< 2 Tarihler 20 >
1 Bundan sonra Moavlılar, Ammonlular ve Meunlular'ın bir kısmı Yehoşafat'la savaşmak için yola çıktılar.
Zitatha izi, Amowabu ndi Aamoni pamodzi ndi Ameuni ena anabwera kudzachita nkhondo ndi Yehosafati.
2 Birkaç kişi Yehoşafat'a gidip, “Gölün öbür yakasından, Edom'dan sana saldırmak için büyük bir ordu geliyor. Şu anda Haseson-Tamar'da –Eyn-Gedi'de–” dediler.
Anthu ena anabwera kudzamuwuza Yehosafati kuti, “Gulu lalikulu kwambiri lankhondo likubwera kudzachita nanu nkhondo lochokera ku Edomu, ku mbali ina ya Nyanja. Gululi lafika kale ku Hazazoni Tamara” (ndiye kuti Eni-Gedi).
3 Korkuya kapılan Yehoşafat RAB'be danışmaya karar verdi ve bütün Yahuda'da oruç ilan etti.
Ndi mantha, Yehosafati anaganiza zofunsira kwa Yehova, ndipo analengeza kuti Ayuda onse asale zakudya.
4 RAB'be yönelmek için Yahuda'nın bütün kentlerinden gelen halk toplanıp RAB'den yardım diledi.
Anthu a ku Yuda anabwera pamodzi kudzafuna thandizo kwa Yehova, ndipo anabweradi kuchokera ku mzinda uliwonse wa mu Yuda kudzafunafuna Yehova.
5 Yehoşafat RAB'bin Tapınağı'nda, yeni avlunun önünde, Yahuda ve Yeruşalim topluluğunun arasına gidip durdu.
Yehosafati anayimirira pakati pa msonkhano wa Yuda ndi Yerusalemu, pa Nyumba ya Yehova patsogolo pa bwalo latsopano
6 “Ey atalarımızın Tanrısı RAB, sen göklerde oturan Tanrı değil misin?” dedi, “Ulusların bütün krallıklarını yöneten sensin. Güç, kudret senin elinde. Kimse sana karşı duramaz.
ndipo anati: “Inu Yehova, Mulungu wa makolo athu, kodi Inu sindinu Mulungu amene muli kumwamba? Inu mumalamulira maufumu onse a mitundu ya anthu. Mphamvu ndi nyonga zili mʼmanja mwanu, ndipo palibe amene angalimbane nanu.
7 Ey Tanrımız, bu ülkede yaşayanları halkın İsrail'in önünden kovan ve ülkeyi sonsuza dek dostun İbrahim'in soyuna veren sen değil misin?
Inu Mulungu wathu, kodi simunathamangitse nzika za dziko lino pamaso pa anthu anu Aisraeli ndipo munalipereka kwa zidzukulu za Abrahamu bwenzi lanu kwamuyaya?
8 Onlar orada yaşadılar, adına bir tapınak kurdular ve,
Iwo akhala mʼdzikolo ndipo anamangira Dzina lanu malo opatulika, nʼkumati,
9 ‘Başımıza bela, savaş, yargı, salgın hastalık, kıtlık gelirse, adının bulunduğu bu tapınağın ve senin önünde duracağız’ dediler, ‘Sıkıntıya düştüğümüzde sana yakaracağız, sen de duyup bizi kurtaracaksın.’
‘Ngati tsoka litigwera kaya ndi lupanga lachiweruzo, kapena mliri, kapenanso njala, ife tidzayima pamaso panu patsogolo pa Nyumba ya Mulungu ino imene imatchedwa ndi Dzina lanu ndipo tidzalirira kwa inu mʼmasautso athu, ndipo Inu mudzatimvera ndi kutipulumutsa.’
10 “İşte Ammonlular, Moavlılar ve Seir dağlık bölgesinde yaşayanlar! Mısır'dan çıktıktan sonra İsrailliler'in onların ülkesine girmelerine izin vermedin. Bu yüzden atalarımız başka yöne döndü, onları yok etmedi.
“Koma tsopano pano pali anthu ochokera ku Amoni, Mowabu ndi Phiri la Seiri amene dziko lawo Inu simunawalole Aisraeli kuti alithire nkhondo pamene amabwera kuchokera ku Igupto. Kotero anatembenuka ndi kuwaleka ndipo sanawawononge.
11 Ama bak, bunun karşılığını bize nasıl ödüyorlar! Bize miras olarak vermiş olduğun mülkünden bizi kovmaya geliyorlar.
Taonani, mmene akutibwezera ife pobwera kudzatithamangitsa mʼdziko limene inu munatipatsa ngati cholowa chathu.
12 Ey Tanrımız, onları yargılamayacak mısın? Çünkü bize saldıran bu büyük orduya karşı koyacak gücümüz yok. Ne yapacağımızı bilemiyoruz. Gözümüz sende.”
Inu Mulungu wathu, kodi simuwaweruza? Pakuti ife tilibe mphamvu zolimbana ndi gulu lalikulu lankhondo limene likutithira nkhondoli. Ife sitikudziwa choti tichite, koma maso athu ali pa Inu.”
13 Bütün Yahudalılar, çoluk çocuklarıyla birlikte RAB'bin önünde duruyordu.
Anthu onse a Yuda, pamodzi ndi akazi awo ndi ana ndi makanda, anayima chilili pamaso pa Yehova.
14 RAB'bin Ruhu topluluğun ortasında duran Asaf soyundan Mattanya oğlu Yeiel oğlu Benaya oğlu Zekeriya oğlu Levili Yahaziel'in üzerine indi.
Ndipo Mzimu wa Yehova unabwera pa Yahazieli mwana wa Zekariya, mwana wa Benaya, mwana wa Yeiyeli, mwana wa Mataniya Mlevi, chidzukulu cha Asafu, atayimirira mu msonkhano.
15 Yahaziel şöyle dedi: “Ey Kral Yehoşafat, ey Yahuda halkı ve Yeruşalim'de oturanlar, dinleyin! RAB size şöyle diyor: ‘Bu büyük ordudan korkmayın, yılmayın! Çünkü savaş sizin değil, Tanrı'nındır.
Iye anati, “Tamverani mfumu Yehosafati ndi onse amene amakhala mu Yuda ndi Yerusalemu! Zimene Yehova akunena kwa inu ndi izi: ‘Musaope kapena kutaya mtima chifukwa cha gulu lalikulu lankhondo ili. Pakuti nkhondoyi si yanu, koma ya Mulungu.
16 Yarın onlarla savaşmaya çıkın. Onları vadinin sonunda, Yeruel kırlarında, Sits Yokuşu'nu çıkarlarken bulacaksınız.
Mawa mupite mukamenyane nawo. Adzakhala akubwera mokweza kudzera Njira ya Zizi, ndipo mukawapeza kumapeto kwa chigwa cha ku chipululu cha Yeruweli.
17 Bu kez savaşmak zorunda kalmayacaksınız. Yerinizde durup bekleyin, RAB'bin size sağlayacağı kurtuluşu görün, ey Yahuda ve Yeruşalim halkı! Korkmayın, yılmayın. Yarın onlara karşı savaşa çıkın. RAB sizinle olacak!’”
Sikudzafunika kuti Inu mumenyane nawo pa nkhondo imeneyi. Inu mukhale pa malo anu; imani molimba ndipo onani chipulumutso chimene Yehova adzakupatsani, Inu Yuda ndi Yerusalemu. Musaope, musataye mtima. Pitani kuti mukakumane nawo mawa, ndipo Yehova adzakhala nanu.’”
18 Yehoşafat yüzüstü yere kapandı. Yahuda halkıyla Yeruşalim'de oturanlar da RAB'bin önünde yere kapanıp O'na tapındılar.
Yehosafati anaweramitsa nkhope yake ndi kugunda pansi, ndiponso anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anagwa pansi ndi kulambira Yehova.
19 Sonra Kehatoğulları'ndan ve Korahoğulları'ndan bazı Levililer ayağa kalkıp İsrail'in Tanrısı RAB'bi yüksek sesle övdüler.
Kenaka Alevi ena ochokera ku mabanja a Kohati ndi Kora anayimirira ndipo anatamanda Yehova Mulungu wa Israeli ndi mawu ofuwula kwambiri.
20 Ertesi sabah erkenden kalkıp Tekoa kırlarına doğru yola çıktılar. Yola koyulduklarında Yehoşafat durup şöyle dedi: “Beni dinleyin, ey Yahuda halkı ve Yeruşalim'de oturanlar! Tanrınız RAB'be güvenin, güvenlikte olursunuz. O'nun peygamberlerine güvenin, başarılı olursunuz.”
Mmamawa, ananyamuka kupita ku chipululu cha Tekowa. Akunyamuka, Yehosafati anayimirira ndipo anati, “Tandimverani ine anthu a Yuda ndi Yerusalemu! Khalani ndi chikhulupiriro mwa Yehova Mulungu wanu ndipo mudzatchinjirizidwa, khalani ndi chikhulupiriro mwa aneneri ake ndipo mudzapambana.”
21 Yehoşafat halka danıştıktan sonra RAB'be ezgi okumak, O'nun kutsallığının görkemini övmek için adamlar atadı. Bunlar ordunun önünde yürüyerek şöyle diyorlardı: “RAB'be şükredin, Çünkü sevgisi sonsuza dek kalıcıdır!”
Atafunsira kwa anthu, Yehosafati anasankha anthu oti ayimbire Yehova ndi kumutamanda chifukwa cha ulemerero wa chiyero chake pamene amapita ali patsogolo pa gulu la ankhondo, akunena kuti: “Yamikani Yehova pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
22 Onlar ezgi okuyup övgüler sunmaya başladığında, RAB Yahuda'ya saldıran Ammonlular'a, Moavlılar'a ve Seir dağlık bölgesinde yaşayanlara pusu kurmuştu. Hepsi bozguna uğratıldı.
Atangoyamba kuyimba ndi kutamanda, Yehova anapereka mʼmanja mwawo anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu ndiponso a ku Phiri la Seiri amene amalimbana ndi Yuda, ndipo anagonjetsedwa.
23 Ammonlular'la Moavlılar, Seir dağlık bölgesinde yaşayan halkı büsbütün yok etmek için onlara saldırdılar. Seirliler'i yok ettikten sonra da birbirlerini öldürmeye başladılar.
Anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu anawukira anthu ochokera ku Phiri la Seiri, ndipo anawawononga ndi kuwatheratu. Atatsiriza kuwapha anthu ochokera ku Seiri anamenyana wina ndi mnzake mpaka kuwonongana.
24 Yahudalılar kırdaki gözcü kulesine varınca, o büyük orduya baktılar, ama sadece yere serilmiş cesetler gördüler. Tek kişi kurtulmamıştı.
Anthu a ku Yuda atafika pa malo oyangʼanana ndi chipululu ndi kuona kumene kunali gulu lalikulu lankhondo, iwo anangoona mitembo yokhayokha itagona pansi ndipo palibe amene anathawa.
25 Malları yağmalamaya giden Yehoşafat'la askerleri, ölülerin arasında çok miktarda mal, giysi ve değerli eşya buldular. Taşıyabileceklerinden çok mal topladılar. Yağma edilecek o kadar çok mal vardı ki, toplama işi üç gün sürdü.
Choncho Yehosafati ndi anthu ake anapita kukafunkha, ndipo pakati pawo anapeza katundu wambiri ndi zovala ndiponso zinthu zina zamtengowapatali kuposa zomwe akanatha kunyamula. Kunali katundu wambiri kotero kuti zinawatengera masiku atatu kuti amutenge.
26 Dördüncü gün Beraka Vadisi'nde toplanarak RAB'be övgüler sundular. Bu yüzden oranın adı bugün de Beraka Vadisi olarak kaldı.
Tsiku lachinayi anasonkhana ku chigwa cha Beraka kumene anatamanda Yehova. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Beraka mpaka lero.
27 Bundan sonra bütün Yahuda ve Yeruşalim halkı Yehoşafat'ın önderliğinde sevinçle Yeruşalim'e döndü. Çünkü RAB düşmanlarını bozguna uğratarak onları sevindirmişti.
Tsono motsogozedwa ndi Yehosafati, anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anabwerera ku Yerusalemu mokondwera pakuti Yehova anawagonjetsera adani awo.
28 Çenk, lir ve borazan çalarak Yeruşalim'e, RAB'bin Tapınağı'na gittiler.
Iwo analowa mu Yerusalemu ndipo anapita ku Nyumba ya Mulungu akuyimba azeze, apangwe ndi malipenga.
29 RAB'bin İsrail'in düşmanlarına karşı savaştığını duyan ülkelerin krallıklarını Tanrı korkusu sardı.
Kuopsa kwa Mulungu kunali pa maufumu onse a mayiko amene anamva mmene Yehova anamenyera adani a Aisraeli.
30 Yehoşafat'ın ülkesi ise barış içindeydi. Çünkü Tanrısı her yandan onu esenlikle kuşatmıştı.
Ndipo ufumu wa Yehosafati unali pa mtendere pakuti Mulungu wake anamupatsa mpumulo ku mbali zonse.
31 Yehoşafat Yahuda'yı yönetti. Otuz beş yaşında kral oldu ve Yeruşalim'de yirmi beş yıl krallık yaptı. Annesi Şilhi'nin kızı Azuva'ydı.
Choncho Yehosafati analamulira Yuda. Iye anali wa zaka 35 pamene anakhala mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 25. Dzina la amayi ake linali Azuba mwana wa Sili.
32 Babası Asa'nın yollarını izleyen ve bunlardan sapmayan Yehoşafat RAB'bin gözünde doğru olanı yaptı.
Iye ankayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanapatuke pa zimenezi pakuti anachita zolungama pamaso pa Yehova.
33 Ancak alışılagelen tapınma yerleri kaldırılmadı. Halk hâlâ atalarının Tanrısı'na bütün yüreğiyle yönelmemişti.
Komabe malo opembedzerapo mafano sanachotsedwe ndipo anthu sanaperekebe mitima yawo kwa Mulungu wa makolo awo.
34 Yehoşafat'ın yaptığı öbür işler, başından sonuna dek, İsrail kralları tarihinin bir bölümü olan Hanani oğlu Yehu'nun tarihinde yazılıdır.
Zochitika zina zokhudza ufumu wa Yehosafati, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la Yehu mwana wa Hanani, zomwe zikupezeka mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
35 Yahuda Kralı Yehoşafat bir süre sonra kendini günaha veren İsrail Kralı Ahazya ile anlaşmaya vardı.
Zitapita izi, Yehosafati mfumu ya Yuda inachita mgwirizano ndi Ahaziya mfumu ya Israeli, amene anachita zoyipa kwambiri.
36 Tarşiş'e gidecek gemiler yapmak için anlaştılar. Gemileri Esyon-Gever'de yaptılar.
Iye anagwirizana ndi Ahaziya kuti apange sitima zapamadzi zochitira malonda. Atazipanga zimenezi ku Ezioni-Geberi,
37 Mareşalı Dodavahu oğlu Eliezer, Yehoşafat'a karşı şöyle peygamberlik etti: “Ahazya ile anlaşmaya vardığın için RAB işini bozacak.” Gemiler Tarşiş'e gidemeden parçalandı.
Eliezara mwana wa Dodavahu wa ku Maresa ananenera motsutsana ndi Yehosafati ndipo anati, “Chifukwa chakuti wachita mgwirizano ndi Ahaziya, Yehova adzawononga zimene mwapangazo!” Sitima za pamadzizo zinawonongeka ndipo sizinapite nʼkomwe kumene zimakachita malonda.