< 2 Samuel 24 >
1 RAB İsrail halkına yine öfkelendi. Davut'u onlara karşı kışkırtarak, “Git, İsrail ve Yahuda halkını say” dedi.
Nthawi inanso Yehova anawakwiyira Aisraeli ndipo anawutsa mtima wa Davide kuti awavutitse ndipo anati, “Pita kawerenge Aisraeli ndi Ayuda.”
2 Kral, yanında bulunan ordu komutanı Yoav'a şu buyruğu verdi: “Dan'dan Beer-Şeva'ya dek İsrail'in bütün oymaklarına gidip halkı sayın ki, halkın sayısını bileyim.”
Choncho mfumu inati kwa Yowabu pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo amene anali nawo. “Pitani pakati pa mafuko onse a Israeli kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba kuti mukawerenge anthu omenya nkhondo ndi cholinga choti ndidziwe chiwerengero chawo.”
3 Ama Yoav, “RAB Tanrın halkını yüz kat daha çoğaltsın, efendim kralım da bunu görsün!” diye karşılık verdi, “Ancak, efendim kralım neden bunu istiyor?”
Koma Yowabu anayankha mfumu kuti, “Yehova Mulungu wanu achulukitse ankhondo anu kukhala miyandamiyanda, ndipo alole inu mbuye wanga mfumu mudzazione zimenezi. Koma nʼchifukwa chiyani inu mbuye wanga mfumu mukufuna kuchita zimenezi?”
4 Gelgelelim kralın sözü Yoav'la birlik komutanlarının sözünden baskın çıktı. Böylece kralın yanından ayrılıp İsrail'de sayım yapmaya gittiler.
Komabe mawu a mfumu anapambana mawu a Yowabu ndi atsogoleri a ankhondo. Choncho anachoka pamaso pa mfumu kupita kukawerenga anthu omenya nkhondo mu Israeli.
5 Şeria Irmağı'ndan geçerek Aroer yakınında, vadinin ortasındaki kentin güneyinde konakladılar. Oradan Gat'ı, Yazer'i, Gilat'ı, Tahtim-Hodşi topraklarını, Dan-Yaan'ı geçip Sayda'ya vardılar.
Atawoloka Yorodani, iwo anamanga misasa yawo pafupi ndi Aroeri kummwera kwa mzinda wa ku chigwa ndipo kenaka iwo anapita ku dziko la Gadi mpaka ku Yazeri.
Iwo anapita ku Giliyadi ndi ku chigwa cha Tahitimu Hodisi ndipo anapitirira mpaka ku Dani Yaani ndi madera ozungulira Sidoni.
7 Sonra Sur Kalesi'ne, Hivliler'le Kenanlılar'ın bütün kentlerine uğradılar. Sonunda Yahuda ülkesinin Negev bölgesindeki Beer-Şeva'ya ulaştılar.
Kenaka iwo anapita molunjika linga la ku Turo ndi ku mizinda yonse ya Ahivi ndi Akanaani. Pomaliza anapita ku Beeriseba ku Negevi wa ku Yuda.
8 Dokuz ay yirmi gün ülkeyi baştan başa dolaştıktan sonra Yeruşalim'e döndüler.
Atayendayenda mʼdziko lonse anabwerera ku Yerusalemu patapita miyezi isanu ndi inayi ndi masiku makumi awiri.
9 Yoav sayımın sonucunu krala bildirdi: İsrail'de kılıç kuşanabilen sekiz yüz bin, Yahuda'daysa beş yüz bin kişi vardı.
Yowabu anapereka chiwerengero cha anthu ankhondo kwa mfumu: Mu Israeli munali anthu 800,000 amphamvu amene amadziwa kugwiritsa ntchito lupanga ndipo mu Yuda munali anthu 500,000.
10 Davut sayım yaptıktan sonra kendisini suçlu buldu ve RAB'be, “Bunu yapmakla büyük günah işledim!” dedi, “Ya RAB, lütfen kulunun suçunu bağışla. Çünkü çok akılsızca davrandım.”
Davide anatsutsika mu mtima mwake atatha kuwerenga anthuwo ndipo anapemphera kwa Yehova kuti, “Ine ndachimwa kwambiri pa zimene ndachita. Tsono Yehova, ndikupempha kuti mukhululuke kulakwa kwa mtumiki wanu. Ine ndachita zopusa kwambiri.”
11 Ertesi sabah Davut uyandığında, RAB Davut'un bilicisi Peygamber Gad'a şöyle dedi: “Gidip Davut'a de ki, ‘RAB şöyle diyor: Önüne üç seçenek koyuyorum. Bunlardan birini seç de sana onu yapayım.’”
Davide asanadzuke mmawa mwake mawu a Yehova anafika kwa mneneri Gadi, mlosi wa Davide kuti,
“Pita ukamuwuze Davide kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikukupatsa zinthu zitatu izi. Usankhepo chimodzi pa zimenezi choti ndikuchitire.’”
13 Gad Davut'a gidip durumu anlattı ve şöyle dedi: “Ülkende yedi yıl kıtlık mı olsun? Yoksa seni kovalayan düşmanlarının önünden üç ay kaçmak mı istersin? Ya da ülkende üç gün salgın hastalık mı olsun? Beni gönderene ne yanıt vereyim, şimdi iyice düşün.”
Choncho Gadi anapita kwa Davide ndipo anati kwa iye, “Kodi mungakonde kuti mʼdziko mwanu mukhale njala kwa zaka zitatu? Kapena kuti mukhale mukuthawa adani anu kwa miyezi itatu? Kapena kuti mʼdziko muno mukhale mliri kwa masiku atatu? Tsopano, ganizirani bwino ndipo musankhe chomwe mudzamuyankhe amene wandituma.”
14 Davut, “Sıkıntım büyük” diye yanıtladı, “İnsan eline düşmektense, RAB'bin eline düşelim. Çünkü O'nun acıması büyüktür.”
Davide anati kwa Gadi, “Ine ndavutika kwambiri mu mtima mwanga. Ife atilange ndi Yehova pakuti chifundo chake ndi chachikulu, koma ndisalangidwe ndi anthu.”
15 Bunun üzerine RAB o sabahtan belirlenen zamana dek İsrail ülkesine salgın hastalık gönderdi. Dan'dan Beer-Şeva'ya dek halktan yetmiş bin kişi öldü.
Choncho Yehova anabweretsa mliri pa Aisraeli, kuyambira mmawa mpaka pa nthawi imene anafuna mwini wake, ndipo unapha anthu 70,000 kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba.
16 Melek Yeruşalim'i yok etmek için elini uzatınca, RAB göndereceği yıkımdan vazgeçti. Halkı yok eden meleğe, “Yeter artık! Elini çek” dedi. RAB'bin meleği Yevuslu Aravna'nın harman yerinde duruyordu.
Pamene mngelo anatambasula dzanja lake kuti awononge Yerusalemu, Yehova anamva chisoni chifukwa cha zowawazo ndipo anati kwa mngelo amene ankawononga anthu uja, “Basi kwakwanira! Leka kuwononga.” Nthawi imeneyo mngelo wa Yehova anali atayima pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.
17 Davut, halkı öldüren meleği görünce, RAB'be, “Günah işleyen benim, ben suç işledim” dedi, “Bu koyunlar ne yaptı ki? Ne olur beni ve babamın soyunu cezalandır.”
Davide ataona mngelo amene ankakantha anthu uja, anati kwa Yehova, “Ine ndi amene ndachimwa. Ine mʼbusa ndiye ndachita zoyipa. Anthuwa ali ngati nkhosa zosalakwa. Kodi iwowa achita chiyani? Langani ineyo pamodzi ndi banja langa.”
18 O gün Gad Davut'a gitti. Ona, “Gidip Yevuslu Aravna'nın harman yerinde RAB'be bir sunak kur” dedi.
Tsiku limenelo Gadi anapita kwa Davide ndi kukanena kuti, “Pitani kamangeni guwa lansembe la Yehova pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.”
19 Davut Gad'ın sözü uyarınca RAB'bin buyurduğu gibi gitti.
Ndipo Davide anapita monga momwe Yehova anamulamulira kudzera mwa Gadi.
20 Aravna bakınca kralla görevlilerinin kendisine doğru yaklaştıklarını gördü. Varıp kralın önünde yüzüstü yere kapandı.
Arauna atayangʼana ndi kuona mfumu ndi anthu ake akubwera kumene kunali iye, iyeyo anatuluka ndi kuwerama pamaso pa mfumu mpaka nkhope yake kugunda pansi.
21 Sonra, “Efendim kral niçin kulunun yanına geldi?” diye sordu. Davut, “RAB'be bir sunak kurmak üzere harman yerini senden satın almak için” diye yanıtladı, “Öyle ki, salgın hastalık halkın üzerinden kalksın.”
Arauna anati, “Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mfumu mwabwera kwa mtumiki wanu?” Davide anayankha kuti, “Kudzagula malo ako opunthira tirigu kuti ndimangire Yehova guwa lansembe kuti mliri uli pa anthuwa usiye.”
22 Aravna, “Efendim kral uygun gördüğünü alıp RAB'be sunsun” dedi, “İşte yakmalık sunu için öküzler ve odun için düvenlerle öküzlerin takımları!
Arauna anati kwa Davide, “Mbuye wanga mfumu mutenge chilichonse chimene chikukondweretseni ndi kuchipereka nsembe. Nazi ngʼombe zazimuna za nsembe yopsereza, nazi zopunthira tirigu ndi magoli angʼombe kuti zikhale nkhuni.
23 Ey kral, Aravna bütün bunları sana veriyor.” Sonra ekledi: “RAB Tanrın senden hoşnut olsun!”
Inu mfumu, Arauna akupereka zonsezi kwa inu mfumu.” Arauna anatinso kwa iye, “Yehova Mulungu wanu akuvomerezeni.”
24 Ne var ki kral, “Olmaz!” dedi, “Senden malını kesinlikle bir ücret karşılığında satın alacağım. Çünkü Tanrım RAB'be karşılığını ödemeden yakmalık sunular sunmam.” Böylece Davut harman yerini ve öküzleri elli şekel gümüş karşılığında satın aldı.
Koma mfumu inayankha Arauna kuti, “Ayi, Ine ndikunenetsa kuti ndikulipira. Sindidzapereka kwa Yehova Mulungu wanga nsembe yopsereza imene sindinavutikire.” Kotero Davide anagula malo wopunthira tiriguwo ndi ngʼombe ndipo anapereka kwa Araunayo masekeli asiliva makumi asanu.
25 Davut orada RAB'be bir sunak kurup yakmalık sunuları ve esenlik sunularını sundu. RAB de ülkeyle ilgili yakarıyı yanıtladı ve salgın hastalık İsrail'den kaldırıldı.
Davide anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo anaperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Ndipo Yehova anayankha pempherolo mʼmalo mwa dziko lonse, ndipo mliri unatha pa Aisraeli.