< Ester 1 >

1 Ahaşveroş Hoddu'dan Kûş'a uzanan bölgedeki yüz yirmi yedi ilin kralıydı.
Izi ndi zimene zinachitika pa nthawi ya ufumu wa Ahasiwero, amene analamulira zigawo 127 kuyambira ku India mpaka ku Kusi.
2 O sırada ülkeyi Sus Kalesi'ndeki tahtından yönetiyordu.
Pa nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Ahasiwero atakhazikika pa mpando wake wa ufumu mu mzinda wa Susa,
3 Krallığının üçüncü yılında bütün önderlerinin ve görevlilerinin onuruna bir şölen verdi. Pers ve Med ordu komutanları, ileri gelenler ve il valileri de oradaydı.
ndipo mʼchaka chachitatu cha ufumu wake anakonza phwando la olemekezeka ndi nduna zake. Atsogoleri a nkhondo a ku Peresiya ndi Mediya, anthu olemekezeka pamodzi ndi nduna za mʼzigawo zonse anasonkhana kwa iye.
4 Ahaşveroş tam yüz seksen gün süren şenliklerle krallığının sonsuz zenginliğini, büyüklüğünün görkemini ve yüceliğini gösterdi.
Pa nthawi yomweyi kwa masiku 180 a phwando mfumu inkaonetsa kulemera kwa ulemerero wa ufumu wake ndiponso kukongola ndi kukula kwa ufumu wake.
5 Bunun ardından, sarayının avlusunda küçük büyük ayırmadan, Sus Kalesi'nde bulunan bütün halka yedi gün süren bir şölen verdi.
Atatha masiku amenewa, kwa masiku ena asanu ndi awiri mfumu inakonzanso phwando la anthu onse okhala mu mzinda wa Susa kuyambira anthu olemekezeka mpaka anthu wamba ku bwalo la munda la nyumba yake yaufumu.
6 Mermer sütunlar üzerindeki gümüş çemberlere mor ve beyaz renkli iplikten yapılmış sicimlerle bağlanmış beyaz ve lacivert kumaşlar asılmıştı. Somaki, mermer, sedef ve pahalı taşlar döşenmiş avluya altın ve gümüş sedirler yerleştirilmişti.
Bwalo la mundali analikongoletsa ndi makatani a nsalu zoyera ndi za mtundu wamtambo zimene anazimangirira ndi zingwe za nsalu zoyera ndi zapepo ku mphete za siliva zimene anazikoloweka pa nsanamira za maburo. Anayika mipando yopumirapo yagolide ndi siliva pabwalo la miyala yoyala yamtengowapatali yofiira, ya marabulo, ndi yonyezimira.
7 Sarayın en iyi şarabı kralın cömertliğine yaraşır biçimde bol bol ve her biri değişik altın kupalar içinde sunuluyordu.
Anapereka zakumwa mʼchikho zagolide zamitundumitundu, ndipo vinyo waufumu anali wochuluka kwambiri monga mwa kukoma mtima kwa mfumu.
8 Kralın buyruğu uyarınca, konuklar içki içmeye zorlanmadı. Kral saray hizmetkârlarına konukların dileklerini yerine getirmeleri için buyruk vermişti.
Monga mwa lamulo la mfumu aliyense anamwa mʼmene anafunira, pakuti mfumu inawuza otumikira ake kuti apatse aliyense monga mwa kukonda kwake.
9 O sırada Kraliçe Vaşti de Kral Ahaşveroş'un sarayındaki kadınlara bir şölen veriyordu.
Mkazi wa mfumu Vasiti nayenso anakonzera phwando amayi ku nyumba ya ufumu ya mfumu Ahasiwero.
10 Yedinci gün, şarabın etkisiyle keyiflenen Kral Ahaşveroş, hizmetindeki yedi haremağasına –Mehuman, Bizta, Harvona, Bigta, Avagta, Zetar ve Karkas'a– Kraliçe Vaşti'yi başında tacıyla huzuruna getirmelerini buyurdu. Kraliçe Vaşti güzeldi. Kral halka ve önderlere onun ne kadar güzel olduğunu göstermek istiyordu.
Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri, pamene mfumu Ahasiwero inaledzera ndi vinyo, inalamula adindo ofulidwa asanu ndi awiri amene ankamutumikira: Mehumani, Bizita, Haribona, Bigita, Abagita, Zetara, ndi Karikasi
kuti abwere naye mfumukazi Vasiti pamaso pa mfumu atavala chipewa chaufumu. Cholinga cha mfumu chinali choti adzamuonetse kwa anthu onse ndi olemekezeka, chifukwa anali wokongola kwambiri.
12 Ama Kraliçe Vaşti haremağalarının kraldan getirdiği buyruğu reddedip gitmedi. Bunun üzerine kral çok kızdı, öfkesinden küplere bindi.
Koma antchito atapereka uthenga wa mfumu kwa mfumukazi, Vasiti anakana kubwera. Tsono mfumu inakwiya ndi kupsa mtima.
13 Kral yasaları bilen bilge kişilerle görüştü. Çünkü kralın, yasaları ve adaleti bilen kişilere danışması gelenektendi.
Mfumu inayankhula ndi anthu anzeru ndi ozindikira choyenera kuchita popeza chinali chikhalidwe chake kufunsa uphungu kwa akatswiri pa nkhani za malamulo ndi kuweruza kolungama.
14 Kendisine en yakın olan Karşena, Şetar, Admata, Tarşiş, Meres, Marsena ve Memukan onunla yüzyüze görüşebiliyorlardı. Pers ve Med İmparatorluğu'nun bu yedi önderi krallığın en üst yöneticileriydi.
Anthu amene ankakhala pafupi ndi mfumu anali awa: Karisena, Setara, Adimata, Tarisisi, Meresi, Marisena ndi Memukani, olemekezeka asanu ndi awiri a ku Peresiya ndi Medina amene ankaloledwa mwapadera kuonana ndi mfumu ndipo anali pamwamba kwambiri mu ufumuwo.
15 Kral Ahaşveroş onlara, “Kralın haremağaları aracılığıyla gönderdiği buyruğa uymayan Kraliçe Vaşti'ye yasaya göre ne yapmalı?” diye sordu.
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi titani naye mfumukazi Vasiti mwa lamulo, popeza sanamvere lamulo la ine mfumu Ahasiwero limene adindo ofulidwa anakamuwuza?”
16 Memukan, kralın ve önderlerin önünde şu yanıtı verdi: “Kraliçe Vaşti yalnız krala karşı değil, bütün önderlere ve kralın bütün illerindeki halklara karşı suç işledi.
Ndipo Memukani anayankha pa maso pa mfumu ndi olemekezeka anzake kuti, “Mfumukazi Vasiti sanalakwire mfumu yokha, koma walakwiranso olemekezeka onse ndi anthu onse okhala mʼzigawo zonse za mfumu Ahasiwero.
17 Bütün kadınlar, kraliçenin davranışıyla ilgili haberi duyunca, ‘Kral Ahaşveroş Kraliçe Vaşti'nin huzuruna getirilmesini buyurdu, ama kraliçe gitmedi’ diyerek kocalarını küçümsemeye başlayacaklar.
Pakuti amayi onse adzadziwa zimene wachita mfumukazi ndipo kotero adzapeputsa amuna awo ndi kunena kuti, ‘Mfumu Ahasiwero analamulira kuti abwere naye mfumukazi Vasiti kwa iye koma sanapite.’
18 Bugün kraliçenin davranışını öğrenen Pers ve Medli soylu kadınlar da kralın soylu adamlarına aynı biçimde davranacak. Bu da alabildiğine kadınların küçümsemesine, erkeklerin de öfkelenmesine yol açacak.
Lero lomwe lino amayi olemekezeka a ku Peresiya ndi Mediya amene amva zimene wachita mfumukazi adzaganiza zochita chimodzimodzi kwa nduna zonse za mfumu. Ndipo kupeputsana ndi kukongola zidzapitirira.”
19 Kral uygun görüyorsa ferman çıkarsın; bu ferman Persler'le Medler'in değişmeyen yasalarına eklensin. Buna göre Vaşti bir daha Kral Ahaşveroş'un huzuruna çıkmasın ve kral ondan daha iyi birini kraliçeliğe seçsin.
“Choncho, ngati chikukomerani mfumu, lamulirani kuti Vasiti asadzaonekerenso pamaso pa mfumu Ahasiwero. Lamuloli lilembedwe mʼmabuku a malamulo a Aperezi ndi Amedi kuti lisadzasinthike. Pamalo pa Vasiti ngati mfumukazi payikidwepo mkazi wina amene ali bwino kuposa iye.
20 Kralın fermanı büyük krallığının dört bir yanına ulaşınca, ister soylu ister halktan olsun, bütün kadınlar kocalarına saygı gösterecektir.”
Ndipo lamulo la mfumuli lilengezedwa mʼdziko lake lonse ngakhale lili lalikulu, amayi onse adzapereka ulemu kwa amuna awo, amuna olemekezeka mpaka amuna wamba.”
21 Bu sözler kralın ve önderlerinin hoşuna gitti. Kral, Memukan'ın önerisine uyarak,
Mfumu ndi nduna zake anakondwera ndi uphungu uwu, kotero mfumu inachita monga momwe ananenera Memukani.
22 krallığın bütün illerine yazılı buyruklar gönderdi. Her ile kendi işaretleriyle ve her halka kendi diliyle yazıldı. Her erkeğin kendi evinin egemeni olduğu her dilde vurgulandı.
Mfumu inatumiza makalata ku madera onse a ufumu wake, chigawo chilichonse mʼzilembo zawo ndi ku mtundu uliwonse mʼchiyankhulo chawochawo kulengeza kuti mwamuna ayankhule chilichonse chimene chikumukomera.

< Ester 1 >