< 2 Krallar 7 >

1 Elişa, “RAB'bin sözüne kulak verin!” dedi, “RAB diyor ki, ‘Yarın bu saatlerde Samiriye Kapısı'nda bir sea ince un da, iki sea arpa da birer şekele satılacak.’”
Ndipo Elisa anati, “Mverani mawu a Yehova. Yehova akuti, ‘Mawa nthawi ngati yomwe ino, makilogalamu atatu a ufa adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ku chipata cha Samariya.’”
2 Kralın özel yardımcısı olan komutan, Tanrı adamına, “RAB göklerin kapaklarını açsa bile olacak şey değil bu!” dedi. Elişa, “Sen her şeyi gözlerinle göreceksin, ama onlardan hiçbir şey yiyemeyeceksin!” diye karşılık verdi.
Mtsogoleri amene mfumu inkamudalira anati kwa munthu wa Mulungu, “Taona, ngakhale Yehova atatsekula zipata zakumwamba, kodi zimenezi zingachitikedi?” Elisa anamuyankha kuti, “Taona, iweyo udzaziona zimenezi ndi maso ako, koma sudzadyako kanthu.”
3 Kent kapısının girişinde deri hastalığına yakalanmış dört adam vardı. Birbirlerine, “Ne diye ölene dek burada kalalım?” diyorlardı,
Tsono pa chipata cholowera mu mzinda wa Samariya pankakhala anthu anayi akhate. Iwo anayankhulana kuti, “Chifukwa chiyani tikungokhala pano kudikira kufa?
4 “Kente girelim desek, orada kıtlık var, ölürüz; burada kalsak da öleceğiz. Bari gidip Aram ordugahına teslim olalım. Canımızı bağışlarlarsa yaşarız, öldürürlerse de öldürsünler.”
Ngati tinganene kuti, ‘Tidzalowa mu mzinda,’ njala ili mu mzindamo ndipo tidzafa. Ndipo ngati tikhalebe pano, tidzafa ndithu. Choncho tiyeni tipite ku msasa wa Aaramu ndi kukadzipereka. Ngati sakatipha, tidzakhala ndi moyo, ngati akatipha, basi tikafa.”
5 Akşam karanlığında kalkıp Aram ordugahına doğru gittiler. Ordugaha yaklaştıklarında, orada kimseyi göremediler.
Iwo ananyamuka ndi kachisisira kupita ku msasa wa Aaramu. Atafika mʼmalire a msasa, taonani, sanapeze munthu ndi mmodzi yemwe,
6 Çünkü Rab Aram ordugahında savaş arabalarıyla, atlarıyla yaklaşan büyük bir ordunun çıkardığı seslerin duyulmasını sağlamıştı. Aramlılar da birbirlerine, “Bakın, İsrail Kralı bize saldırmak için Hitit ve Mısır krallarını kiralamış!” demişlerdi.
pakuti Ambuye anali atamveketsa phokoso la magaleta ndi akavalo ndiponso mdidi wa gulu lalikulu la ankhondo, kotero anayamba kuwuzana kuti, “Taonani, mfumu ya ku Israeli yalemba ganyu mafumu a Ahiti ndi a Aigupto kuti adzatithire nkhondo!”
7 Böylece, gün batarken çadırlarını, atlarını, eşeklerini bırakıp kaçmışlar, canlarını kurtarmak için ordugahı olduğu gibi bırakmışlardı.
Choncho ananyamuka nathawa ndi kachisisira ndipo anasiya matenti, akavalo ndi abulu awo. Iwo anasiya msasa wawo momwe unalili nathawa kupulumutsa miyoyo yawo.
8 Deri hastalığına yakalanmış adamlar ordugaha varıp çadırların birine girdiler. Yiyip içtikten sonra oradaki altın, gümüş ve giysileri götürüp gizlediler. Sonra dönüp başka bir çadıra girdiler, orada bulduklarını da götürüp gizlediler.
Anthu akhate aja atafika mʼmalire mwa msasa analowa mʼtenti imodzi. Anadya ndi kumwa, natenga siliva, golide ndi zovala ndipo anachoka kupita kukazibisa. Atabwerera anakalowa mʼtenti ina ndipo anatenga zinthu mʼmenemo nakazibisanso.
9 Ardından birbirlerine, “Yaptığımız doğru değil” dediler, “Bugün müjde günü. Oysa biz susuyoruz. Gün doğuncaya kadar beklersek, cezaya çarptırılacağımız kesin. Haydi saraya gidip durumu bildirelim.”
Kenaka akhate aja anawuzana kuti, “Ife sitikuchita bwino. Lero ndi tsiku la uthenga wabwino ndipo tikungokhala chete. Tikadikira mpaka kucha, tidzalangidwa. Tiyeni msanga tikafotokoze zimenezi ku nyumba yaufumu.”
10 Böylece gidip kent kapısındaki nöbetçilere seslendiler. “Aram ordugahına gittik” dediler, “Hiç kimseyi göremedik; ne de bir insan sesi duyduk. Yalnızca bağlı atlar, eşekler vardı. Çadırları da olduğu gibi bırakıp gitmişler.”
Choncho anapita nakayitana alonda a pa chipata cha mzinda ndi kufotokoza kuti, “Ife tinapita ku msasa wa Aaramu ndipo sitinapezeko munthu, kapena phokoso la wina aliyense koma tinangopeza akavalo okha pamodzi ndi abulu ali chimangire.”
11 Kapı nöbetçileri haberi duyurdu. Haber kralın sarayına ulaştırıldı.
Alonda a pa chipata aja analengeza uthengawu kwa okhala mʼnyumba yaufumu.
12 Kral gece kalkıp görevlilerine, “Aramlılar'ın ne tasarladığını size söyleyeyim” dedi, “Aç kaldığımızı biliyorlar. Onun için ordugahlarını bırakıp kırda gizlenmişler. Kentin dışına çıktığımızda, bizi canlı yakalayıp kenti ele geçirmeyi düşünüyorlar.”
Mfumu inadzuka usiku ndipo inawuza atsogoleri ake a ankhondo kuti, “Ndikukuwuzani zimene Aaramu atichitira ife. Akudziwa kuti tikufa ndi njala; kotero achoka mu msasa wawo kukabisala kuthengo ndi kuti, ‘Iwowa atuluka ndithu, ndipo ife tidzawagwira amoyo ndi kulowa mu mzindamo.’”
13 Görevlilerden biri, “Kentte kalan beş atla birkaç adam gönderelim, o zaman durumu anlarız” dedi, “Nasıl olsa gidecek olanlar da burada, kentte kalan nice İsrailli gibi ölüme mahkûm!”
Mmodzi mwa atsogoleri ake ankhondo anayankha kuti, “Chonde uzani anthu ena atenge akavalo asanu amene atsala mu mzinda muno. Taonani, zomwe zingawachitikire zidzakhala zofanana ndi zomwe zingachitikire ena onse amene atsala. Inde iwo adzangokhala ngati Aisraeli ena onse amene awonongeka kale. Choncho tiyeni tiwatume akafufuze zomwe zachitika.”
14 Adamlar yanlarına iki atlı araba aldılar. Kral, “Gidin, ne olduğunu öğrenin” diyerek onları Aram ordusunun ardından gönderdi.
Choncho anasankha magaleta awiri pamodzi ndi akavalo ake, ndipo mfumu inawatuma kuti alondole gulu lankhondo la Aaramu. Mfumuyo inalamula oyendetsa akavalowo kuti, “Pitani kaoneni.”
15 Adamlar Şeria Irmağı'na kadar Aram ordusunu izlediler. Yol baştan sona kadar Aramlılar'ın kaçarken attıkları giysi ve eşyalarla doluydu. Haberciler dönüp krala durumu bildirdiler.
Anthuwa anawalondola mpaka ku Yorodani, ndipo taonani, mʼnjira monse munali zovala zokhazokha ndi zinthu zimene Aaramu ankazitaya pamene ankathawa mofulumira. Ndipo amithengawo anabwerera ndi kudzafotokozera mfumu.
16 Bunun üzerine halk kentten çıkıp Aram ordugahını yağmaladı. RAB'bin dediği gibi, bir sea ince unun da, iki sea arpanın da fiyatı bir şekele düştü.
Tsono anthu a mu Samariya anatuluka nakafunkha ku msasa wa Aaramu. Kotero kuti makilogalamu atatu a ufa ankawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele ankawagulitsanso pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, monga momwe ananenera Yehova.
17 Kral özel yardımcısı olan komutanı kentin kapısında bırakmıştı. Halk onu kapının ağzında çiğneyerek öldürdü. Kral Elişa'nın evine gittiğinde, Tanrı adamı ona olacakları önceden bildirmişti.
Tsono mfumu inayika mtsogoleri amene ankamudalira uja kuti akhale woyangʼanira pa chipata ndipo anthu anamupondaponda ku chipata kuja, ndipo anafa, monga momwe Elisa munthu wa Mulungu ananenera mfumu itapita ku nyumba yake.
18 Her şey Tanrı adamının krala dediği gibi oldu. “Yarın bu saatlerde Samiriye Kapısı'nda bir sea ince un da, iki sea arpa da birer şekele satılacak” demişti.
Zinachitika molingana ndi zomwe ananena munthu wa Mulungu zija kuti “Mawa nthawi ngati yomwe ino, makilogalamu atatu a ufa adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ku chipata cha Samariya.”
19 Komutan da Tanrı adamına şöyle karşılık vermişti: “RAB göklerin kapaklarını açsa bile, olacak şey değil bu!” Elişa, “Sen her şeyi gözlerinle görecek, ama onlardan hiçbir şey yiyemeyeceksin!” demişti.
Mtsogoleriyu ananena kwa munthu wa Mulungu kuti, “Taona, ngakhale Yehova atatsekula zipata zakumwamba, kodi zimenezi zingachitikedi?” Munthu wa Mulungu anamuyankha kuti, “Iwe udzaziona zimenezi ndi maso ako, koma sudzadyako kanthu.”
20 Tam dediği gibi oldu. Komutan kentin kapısında halk tarafından çiğnenerek öldü.
Ndipo izi ndi zomwe zinamuchitikiradi mtsogoleriyu, pakuti anthu anamupondaponda pa chipata ndipo anafa.

< 2 Krallar 7 >