< 2 Krallar 14 >

1 İsrail Kralı Yehoahaz oğlu Yehoaş'ın krallığının ikinci yılında Yoaş oğlu Amatsya Yahuda Kralı oldu.
Mʼchaka chachiwiri cha Yehowasi mwana wa Yowahazi mfumu ya Israeli, Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 Amatsya yirmi beş yaşında kral oldu ve Yeruşalim'de yirmi dokuz yıl krallık yaptı. Annesi Yeruşalimli Yehoaddan'dı.
Iye anali ndi zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
3 Amatsya RAB'bin gözünde doğru olanı yaptıysa da atası Davut gibi değildi. Her konuda babası Yoaş'ı örnek aldı.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi zomwe anachita Davide kholo lake. Iye anatsatira zochita zonse za Yowasi abambo ake.
4 Ancak alışılagelen tapınma yerleri henüz kaldırılmamıştı ve halk oralarda hâlâ kurban kesip buhur yakıyordu.
Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano. Anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
5 Amatsya krallığını güçlendirdikten sonra, babasını öldüren görevlileri ortadan kaldırdı.
Atakhazikika mu ufumu wake, Amaziya anapha atumiki ake amene anapha abambo ake, mfumu ija.
6 Ancak Musa'nın Kitabı'ndaki yasaya uyarak katillerin çocuklarını öldürtmedi. Çünkü RAB, “Ne babalar çocuklarının yerine öldürülecek, ne de çocuklar babalarının yerine. Herkes kendi günahı için öldürülecek” diye buyurmuştu.
Komatu iye sanaphe ana a anthu amene anapha abambo ake potsatira zomwe zinalembedwa mʼbuku la Malamulo a Mose. Mʼmenemo Yehova analamula kuti, “Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.”
7 Amatsya Tuz Vadisi'nde on bin Edomlu asker öldürdü. Savaşarak Sela'yı ele geçirdi ve oraya Yokteel adını verdi. Orası hâlâ aynı adla anılmaktadır.
Iye ndiye amene anapha Aedomu 10,000 mʼchigwa cha Mchere nalanda mzinda wa Sela pa nkhondo ndipo anawutcha Yokiteeli, dzina lake ndi lomwelo mpaka lero lino.
8 Bundan sonra Amatsya, Yehu oğlu Yehoahaz oğlu İsrail Kralı Yehoaş'a, “Gel, yüz yüze görüşelim” diye haber gönderdi.
Tsono Amaziya anatuma amithenga kwa Yehowasi mwana wa Yehowahazi, mwana wa Yehu mfumu ya Israeli ndi kumuopseza kuti, “Bwera tidzaonane maso ndi maso.”
9 İsrail Kralı Yehoaş da karşılık olarak Yahuda Kralı Amatsya'ya şu haberi gönderdi: “Lübnan'da dikenli bir çalı, sedir ağacına, ‘Kızını oğluma eş olarak ver’ diye haber yollar. O sırada oradan geçen yabanıl bir hayvan basıp çalıyı çiğner.
Koma Yehowasi mfumu ya Israeli anabweza mawu kwa Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Mtengo wa minga wa ku Lebanoni unatumiza uthenga kwa mkungudza wa ku Lebanoni. ‘Patse mwana wako wamkazi kuti ndimukwatire.’ Kenaka chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa mingawo.
10 Edomlular'ı bozguna uğrattın diye böbürleniyorsun. Bu zafer sana yeter. Otur evinde! Niçin bela arıyorsun? Kendi başını da, Yahuda halkının başını da derde sokacaksın.”
Inde iwe wagonjetsa Edomu ndipo tsopano wayamba kudzikuza. Dzitamandire chifukwa cha kupambana kwako, koma khala kwanu konko! Nʼchifukwa chiyani ukuyamba dala mavuto amene adzakuwononga pamodzi ndi Yuda?”
11 Ne var ki, Amatsya dinlemek istemedi. Derken İsrail Kralı Yehoaş Yahuda Kralı Amatsya'nın üzerine yürüdü. İki ordu Yahuda'nın Beytşemeş Kenti'nde karşılaştı.
Koma Amaziya sanamvere zimenezi. Choncho Yehowasi mfumu ya Israeli anakamuthira nkhondo. Yehowasi ndi Amaziya anakumana maso ndi maso ku Beti-Semesi mʼdziko la Yuda.
12 İsrailliler'in önünde bozguna uğrayan Yahudalılar evlerine kaçtı.
Israeli anagonjetsa Yuda ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
13 İsrail Kralı Yehoaş, Ahazya oğlu Yoaş oğlu Yahuda Kralı Amatsya'yı Beytşemeş'te yakaladı. Sonra Yeruşalim'e girip Efrayim Kapısı'ndan Köşe Kapısı'na kadar Yeruşalim surlarının dört yüz arşınlık bölümünü yıktırdı.
Yehowasi mfumu ya Israeli anagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Ndipo anapita ku Yerusalemu nakagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira ku Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, gawo lotalika mamita 180.
14 RAB'bin Tapınağı'nda ve sarayın hazinelerinde bulduğu altını, gümüşü ve bütün eşyaları aldı. Ayrıca bazı adamları da rehine olarak yanına alıp Samiriye'ye döndü.
Iye anatenga golide ndi siliva yense pamodzi ndi ziwiya zonse zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndi zimene zinali mosungira chuma cha nyumba ya mfumu. Iye anagwiranso anthu nabwerera ku Samariya.
15 Yehoaş'ın krallığı dönemindeki öteki olaylar, yaptıkları ve Yahuda Kralı Amatsya ile savaşırken gösterdiği başarılar İsrail krallarının tarihinde yazılıdır.
Ntchito zina za Yehowasi ndi zonse zimene anachita, kuwonjezera za nkhondo yake ndi Amaziya mfumu ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
16 Yehoaş ölüp atalarına kavuşunca, Samiriye'de İsrail krallarının yanına gömüldü. Yerine oğlu Yarovam kral oldu.
Yehowasi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Samariya pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo mwana wake Yeroboamu analowa ufumu mʼmalo mwake.
17 Yahuda Kralı Yoaş oğlu Amatsya, İsrail Kralı Yehoahaz oğlu Yehoaş'ın ölümünden sonra on beş yıl daha yaşadı.
Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
18 Amatsya'nın krallığı dönemindeki öteki olaylar Yahuda krallarının tarihinde yazılıdır.
Ntchito zina za Amaziya, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
19 Yeruşalim'de Amatsya'ya bir düzen kurulmuştu. Amatsya Lakiş'e kaçtı. Ardından adam göndererek onu öldürttüler.
Anthu anapangana zomuchita chiwembu mu Yerusalemu ndipo Amaziya anathawira ku Lakisi, koma anatumiza anthu ku Lakisiko nakamuphera komweko.
20 Ölüsü at sırtında Yeruşalim'e getirildi, Davut Kenti'nde atalarının yanına gömüldü.
Anabwera naye ku pa kavalo ku Yerusalemu ndi kumuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide.
21 Yahuda halkı Amatsya'nın yerine on altı yaşındaki oğlu Azarya'yı kral yaptı.
Ndipo anthu onse a ku Yuda anatenga Azariya, amene anali ndi zaka 16 namulonga ufumu mʼmalo mwa abambo ake Amaziya.
22 Babası Amatsya ölüp atalarına kavuştuktan sonra Azarya Eylat Kenti'ni onarıp Yahuda topraklarına kattı.
Azariya anamanga mzinda wa Elati ndi kuwubwezeretsa ku Yuda, Amaziya atamwalira.
23 Yahuda Kralı Yoaş oğlu Amatsya'nın krallığının on beşinci yılında Yehoaş oğlu Yarovam Samiriye'de İsrail Kralı oldu ve kırk bir yıl krallık yaptı.
Mʼchaka cha khumi ndi chisanu cha Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda, Yeroboamu mwana wa Yehowasi mfumu ya Israeli analowa ufumu ku Samariya ndipo analamulira za 41.
24 Yarovam RAB'bin gözünde kötü olanı yaptı ve Nevat oğlu Yarovam'ın İsrail'i sürüklediği günahlardan ayrılmadı.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
25 İsrail'in Tanrısı RAB'bin, kulu Gat-Heferli Amittay oğlu Yunus Peygamber aracılığıyla söylediği söz uyarınca, Yarovam Levo-Hamat'tan Arava Gölü'ne kadar İsrail topraklarını yeniden ele geçirdi.
Iye ndi amene anabwezeretsanso malire a Israeli kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku Nyanja ya Araba, molingana ndi zimene ananena Yehova Mulungu wa Israeli, kudzera mwa mtumiki wake Yona mwana wa Amitai, mneneri wochokera ku Gati-Heferi.
26 RAB İsrail'in çektiği sıkıntıyı görmüştü. Genç yaşlı herkes acı içinde kıvranıyordu. İsrail'e yardım edecek kimse yoktu.
Pakuti Yehova anaona masautso a Israeli amene anali owawa kwambiri, panalibe kapolo kapena mfulu ngakhale wina aliyense amene akanathandiza Israeli.
27 RAB İsrail'in adını yeryüzünden silmek istemiyordu. Onun için, Yehoaş oğlu Yarovam aracılığıyla onları kurtardı.
Pakuti Yehova anali asananene zofafaniza ufumu wa Israeli pa dziko lapansi, Iye anawapulumutsa kudzera mʼdzanja la Yeroboamu mwana wa Yowasi.
28 Yarovam'ın krallığı dönemindeki öteki olaylar, bütün yaptıkları, askeri başarıları, eskiden Yahuda'ya ait olan Şam ve Hama kentlerini yeniden İsrail topraklarına katışı İsrail krallarının tarihinde yazılıdır.
Ntchito zina za Yeroboamu ndi zonse zimene anachita, za kupambana kwake pa nkhondo, za mmene anagonjetsera Damasiko ndi Hamati, imene inali mizinda ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
29 Yarovam ölüp ataları olan İsrail krallarına kavuştu. Yerine oğlu Zekeriya kral oldu.
Yeroboamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo Zekariya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Krallar 14 >