< Daniel 11 >

1 “Medli Darius'un krallığının birinci yılında Mikail'i destekleyip korumak için onun yanında durdum.”
Ndipo chaka choyamba cha Dariyo Mmedi ine Mikayeli ndinabwera kumuthandiza ndi kumuteteza Gabrieli.
2 “Şimdi sana gerçeği bildireceğim: Pers krallığında üç kral daha ortaya çıkacak. Ama dördüncü kral öbür üçünden daha zengin olacak. Zenginliği sayesinde elde edeceği güçle herkesi Grek ülkesine karşı kışkırtacak.
“Ndipo tsopano ndikuwuza zoona: Mafumu ena atatu adzalamulira ku Peresiya, ndipo kenaka padzadzuka mfumu yachinayi imene idzakhala yolemera kwambiri kuposa onsewo. Popeza kuti idzakhala ndi mphamvu chifukwa cha chuma chake, idzadzutsa onse kuti alimbane ndi ufumu wa Grisi.
3 Sonra güçlü bir kral çıkacak. Büyük yetkiyle krallık edecek ve dilediği gibi davranacak.
Kenaka mfumu yamphamvu idzafika imene idzalamulira ndi ufumu waukulu ndi kuchita zimene ifuna.
4 Ne var ki, o gücünün doruğundayken, krallığı darmadağın edilecek, göğün dört rüzgarı gibi dört parçaya bölünecek. Krallık onun soyundan gelenlere geçmeyecek, yerine geçenlerin hiçbiri onun gibi egemenlik sürmeyecek. Krallığı yıkılıp başkalarına verilecek.
Koma ufumu wake ukadzafika pachimake, udzawonongedwa ndi kugawidwa mʼzigawo zinayi. Ufumuwo sudzaperekedwa kwa zidzukulu zake, ndipo olowa mʼmalo mwake sadzakhala ndi mphamvu monga anali nazo, chifukwa ufumu wake udzazulidwa ndi kuperekedwa kwa ena.
5 “Güney Kralı güçlenecek. Ancak komutanlarından biri ondan daha çok güçlenecek ve krallığı büyük olacak.
“Mfumu ya kummwera idzakhala yamphamvu, koma mmodzi mwa akalonga ake adzakhala ndi mphamvu kuposa iyo; adzalamulira ufumu wake waukulu kwambiri.
6 Birkaç yıl sonra bu ikisi uzlaşacak. Güney Kralı yapılan uzlaşmayı onaylamak için kızını Kuzey Kralı'na eş olarak verecek. Ama kız gücünü koruyamayacak. Kralın ömrü de gücü de uzun sürmeyecek. Bu arada kızla babası da, ona eşlik edenlerle onu destekleyen de ele verilecek.
Patapita zaka zingapo, mfumu ya kummwera ndi mfumu ya kumpoto adzachita pangano. Mwana wamkazi wa mfumu ya kummwera adzapita nakakwatiwa ndi mfumu ya kumpoto pokhazikitsa pangano la mtendere, koma ulamuliro wake pamodzi ndi wa mwana wake sudzakhalitsa. Mʼmasiku amenewo iye, mwamuna wake, mwana wake ndi atumiki ake, onse adzaperekedwa kwa adani.
7 “Babasının yerine kızın ailesinden biri ortaya çıkacak. Kuzey Kralı'nın ordusuna saldırıp kalesini alacak. Onlarla savaşıp yenecek.
“Mmodzi wochokera ku banja la mkaziyo adzadzuka nadzalamulira mʼmalo mwake. Iye adzamenyana ndi ankhondo a mfumu ya kumpoto ndi kulowa mʼmalo ake otetezedwa; adzachita nawo nkhondo ndi kupambana.
8 Onların ilahlarını, dökme putlarını, değerli altın ve gümüş kaplarını alıp Mısır'a götürecek. Kuzey Kralı'nı birkaç yıl rahat bırakacak.
Iye adzalandanso milungu yawo, mafano awo achitsulo, ndi ziwiya zawo zamtengowapatali zasiliva ndi golide ndi kubwerera nazo ku Igupto. Adzaleka osayithira nkhondo mfumu ya kumpoto kwa zaka zingapo.
9 Sonra Kuzey Kralı gidip Güney Kralı'nın ülkesine saldıracak, ardından kendi ülkesine dönecek.
Kenaka mfumu ya kumpoto idzathira nkhondo dziko la mfumu ya kummwera koma idzalephera ndi kubwerera kwawo.
10 Kuzey Kralı'nın oğulları savaşa hazırlanarak çok büyük bir ordu toplayacaklar. Ordu sel gibi taşacak, önüne geleni alıp götürecek, gelip Güney Kralı'nın kalesine dayanacak.
Ana ake adzakonzekera nkhondo ndi kusonkhanitsa gulu lankhondo lalikulu, limene lidzathira nkhondo mfumu yakummwera ngati chigumula mpaka kumalo ake otetezedwa.
11 “Güney Kralı öfkeyle çıkıp Kuzey Kralı'na karşı savaşacak. Kuzey Kralı büyük bir ordu topladığı halde, bu ordu Güney Kralı'nın eline teslim edilecek.
“Kenaka mfumu yakummwera idzatuluka mokwiya ndi kumenya nkhondo ndi mfumu yakumpoto, imene idzasonkhanitsa gulu lalikulu la nkhondo, koma idzayigonjetsa.
12 Bu büyük ordu yenilgiye uğrayınca Güney Kralı gurura kapılacak. On binlerce insanı öldürecek, ama zaferi uzun sürmeyecek.
Gulu la nkhondoli likadzagwidwa, mfumu yakummwera idzayamba kudzikuza ndipo idzapha anthu miyandamiyanda, koma kupambanaku sikudzapitirira.
13 Çünkü Kuzey Kralı öncekinden daha büyük bir ordu toplayacak ve birkaç yıl sonra büyük, iyi donatılmış bir orduyla ülkeye doğru ilerleyecek.
Popeza mfumu ya kumpoto idzasonkhanitsa gulu lina lankhondo, lochulukirapo kuposa loyamba; ndipo patapita zaka zingapo idzabwera ndi chigulu chachikulu cha nkhondo chokonzekeratu ndi zida.
14 “Bu sırada birçokları Güney Kralı'na karşı çıkacak. Senin halkından bazı zorbalar da, görüm yerine gelsin diye ayaklanacak, ama yenilgiye uğrayacaklar.
“Nthawi imeneyo ambiri adzawukira mfumu ya kummwera. Anthu achisokonezo pakati panu nawonso adzawukira pokwaniritsa masomphenya, koma sadzapambana.
15 Sonra Kuzey Kralı gelip toprak yığarak tepecikler yapacak ve surlu kenti ele geçirecek. Güney Kralı'nın güçleri buna karşı duramayacak. En seçme askerlerinin bile karşı durmaya güçleri yetmeyecek.
Kenaka mfumu ya kumpoto idzafika ndikuzinga mzinda powunda nthumbira za nkhondo ndipo idzagonjetsa mzinda wotetezedwa. Gulu lankhondo la kummwera lidzasowa mphamvu; ngakhale akatswiri awo ankhondo sadzakhala ndi mphamvu zogonjetsera ankhondo a kumpoto.
16 Kente saldıran Kuzey Kralı dilediği gibi davranacak, kimse ona karşı duramayacak. Güzel Ülke'yi yönetecek, yıkıp yok etme yetkisi onun elinde olacak.
Mfumu ya kumpoto idzachita zofuna zake; palibe aliyense adzayigonjetse. Idzakhazikitsa ulamuliro wake mu Dziko Lokongola. Zonse zidzakhala mu ulamuliro wa mfumu yakumpoto ija.
17 Krallığının bütün gücünü toplayıp Güney Kralı'nın üzerine yürümeyi amaçlayacak ve Güney Kralı'yla bir antlaşma yapacak. Ülkesini yerle bir etmek için kızını eş olarak ona verecek. Ama tasarısı başarılı olmayacak, ona yarar sağlamayacak.
Idzafika ndi mphamvu za ufumu wake wonse ndipo idzayesa kuchita pangano la mtendere ndi mfumu ya kummwera. Ndipo idzamupatsa mwana wake wamkazi kuti amukwatire ndi cholinga cholanda ufumu, koma zolinga zake sizidzatheka kapena kumuthandiza.
18 Bundan sonra deniz kıyısındaki bölgelere yönelecek, birçoklarını ele geçirecek. Ne var ki, bir komutan onun saygısızlıklarını sona erdirecek, saygısızlığının karşılığını verecek.
Kenaka idzatembenukira ku mayiko a mʼmbali mwa nyanja ndi kulanda mizinda yambiri, koma mtsogoleri wina wa nkhondo adzathetsa kudzikuza kwakeko ndipo adzabwezera chipongwecho kwa iye.
19 Bunun üzerine Kuzey Kralı kendi ülkesinin kalelerine yönelecek, ama tökezleyip düşecek. Bir daha da ortaya çıkmayacak.
Zikadzatha izi, mfumu idzabwerera ku malo otetezedwa a dziko la kwawo koma idzapunthwa ndi kugwa osapezekanso.
20 “Yerine geçen kral, krallığının yüceliği için zorla vergi toplayacak birini gönderecek. Ama birkaç gün içinde öfkesiz ve savaşsız yok edilecek.
“Mfumu imene idzatenga malo ake idzatumiza wokhometsa msonkho kuti chuma cha ufumu wake chichuluke. Komabe mʼzaka zochepa mfumuyo idzawonongedwa osati mu mkwiyo kapena ku nkhondo.
21 “Yerine krallıkla onurlandırılmamış değersiz biri geçecek. Halk güvenlik içindeyken, kurduğu düzenler sayesinde gelip krallığı ele geçirecek.
“Mʼmalo mwake mudzalowa munthu wonyozeka amene si wa banja laufumu. Iye adzabwera pamene anthu akuganiza kuti ali pa mtendere, ndipo adzalanda ufumuwo mwa chinyengo.
22 Çok güçlü orduları süpürüp yok edecek; antlaşma önderi de yok edilecek.
Kenaka adzagonetsa gulu lalikulu lankhondo kuphatikizapo Mkulu wa Ansembe wapangano.
23 Onunla antlaşma yaptıktan sonra hileye başvuracak. Az sayıda insanla gittikçe güçlenecek.
Atatha kuchita naye pangano, iye adzachita monyenga, ndipo ngakhale adzakhale ndi anthu ochepa adzakhalabe ndi mphamvu.
24 Beklenmedik bir anda ilin zengin bölgelerine saldırıp babalarının, atalarının yapmadığı şeyleri yapacak. Adamlarına yağma ve çapul malı, servetler dağıtacak. Kalelere saldırmak için düzenler kuracak, ama bu uzun sürmeyecek.
Mwadzidzidzi, iye adzazithira nkhondo zigawo zolemera kwambiri ndipo adzachita zimene makolo ake ngakhale agogo ake sanachitepo. Iye adzagawira zolanda, zofunkha ndi chuma kwa omutsatira. Adzachita chiwembu cholanda mizinda yotetezedwa koma kwa kanthawi kochepa.
25 “Gücünü ve cesaretini toplayarak büyük bir orduyla Güney Kralı'na karşı çıkacak. Güney Kralı da büyük ve çok güçlü bir orduyla savaşacak. Ne var ki, kurulan düzenler yüzünden ona karşı duramayacak.
“Mfumu ya kumpoto idzalimba mtima, ndipo idzasonkhanitsa gulu lalikulu la ankhondo kuti lithire nkhondo mfumu yakummwera. Mfumu yakummwera ndi gulu lake lankhondo lalikulu ndi lamphamvu idzathirana nkhondo ndi mfumu yakumpoto koma sidzapambana chifukwa cha ziwembu zimene adzamukonzera.
26 Sofrasından yiyenler Güney Kralı'nı yıkmaya çalışacaklar; ordusu dağılacak, birçokları vurulup öldürülecek.
Amene amadya chakudya ndi mfumu adzamuukira; gulu lake lankhondo lidzagonjetsedwa, ndipo ambiri adzafera ku nkhondo.
27 Her iki kral da kötülük tasarlayacak. Aynı masada oturup birbirlerine yalan söyleyecekler. Ancak bu bir yarar sağlamayacak. Çünkü son yine de belirlenen zamanda gelecek.
Mafumu awiriwa mitima yawo idzalinga ku zoyipa. Azidzanamizana ali pa tebulo limodzi, koma zolinga zawo sizidzatheka chifukwa nthawi idzakhala isanakwane.
28 Kuzey Kralı büyük bir servetle ülkesine dönecek, ama amacı kutsal antlaşmaya karşı gelmek olacak. Dilediğini yaptıktan sonra ülkesine dönecek.
Mfumu ya kumpoto idzabwerera ku dziko la kwawo ndi chuma chambiri, koma mtima wake udzafunitsitsa pangano lopatulika. Idzawononga panganolo ndipo kenaka idzabwerera ku dziko lake.
29 “Belirlenen zamanda dönüp yine Güney'e saldıracak. Ancak bu kez sonuç öncekinden farklı olacak.
“Patapita nthawi mfumu ya kumpoto idzabwereranso kummwera koma sidzapambana monga inachitira kale.
30 Ona karşı koymak için Kittim'den gelen gemiler cesaretini kıracak. Geri dönecek ve öfkeyle kutsal antlaşmaya karşı çıkacak, kutsal antlaşmayı bırakanları yine kayıracak.
Sitima zapamadzi zochokera ku mayiko a ku madzulo zidzalimbana naye, ndipo adzataya mtima. Kenaka idzabwerera mopsa mtima ndi kudzalimbana ndi chipembedzo cha anthu opatulika. Idzabwerera ndi kuchitira chifundo amene sadzasunga pangano loyera.
31 “Askerleri gidip tapınakla kaleyi kirletecek, günlük sunuları kaldırıp yıkıcı iğrenç şeyi koyacaklar.
“Ankhondo ake adzayipitsa linga la Nyumba ya Mulungu ndipo adzathetsa nsembe za tsiku ndi tsiku. Kenaka adzakhazikitsa chonyansa chimene chabweretsa chiwonongeko.
32 Kuzey Kralı antlaşmayı bozanları yaltaklanarak ayartacak, ama Tanrısı'nı tanıyan halk var gücüyle ona karşı duracak.
Ndi mawu oshashalika mfumuyo idzakopa amene anaphwanya pangano, koma anthu amene amadziwa Mulungu wawo adzalimbika ndipo adzayikana mfumuyo kwathunthu.
33 “Halkın arasındaki bilge kişiler birçoklarını eğitecekler. Ama bir süre bu kişiler ya kılıçla öldürülecek, yakılacak, tutsak edilecek ya da mallarından edilecekler.
“Amene ndi anzeru adzalangiza ambiri. Koma patapita kanthawi adzaphedwa ndi lupanga kapena kutenthedwa, kapena kugwidwa kapena kulandidwa katundu.
34 Yenilgiye uğrayınca biraz yardım görecekler. İçtenlikten uzak birçok kişi onlardan yana geçecek.
Pa nthawi yozunzikayi ena adzawathandiza pangʼono, koma ambiri othandizawo adzakhala achinyengo.
35 Bilgelerden kimisi tökezleyecek; öyle ki, son gelinceye dek arınıp temizlenebilsin, lekesiz duruma gelebilsinler. Çünkü son yine de belirlenen zamanda gelecek.
Ena mwa anzeruwo adzaphedwa ndi cholinga chakuti ayengedwe, otsala mwa iwo ayeretsedwe ndi kukhala wopanda banga kufikira nthawi yomaliza, popeza idzafika ndithu nthawi imene Mulungu wayika.
36 “Kral dilediği gibi davranacak. Kendini bütün tanrılardan daha büyük, daha yüce gösterecek, tanrıların Tanrısı'na karşı duyulmamış sözler söyleyecek. Tanrı'nın öfkesi tamamlanıncaya dek başarılı olacak. Çünkü tasarlanan, yerine gelecektir.
“Mfumu ya kumpoto idzachita zimene ikufuna. Idzadzikweza ndi kudziyesa yopambana mulungu aliyense ndipo idzanenera za mwano Mulungu wa milungu. Iyo idzapambana mpaka nthawi yoti Mulungu ayilange mwa mkwiyo itakwana popeza chimene chatsimikizika chiyenera kuchitika.
37 Kral hiçbir tanrıya, atalarının ilahlarına da kadınların bağlandığına da ilgi göstermeyecek. Kendisini hepsinden üstün görecek.
Mfumuyo idzanyoza milungu ya makolo ake ndiponso mulungu wokondedwa ndi akazi, sidzachitiranso ulemu mulungu aliyense, koma idzadzikweza yokha pamwamba pa onse.
38 Bu ilahların yerine, kaleler ilahını yüceltecek. Atalarının tanımadığı bu ilaha altın, gümüş, değerli taşlar, pahalı armağanlar sunup onu onurlandıracak.
Mʼmalo mwa onsewo, idzachitira ulemu mulungu wachitetezo; mulungu wosadziwika ndi makolo ake. Iyo idzapereka kwa mulunguyo golide ndi siliva, ndi miyala yokongola, ndiponso mphatso za pamwamba kwambiri.
39 Bu yabancı ilahın yardımıyla en güçlü kalelere saldıracak; onu kabul edenleri alabildiğine onurlandıracak, onları birçoklarının başına önder atayacak, ülkeyi ödül olarak onlar arasında bölüştürecek.
Anthu opembedza mulungu wachilendo adzakhala ngati linga lake. Idzalemekeza iwowa kwambiri, ndipo idzawayika kuti alamulire anthu ambiri. Idzawagawira dziko ngati malipiro awo.
40 “Son gelince, Güney Kralı Kuzey Kralı'yla savaşa tutuşacak. Kuzey Kralı savaş arabalarıyla, atlılarla, birçok gemilerle saldıracak. Her şeyi süpürüp götüren sel gibi taşarak birçok ülkeden geçecek.
“Pa nthawi yomaliza mfumu yakummwera idzachita nkhondo ndi mfumu yakumpoto. Koma mfumu yakumpotoyi idzayikantha ndi magaleta ndi akavalo ndi sitima zapamadzi zambiri ngati mphepo yamkokomo. Idzalowa mʼmayiko ambiri ndikuwakokolola onse ngati madzi osefukira.
41 Güzel Ülke'ye de girecek, birçok ülke yenilgiye uğrayacak. Ancak Edom, Moav ve Ammon önderleri onun elinden kurtulacak.
Idzalowanso mʼDziko Lokongola ndipo anthu ambiri adzaphedwa. Koma Edomu, Mowabu ndi olamulira a Amoni adzapulumuka.
42 Öbür ülkelere de saldıracak. Mısır bile elinden kurtulmayacak.
Idzathira nkhondo mayiko ambiri ndipo ngakhale Igupto sadzapulumuka.
43 Altın ve gümüş hazinelerine, Mısır'ın bütün değerli eşyalarına el koyacak. Luvlular'la Kûşlular onun ardınca yürüyecekler.
Idzalanda chuma cha golide, siliva, ndi zonse za mtengowapatali za ku Igupto, ndiponso anthu a ku Libiya ndi Akusi adzagonja kwa iwo.
44 Ne var ki, doğudan ve kuzeyden gelen haberler onu ürkütecek. Birçoklarını yıkıp yok etmek için büyük öfkeyle yola çıkacak.
Koma uthenga wochokera kummawa ndi kumpoto udzayiopsa, ndipo idzapita ndi ukali kukawononga ndi kutheratu anthu ambiri.
45 Denizle güzel kutsal dağ arasında saray çadırlarını kuracak. Yine de yaşamı son bulacak ve ona yardım eden olmayacak.”
Mfumuyo idzayimika matenti ake aufumu, pakati pa nyanja ndi phiri lokongola. Komabe mapeto ake mfumuyo idzaphedwa, ndipo palibe amene adzayithandize.”

< Daniel 11 >