< 2 Krallar 1 >

1 İsrail Kralı Ahav'ın ölümünden sonra Moavlılar İsrail'e karşı ayaklandı.
Atamwalira Ahabu, Mowabu anawukira Israeli.
2 İsrail Kralı Ahazya Samiriye'de yaşadığı sarayın üst katındaki kafesli pencereden düşüp yaralandı. Habercilerine, “Gidin, Ekron ilahı Baalzevuv'a danışın, yaralarımın iyileşip iyileşmeyeceğini öğrenin” dedi.
Ndipo Ahaziya anagwa kuchokera pa khonde la chipinda chake chammwamba ku Samariya, ndipo anavulala kwambiri. Choncho iye anatuma amithenga nawawuza kuti, “Pitani mukafunse kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, ngati ndichire matendawa.”
3 Ama RAB'bin meleği, Tişbeli İlyas'a şöyle dedi: “Kalk, Samiriye Kralı'nın habercilerini karşıla ve onlara de ki, ‘İsrail'de Tanrı yok mu ki Ekron ilahı Baalzevuv'a danışmaya gidiyorsunuz?’
Koma mngelo wa Yehova anawuza Eliya wa ku Tisibe kuti, “Nyamuka, pita ukakumane ndi amithenga a mfumu ya ku Samariya ndipo ukawafunse kuti, ‘Kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake inu mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni?’
4 Kralınıza deyin ki, ‘RAB, Yattığın yataktan kalkamayacak, kesinlikle öleceksin! diyor.’” Böylece İlyas oradan ayrıldı.
Tsono Yehova akuti, ‘Iweyo sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’” Ndipo Eliya ananyamuka.
5 Haberciler kralın yanına döndüler. Kral, “Neden geri döndünüz?” diye sordu.
Amithenga aja atabwerera kwa mfumu, mfumuyo inawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwabwerera?”
6 Şöyle karşılık verdiler: “Yolda bir adamla karşılaştık. Bize dedi ki, ‘Gidin, sizi gönderen krala RAB şöyle diyor deyin: İsrail'de Tanrı yok mu ki Ekron ilahı Baalzevuv'a danışmak için haberciler gönderdin? Bu yüzden yattığın yataktan kalkamayacak, kesinlikle öleceksin!’”
Iwo anayankha kuti, “Munthu wina anabwera kudzakumana nafe, ndipo anatiwuza kuti, bwererani kwa mfumu imene inakutumani ndipo mukayiwuze kuti, ‘Yehova akuti, kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni? Tsono sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’”
7 Kral, “Sizi karşılayıp bu sözleri söyleyen nasıl bir adamdı?” diye sordu.
Mfumu inafunsa amithengawo kuti, “Kodi munthu amene anabwera kudzakumana nanuyo ndi kukuwuzani zimenezi amaoneka bwanji?”
8 “Üzerinde tüylü bir giysi, belinde deri bir kuşak vardı” diye yanıtladılar. Kral, “O Tişbeli İlyas'tır” dedi.
Iwo anayankha kuti, “Munthuyo anavala zovala zaubweya ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake.” Mfumu inati, “Munthu ameneyo ndi Eliya wa ku Tisibe.”
9 Sonra bir komutanla birlikte elli adamını İlyas'a gönderdi. Komutan tepenin üstünde oturan İlyas'ın yanına çıkıp ona, “Ey Tanrı adamı, kral aşağı inmeni istiyor” dedi.
Pamenepo mfumu inatuma mtsogoleri wa ankhondo ndi anthu ake makumi asanu kwa Eliya. Mtsogoleriyo anapita kwa Eliya, amene anali atakhala pamwamba pa phiri, ndipo anati, “Munthu wa Mulungu, mfumu ikuti, ‘Tsikani!’”
10 İlyas, “Eğer ben Tanrı adamıysam, şimdi göklerden ateş yağacak ve seninle birlikte elli adamını yok edecek!” diye karşılık verdi. O anda göklerden ateş yağdı, komutanla birlikte elli adamını yakıp yok etti.
Eliya anayankha mtsogoleriyo kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu makumi asanu akowo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
11 Bunun üzerine kral, İlyas'a başka bir komutanla birlikte elli adam daha gönderdi. Komutan İlyas'a, “Ey Tanrı adamı, kral hemen aşağı inmeni istiyor!” dedi.
Zitachitika izi, mfumu inatumanso mtsogoleri wina pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleriyo anati kwa Eliya, “Munthu wa Mulungu, zimene mfumu ikunena ndi izi, ‘Tsikani msangamsanga!’”
12 İlyas, “Eğer ben Tanrı adamıysam, göklerden ateş yağacak ve seninle birlikte elli adamını yok edecek!” diye karşılık verdi. O anda göklerden ateş yağdı, komutanla birlikte elli adamını yakıp yok etti.
Eliya anayankha kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu ako makumi asanuwo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
13 Kral üçüncü kez bir komutanla elli adam gönderdi. Üçüncü komutan çıkıp İlyas'ın önünde diz çöktü ve ona şöyle yalvardı: “Ey Tanrı adamı, lütfen bana ve adamlarıma acı, canımızı bağışla!
Ndipo mfumu inatumanso mtsogoleri wachitatu pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleri wachitatuyu anakwera pa phiripo ndi kugwada pamaso pa Eliya. Iye anayankhula mopemba kuti, “Munthu wa Mulungu, chonde musandiwononge ineyo pamodzi ndi atumiki makumi asanu anuwa!
14 Göklerden yağan ateş daha önce gelen iki komutanla ellişer adamını yakıp yok etti, ama lütfen bana acı.”
Taonani, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kupsereza atsogoleri awiri pamodzi ndi anthu awo onse. Koma tsopano musawononge moyo wanga!”
15 RAB'bin meleği, İlyas'a, “Onunla birlikte aşağı in, korkma” dedi. İlyas kalkıp komutanla birlikte kralın yanına gitti
Mngelo wa Yehova anati kwa Eliya, “Pita naye, usamuope.” Choncho Eliya ananyamuka natsika naye limodzi kupita kwa mfumu.
16 ve ona şöyle dedi: “RAB diyor ki, ‘İsrail'de danışacak Tanrı yok mu ki Ekron ilahı Baalzevuv'a danışmak için haberciler gönderdin? Bu yüzden yattığın yataktan kalkamayacak, kesinlikle öleceksin!’”
Eliya anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chiyani munatumiza amithenga kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, kukafunsa ngati muti muchire? Kodi mu Israeli mulibe Mulungu woti nʼkukuyankhani funso lanu? Choncho, popeza mwachita izi, simudzadzuka pamene mwagonapo; mudzafa ndithu.’”
17 RAB'bin İlyas aracılığıyla söylediği söz uyarınca Kral Ahazya öldü. Oğlu olmadığı için yerine kardeşi Yoram geçti. Bu olay Yahuda Kralı Yehoşafat oğlu Yehoram'ın krallığının ikinci yılında oldu.
Motero Ahaziya anafadi, monga mwa mawu a Yehova amene Eliya anayankhula. Tsono popeza Ahaziya analibe mwana, Yoramu analowa ufumu mʼmalo mwake mʼchaka chachiwiri cha Yehoramu mwana wa Yehosafati mfumu ya ku Yuda.
18 Ahazya'nın krallığı dönemindeki öteki olaylar ve yaptıkları İsrail krallarının tarihinde yazılıdır.
Ntchito zina zonse zimene Ahaziya anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?

< 2 Krallar 1 >