< Misir'Dan Çikiş 23 >

1 “Yalan haber taşımayacaksınız. Haksız yere tanıklık ederek kötü kişiye yan çıkmayacaksınız.
“Usafalitse mbiri yabodza. Usathandize munthu wolakwa pomuchitira umboni wonama.
2 “Kötülük yapan kalabalığı izlemeyeceksiniz. Bir davada çoğunluktan yana konuşarak adaleti saptırmayacaksınız.
“Usatsate gulu la anthu ndi kuchita choyipa. Pamene ukupereka umboni mʼbwalo lamilandu, usakhotetse mlandu chifukwa chofuna kukondweretsa anthu ambiri.
3 Duruşmada yoksulu kayırmayacaksınız.
Ndipo poweruza mlandu wa munthu wosauka usamukondere.
4 “Düşmanınızın yolunu şaşırmış öküzüne ya da eşeğine rastlarsanız, onu kendisine geri götüreceksiniz.
“Ngati ukumana ndi ngʼombe kapena bulu wa mdani wako zitasochera, uwonetsetse kuti wazitenga kupita nazo kwa mwini wakeyo.
5 Sizden nefret eden kişinin eşeğini yük altında çökmüş görürseniz, kendi haline bırakıp gitmeyecek, ona yardımcı olacaksınız.
Ngati uwona bulu wa munthu wina amene amakuda atagwa ndi katundu, usamusiye pomwepo, uwonetsetse kuti wamuthandiza.
6 “Duruşmada yoksula karşı adaleti saptırmayacaksınız.
“Usakhotetse milandu ya anthu osauka.
7 Yalandan uzak duracak, suçsuz ve doğru kişiyi öldürmeyeceksiniz. Çünkü ben kötü kişiyi aklamam.
Upewe zabodza ndipo usaphetse munthu wosalakwa ndi wolungama, chifukwa Ine sindidzakhululukira wochimwa.
8 “Rüşvet almayacaksınız. Çünkü rüşvet göreni kör eder, haklıyı haksız çıkarır.
“Musamalandire chiphuphu, pakuti chiphuphu chimadetsa mʼmaso anthu oweruza ndi kusintha mawu awo kuti mlandu uyipire osalakwa.
9 “Yabancıya baskı yapmayacaksınız. Yabancılığın ne olduğunu bilirsiniz. Çünkü siz de Mısır'da yabancıydınız.
“Usamuzunze mlendo, pakuti inu nomwe mukudziwa mmene amamvera mlendo chifukwa nanunso munali alendo mʼdziko la Igupto.
10 “Toprağınızı altı yıl ekecek, ürününü toplayacaksınız.
“Muzidzala mbewu zanu mʼmunda ndi kumakolola mbewuzo kwa zaka zisanu ndi chimodzi.
11 Ama yedinci yıl nadasa bırakacaksınız; öyle ki, halkınızın arasındaki yoksullar yiyecek bulabilsin, onlardan artakalanı da yabanıl hayvanlar yesin. Bağınıza ve zeytinliğinize de aynı şeyi yapın.
Koma chaka chachisanu ndi chiwiri muzisiya osalima mindayo kuti anthu osauka pakati panu azipezamo chakudya, ndipo nyama zakuthengo zizidya zotsalazo. Muzichita chimodzimodzi ndi minda ya mpesa ndi mitengo ya olivi.
12 “Altı gün çalışacak, yedinci gün dinleneceksiniz. Böylece hem öküzünüz, eşeğiniz dinlenir, hem de kadın kölenizin oğulları ve yabancılar rahat eder.
“Muzigwira ntchito masiku asanu ndi limodzi koma tsiku lachisanu ndi chiwiri musagwire ntchito kuti ngʼombe yanu ndi bulu wanu apume ndiponso kuti kapolo wobadwira mʼnyumba yanu ndi mlendo yemwe apezenso mphamvu.
13 “Söylediğim her şeyi yerine getirin. Başka ilahların adını anmayın, ağzınıza almayın.”
“Samalani pochita zonse zimene ine ndanena. Musamapemphere kwa milungu ina ndipo mayina awo musamawatchule.
14 “Yılda üç kez bana bayram yapacaksınız.
“Muzichita zikondwerero zolemekeza Ine katatu pa chaka.
15 Size buyurduğum gibi, Aviv ayının belirli günlerinde yedi gün mayasız ekmek yiyerek Mayasız Ekmek Bayramı'nı kutlayacaksınız. Çünkü Mısır'dan o ay çıktınız. “Kimse huzuruma eli boş çıkmasın.
“Muzichita Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti. Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti monga ndinakulamulirani. Muzichita zimenezi mwezi wa Abibu pa nthawi yomwe ndayika, pakuti mʼmwezi umenewu munatuluka mʼdziko la Igupto. “Pasapezeke munthu wobwera pamaso panga wopanda kanthu mʼmanja.
16 “Tarlaya ektiğiniz ürünleri biçtiğinizde ilk ürünlerle Hasat Bayramı'nı kutlayacaksınız. “Yıl sonunda tarladan ürünlerinizi topladığınızda Ürün Devşirme Bayramı'nı kutlayacaksınız.
“Muzichita Chikondwerero cha Masika pogwiritsa ntchito zipatso zoyambirira kucha zimene munadzala mʼmunda. “Muzichitanso Chikondwerero cha Zokolola pakutha pa chaka, pamene mukututa zokolola zanu mʼmunda.
17 “Bütün erkekleriniz yılda üç kez ben Egemen RAB'bin huzuruna çıkacaklar.
“Amuna onse azionekera pamaso pa Ambuye Yehova katatu pa chaka.
18 “Evinizde maya bulunduğu sürece bana kurban kesmeyeceksiniz. “Bayramda bana kurban edilen hayvanın yağı sabaha bırakılmamalı.
“Musapereke magazi anyama ngati nsembe kwa Ine pamodzi ndi chilichonse chimene chili ndi yisiti. “Ndipo musasunge mafuta anyama yansembe ya pa chikondwerero mpaka mmawa.
19 “Toprağınızın seçme ilk ürünlerini Tanrınız RAB'bin Tapınağı'na getireceksiniz. “Oğlağı anasının sütünde haşlamayacaksınız.”
“Muzibwera ndi zipatso zoyambirira kucha zabwino kwambiri ku Nyumba ya Yehova Mulungu wanu. “Musamaphike kamwana kambuzi mu mkaka wa mayi wake.
20 “Yolda sizi koruması, hazırladığım yere götürmesi için önünüzden bir melek gönderiyorum.
“Taona Ine ndikutuma mngelo wanga patsogolo panu kuti akutetezeni mʼnjiramo ndi kukakufikitsani ku malo amene ndakonza.
21 Ona dikkat edin, sözünü dinleyin, başkaldırmayın. Çünkü beni temsil ettiği için başkaldırınızı bağışlamaz.
Muzimumvera ndi kumvetsetsa zimene akunena. Musamuwukire chifukwa sadzakhululuka kuwukira kwanu, pakuti akuchita zimenezi mʼdzina langa.
22 Ama onun sözünü dikkatle dinler, bütün söylediklerimi yerine getirirseniz, düşmanlarınıza düşman, hasımlarınıza hasım olacağım.
Ngati mudzamvera iyeyu ndi kuchita zonse zimene Ine ndikunena, Ine ndidzakhala mdani wa adani anu ndipo ndidzatsutsana ndi onse otsutsana nanu.
23 Meleğim önünüzden gidecek, sizi Amor, Hitit, Periz, Kenan, Hiv ve Yevus topraklarına götürecek. Onları yok edeceğim.
Mngelo wanga adzakhala patsogolo panu ndipo adzakufikitsani mʼdziko la Aamori, Ahiti, Aperezi, Akanaani, Ahivi ndi Ayebusi, ndipo ndidzawapheratu onsewo.
24 Onların ilahları önünde eğilmeyecek, tapınmayacaksınız; törelerini izlemeyeceksiniz. Tersine, ilahlarını yok edecek, dikili taşlarını büsbütün parçalayacaksınız.
Musagwadire milungu yawo kapena kuyipembedza. Ndipo musatsatire zinthu zomwe amachita. Koma inu mukawononge milungu yawo ndi kuphwasula malo amene amapembedzerapo.
25 Tanrınız RAB'be tapacaksınız. Ekmeğinizi, suyunuzu bereketli kılacak, aranızdaki hastalıkları yok edeceğim.
Muzipembedza Yehova Mulungu wanu ndipo adzakudalitsani ndi chakudya ndi madzi ndiponso ndidzachotsa nthenda pakati panu.
26 Ülkenizde kısır ve çocuk düşüren kadın olmayacak. Size uzun ömür vereceğim.
Palibe mkazi amene adzapite padera kapena kukhala wosabereka mʼdziko mwanu. Ndidzakupatsani moyo wautali.
27 “Dehşetimi önünüzden gönderecek, karşılaşacağınız bütün halkları şaşkına çevireceğim. Düşmanlarınız önünüzden kaçacak.
“Ine ndidzawachititsa mantha ndi kusokoneza anthu onse amene adzalimbana ndi inu ndipo adani anu onse adzakuthawani.
28 Hivliler'i, Kenanlılar'ı, Hititler'i önünüzden kovmaları için önünüzsıra eşekarısı göndereceğim.
Ahivi, Akanaani ndi Ahiti adzathawa ngati kuti ndawatumizira mavu.
29 Ama onları bir yıl içinde kovmayacağım. Yoksa ülke viran olur, yabanıl hayvanlar çoğaldıkça çoğalır, sayıları sizi aşar.
Komabe sindidzawachotseratu onse mʼchaka chimodzi chifukwa dziko lingadzakhale lopanda anthu ndipo nyama zakuthengo zidzakuchulukirani.
30 Siz çoğalıncaya, toprağı yurt edininceye dek onları azar azar kovacağım.
Ndidzawathamangitsa pangʼonopangʼono mpaka inu mutachuluka kokwanira mwakuti nʼkutenga dzikolo.
31 “Sınırlarınızı Kamış Denizi'nden Filist Denizi'ne, çölden Fırat Irmağı'na kadar genişleteceğim. Ülke halkını elinize teslim edeceğim. Onları önünüzden kovacaksınız.
“Malire a dziko lanu adzakhala kuyambira ku Nyanja Yofiira mpaka ku nyanja ya Afilisti, ndiponso kuyambira ku chipululu mpaka ku mtsinje wa Yufurate. Anthu onse okhala mʼdziko limeneli ndidzawapereka mʼmanja mwanu ndipo mudzawathamangitsa.
32 Onlarla ya da ilahlarıyla antlaşma yapmayacaksınız.
Musachite pangano ndi iwo kapena ndi milungu yawo.
33 Onları ülkenizde barındırmayacaksınız. Yoksa bana karşı günah işlemenize neden olurlar. İlahlarına taparsanız, size tuzak olur.”
Asadzakhale mʼdziko lanu chifukwa angadzakuchimwitseni ndi kuyamba kupembedza milungu yawo. Mukadzatero ndiye kuti mwakodwa mu msampha.”

< Misir'Dan Çikiş 23 >