< Amos 2 >

1 RAB şöyle diyor: “Moavlılar'ın cezasını kaldırmayacağım. Çünkü günah üstüne günah işlediler, Edom Kralı'nın kemiklerini Kireçleşinceye dek yaktılar.
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu, mpaka kuwasandutsa phulusa,
2 Bu yüzden Moav'a ateş yağdıracağım, Yakıp yok edecek Keriyot saraylarını. Kargaşa, savaş naraları, Boru sesleri arasında ölecek Moav halkı.
Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti. Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa, mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.
3 Söküp atacağım içinden yöneticisini, Öldüreceğim onunla bütün görevlilerini.” RAB böyle diyor.
Ndidzawononga wolamulira wake ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,” akutero Yehova.
4 RAB şöyle diyor: “Yahudalılar'ın cezasını kaldırmayacağım. Çünkü günah üstüne günah işlediler, Reddettiler yasamı, Kurallarıma uymadılar; Yalancı putlar saptırdı onları, Atalarının da izlediği putlar.
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo akana lamulo la Yehova ndipo sanasunge malangizo ake, popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza, milungu imene makolo awo ankayitsatira,
5 Bu yüzden Yahuda'ya ateş yağdıracağım, Yakıp yok edecek Yeruşalim saraylarını.”
Ine ndidzatumiza moto pa Yuda, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”
6 RAB şöyle diyor: “İsrailliler'in cezasını kaldırmayacağım, Çünkü günah üstüne günah işlediler, Doğruyu para için, Yoksulu bir çift çarık için sattılar.
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva, ndi osauka ndi nsapato.
7 Onlar ki, Yoksulun başını toz toprak içinde çiğner Ve mazlumun hakkını bir yana iterler. Baba oğul aynı kızla yatarak Kutsal adımı kirletirler.
Amapondereza anthu osauka ngati akuponda fumbi, ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa. Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo, ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.
8 Her sunağın yanına, Rehin alınan giysilerin üzerine uzanır, Tanrıları'nın Tapınağı'nda Ceza karşılığı alınan şarabı içerler.
Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe pa zovala zimene anatenga ngati chikole. Mʼnyumba ya mulungu wawo amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.
9 Ama ben onların önünde Amorlular'ı yok ettim; Sedir ağaçları kadar boylu, Meşe kadar güçlü olsa da, Yukarıdan meyvesini, Aşağıdan kökünü kuruttum.
“Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo, ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu. Ndinawononga zipatso zawo ndiponso mizu yawo.
10 Sizi Mısır'dan ben çıkardım, Amor topraklarını sahiplenesiniz diye Çölde kırk yıl size yol gösterdim.
“Ine ndinakutulutsani ku Igupto, ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kudzakupatsani dziko la Aamori.
11 Oğullarınızdan peygamberler, Gençlerinizden bana adanmış kişiler atadım. Doğru değil mi, ey İsrailliler?” RAB böyle diyor.
Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri, ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri. Kodi si choncho, inu Aisraeli?” akutero Yehova.
12 “Sizse bana adanmış kişilere şarap içirdiniz Ve peygamberlere, ‘Peygamberlik etmeyin!’ Diye buyruk verdiniz.
“Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja, ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.
13 “Tahıl yüklü araba toprağı nasıl ezerse, İşte ben de sizi öyle ezeceğim.
“Tsono Ine ndidzakupsinjani monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.
14 Hızlı koşan kaçamayacak, Güçlü gücünü gösteremeyecek, Yiğit canını kurtaramayacak,
Munthu waliwiro sadzatha kuthawa, munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga, wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.
15 Okçu yerini koruyamayacak, Ayağı tez olan uzaklaşamayacak, Atlı canını kurtaramayacak,
Munthu wa uta sadzalimbika, msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka, ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.
16 En yürekli yiğitler bile O gün silahlarını bırakıp kaçacak.” RAB böyle diyor.
Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri adzathawa ali maliseche pa tsikulo,” akutero Yehova.

< Amos 2 >