< 2 Samuel 7 >

1 Kral sarayına yerleşmişti. RAB de onu çevresindeki bütün düşmanlarından koruyarak rahata kavuşturdu.
Mfumu itakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, Yehova atayipatsa mpumulo kwa adani ake onse woyizungulira,
2 O sırada kral, Peygamber Natan'a, “Bak, ben sedir ağacından yapılmış bir sarayda oturuyorum. Oysa Tanrı'nın Sandığı bir çadırda duruyor!” dedi.
mfumuyo inawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Mulungu lili mu tenti.”
3 Natan, “Git, tasarladığın her şeyi yap, çünkü RAB seninledir” diye karşılık verdi.
Natani anayankha mfumu kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu chifukwa Yehova ali nanu.”
4 O gece RAB Natan'a şöyle seslendi:
Usiku umenewo mawu a Yehova anafika kwa Natani ndipo anati,
5 “Git, kulum Davut'a şöyle de: ‘RAB diyor ki, oturmam için bana sen mi tapınak yapacaksın?
“Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti: kodi ndiwe amene udzandimangira Ine nyumba yokhalamo?
6 İsrail halkını Mısır'dan çıkardığım günden bu yana konutta oturmadım. Bir çadırda orada burada konaklayarak dolaşıyordum.
Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda uku ndi uku ndipo mokhala mwanga munali mu tenti.
7 İsrailliler'le birlikte dolaştığım yerlerin herhangi birinde, halkım İsrail'i gütmesini buyurduğum İsrail önderlerinden birine, neden bana sedir ağacından bir konut yapmadınız diye hiç sordum mu?’
Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense atsogoleri awo, amene ndinamulamula kuweta anthu anga Aisraeli kuti, nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”
8 “Şimdi kulum Davut'a şöyle diyeceksin: ‘Her Şeye Egemen RAB diyor ki, halkım İsrail'e önder olasın diye seni otlaklardan ve koyun gütmekten aldım.
“Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
9 Her nereye gittiysen seninleydim. Önünden bütün düşmanlarını yok ettim. Adını dünyadaki büyük adamların adı gibi büyük kılacağım.
Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi.
10 Halkım İsrail için bir yurt sağlayıp onları oraya yerleştireceğim. Bundan böyle kendi yurtlarında otursunlar, bir daha rahatsız edilmesinler. Kötü kişiler de halkım İsrail'e hâkimler atadığım günden bu yana yaptıkları gibi, bir daha onlara baskı yapmasınlar. Seni bütün düşmanlarından kurtarıp rahata kavuşturacağım. “‘RAB senin için bir soy yetiştireceğini belirtiyor:
Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja,
monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzakupatsaninso mpumulo kwa adani anu onse. “‘Yehova akulengeza kwa iwe kuti Iye mwini adzakhazikitsa banja lako:
12 Sen ölüp atalarına kavuşunca, senden sonra soyundan birini ortaya çıkarıp krallığını pekiştireceğim.
Masiku ako akadzatha ndipo ukadzakapuma ndi makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, imene idzachokera mʼthupi mwako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.
13 Adıma bir tapınak kuracak olan odur. Ben de onun krallığının tahtını sonsuza dek sürdüreceğim.
Iye ndiye amene adzamangire nyumba Dzina langa, ndipo Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya.
14 Ben ona baba olacağım, o da bana oğul olacak. Kötülük yapınca, onu insanların değneğiyle, insanların vuruşlarıyla yola getireceğim.
Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Akadzachita choyipa, Ineyo ndidzamulanga ndi ndodo ndi zikwapu za anthu.
15 Ama senin önünden kaldırdığım Saul'dan esirgediğim sevgiyi hiçbir zaman esirgemeyeceğim.
Koma sindidzasiya kumukonda, monga ndinachitira ndi Sauli, amene ndinamuchotsa iwe usanakhale mfumu.
16 Soyun ve krallığın sonsuza dek önümde duracak; tahtın sonsuza dek sürecektir.’”
Nyumba yako ndi ufumu wako zidzakhala zamuyaya pamaso panga. Mpando wako waufumu udzakhazikika kwamuyaya!’”
17 Böylece Natan bütün bu sözleri ve görümleri Davut'a aktardı.
Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
18 Bunun üzerine Kral Davut gelip RAB'bin önünde oturdu ve şöyle dedi: “Ey Egemen RAB, ben kimim, ailem nedir ki, beni bu duruma getirdin?
Choncho Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati: “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ine ndine yani, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?”
19 Ey Egemen RAB, sanki bu yetmezmiş gibi, kulunun soyunun geleceği hakkında da söz verdin. Ey Egemen RAB, insanlarla hep böyle mi ilgilenirsin?
Ndipo kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Kodi umu ndi mmene mumachitira ndi munthu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse?
20 Ben sana başka ne diyebilirim ki! Çünkü, ey Egemen RAB, kulunu tanıyorsun.
Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu? Pakuti Inu Ambuye Wamphamvuzonse mukumudziwa mtumiki wanu.
21 Sözünün hatırı için ve isteğin uyarınca bu büyüklüğü gösterdin ve kuluna bildirdin.
Chifukwa cha mawu anu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwachiwulula kwa mtumiki wanu.
22 “Yücesin, ey Egemen RAB! Bir benzerin yok, senden başka Tanrı da yok! Bunu kendi kulaklarımızla duyduk.
Inu ndinu wamkulu, Yehova Wamphamvuzonse! Palibe wina wofanana nanu, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha, monga tamvera ndi makutu athu.
23 Halkın İsrail'e benzer tek bir ulus yok dünyada. Kendi halkın olsun diye onları kurtarmaya gittin. Çünkü onlar için de, ülken için de büyük ve görkemli işler yapmakla ün saldın. Mısır'dan kendin için kurtardığın halkın önünden ulusları ve tanrılarını kovdun.
Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina ndi milungu yawo pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto?
24 Halkın İsrail'i sonsuza dek kendi halkın olarak benimsedin ve sen de, ya RAB, onların Tanrısı oldun.
Inu mwawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
25 “Şimdi, ya RAB Tanrı, kuluna ve onun soyuna ilişkin verdiğin sözü sonsuza dek tut, sözünü yerine getir.
“Ndipo tsopano Yehova Mulungu, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake. Chitani monga mwalonjezera,
26 Öyle ki, insanlar, ‘Her Şeye Egemen RAB İsrail'in Tanrısı'dır!’ diyerek adını sonsuza dek yüceltsinler ve kulun Davut'un soyu da önünde sürsün.
kotero dzina lanu lidzakhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
27 “Ey Her Şeye Egemen RAB, İsrail'in Tanrısı! ‘Senin için bir soy çıkaracağım’ diye kuluna açıkladın. Bundan dolayı kulun sana bu duayı etme yürekliliğini buldu.
“Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, mwaululira mtumiki wanu ponena kuti, ‘Ine ndidzakumangira iwe nyumba!’ Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere.
28 Ey Egemen RAB, sen Tanrı'sın! Sözlerin gerçektir ve kuluna bu iyilikleri söz verdin.
Inu Ambuye Wamphamvuzonse, ndinu Mulungu! Mawu anu ndi odalirika, ndipo mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu.
29 Şimdi önünde sonsuza dek sürmesi için kulunun soyunu kutsamanı diliyorum. Çünkü, ey Egemen RAB, sen böyle söz verdin ve kulunun soyu kutsamanla sonsuza dek kutlu kılınacak.”
Ndipo tsopano chikukomereni kudalitsa banja la mtumiki wanu, kuti likhale mpaka muyaya pamaso panu. Pakuti Inu, Yehova Wamphamvuzonse, mwayankhula, ndipo ndi mʼdalitso wanu banja la mtumiki wanu lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”

< 2 Samuel 7 >