< 2 Krallar 5 >

1 Aram Kralı'nın ordu komutanı Naaman efendisinin gözünde saygın, değerli bir adamdı. Çünkü RAB onun aracılığıyla Aramlılar'ı zafere ulaştırmıştı. Naaman yiğit bir askerdi, ama bir deri hastalığına yakalanmıştı.
Tsono Naamani anali mtsogoleri wa gulu lankhondo a mfumu ya ku Aramu. Iye anali munthu wodalirika pamaso pa mbuye wake ndipo anali wokondedwa kwambiri, chifukwa kudzera mwa iye Yehova anapambanitsa Aaramu. Anali msilikali wolimba mtima, koma anali ndi khate.
2 Aramlılar düzenledikleri akınlar sırasında İsrail'den küçük bir kızı tutsak almışlardı. Bu kız Naaman'ın karısının hizmetine verilmişti.
Tsono magulu a Aaramu anapita ku nkhondo ndipo anakagwira ukapolo mtsikana wamngʼono wa ku Israeli, ndipo ankatumikira mkazi wa Naamani.
3 Bir gün hanımına, “Keşke efendim Samiriye'deki peygamberin yanına gitse! Peygamber onu deri hastalığından kurtarırdı” dedi.
Mtsikanayo anawuza mkazi wa Naamani kuti, “Mbuye wanga akanapita kukaonana ndi mneneri amene amakhala ku Samariya, akanachiritsidwa khate lawo.”
4 Naaman gidip İsrailli kızın söylediklerini efendisi krala anlattı.
Naamani anapita kwa mbuye wake kukamuwuza zomwe mtsikana wochokera ku Israeli ananena.
5 Aram Kralı şöyle karşılık verdi: “Kalk git, seninle İsrail Kralı'na bir mektup göndereceğim.” Naaman yanına on talant gümüş, altı bin şekel altın ve on takım giysi alıp gitti.
Mfumu ya ku Aramu inayankha kuti, “Iwe uyenera kupita. Ine ndilembera kalata mfumu ya ku Israeli.” Choncho Naamani ananyamuka kupita ku Samariya, atatenga ndalama za siliva 30,000, ndalama zagolide 6,000 ndiponso zovala khumi za pa chikondwerero.
6 Mektubu İsrail Kralı'na verdi. Mektupta şunlar yazılıydı: “Bu mektupla birlikte sana kulum Naaman'ı gönderiyorum. Onu deri hastalığından kurtarmanı dilerim.”
Kalata imene anapita nayo kwa mfumu ya ku Israeli inali ndi mawu awa: “Taonani, ndikutumiza Naamani mtumiki wanga pamodzi ndi kalatayi kwa inu kuti mumuchiritse khate lake.”
7 İsrail Kralı mektubu okuyunca giysilerini yırtıp şöyle haykırdı: “Ben Tanrı mıyım, can alıp can vereyim? Nasıl bana bir adam gönderip onu deri hastalığından kurtar der? Görüyor musunuz, açıkça benimle kavga çıkarmaya çalışıyor!”
Mfumu ya ku Israeli itangowerenga kalatayo, inangʼamba mkanjo wake ndipo inati, “Kodi ine ndine Mulungu? Kodi ndingathe kupha kapena kupereka moyo? Chifukwa chiyani munthu ameneyu wanditumizira munthu woti ndimuchiritse khate lake? Taonani, iyeyu akungofuna kuti apeze chifukwa choyambanirana nane!”
8 İsrail Kralı'nın giysilerini yırttığını duyan Tanrı adamı Elişa ona şu haberi gönderdi: “Neden giysilerini yırttın? Adam bana gelsin, İsrail'de bir peygamber olduğunu anlasın!”
Elisa munthu wa Mulungu atamva kuti mfumu ya ku Israeli yangʼamba mkanjo wake, anatumiza uthenga uwu: “Chifukwa chiyani mwangʼamba mkanjo wanu? Mutumizeni munthuyo kwa ine ndipo iyeyo adzadziwa kuti muli mneneri mu Israeli.”
9 Böylece Naaman atları ve savaş arabalarıyla birlikte gidip Elişa'nın evinin kapısı önünde durdu.
Choncho Naamani anapita pamodzi ndi akavalo ake ndi magaleta nakayima pa khomo la nyumba ya Elisa.
10 Elişa ona şu haberi gönderdi: “Git, Şeria Irmağı'nda yedi kez yıkan. Tenin eski halini alacak, tertemiz olacaksın.”
Elisa anatumiza uthenga kwa iye woti, “Pita, kasambe kasanu ndi kawiri mu mtsinje wa Yorodani, thupi lako lidzachira ndi kukhalanso monga kale ndipo udzayeretsedwa.”
11 Gelgelelim Naaman oradan öfkeyle ayrıldı. “Sandım ki dışarı çıkıp yanıma gelecek, Tanrısı RAB'bi adıyla çağırarak eliyle hastalıklı derime dokunup beni iyileştirecek” dedi,
Koma Naamani anachoka mokwiya ndipo anati, “Ine ndimaganiza kuti munthuyu atuluka ndipo ayimirira nayitana dzina la Yehova Mulungu wake, nayendetsa dzanja lake pamwamba pa nthendayi ndi kundichiritsa khate langa.
12 “Şam'ın Avana ve Farpar ırmakları İsrail'in bütün ırmaklarından daha iyi değil mi? Oralarda yıkanıp paklanamaz mıydım sanki?” Sonra öfkeyle dönüp gitti.
Kodi Abana ndi Faripara, mitsinje ya ku Damasiko, siyoposa mitsinje ina yonse ya ku Israeli? Kodi sindikanasamba mʼmitsinje imeneyo ndi kuyeretsedwa?” Kotero anatembenuka nachoka ali wokwiya kwambiri.
13 Naaman'ın görevlileri yanına varıp, “Efendim, peygamber senden daha zor bir şey istemiş olsaydı, yapmaz mıydın?” dediler, “Oysa o sana sadece, ‘Yıkan, temizlen’ diyor.”
Antchito ake anamuyandikira namufunsa kuti, “Abambo anga, mneneri akanakulamulani chinthu chachikulu, kodi inu simukanachita? Nanga nʼzovuta motani zomwe mneneri wanena kuti ‘Kasambeni ndipo mudzayeretsedwa!’”
14 Bunun üzerine Naaman Tanrı adamının sözü uyarınca gidip Şeria Irmağı'nda yedi kez suya daldı. Teni eski haline döndü, bebek teni gibi tertemiz oldu.
Choncho Naamani anapita ku Yorodani nakadzimiza mʼmadzimo kasanu nʼkawiri, monga momwe munthu wa Mulungu anamuwuzira. Thupi lake linakhalanso monga kale ndipo linakhala losalala ngati la kamnyamata.
15 Naaman adamlarıyla birlikte Tanrı adamının yanına döndü. Onun önünde durup şöyle dedi: “Şimdi anladım ki, İsrail dışında dünyanın hiçbir yerinde Tanrı yoktur. Lütfen, bu kulunun armağanını kabul et.”
Pamenepo Naamani ndi atumiki ake onse anabwerera kwa munthu wa Mulungu uja. Naamani anayima pamaso pa Elisa ndipo anati, “Tsopano ndikudziwa kuti kulibe Mulungu wina pa dziko lonse lapansi koma mu Israeli mokha. Chonde, tsopano landirani mphatso ya mtumiki wanu.”
16 Elişa, “Hizmetinde olduğum yaşayan RAB'bin adıyla ant içerim ki, hiçbir şey alamam” diye karşılık verdi. Naaman direttiyse de, Elişa almak istemedi.
Mneneri anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene ine ndimamutumikira, sindidzalandira zimenezi.” Ndipo ngakhale Naamani anamukakamiza, iye anakanabe.
17 Bunun üzerine Naaman, “Madem armağan istemiyorsun, öyleyse buradan iki katır yükü toprak almama izin ver” dedi, “Çünkü bu kulun artık RAB'bin dışında başka ilahlara yakmalık sunu ve kurban sunmayacaktır.
Naamani anati, “Ngati inu simulandira, chonde lolani mtumiki wanu kuti atengeko dothi lokwanira kunyamula abulu awiri, popeza mtumiki wanu sadzaperekanso nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa mulungu wina koma Yehova.
18 Ama RAB kulunu bir konuda bağışlasın. Efendim tapınmak için Rimmon Tapınağı'na girip kendisine eşlik etmemi isteyince, tapınakta onunla birlikte yere kapandığımda RAB bu kulunu bağışlasın.”
Koma Yehova andikhululukire ine pa chinthu ichi: Pamene mbuye wanga alowa mʼnyumba ya mapemphero ya Rimoni ine ndimapita naye ndipo ndimakagwada naye limodzi. Pamene ndikugwada mʼnyumba ya mapemphero ya Rimoni, Yehova azikhululukira mtumiki wanu pa chinthu chimenechi.”
19 Elişa ona, “Esenlikle git” dedi. Naaman oradan ayrılıp biraz uzaklaşınca,
Elisa anati, “Pita mu mtendere.” Choncho anachoka nayenda pangʼono.
20 Tanrı adamı Elişa'nın uşağı Gehazi, “Efendim, Aramlı Naaman'a çok yumuşak davrandı; getirdiği armağanları kabul etmedi” dedi, “Yaşayan RAB'bin hakkı için, peşinden koşup ondan bir şey alacağım.”
Koma Gehazi, mtumiki wa Elisa munthu wa Mulungu, anaganiza mu mtima mwake kuti, “Taonani, mbuye wanga wamulekerera Naamani Mwaramuyu, posalandira zomwe anabweretsa. Pali Yehova wamoyo, ine ndimuthamangira ndipo ndikatengako zinthu kwa iye.”
21 Böylece Gehazi Naaman'ın peşine düştü. Naaman ardından birinin koştuğunu görünce, arabasından inip onu karşıladı ve, “Ne oldu?” diye sordu.
Choncho Gehazi anamuthamangira Naamani uja. Naamani ataona Gehazi akumuthamangira, anatsika mʼgaleta lake ndi kukakumana naye. Iye anafunsa Gehazi kuti, “Kodi nʼkwabwino?”
22 Gehazi, “Bir şey yok” dedi, “Yalnız efendimin bir ricası var. Biraz önce Efrayim'in dağlık bölgesinden iki genç peygamber geldi. Efendim onlara bir talant gümüşle iki takım giysi vermen için beni gönderdi.”
Gehazi anayankha kuti, “Inde nʼkwabwino. Mbuye wanga wandituma kuti ndidzakuwuzeni kuti, ‘Anyamata awiri mwa ana a aneneri angondipeza kumene kuchokera ku dziko la mapiri la Efereimu. Chonde apatseniko ndalama za siliva 3,000 ndi zovala ziwiri za pa phwando.’”
23 Naaman, “Lütfen iki talant al!” dedi ve ısrarla iki talant gümüşü iki torbaya koyup bağladı. Ayrıca iki uşağına da birer takım giysi verdi. Uşaklar Gehazi'nin önüsıra bunları taşıdılar.
Naamani anati, “Kuli bwino utenge ndalama zasiliva 6,000.” Iye anakakamiza Gehazi kuti alandire, ndipo kenaka anamanga matumba awiri a ndalama zasiliva pamodzi ndi zovala zinayi za pa mphwando. Naamani anazipereka kwa antchito ake awiri ndipo anazinyamula nayenda patsogolo pa Gehazi.
24 Tepeye varınca Gehazi eşyaları ellerinden alıp eve koydu, adamları da geri gönderdi.
Gehazi atafika ku phiri, anawalanda antchito aja zinthu zija nazibisa mʼnyumbamo. Iye anawawuza anthu aja kuti abwerere ndipo anapita.
25 Sonra gidip efendisi Elişa'nın huzuruna çıktı. Elişa, “Neredeydin, Gehazi?” diye sordu. Gehazi, “Kulun hiçbir yere gitmedi” diye karşılık verdi.
Kenaka analowa mʼnyumbamo nakayima pamaso pa mbuye wake Elisa. Elisa anafunsa kuti, “Kodi Gehazi unali kuti?” Iye anayankha kuti, “Mtumiki wanu sanapite kwina kulikonse.”
26 Bunun üzerine Elişa, “O adam arabasından inip seni karşılarken ruhum seninle değil miydi?” diye sordu, “Şimdi gümüş ya da giysi, zeytinlik, bağ, koyun, sığır, erkek ve kadın köle almanın zamanı mı?
Koma Elisa anati kwa Gehazi, “Kodi mzimu wanga sunali nawe pamene munthu uja anatsika mʼgaleta lake ndi kukumana nawe? Kodi ino ndi nthawi yolandira ndalama, kapena kulandira zovala, mitengo ya olivi, minda ya mpesa, nkhosa, ngʼombe kapena antchito aamuna kapena antchito aakazi?
27 Bu yüzden Naaman'ın deri hastalığı sonsuza dek senin ve soyunun üzerinde kalacak.” Böylece Gehazi Elişa'nın huzurundan kar gibi beyaz bir deri hastalığıyla ayrıldı.
Khate la Naamani lidzakumatirira iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya.” Ndipo Gehazi anachoka pamaso pa Elisa ali ndi khate lotuwa ngati phulusa.

< 2 Krallar 5 >