< 2 Krallar 25 >

1 Sidkiya'nın krallığının dokuzuncu yılında, onuncu ayın onuncu günü, Babil Kralı Nebukadnessar bütün ordusuyla Yeruşalim önlerine gelip ordugah kurdu. Kentin çevresine rampa yaptılar.
Choncho mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku lakhumi la mwezi, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ndi gulu lake lonse la ankhondo, nadzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu. Iye anamanga misasa kunja kwa mzindawo ndipo anamanga mitumbira ya nkhondo kuzungulira mzindawo.
2 Kral Sidkiya'nın krallığının on birinci yılına kadar kent kuşatma altında kaldı.
Mzindawo anawuzinga mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha Mfumu Zedekiya.
3 Dördüncü ayın dokuzuncu günü kentte kıtlık öyle şiddetlendi ki, halk bir lokma ekmek bulamaz oldu.
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi pa mwezi wachinayi, njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti anthu analibe chakudya.
4 Sonunda kentin surlarında bir gedik açıldı. Kildaniler kenti çepeçevre kuşatmış olmasına karşın, bütün askerler gece kral bahçesinin yolundan iki duvarın arasındaki kapıdan kaçarak Arava yoluna çıktılar.
Pamenepo khoma la mzindawo linabowoledwa ndipo gulu lonse la ankhondo linathawa usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Iwo anathawira cha ku Araba,
5 Ama Kildani ordusu kralın ardına düşerek Eriha ovalarında ona yetişti. Sidkiya'nın bütün ordusu dağıldı.
koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
6 Kral Sidkiya yakalanıp Rivla'da Babil Kralı'nın huzuruna çıkarıldı ve hakkında karar verildi.
Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula, kumene anagamula mlandu wa Zedekiyayo.
7 Sidkiya'nın gözü önünde oğullarını öldürdüler; kendisinin de gözlerini oydular, zincire vurup Babil'e götürdüler.
Iwo anapha ana a Zedekiya iyeyo akuona. Kenaka anakolowola maso a Zedekiya namumanga ndi unyolo wamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
8 Babil Kralı Nebukadnessar'ın krallığının on dokuzuncu yılında, beşinci ayın yedinci günü muhafız birliği komutanı, Babil Kralı'nın görevlisi Nebuzaradan Yeruşalim'e girdi.
Mwezi wachisanu, pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi, mʼchaka cha 19 cha Nebukadinezara, mfumu ya Babuloni, Nebuzaradani, mkulu wa asilikali oteteza mfumu, nduna ya mfumu ya Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
9 RAB'bin Tapınağı'nı, sarayı ve Yeruşalim'deki bütün evleri ateşe verip önemli yapıları yaktı.
Iye anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu pamodzi ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse yofunika.
10 Muhafız birliği komutanı önderliğindeki Kildani ordusu Yeruşalim'i çevreleyen surları yıktı.
Gulu lonse la ankhondo la ku Babuloni limene linali ndi mkulu wa asilikali oteteza mfumu ija, linagumula malinga ozungulira Yerusalemu.
11 Komutan Nebuzaradan kentte sağ kalanları, Babil Kralı'nın safına geçen kaçakları ve geri kalan halkı sürgün etti.
Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, ndi ena amene anathawira kwa mfumu ya Babuloni, pamodzi ndi ena onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
12 Ancak bağcılık, çiftçilik yapsınlar diye bazı yoksulları orada bıraktı.
Koma mkulu wa asilikaliyo anasiya anthu ena osauka kwambiri mʼdzikomo kuti azisamalira minda ya mpesa ndi minda ina.
13 Kildaniler RAB'bin Tapınağı'ndaki tunç sütunları, ayaklıkları, tunç havuzu parçalayıp tunçları Babil'e götürdüler.
Ababuloni anaphwanya zipilala zamkuwa, maphaka ndiponso mbiya ya mkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndipo anatenga mkuwawo napita nawo ku Babuloni.
14 Tapınak törenlerinde kullanılan kovaları, kürekleri, fitil maşalarını, tabakları, bütün tunç eşyaları aldılar.
Iwo anatenganso miphika, mafosholo, mbaniro za nyale, mbale ndi ziwiya zonse zamkuwa zimene ankagwiritsa ntchito potumikira mʼNyumbayo.
15 Muhafız birliği komutanı saf altın ve gümüş buhurdanları, çanakları alıp götürdü.
Mkulu wa asilikali uja anatenganso zofukizira lubani ndi mbale zowazira magazi. Zonsezi zinali zopangidwa ndi golide wabwino kwambiri kapena siliva.
16 RAB'bin Tapınağı için Süleyman'ın yaptırmış olduğu iki sütun, havuz ve ayaklıklar için hesapsız tunç harcanmıştı.
Mkuwa wochokera ku zipilala ziwiri zija, mbiya ija ndi maphaka aja, zimene Solomoni anapanga mʼNyumba ya Yehova, kuchuluka kwake kunali kosawerengeka.
17 Her sütun on sekiz arşın yüksekliğindeydi, üzerlerinde tunç birer başlık vardı. Başlığın yüksekliği üç arşındı, çevresi tunçtan ağ ve nar motifleriyle bezenmişti. Öbür sütun da ağ motifleriyle süslenmişti ve ötekine benziyordu.
Chipilala chilichonse chinali chotalika mamita asanu ndi atatu. Mutu wa mkuwa umene unali pamwamba pa chipilalacho unali mita imodzi ndi theka ndipo unakongoletsedwa ndi ukonde wa makangadza a mkuwa amene anazungulira mutuwo. Chipilala chachiwiri chinali chofanana ndi chinacho, ndipo chinali ndi ukonde.
18 Muhafız birliği komutanı Nebuzaradan Başkâhin Seraya'yı, Başkâhin Yardımcısı Sefanya'yı ve üç kapı nöbetçisini tutsak aldı.
Mkulu wa asilikali uja anagwira ukapolo mkulu wa ansembe Seraya, Zefaniya wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apakhomo.
19 Kentte kalan askerlerin komutanını, kralın beş danışmanını, ayrıca ülke halkını askere yazan ordu komutanının yazmanını ve ülke halkından kentte bulunan altmış kişiyi tutsak etti.
Mwa anthu amene anali mu mzindamo, anatenga mkulu amene ankalamulira ankhondo ndiponso alangizi asanu a mfumu. Anatenganso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo amene ankalemba anthu ntchito ya usilikali mʼdzikomo pamodzi ndi anthu ake 60 amene anali mu mzindamo.
20 Hepsini Rivla'ya, Babil Kralı'nın yanına götürdü.
Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anawatenga onsewo napita nawo kwa mfumu ya Babuloni ku Ribula.
21 Babil Kralı Hama ülkesinde, Rivla'da onları idam etti. Böylece Yahuda halkı ülkesinden sürülmüş oldu.
Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloni inalamula kuti awakwapule ndi kuwapha. Choncho Ayuda anatengedwa ukapolo kuwachotsa mʼdziko lawo.
22 Babil Kralı Nebukadnessar Yahuda'da kalan halkın üzerine Şafan oğlu Ahikam oğlu Gedalya'yı vali atadı.
Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala woyangʼanira anthu amene anatsala ku Yuda.
23 Ordu komutanlarıyla adamları, Babil Kralı'nın Gedalya'yı vali atadığını duyunca, Mispa'ya, Gedalya'nın yanına geldiler. Gelenler Netanya oğlu İsmail, Kareah oğlu Yohanan, Netofalı Tanhumet oğlu Seraya, Maakalı oğlu Yaazanya ve adamlarıydı.
Atsogoleri onse ankhondo ndi anthu awo atamva kuti mfumu ya Babuloni yasankha Gedaliya kukhala bwanamkubwa, anabwera kwa Gedaliya ku Mizipa. Atsogoleriwo mayina awo anali awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani mwana wa Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti wa ku Netofa ndi Yaazaniya mwana wa Maakati, pamodzi ndi anthu awo.
24 Gedalya onlara ve adamlarına ant içerek, “Kildani yetkililerden korkmayın” dedi, “Ülkeye yerleşip Babil Kralı'na hizmet edin. Böylesi sizin için daha iyi olur.”
Gedaliya analumbira powatsimikizira iwo ndi anthu awo. Iye anati, “Musachite mantha ndi atsogoleri Ababuloniwa. Khalani mʼdziko muno ndipo tumikirani mfumu ya Babuloni. Mukatero zinthu zidzakuyenderani bwino.”
25 O yılın yedinci ayında kral soyundan Elişama oğlu Netanya oğlu İsmail on adamıyla birlikte Mispa'ya gidip Gedalya'yı öldürdü. Ayrıca, Gedalya'yı destekleyen Yahudiler'i ve Kildaniler'i de kılıçtan geçirdi.
Koma pa mwezi wachisanu ndi chiwiri, Ismaeli mwana wa Netaniya, mwana wa Elisama, wa banja laufumu, anabwera ndi anthu khumi ndipo anapha Gedaliya pamodzi ndi Ayuda ndi anthu a ku Babuloni amene anali naye limodzi ku Mizipa.
26 Bunun üzerine büyük küçük bütün halk ordu komutanlarıyla birlikte Mısır'a kaçtı. Çünkü Kildaniler'den korkuyorlardı.
Chifukwa cha zimenezi, anthu onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo anathawira ku Igupto chifukwa choopa Ababuloni.
27 Yahuda Kralı Yehoyakin'in sürgündeki otuz yedinci yılı Evil-Merodak Babil Kralı oldu. Evil-Merodak o yılın on ikinci ayının yirmi yedinci günü, Yahuda Kralı Yehoyakin'i cezaevinden çıkardı.
Pa chaka cha 37 cha ukapolo wa Yehoyakini mfumu ya Yuda, chaka chimene Evili-Merodaki anakhala mfumu ya Babuloni, anamasula Yehoyakini mʼndende pa mwezi wa 12 pa tsiku la 27.
28 Kendisiyle tatlı tatlı konuştu ve ona Babil'deki öteki sürgün krallardan daha üstün bir yer verdi.
Anamukomera mtima namukweza kupambana mafumu ena onse amene anali naye ku Babuloni.
29 Yehoyakin cezaevi giysilerini üstünden çıkardı. Yaşadığı sürece Babil Kralı'nın sofrasında yer aldı.
Choncho Yoyakini anavula zovala zake za ku ndende, ndipo ankadya ndi mfumu masiku onse a moyo wake.
30 Yaşamı boyunca kral tarafından günlük yiyeceği sürekli karşılandı.
Mfumu inkamupatsa Yehoyakini chakudya tsiku lililonse pa moyo wake wonse.

< 2 Krallar 25 >