< 2 Krallar 19 >

1 Kral Hizkiya olanları duyunca giysilerini yırttı, çul kuşanıp RAB'bin Tapınağı'na girdi.
Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova.
2 Saray sorumlusu Elyakim'i, Yazman Şevna'yı ve ileri gelen kâhinleri Amots oğlu Peygamber Yeşaya'ya gönderdi. Hepsi çul kuşanmıştı.
Iye anatuma Eliyakimu, woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
3 Yeşaya'ya şöyle dediler: “Hizkiya diyor ki, ‘Bugün sıkıntı, azar ve utanç günü. Çünkü çocukların doğum vakti geldi, ama doğuracak güç yok.
Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera.
4 Yaşayan Tanrı'yı aşağılamak için efendisi Asur Kralı'nın gönderdiği komutanın söylediklerini belki Tanrın RAB duyar da duyduğu sözlerden ötürü onları cezalandırır. Bu nedenle sağ kalanlarımız için dua et.’”
Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a Rabusake amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.’”
5 Yeşaya, Kral Hizkiya'dan gelen görevlilere şöyle dedi: “Efendinize şunları söyleyin: ‘RAB diyor ki, Asur Kralı'nın adamlarından benimle ilgili duyduğunuz küfürlerden korkma.
Akuluakulu a Mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya,
6
Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti, ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine.
7 Onun içine öyle bir ruh koyacağım ki, bir haber üzerine kendi ülkesine dönecek. Orada onu kılıçla öldürteceğim.’”
Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’”
8 Komutan, Asur Kralı'nın Lakiş'ten ayrılıp Livna'ya karşı savaştığını duydu. Krala danışmak için oraya gitti.
Rabusake atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.
9 Kûş Kralı Tirhaka'nın kendisiyle savaşmak üzere yola çıktığını haber alan Asur Kralı, Hizkiya'ya yine ulaklar göndererek şöyle dedi:
Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi, akubwera kudzachita naye nkhondo. Choncho iye anatumanso amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa:
10 “Yahuda Kralı Hizkiya'ya deyin ki, ‘Güvendiğin Tanrın, Yeruşalim Asur Kralı'nın eline teslim edilmeyecek diyerek seni aldatmasın.
“Kawuzeni Hezekiya mfumu ya Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’
11 Asur krallarının bütün ülkelere neler yaptığını, onları nasıl yerle bir ettiğini duymuşsundur. Sen kurtulacağını mı sanıyorsun?
Ndithu iwe unamva chimene mafumu a Asiriya anachita ku mayiko ena onse, kuti anawawononga kotheratu. Ndipo kodi iwe nʼkupulumuka?
12 Atalarımın yok ettiği ulusları –Gozanlılar'ı, Harranlılar'ı, Resefliler'i, Telassar'da yaşayan Edenliler'i– ilahları kurtarabildi mi?
Kodi milungu ya mitundu imene makolo anga anayigonjetsa, milungu ya anthu a ku Gozani, Harani, Rezefi ndi Aedeni amene anali ku Teli Asara, inawapulumutsa?
13 Hani nerede Hama ve Arpat kralları? Lair, Sefarvayim, Hena, İvva kralları nerede?’”
Kodi mafumu a Hamati, Aripadi ndi mafumu a mizinda ya Sefaravaimu, Hena ndi Iva, ali kuti?”
14 Hizkiya mektubu ulakların elinden alıp okuduktan sonra RAB'bin Tapınağı'na çıktı. RAB'bin önünde mektubu yere yayarak
Hezekiya analandira kalata kwa amithenga aja nayiwerenga. Pomwepo anapita ku Nyumba ya Yehova nayika kalatayo pamaso pa Yehova.
15 şöyle dua etti: “Ey Keruvlar arasında taht kuran İsrail'in Tanrısı RAB, bütün dünya krallıklarının tek Tanrısı sensin. Yeri, göğü sen yarattın.
Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova nati, “Inu Yehova Mulungu wa Israeli, Inu amene mumakhala pa Akerubi, Inu nokha ndinu Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 Ya RAB, kulak ver de işit, gözlerini aç da gör, ya RAB; Sanherib'in söylediklerini, yaşayan Tanrı'yı nasıl aşağıladığını duy.
Inu Yehova, tcherani khutu lanu ndipo mumve Yehova tsekulani maso anu ndipo muone, imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza kunyoza Inu Mulungu wamoyo.
17 Ya RAB, gerçek şu ki, Asur kralları birçok ulusu ve ülkelerini viraneye çevirdiler.
“Inu Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu iyi ndi mayiko awo.
18 İlahlarını yakıp yok ettiler. Çünkü onlar tanrı değil, insan eliyle biçimlendirilmiş tahta ve taşlardı.
Iwo anaponya milungu yawo pa moto ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mitengo ndi miyala chabe, yopangidwa ndi anthu.
19 Ya RAB Tanrımız, şimdi bizi Sanherib'in elinden kurtar ki, bütün dünya krallıkları senin tek Tanrı olduğunu anlasın.”
Ndipo tsopano Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni ndithu mʼdzanja lake, kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndinu Mulungu.”
20 Bunun üzerine Amots oğlu Yeşaya, Hizkiya'ya şu haberi gönderdi: “İsrail'in Tanrısı RAB şöyle diyor: ‘Asur Kralı Sanherib'le ilgili olarak bana yalvardığın için diyorum ki, “‘Erden kız Siyon seni hor görüyor, Alay ediyor seninle. Yeruşalim kızı ardından alayla baş sallıyor.
Ndipo Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga kwa Hezekiya wakuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndamva pemphero lako lonena za Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.’”
Mawu amene Yehova wayankhula wotsutsana naye ndi awa: “Namwali wa Ziyoni akukunyoza ndi kukuseka iwe. Mwana wamkazi wa Yerusalemu akupukusa mutu wake kumbuyo kwako.
22 Sen kimi aşağıladın, kime küfrettin? Kime sesini yükselttin? İsrail'in Kutsalı'na tepeden baktın!
Kodi iweyo wanyoza ndi kuchitira chipongwe yani? Kodi ndani amene wamufuwulira mawu ako ndi kumuyangʼana monyada? Wachitiratu izi Woyera wa Israeli!
23 Ulakların aracılığıyla Rab'bi aşağıladın. Bir sürü savaş arabamla dağların tepesine, Lübnan'ın doruklarına çıktım, dedin. Yüksek sedir ağaçlarını, seçme çamlarını kestim, Lübnan'ın en iç noktalarına, Gür ormanlarına ulaştım.
Kudzera mwa amithenga ako wonyoza Ambuye. Ndipo wanena kuti, ‘Ndi magaleta ochuluka ndinakwera mapiri ataliatali, pa msonga za mapiri a Lebanoni. Ndigwetsa mitengo yake ya mkungudza yayitali kwambiri, mitengo yake ya payini yabwino kwambiri. Ndalowanso mʼkati mwake mwenimweni, mwa nkhalango yake yowirira kwambiri.
24 Yabancı ülkelerde kuyular kazdım, sular içtim, Mısır'ın bütün kanallarını ayağımın tabanıyla kuruttum, dedin.
Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo ndipo ndinamwa madzi a kumeneko. Ndi mapazi anga ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’”
25 “‘Bütün bunları çoktan yaptığımı, Çok önceden tasarladığımı duymadın mı? Surlu kentleri enkaz yığınlarına çevirmeni Şimdi ben gerçekleştirdim.
“‘Kodi sunamvepo? Zimenezi ndinazikhazikitsa kalekale. Ndinazikonzeratu masiku amakedzana; tsopano ndachita kuti zichitikedi, iwe kwako kunali kungosandutsa mizinda yotetezedwa kukhala milu ya miyala.
26 O kentlerde yaşayanların kolu kanadı kırıldı. Yılgınlık ve utanç içindeydiler; Kır otuna, körpe filizlere, Damlarda büyümeden kavrulup giden ota döndüler.
Anthu a kumeneko ndi opanda mphamvu, athedwa nzeru ndipo ali ndi manyazi. Ali ngati mbewu za mʼmunda, ngati udzu wanthete, ali ngati udzu womera pa denga, umene umawuma usanakule nʼkomwe.’”
27 Senin oturuşunu, kalkışını, Ne zaman gidip geldiğini, Bana nasıl öfkelendiğini biliyorum.
“‘Koma Ine ndimadziwa kukhala kwako, kutuluka kwako ndi kulowa kwako, ndi mkwiyo wako pa Ine.
28 Bana duyduğun öfkeden, Kulağıma erişen küstahlığından ötürü Halkamı burnuna, gemimi ağzına takacak, Seni geldiğin yoldan geri çevireceğim.
Chifukwa chakuti wandikwiyira ndipo ndamva za mwano wako, ndidzakola mphuno yako ndi mbedza ndi kuyika chitsulo changa mʼkamwa mwako, ndipo ndidzakubweza pokudzeretsa njira yomwe unadzera pobwera.’
29 “‘Senin için belirti şu olacak, ey Hizkiya: Bu yıl kendiliğinden yetişeni yiyeceksiniz, İkinci yıl ise ardından biteni. Üçüncü yıl ekip biçin, Bağlar dikip ürününü yiyin.
“Koma iwe Hezekiya, chizindikiro chako chidzakhala ichi: “Chaka chino mudzadya tirigu wamphulumukwa, ndipo chaka chamawa mudzadya tirigu wongodzimerera. Koma chaka chachitatu mudzadzala ndi kukolola, mudzawoka mphesa ndipo mudzadya zipatso zake.
30 Yahudalılar'ın kurtulup sağ kalanları Yine aşağıya doğru kök salacak, Yukarıya doğru meyve verecek.
Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsale adzazika mizu ndi kubereka zipatso.
31 Çünkü sağ kalanlar Yeruşalim'den, Kurtulanlar Siyon Dağı'ndan çıkacak. Her Şeye Egemen RAB'bin gayretiyle olacak bu.’
Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala, ndi ku phiri la Ziyoni kudzachokera gulu la anthu opulumuka.” “Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.
32 “Bundan dolayı RAB Asur Kralı'na ilişkin şöyle diyor: ‘Bu kente girmeyecek, ok atmayacak. Kente kalkanla yaklaşmayacak, Karşısında rampa kurmayacak.
“Choncho chimene Yehova akunena za mfumu ya ku Asiriya ndi ichi: “‘Iye sadzalowa mu mzinda umenewu kapena kuponyamo muvi. Sadzayandikira mzindawu ndi zishango zake kapena kumanga nthumbira ya nkhondo.
33 Geldiği yoldan dönecek ve kente girmeyecek’ diyor RAB,
Adzabwerera potsata njira imene anadzera pobwera; sadzalowa mu mzinda umenewu, akutero Yehova.
34 ‘Kendim için ve kulum Davut'un hatırı için Bu kenti savunup kurtaracağım’ diyor.”
Ndidzateteza mzinda umenewu kuwupulumutsa, chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
35 O gece RAB'bin meleği gidip Asur ordugahında yüz seksen beş bin kişiyi öldürdü. Ertesi sabah uyananlar salt cesetlerle karşılaştılar.
Usiku umenewo mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya ku Asiriya ndi kupha ankhondo 185,000. Ndipo pamene anthu anadzuka mmawa, taonani, mitembo inali ngundangunda!
36 Bunun üzerine Asur Kralı Sanherib ordugahını bırakıp çekildi. Ninova'ya döndü ve orada kaldı.
Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anapasula misasa ndi kuchoka. Anabwerera ku Ninive nakakhala kumeneko.
37 Bir gün ilahı Nisrok'un tapınağında tapınırken, oğullarından Adrammelek'le Şareser, onu kılıçla öldürüp Ararat ülkesine kaçtılar. Yerine oğlu Esarhaddon kral oldu.
Tsiku lina, pamene Senakeribu ankapembedza mʼnyumba ya Nisiroki mulungu wake, ana ake Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga ndipo anathawira ku dziko la Ararati. Tsono Esrahadoni, mwana wake, analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Krallar 19 >