< Vaiz 9 >

1 Böylece bütün bunları düşünüp taşındım ve şu sonuca vardım: Doğrular, bilgeler ve yaptıkları her şey Tanrı'nın elindedir. Onları sevginin mi, nefretin mi beklediğini kimse bilmez.
Ndinalingalira zonse ndanenazi ndipo ndinapeza kuti anthu olungama ndi anthu anzeru ali mʼmanja mwa Mulungu pamodzi ndi zimene amachita, koma palibe amene amadziwa zimene zikumudikira mʼtsogolo mwake, kaya chikondi kapena chidani.
2 Herkesin başına aynı şey geliyor. Doğrunun, iyinin, kötünün, temizin, kirlinin, kurban sunanla sunmayanın başına gelen şey aynı. İyi insana ne oluyorsa, günahlıya da oluyor; Ant içene ne oluyorsa, ant içmekten korkana da aynısı oluyor.
Onsewa mathero awo ndi amodzi, anthu olungama ndi anthu oyipa, abwino ndi oyipa, oyera ndi odetsedwa, amene amapereka nsembe ndi amene sapereka nsembe. Zomwe zimachitikira munthu wabwino, zimachitikiranso munthu wochimwa, zomwe zimachitikira amene amalumbira, zimachitikiranso amene amaopa kulumbira.
3 Güneşin altında yapılan işlerin tümünün kötü yanı şu ki, herkesin başına aynı şey geliyor. Üstelik insanların içi kötülük doludur, yaşadıkları sürece içlerinde delilik vardır. Ardından ölüp gidiyorlar.
Choyipa chimene chili mʼzonse zochitika pansi ndi ichi: Mathero a zonse ndi amodzi. Ndithu, mitima ya anthu ndi yodzaza ndi zoyipa, ndipo mʼmitima mwawo muli zamisala pamene ali ndi moyo, potsiriza pake iwo amakakhala pamodzi ndi anthu akufa.
4 Yaşayanlar arasındaki herkes için umut vardır. Evet, sağ köpek ölü aslandan iyidir!
Aliyense amene ali ndi moyo amakhala ndi chiyembekezo, pajatu galu wamoyo aposa mkango wakufa!
5 Çünkü yaşayanlar öleceğini biliyor, Ama ölüler hiçbir şey bilmiyor. Onlar için artık ödül yoktur, Anıları bile unutulmuştur.
Pakuti amoyo amadziwa kuti adzafa, koma akufa sadziwa kanthu; alibe mphotho ina yowonjezera, ndipo palibe amene amawakumbukira.
6 Sevgileri, nefretleri, Kıskançlıkları çoktan bitmiştir. Güneşin altında yapılanlardan Bir daha payları olmayacaktır.
Chikondi chawo, chidani chawo ndiponso nsanje yawo, zonse zinatha kalekale; sadzakhalanso ndi gawo pa zonse zochitika pansi pano.
7 Git, sevinçle ekmeğini ye, neşeyle şarabını iç. Çünkü yaptıkların baştan beri Tanrı'nın hoşuna gitti.
Pita, kadye chakudya chako mokondwera ndi kumwa vinyo wako ndi mtima wosangalala, pakuti tsopano Mulungu akukondwera ndi zochita zako.
8 Giysilerin hep ak olsun. Başından zeytinyağı eksilmesin.
Uzivala zovala zoyera nthawi zonse, uzidzola mafuta mʼmutu mwako nthawi zonse.
9 Güneşin altında Tanrı'nın sana verdiği boş ömrün bütün günlerini, bütün anlamsız günlerini sevdiğin karınla güzel güzel yaşayarak geçir. Çünkü hayattan ve güneşin altında harcadığın emekten payına düşecek olan budur.
Uzikondwerera moyo pamodzi ndi mkazi wako amene umamukonda, masiku onse a moyo uno wopanda phindu, amene Mulungu wakupatsa pansi pano. Pakuti mkaziyo ndiye gawo la moyo wako pa ntchito yako yolemetsa pansi pano.
10 Çalışmak için eline ne geçerse, var gücünle çalış. Çünkü gitmekte olduğun ölüler diyarında iş, tasarı, bilgi ve bilgelik yoktur. (Sheol h7585)
Ntchito iliyonse imene ukuyigwira, uyigwire ndi mphamvu zako zonse, pakuti ku manda kumene ukupita kulibe kugwira ntchito, kulibe malingaliro, chidziwitso ndiponso nzeru. (Sheol h7585)
11 Güneşin altında bir şey daha gördüm: Yarışı hızlı koşanlar, Savaşı yiğitler, Ekmeği bilgeler, Serveti akıllılar, Beğeniyi bilgililer kazanmaz. Ama zaman ve şans hepsinin önüne çıkar.
Ine ndinaonanso chinthu china pansi pano: opambana pa kuthamanga si aliwiro, kapena opambana pa nkhondo si amphamvu, ndiponso okhala ndi chakudya si anzeru, kapena okhala ndi chuma si odziwa zambiri, kapena okomeredwa mtima si ophunzira; koma mwayi umangowagwera onsewa pa nthawi yake.
12 Dahası insan kendi vaktini bilmez: Balığın acımasız ağa, kuşun kapana düştüğü gibi, İnsanlar da üzerlerine ansızın çöken kötü zamana yakalanırlar.
Kungoti palibe munthu amene amadziwa kuti nthawi yake idzafika liti: monga momwe nsomba zimagwidwira mu ukonde, kapena mmene mbalame zimakodwera mu msampha, chimodzimodzinso anthu amakodwa mu msampha pa nthawi yoyipa, pamene tsoka limawagwera mosayembekezera.
13 Güneşin altında bilgelik olarak şunu da gördüm, beni çok etkiledi:
Ine ndinaonanso pansi pano chitsanzo ichi cha nzeru chimene chinandikhudza kwambiri:
14 Çok az insanın yaşadığı küçük bir kent vardı. Güçlü bir kral saldırıp onu kuşattı. Karşısına büyük rampalar kurdu.
Panali mzinda waungʼono umene unali ndi anthu owerengeka. Ndipo mfumu yamphamvu inabwera kudzawuthira nkhondo, inawuzungulira ndi kumanga mitumbira yankhondo.
15 Kentte yoksul ama bilge bir adam vardı. Bilgeliğiyle kenti kurtardı. Ne var ki, kimse bu yoksul adamı anmadı.
Tsono mu mzindamo munali munthu wosauka koma wanzeru, ndipo anapulumutsa mzindawo ndi nzeru zakezo. Koma palibe amene anakumbukira munthu wosaukayo.
16 Bunun üzerine, “Bilgelik güçten iyidir” dedim, “Ne yazık ki, yoksul insanın bilgeliği küçümseniyor, söyledikleri dikkate alınmıyor.”
Choncho ine ndinati, “Nzeru ndi yopambana mphamvu.” Koma nzeru ya munthu wosauka imanyozedwa, ndipo palibe amene amalabadirako za mawu ake.
17 Bilgenin sessizce söylediği sözler, Akılsızlar arasındaki önderin bağırışından iyidir.
Mawu oyankhula mofatsa a munthu wanzeru, anthu amawasamalira kwambiri kupambana kufuwula kwa mfumu ya zitsiru.
18 Bilgelik silahtan iyidir, Ama bir deli çıkar, her şeyi berbat eder.
Nzeru ndi yabwino kupambana zida zankhondo, koma wochimwa mmodzi amawononga zinthu zambiri zabwino.

< Vaiz 9 >