< 2 Tarihler 5 >

1 RAB'bin Tapınağı'nın yapımı tamamlanınca Süleyman, babası Davut'un adadığı altın, gümüş ve öbür eşyaları getirip Tanrı'nın Tapınağı'nın hazine odalarına yerleştirdi.
Pamene ntchito yonse imene Solomoni anagwira pa Nyumba ya Yehova inatha, anabwera ndi zinthu zonse zimene abambo ake Davide anazipereka; siliva, golide ndi ziwiya. Anaziyika mʼzipinda zosungiramo chuma cha ku Nyumba ya Mulungu.
2 Süleyman RAB'bin Antlaşma Sandığı'nı Davut Kenti olan Siyon'dan getirmek üzere İsrail halkının ileri gelenleriyle bütün oymak ve boy başlarını Yeruşalim'e çağırdı.
Kenaka Solomoni anasonkhanitsa akuluakulu a Israeli mu Yerusalemu, atsogoleri onse a mafuko ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli, kuti akatenge Bokosi la Chipangano la Yehova ku Ziyoni, mzinda wa Davide.
3 Hepsi yedinci aydaki bayramda kralın önünde toplandı.
Ndipo Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa mfumu nthawi ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
4 İsrail'in bütün ileri gelenleri toplanınca, Levililer Antlaşma Sandığı'nı yerden kaldırdılar.
Akuluakulu onse a Israeli atafika, Alevi ananyamula Bokosi la Chipangano,
5 Sandığı, Buluşma Çadırı'nı ve çadırdaki bütün kutsal eşyaları Levili kâhinler tapınağa taşıdılar.
ndipo anabwera nalo bokosi lija pamodzi ndi tenti ya msonkhano ndi ziwiya zonse zopatulika zimene zinali mʼmenemo. Ansembe ndi Alevi ndiye anazinyamula,
6 Kral Süleyman ve bütün İsrail topluluğu Antlaşma Sandığı'nın önünde sayısız davar ve sığır kurban etti.
ndipo Mfumu Solomoni ndi gulu lonse la Aisraeli amene anasonkhana naye anali patsogolo pa Bokosi la Chipangano, akupereka nsembe nkhosa zambiri ndi ngʼombe zambiri zosawerengeka.
7 Kâhinler RAB'bin Antlaşma Sandığı'nı tapınağın iç odasına, En Kutsal Yer'e taşıyıp Keruvlar'ın kanatlarının altına yerleştirdiler.
Ansembe anafika nalo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼchipinda chamʼkati mwenimweni, Malo Opatulika Kwambiri, ndipo analiyika pansi pa mapiko a Akerubi.
8 Keruvlar'ın kanatları sandığın konduğu yerin üstüne kadar uzanıyor ve sandığı da, sırıklarını da örtüyordu.
Akerubiwo anatambalitsa mapiko awo pamwamba pa Bokosi la Chipangano ndipo anaphimba bokosilo pamodzi ndi mitengo yonyamulira.
9 Sırıklar öyle uzundu ki, uçları iç odanın önünden görünüyordu. Ancak dışarıdan görünmüyordu. Bunlar hâlâ oradadır.
Mitengoyi inali yayitali kwambiri ndipo inkaonekera kunja kwa chipinda chamʼkati cha Malo Opatulika, koma osati kunja kwa Malo Opatulikawo; ndipo mitengoyi ilipo mpaka lero lino.
10 Sandığın içinde Musa'nın Horev Dağı'nda koyduğu iki levhadan başka bir şey yoktu. Bunlar Mısır'dan çıkışlarında RAB'bin İsrailliler'le yaptığı antlaşmanın levhalarıydı.
Mʼbokosimo munalibe kanthu kena kalikonse kupatula miyala iwiri imene Mose anayikamo ku Horebu, kumene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
11 Kâhinler Kutsal Yer'den çıktılar. Orada bulunan kâhinlerin hepsi, bölüklerinin sırasını beklemeden, kendilerini kutsamışlardı.
Kenaka ansembe anatulukamo mʼMalo Opatulika. Ansembe onse amene anali mʼmenemo anali atadziyeretsa posayangʼaniranso magulu awo ochokera.
12 Bütün Levili ezgiciler –Asaf, Heman, Yedutun, oğullarıyla kardeşleri– zillerle, çenk ve lirlerle, ince keten kuşanmış olarak sunağın doğusunda yerlerini almışlardı. Borazan çalan yüz yirmi kâhin onlara eşlik ediyordu.
Alevi onse amene anali oyimba: Asafu, Hemani, Yedutuni ndi ana ndiponso abale awo, amayima mbali ya kummawa kwa guwa lansembe atavala zovala zofewa zosalala akuyimba ziwaya zamalipenga, azeze ndi apangwe. Ansembe onse amene amayimba malipenga analipo 120 pamodzi.
13 Borazan çalanlarla ezgiciler tek ses halinde RAB'be şükredip övgüler sunmaya başladılar. Borazan, zil ve çalgıların eşliğinde seslerini yükselterek RAB'bi şöyle övdüler: “RAB iyidir; Sevgisi sonsuza dek kalıcıdır.” O anda RAB'bin Tapınağı'nı bir bulut doldurdu.
Oyimba malipenga ndi oyimba nyimbo aja amayimba mogwirizana, monga liwu la munthu mmodzi, kutamanda ndi kuyamika Yehova. Mogwirizana ndi malipenga, ziwaya zamalipenga ndi zida zina, anakweza mawu awo motamanda Yehova poyimba kuti, “Yehova ndi wabwino; chikondi chake chikhala mpaka muyaya.” Ndipo Nyumba ya Mulungu wa Yehova inadzaza ndi mtambo,
14 Bu bulut yüzünden kâhinler görevlerini sürdüremediler. Çünkü RAB Tanrı'nın görkemi tapınağı doldurmuştu.
choncho ansembe sanathe kugwira ntchito yawo chifukwa cha mtambowo, pakuti ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulungu.

< 2 Tarihler 5 >