< Ester 7 >
1 Böylece kral ve Haman, Kraliçe Ester'in şölenine gittiler.
Choncho mfumu ndi Hamani anabwera kudzadya phwando la mfumukazi Estere.
2 O gün şarap içerlerken kral Ester'e yine sordu: “İsteğin nedir, Kraliçe Ester? Ne istersen verilecek. Dileğin nedir? Krallığın yarısını bile istesen sana bağışlanacak.”
Pa tsiku lachiwiri akumwa vinyo, mfumu inafunsanso kuti, “Kodi iwe mfumukazi Estere, chimene ufuna kupempha nʼchiyani? Chimene uti upemphe ndidzakupatsa. Choncho ukufuna chiyani? Ngakhale utafuna theka la ufumu ndidzakupatsa.”
3 Kraliçe Ester şöyle yanıtladı: “Ey kralım, eğer benden hoşnutsan ve uygun görüyorsan, isteğim canımı bağışlaman, dileğim de halkımı esirgemendir.
Kenaka mfumukazi Estere anayankha kuti, “Ngati mwandikomera mtima, inu mfumu, ndipo ngati chingakukomereni mfumu, pempho ndi chokhumba changa ndi ichi, mulole kuti ine ndi abale anga tisungidwe tonse ndi moyo.
4 Çünkü ben ve halkım öldürülüp yok edilmek, yeryüzünden silinmek üzere satıldık. Eğer köle ve cariye olarak satılmış olsaydık sesimi çıkartmazdım; böyle bir sorun için kralı rahatsız etmek uygun olmazdı.”
Popeza ine ndi anthu a mtundu wanga tagulitsidwa kuti atiwononge, atiphe ndi kutifafaniziratu. Akanangotigulitsa kokha tikanakhala chete, chifukwa chimene mdani wathuyo akanakupatsani mfumu sibwenzi mutasowa nacho mtendere.”
5 Kral Ahaşveroş Kraliçe Ester'e, “Böyle bir şeyi yapmaya cüret eden kim, nerede bu adam?” diye sordu.
Mfumu Ahasiwero anamufunsa mfumukazi Estere, “Kodi iyeyu ndi ndani ndipo ali kuti amene saopa kuchita chinthu chotere?”
6 Ester, “Düşmanımız, hasmımız, işte bu kötü Haman'dır!” dedi. Haman kralla kraliçenin önünde dehşete kapıldı.
Estere anati, “Wotizunza ndiponso mdani wathu! Munthu woyipayo ndi Hamani.” Kenaka Hamani anagwidwa ndi mantha pamaso pa mfumu ndi mfumukazi.
7 Kral öfkeyle içki masasından kalkıp sarayın bahçesine çıktı. Haman ise Kraliçe Ester'den canını bağışlamasını istemek için içerde kaldı. Çünkü kralın kendisini yok etmeye kararlı olduğunu anlamıştı.
Mfumu itakwiya kwambiri inanyamuka pa phwando nipita ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu. Koma Hamani, pozindikira kuti mfumu yaganiza kale kumuchitira choyipa, anatsalira mʼnyumba kupempha Estere kuti apulumutse moyo wake.
8 Kral sarayın bahçesinden şölen salonuna dönünce, Haman'ı Ester'in uzandığı sedire kapanmış olarak gördü ve, “Bu adam sarayda, gözümün önünde kraliçeye bile el uzatmaya mı kalkıyor?” diye bağırdı. Kral sözlerini bitirir bitirmez Haman'ın yüzünü örttüler.
Mfumu itabwerera kuchokera ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu uja ndi kulowanso mʼchipinda chaphwando, anapeza Hamani atagona chafufumimba pa mpando wa khutagone pomwe Estere anakhalapo. Mfumu inayankhula mokweza kuti, “Kodi afunanso kuvula mfumukazi momukakamiza pamene ine ndili mʼnyumba?” Mfumu isanatsirize kuyankhula mawu awa, atumiki ake anaphimba nkhope ya Hamani.
9 Krala hizmet eden haremağalarından biri olan Harvona şöyle dedi: “Bakın, kralı uyarıp hayatını kurtaran Mordekay için Haman'ın hazırlattığı elli arşın yüksekliğindeki darağacı Haman'ın evinin önünde hazır duruyor.” Kral, “Haman o darağacına asılsın!” diye buyurdu.
Haribona, mmodzi wa adindo ofulidwa amene ankatumikira mfumu anati, “Mtanda wotalika mamita 23 uli mʼnyumba ya Hamani. Mtandawu, Hamani anapangira Mordekai, uja amene anapulumutsa mfumu ku chiwembu.” Mfumu inati, “Mpachikeni pamenepo!”
10 Böylece Haman Mordekay için hazırlattığı darağacına asıldı; kralın öfkesi de yatıştı.
Choncho anamupachika Hamani pa mtanda umene anakonzera Mordekai. Kenaka mkwiyo wa mfumu unatsika.