mi?
Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?
30 “Bu yüzden, ey İsrail halkı, sizleri, her birinizi yolunuza göre yargılayacağım. Egemen RAB böyle diyor. Dönün! İsyanlarınızdan dönün! Günahın sizi yıkıma sürüklemesine izin vermeyin.
“Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo.
31 İsyanlarınızı kendinizden uzaklaştırın. Yeni bir yürek, yeni bir ruh edinin. Neden öleceksin, ey İsrail halkı?
Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli?
32 Çünkü ben kimsenin ölümünden sevinç duymam. Egemen RAB böyle diyor. Öyleyse günahınızdan dönün de yaşayın!”
Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”

< Hezekiel 18 >