< Hezekiel 13 >

1 RAB bana şöyle seslendi:
Yehova anayankhulanso nane kuti,
2 “İnsanoğlu, peygamberlikte bulunan İsrail peygamberlerine karşı sen peygamberlik et. Kendiliğinden peygamberlik eden o peygamberlere de ki, ‘RAB'bin sözüne kulak verin!
“Iwe mwana wa munthu unenere modzudzula aneneri a Israeli amene akunenera za kukhosi kwawo. Uwawuze iwowa kuti, ‘Imvani mawu a Yehova!’
3 Egemen RAB şöyle diyor: Hiçbir görüm görmemiş ama kurdukları hayaller uyarınca davranan akılsız peygamberlerin vay başına!
Ambuye Yehova akuti, ‘Tsoka kwa aneneri opusa amene amangonenera zopeka ngakhale kuti sanaone kanthu konse!’
4 Ey İsrail, peygamberlerin yıkıntılar arasındaki çakallara benziyor.
Iwe Israeli, aneneri ako ali ngati nkhandwe pa mabwinja.
5 RAB'bin gününde İsrail halkının savaşta direnmesi için gidip duvardaki gedikleri onarmadınız.
Simunakwere khoma kuti mukakonze mʼmene munagumuka, kuti Aisraeli adziteteze kolimba pa nkhondo pa tsiku la Yehova.
6 Onların görümleri uydurmadır. Yaptıkları yalan peygamberliklere RAB'bin sözüdür diyorlar. Oysa onları ben göndermedim. Yine de söylediklerinin yerine geleceğini umuyorlar.
Masomphenya awo ndi achabe ndipo kuwombeza kwawo ndi kwabodza. Iwo amati, ‘Yehova akutero,’ pomwe Yehova sanawatume. Komabe iwo amayembekezera kuti zimene ayankhulazo zichitikadi.
7 Ben söylemediğim halde, RAB'bin sözüdür diyorsunuz. Oysa gördüğünüz görümler uydurma, yaptığınız falcılık yalan değil mi?
Koma Ine ndikuti masomphenya anu ngachabechabe ndi zimene mwawombedzazo nʼzabodza. Mumanena kuti, ‘Akutero Yehova,’ pamene sindinayankhule nʼkomwe.
8 “‘Bu yüzden Egemen RAB şöyle diyor: Söylediğiniz boş sözler, gördüğünüz yalan görümlerden ötürü size karşıyım. Böyle diyor Egemen RAB.
“Tsono Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndikukutsutsani chifukwa cha zoyankhula zanu zonama ndi masomphenya anu abodzawo. Ndikutero Ine Yehova.
9 Elim uydurma görüm gören, yalan yere falcılık eden peygamberlere karşı olacak. Onlar halkımın topluluğunda bulunmayacak, İsrail halkının kütüğüne yazılmayacak, İsrail ülkesine girmeyecekler. O zaman benim Egemen RAB olduğumu anlayacaksınız.
Ndidzalanga aneneri amene amanenera zabodza za zinthu zimene amati anaziona mʼmasomphenya. Sadzakhala nawo mʼbwalo la anthu anga ndipo mayina awo sadzalembedwa mu kawundula wa nzika za Israeli. Sadzalowa nawo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
10 “‘Esenlik yokken esenlik diyerek halkımı aldatıyorlar. Biri dayanıksız bir duvar yapınca, sahte peygamberler üzerine sıva vuruyorlar.
“Popeza kuti aneneri asocheretsa anthu anga pomanena kuti, ‘Kuli mtendere’ pamene mtendere palibe; ndiponso anthu akamanga khoma iwo nʼkumalipaka njereza,
11 Duvarı sıvayanlara de ki: Duvar yıkılacak; sağanak yağmur yağacak, ardından dolu yağdıracağım. Şiddetli bir rüzgar çıkıp duvara karşı esecek.
choncho ufotokozere amene alipaka njerezawo kuti khomalo lidzagwa. Mvula idzagwa mwamphamvu, kudzagwa matalala akuluakulu, ndipo kudzawomba mphepo yamkuntho.
12 Duvar çökünce size, nerede duvara vurduğunuz sıva demeyecekler mi?
Pamene khomalo lagwa, kodi anthu sadzakufunsani kuti, ‘Kodi njereza yemwe munapaka uja ali kuti?’
13 “‘Onun için Egemen RAB şöyle diyor: Öfkemden duvarı yerle bir etmek için şiddetli bir rüzgar göndereceğim; kızgınlığımdan sağanak yağmur ve dolu yağdıracağım.
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Mwa ukali ndidzakunthitsa mphepo ya mkuntho. Ndidzagwetsa matalala akuluakulu ndili ndi ukali ndipo ndidzavumbwitsa mvula yamphamvu ndi mkwiyo mpaka khomalo litawonongeka kotheratu.
14 Sıva vurduğunuz duvarı yıkıp yerle bir edeceğim. Temeli açılıp ortaya çıkacak. Yıkılacak ve altında yok olacaksınız. O zaman benim RAB olduğumu anlayacaksınız.
Ndidzagwetsa khoma limene munalipaka njerezalo. Ndidzaligumuliratu mpaka pansi kotero kuti maziko ake adzaoneka. Khomalo likadzagwa, inu mudzawonongekamo; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
15 Böylece öfkemi duvarın ve duvara sıva vuranların üzerine boşaltacağım. Size duvar da duvara sıva vuran da Yeruşalim'de esenlik yokken esenlik görümleri gören İsrailli peygamberler de yok oldu diyeceğim. Egemen RAB böyle diyor.’”
Kotero ndidzagwiritsa ntchito mkwiyo wanga pa khomali ndi pa amene analipaka njereza. Pambuyo pake ndidzakuwuzani kuti, ‘Khoma lagwa pamodzi ndi amene analipaka njereza.
Agwanso aneneri a Yerusalemu amene ankalosa za Yerusalemu nʼkumati anaona mʼmasomphenya za mtendere wa Yerusalemu pamene mtendere kunalibe konse, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.’
17 “Sen, ey insanoğlu, kendiliğinden peygamberlik eden halkının kızlarına yüzünü çevir. Onlara karşı peygamberlik et.
“Tsono iwe mwana wa munthu, yankhulapo pa nkhani za akazi amene ali pakati pa anthu ako. Iwo amanenera zopeka za mʼmutu mwawo. Tsono adzudzule.
18 De ki, ‘Egemen RAB şöyle diyor: İnsanları tuzağa düşürmek için herkese bilek bağı diken, her boyda baş örtüsü yapan kadınların vay başına! Kendi canınızı korurken halkımın canını mı tuzağa düşüreceksiniz?
Uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Tsoka kwa akazi amene amasoka zithumwa zapamkono, amenenso amasoka nsalu za kumutu za anthu. Kodi mufuna kukola mitima ya anthu anga, inuyo nʼkupulumutsa moyo wanu?
19 Birkaç avuç arpayla birkaç dilim ekmek için halkımın arasında beni küçük düşürdünüz. Yalana kulak veren halkıma yalan söyleyerek ölümü hak etmemiş canları öldürdünüz, ölümü hak etmiş canları yaşattınız.
Ponamiza anthu anga amene amamva za mabodza anu, inu mwapha anthu amene sanayenera kufa ndipo mwasiya ndi moyo amene sanayenera kukhala ndi moyo.
20 “‘Bundan ötürü Egemen RAB şöyle diyor: İnsanları kuş gibi tuzağa düşüren sihirli bilek bağlarınıza karşıyım. Onları bileklerinizden koparacağım. Kuş gibi tuzağa düşürdüğünüz insanları özgür kılacağım.
“‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikudana ndi zithumwa zanu zimene mumakokera nazo mitima ya anthu ngati mbalame. Ndidzazingʼamba kudzichotsa pa mikono yanu. Choncho ndidzapulumutsa miyoyo ya anthu amene munawakola ngati mbalame.
21 Örtülerinizi yırtacak, halkımı elinizden kurtaracağım. Bir daha tuzağınıza düşmeyecekler. O zaman benim RAB olduğumu anlayacaksınız.
Ndidzangʼamba nsalu zanu za matsengazo ndi kupulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu, ndipo simudzakhalanso ndi mphamvu yowakolera. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
22 Madem incitmek istemediğim doğru kişinin cesaretini yalanlarınızla kırdınız ve canını kurtarmak için kötü kişiyi kötü yolundan dönmemeye yüreklendirdiniz,
Popeza kuti munatayitsa mtima anthu olungama ngakhale sindinafune kuti ataye mtima; ndipo munalimbitsa anthu oyipa kuti asaleka machimo awo motero sakutha kupulumutsa moyo wawo,
23 bir daha uydurma görümler görmeyecek, falcılık etmeyeceksiniz. Halkımı elinizden kurtaracağım. O zaman benim RAB olduğumu anlayacaksınız.’”
choncho inu simudzaonanso masomphenya abodza kapena kuwombeza. Ine ndidzapulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu. Ndipo pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”

< Hezekiel 13 >