< 2 Samuel 18 >

1 Davut kendini destekleyen askerleri bir araya topladı. Onlara binbaşılar ve yüzbaşılar atadı.
Davide anasonkhanitsa anthu amene anali naye ndipo anasankha atsogoleri ena olamulira ankhondo 1,000 ndi ena olamulira ankhondo 100.
2 Sonra orduyu Seruya oğlu Yoav'ın, kardeşi Avişay'ın ve Gatlı İttay'ın denetiminde üç kol halinde gönderdi. Kral askerlere, “Ben de sizinle birlikte gideceğim” dedi.
Davide anatumiza asilikaliwo atawagawa patatu: gulu loyamba limalamulidwa ndi Yowabu, gulu lachiwiri limalamulidwa ndi Abisai ndipo gulu lachitatu limalamulidwa ndi Itai Mgiti. Mfumu inawuza asilikaliwo kuti, “Inenso ndipita nanu ndithu.”
3 Ancak askerler, “Bizimle gelmemelisin” diye karşılık verdiler, “Çünkü kaçmak zorunda kalırsak düşmanlarımız bizi umursamaz; yarımız ölse bile umursamazlar. Sen bizim gibi on bin adama değersin. Sen kentten bize yardım et, daha iyi.”
Koma anthuwo anati, “Inu musapite nafe. Ngati tidzathamangitsidwa, iwowo sadzasamala za ife. Ngakhale theka la ife litafa, iwo sadzasamalako. Koma inuyo ndinu ofunika kuposa asilikali 10,000. Nʼkwabwino kwambiri kuti inu muzititumizira chithandizo kuchokera ku mzindako.”
4 Kral, “Gözünüzde iyi olanı yapacağım” dedi. Adamları yüzer ve biner kişilik birlikler halinde kentten çıkarken kral kapının yanında duruyordu.
Mfumu inayankha kuti, “Ine ndichita chimene chili chokukomerani.” Kotero mfumu inayima pambali pa chipata pamene ankhondo onse amayenda mʼmagulu a anthu 100 ndi a 1,000.
5 Kral, Yoav'a, Avişay'a ve İttay'a, “Benim hatırım için genç Avşalom'a sert davranmayın” diye buyurdu. Bütün askerler kralın komutanlara Avşalom'a ilişkin buyruk verdiğini duydular.
Mfumu inalamulira Yowabu, Abisai ndi Itai kuti, “Mumukomere mtima Abisalomu chifukwa cha ine.” Ndipo asilikali onse anamva pamene mfumu imalamula izi za Abisalomu kwa wolamulira aliyense.
6 Davut'un ordusu İsrailliler'le savaşmak üzere tarlalara çıktı. Savaş Efrayim Ormanı'nda başladı.
Ankhondo anayenda kupita kukachita nkhondo ndi Israeli, ndipo nkhondo inachitika mʼnkhalango ya Efereimu.
7 İsrail ordusu Davut'un adamları önünde yenilgiye uğradı. Büyük bir kırım oldu. O gün yirmi bin kişi öldü.
Aisraeli anagonjetsedwa kumeneko ndi ankhondo a Davide. Tsiku limenelo anaphedwa anthu okwanira 20,000.
8 Savaş her yana yayıldı. O gün ormanda yok olanların sayısı kılıçtan geçirilenlerin sayısından daha çoktu.
Nkhondo inafalikira ku madera onse akumidzi ndipo anthu akufa chifukwa cha zoopsa za mʼnkhalango anali ambiri tsiku limenelo kuposa akufa ndi lupanga.
9 Avşalom ansızın Davut'un adamlarıyla karşılaştı. Avşalom katıra binmişti. Katır büyük bir yabanıl fıstık ağacının sık dalları altından geçerken, Avşalom'un başı dallara takıldı. Katır yoluna devam edince, Avşalom havada asılı kaldı.
Tsono zinachitika kuti Abisalomu anakumana ndi asilikali a Davide. Iye anali atakwera bulu ndipo pamene buluyo amadutsa pansi pa nthambi zambiri za mtengo wa thundu, mutu wa Abisalomu unakodwa mu mtengomo. Iye anasiyidwa atatsakamira mʼmalele, pamene bulu amene anakwerapoyo amapitirira.
10 Adamlardan biri bunu gördü. Yoav'a, “Avşalom'u bir yabanıl fıstık ağacına asılı gördüm” diye bildirdi.
Mmodzi mwa asilikali ataona zimenezi, anamuwuza Yowabu kuti, “Ine ndamuona Abisalomu ali lende mu mtengo wa thundu.”
11 Yoav, haberi verene, “Onu gördün mü? Neden onu orada öldürmedin? Sana on parça gümüşle bir kemer verirdim” dedi.
Yowabu anati kwa munthu amene anamuwuza zimenezi, “Ukuti chiyani! Unamuona? Nʼchifukwa chiyani sunamukanthire pansi pomwepo? Ndipo ine ndikanakupatsa ndalama za siliva khumi ndi lamba wausilikali.”
12 Ama adam, “Elime bin parça gümüş saysan bile, kralın oğluna elimi kaldırmam” diye yanıtladı, “Çünkü kralın sana, Avişay'a ve İttay'a, ‘Benim hatırım için genç Avşalom'u koruyun’ diye buyruk verdiğini duyduk.
Koma munthuyo anayankha kuti, “Ngakhale atandipatsa mʼmanja mwanga ndalama zasiliva 1,000, sindingatambasule dzanja langa kupha mwana wa mfumu. Ife tikumva, mfumu inalamula inu Abisai ndiponso Itai kuti, ‘Mutetezeni mnyamatayo Abisalomu chifukwa cha ine!’
13 Oysa Avşalom'u öldürseydim –hiçbir şey kraldan gizli kalmaz– o zaman sen de beni savunmazdın.”
Ndipo sindikanayika moyo wanga pa chiswe pakuti palibe chimene chimabisika pamaso pa mfumu komanso inu simukanditeteza.”
14 Yoav, “Seninle böyle vakit kaybedemem” dedi. Üç kargı aldı, yabanıl fıstık ağacında asılı duran ve hâlâ sağ olan Avşalom'un yüreğine sapladı.
Yowabu anati, “Ine sinditayanso nthawi ndi iwe.” Ndipo anatenga mikondo itatu mʼmanja mwake ndipo anabaya pamtima pa Abisalomu, Abisalomuyo akanali ndi moyo pa mtengo wa thundu.
15 Bunun üzerine Yoav'ın silahlarını taşıyan on genç Avşalom'un çevresini sarıp onu öldürdüler.
Ndipo anthu khumi onyamula zida za Yowabu anazungulira Abisalomu, kumubaya ndi kumupha.
16 Yoav boru çaldırınca, askerler İsrailliler'i kovalamayı bırakıp geri döndüler. Yoav onların savaşı sürdürmelerine engel oldu.
Kenaka Yowabu analiza lipenga ndipo asilikali analeka kuthamangitsa Israeli pakuti Yowabu anawaletsa.
17 Yoav'ın askerleri Avşalom'u alıp ormanda derin bir çukura attılar; üzerine büyük bir taş yığını yaptılar. Bütün İsrailliler evlerine kaçtılar.
Iwo anatenga Abisalomu ndi kumuponya mʼdzenje lalikulu mʼchipululumo ndipo anawunjikapo miyala ikuluikulu. Nthawiyi Aisraeli onse anathawa kupita ku nyumba zawo.
18 Avşalom daha sağken bir direk alıp kendisi için Kral Vadisi'ne dikmişti. Çünkü, “Adımı anımsatacak bir oğlum yok” diye düşünmüştü. Direğe kendi adını vermişti. Bu direk bugün de Avşalom Anıtı diye bilinir.
Abisalomu ali ndi moyo anadzimangira chipilala mʼchigwa cha mfumu, pakuti ankaganiza kuti, “Ine ndilibe mwana wamwamuna amene adzakhale chikumbutso changa.” Chipilalacho anachitchula dzina lake lomwe ndipo mpaka lero chimatchedwa chipilala cha Abisalomu.
19 Sadok oğlu Ahimaas Yoav'a, “İzin ver de koşup krala RAB'bin onu düşmanlarının elinden kurtardığını haber vereyim” dedi.
Tsono Ahimaazi mwana wa Zadoki anati, “Ndiloleni ndithamange ndi kukapereka uthenga kwa mfumu kuti Yehova wayipulumutsa mʼdzanja la adani ake.”
20 Yoav, “Olmaz, bugün haberi götüren sen olmayacaksın” dedi, “Başka bir zaman haber götürürsün, ama bugün değil. Çünkü kralın oğlu öldü.”
Yowabu anamuwuza iye kuti, “Iwe si amene uti ukanene zimenezi lero. Ukapereka uthenga nthawi ina, koma usatero lero, chifukwa mwana wa mfumu wafa.”
21 Sonra bir Kûşlu'ya, “Sen git, gördüklerini krala bildir” dedi. Kûşlu Yoav'ın önünde yere kapandı, sonra koşmaya başladı.
Kenaka Yowabu anawuza Mkusi kuti, “Pita ukawuze mfumu zimene waona.” Mkusiyo anawerama pamaso pa Yowabu ndipo anathamanga kupita.
22 Ama Sadok oğlu Ahimaas yine, “Ne olursa olsun, izin ver, ben de Kûşlu'nun ardısıra koşayım” dedi. Yoav, “Oğlum, neden koşmak istiyorsun?” dedi, “Sana ödül kazandıracak bir haberin yok ki!”
Ahimaazi mwana wa Zadoki ananenanso kwa Yowabu kuti, “Zivute zitani, chonde mundilole kuti ndipite pambuyo pa Mkusiyo.” Koma Yowabu anayankha kuti, “Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukufuna kupita? Ulibe nkhani yoti ukalandire nayo mphotho.”
23 Ahimaas, “Ne olursa olsun koşacağım” diye karşılık verdi. Yoav, “Koş öyleyse” dedi. Böylece Ahimaas Şeria Ovası yolundan koşarak Kûşlu'yu geçti.
Iye anati, “Zivute zitani ine ndikufuna kuti ndipite.” Choncho Yowabu anati “Pita!” Ndipo Ahimaazi anathamanga kudzera njira ya ku chigwa ndipo anamupitirira Mkusi uja.
24 Davut kentin iç ve dış kapıları arasında oturuyordu. Nöbetçi surun yanındaki kapının tepesine çıktı. Çevreye göz gezdirince, tek başına koşan birini gördü.
Nthawi imeneyo nʼkuti Davide atakhala pakati pa zipata ziwiri, chakubwalo ndi chamʼkati. Mlonda anakwera pa khoma nakayimirira pa denga la chipata. Anati atayangʼana, anaona munthu akuthamanga yekhayekha.
25 Krala seslenerek gördüğünü bildirdi. Kral, “Tek başına geliyorsa, iyi haber getiriyor demektir” dedi. Adam gitgide yaklaşıyordu.
Mlonda uja anapita kwa mfumu ndipo anafotokoza. Mfumu inati, “Ngati ali yekha ali ndi nkhani yabwino” Ndipo munthuyo anayandikira.
26 Nöbetçi koşan başka birini görünce, kapıcıya, “İşte tek başına koşan bir adam daha!” diye seslendi. Kral, “O da iyi haber getiriyor” dedi.
Mlonda uja anaonanso munthu wina akuthamanga, ndipo anayitana woyangʼanira pa chipata, “Taona, munthu winanso akuthamanga ali yekha!” Mfumu inati, “Iye akubweretsanso nkhani yabwino.”
27 Nöbetçi, “Sanırım birinci adamın koşuşu Sadok oğlu Ahimaas'ın koşuşuna benziyor” dedi. Kral, “Ahimaas iyi adamdır” diye karşılık verdi, “İyi haberle gelir.”
Mlonda uja anati, “Munthu akuthamanga patsogoloyo, kathamangidwe kake kakufanafana ndi mmene amathamangira Ahimaazi, mwana wa Zadoki.” Mfumu inati, “Ameneyo ndi munthu wabwino, ndipo akubwera ndi nkhani yabwino.”
28 Ahimaas krala, “Her şey yolunda!” diye seslendi. Kralın önünde yüzüstü yere kapanarak, “Efendimiz krala el kaldıranları teslim eden Tanrın RAB'be övgüler olsun!” dedi.
Ndipo Ahimaazi anafuwula kwa mfumu, “Zonse zili bwino!” Iye anagwada pamaso pa mfumu nkhope yake atagunditsa pansi ndipo anati, “Yehova Mulungu wathu alemekezedwe! Iye wapereka mʼdzanja lathu anthu amene anawukira inu mbuye wanga mfumu.”
29 Kral, “Genç Avşalom güvenlikte mi?” diye sordu. Ahimaas şöyle yanıtladı: “Yoav kralın hizmetkârı Kûşlu'yla beni gönderdiği sırada büyük bir karışıklık gördüm, ama ne olduğunu anlamadım.”
Mfumu inafunsa, “Kodi mnyamata uja Abisalomu watetezedwa?” Ahimaazi anayankha, “Pamene Yowabu amati azindituma ine mtumiki wanu ndinaona chipiringu cha anthu, koma sindikudziwa chinali chiyani.”
30 Kral, “Bir yana çekilip burada bekle” dedi. Ahimaas da çekilip beklemeye başladı.
Mfumu inati, “Ima apo ndipo udikire.” Kotero iye anapita pa mbali nayima pamenepo.
31 Tam o sırada Kûşlu geldi. “Efendimiz krala müjde!” dedi, “Bugün RAB sana karşı bütün ayaklananların elinden seni kurtardı.”
Kenaka Mkusi uja anafika ndipo anati, “Mbuye wanga mfumu imvani nkhani yabwino! Yehova wakupulumutsani inu lero kwa onse amene anakuwukirani.”
32 Kral Kûşlu'ya, “Genç Avşalom güvenlikte mi?” diye sordu. Kûşlu, “Efendimiz kral!” diye yanıtladı, “Düşmanlarının ve kötü amaçla sana karşı ayaklananların hepsinin sonu bu gencin sonu gibi olsun.”
Mfumu inafunsa Mkusiyo kuti, “Kodi mnyamata uja Abisalomu watetezedwa?” Mkusiyo anayankha kuti, “Adani anu mbuye wanga mfumu, pamodzi ndi anthu onse amene amakuwukirani, ziwaonekere zomwe zamuonekera mnyamatayo.”
33 Kral sarsıldı. Giriş kapısının üstündeki odaya çıkıp ağladı. Giderken, “Ah oğlum Avşalom! Ah oğlum, oğlum Avşalom!” diye inliyordu, “Keşke senin yerine ben ölseydim, oğlum! Ah oğlum Avşalom!”
Mfumu inanthunthumira. Inapita ku chipinda cha mmwamba cha pa chipata kukalira. Pamene imapita, inkati: “Iwe mwana wanga Abisalomu! Mwana wanga! Mwana wanga Abisalomu! Zikanakhala bwino ndikanafa ndine mʼmalo mwako! Iwe Abisalomu, mwana wanga, mwana wanga!”

< 2 Samuel 18 >