< Ester 10 >
1 Kral Ahaşveroş ülkeyi en uzak kıyılarına dek haraca bağlamıştı.
Mfumu Ahasiwero anakhometsa msonkho mʼdziko lake lonse mpaka ku zilumba zonse.
2 Büyüklüğü, kahramanlıkları ve Mordekay'ı her bakımdan nasıl onurlandırdığı Pers ve Med krallarının tarihinde yazılıdır.
Ndipo ntchito zonse zochitika ndi mphamvu zake komanso ndi zonse zofotokoza za ukulu wa Mordekai, kukwezedwa kwake ndi mfumu, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Mediya ndi Peresiya?
3 Yahudi Mordekay, Kral Ahaşveroş'tan sonra ikinci adam olmuştu. Yahudi soydaşları arasında saygı gören ve çoğunluk tarafından sevilen biriydi. Çünkü halkının iyiliğini düşünüyor, bütün soydaşlarının esenliği için çaba gösteriyordu.
Pakuti Mordekai Myuda uja anali wachiwiri wa mfumu Ahasiwero. Kwa Ayuda onse Mordekai anali munthu wamkulu ndipo ankamukonda chifukwa ankachitira zabwino mtundu wake ndi kufunira mtendere abale ake.