< 2 Samuel 8 >
1 Bir süre sonra Davut Filistliler'i yenip boyunduruğu altına aldı ve Meteg-Amma'yı Filistliler'in yönetiminden çıkardı.
Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndi kuwapambana ndipo analanda Metegi Ama kuchoka mʼmanja mwa Afilistiwo.
2 Moavlılar'ı da bozguna uğrattı. Onları yere yatırıp iple ölçtü. Ölçtüğü iki sırayı öldürdü, bir bütün sırayı sağ bıraktı. Moavlılar Davut'un haraç ödeyen köleleri oldular.
Davide anagonjetsanso Amowabu. Iye anawalamula kuti agone pansi mʼmizere itatu pa gulu lililonse ndipo anawayeza ndi chingwe. Pa gulu lililonse ankapha anthu amene anali pa mizere iwiri yoyamba, kusiyapo mzere wachitatu. Kotero Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Davide ndipo ankapereka msonkho.
3 Davut Fırat'a kadar krallığını yeniden kurmaya giden Sova Kralı Rehov oğlu Hadadezer'i de yendi.
Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
4 Bin yedi yüz atlısıyla yirmi bin yaya askerini ele geçirdi. Yüz savaş arabası için gereken atların dışındaki bütün atları da sakatladı.
Davide analanda magaleta 1,000, anthu 7,000 okwera magaleta pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
5 Sova Kralı Hadadezer'e yardıma gelen Şam Aramlıları'ndan yirmi iki bin kişiyi öldürdü.
Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
6 Sonra Şam Aramlıları'nın ülkesine askeri birlikler yerleştirdi. Onlar da Davut'un haraç ödeyen köleleri oldular. RAB Davut'u gittiği her yerde zafere ulaştırdı.
Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
7 Davut Hadadezer'in komutanlarının taşıdığı altın kalkanları alıp Yeruşalim'e götürdü.
Davide anatenga zishango zagolide za akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
8 Ayrıca Hadadezer'in yönetimindeki Betah ve Berotay kentlerinden bol miktarda tunç aldı.
Mfumu Davide inatenga mkuwa wambiri kuchokera ku Beta ndi Berotai, mizinda ya Hadadezeri.
9 Hama Kralı Toi, Davut'un Hadadezer'in bütün ordusunu bozguna uğrattığını duydu.
Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri,
10 Toi Kral Davut'u selamlamak ve Hadadezer'le savaşıp yendiği için onu kutlamak üzere oğlu Yoram'ı ona gönderdi. Çünkü Toi Hadadezer'le sürekli savaşmıştı. Yoram Davut'a altın, gümüş, tunç armağanlar getirdi.
anatumiza mwana wake Yoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Yoramu anabweretsa ziwiya zasiliva, zagolide ndi zamkuwa.
11 Kral Davut bu armağanları yendiği bütün uluslardan –Aram, Moav, Ammonlular, Filistliler ve Amalekliler'den– ele geçirdiği altın ve gümüşle birlikte RAB'be adadı. Bunun yanısıra Sova Kralı Rehov oğlu Hadadezer'den yağmalanan altınla gümüşü de RAB'be adadı.
Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko onse amene anawagonjetsa:
Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki. Iye anaperekanso zolanda ku nkhondo zochokera kwa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba.
13 Davut Tuz Vadisi'nde on sekiz bin Edomlu öldürüp dönünce üne kavuştu.
Ndipo Davide anatchuka atabwera kokakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
14 Edom'un her yanına askeri birlikler yerleştirdi. Edomlular'ın tümü Davut'un köleleri oldular. RAB Davut'u gittiği her yerde zafere ulaştırdı.
Iye anayika maboma mʼdera lonse la Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
15 Bütün İsrail'de krallık yapan Davut halkına doğruluk ve adalet sağladı.
Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
16 Seruya oğlu Yoav ordu komutanı, Ahilut oğlu Yehoşafat devlet tarihçisiydi.
Yowabu mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika.
17 Ahituv oğlu Sadok'la Aviyatar oğlu Ahimelek kâhin, Seraya yazmandı.
Zadoki mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Seraya anali mlembi;
18 Yehoyada oğlu Benaya Keretliler'le Peletliler'in komutanıydı. Davut'un oğullarıysa kâhindi.
Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti; ndipo ana a Davide anali ansembe.