< 2 Tarihler 19 >
1 Yahuda Kralı Yehoşafat ise Yeruşalim'deki sarayına güvenlik içinde döndü.
Yehosafati, mfumu ya Yuda itabwerera mwamtendere ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu,
2 Hanani oğlu Bilici Yehu, Kral Yehoşafat'ı karşılamaya giderek ona şöyle dedi: “Kötülere yardım edip RAB'den nefret edenleri mi sevmen gerekir? Bunun için RAB'bin öfkesi senin üstünde olacak.
mlosi Yehu, mwana wa Hanani, anatuluka kukakumana naye ndipo anati kwa mfumu, “Kodi nʼkoyenera kuthandiza oyipa ndi kukonda iwo amene amadana ndi Yehova? Chifukwa cha zimenezi mkwiyo wa Yehova uli pa inu.
3 Ancak, bazı iyi yönlerin de var. Ülkeden Aşera putlarını kaldırıp attın ve yürekten Tanrı'ya yönelmeye karar verdin.”
Komabe, muli zinthu zina zabwino mwa inu, pakuti inu mwachotsa mʼdziko muno mafano a Asera ndipo mwakhazikitsa mtima wanu pa kufunafuna Mulungu.”
4 Yehoşafat Yeruşalim'de yaşadı. Beer-Şeva'dan Efrayim dağlık bölgesine kadar yine halkın arasında dolaşarak onları atalarının Tanrısı RAB'be döndürdü.
Yehosafati anakakhala ku Yerusalemu, ndipo amayenda pakati pa anthu kuchokera ku Beeriseba mpaka ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anawatembenuzira kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo.
5 Ülkeye, Yahuda'nın bütün surlu kentlerine yargıçlar atadı.
Iye anasankha oweruza mʼdzikomo, mu mzinda uliwonse wotetezedwa wa Yuda.
6 Onlara, “Yaptıklarınıza dikkat edin” dedi, “Çünkü insan adına değil, yargı verirken sizinle olan RAB adına yargılayacaksınız.
Ndipo anawawuza kuti, “Muganize bwino zimene mukuchita, chifukwa simukuweruza mʼmalo mwa munthu koma Yehova, amene ali nanu pamene mukupereka chiweruzo.
7 Onun için RAB'den korkun, dikkatle yargılayın. Çünkü Tanrımız RAB kimsenin haksızlık yapmasına, kimseyi kayırmasına, rüşvet almasına göz yummaz.”
Tsopano kuopsa kwa Yehova kukhale pa inu. Muweruze mosamala, pakuti ndi Yehova Mulungu wathu palibe kupotoza chilungamo kapena kukondera kapenanso kulandira ziphuphu.”
8 RAB'bin yargılarını uygulamak, davalara bakmak için Yehoşafat Yeruşalim'e de bazı Levililer'i, kâhinleri, İsrail boy başlarını atadı. Bunlar Yeruşalim'de yaşadılar.
Mu Yerusalemu, Yehosafati anasankha Alevi ena, ansembe ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli kuti aziyangʼanira Malamulo a Yehova ndi kuweruza milandu. Ndipo iwo amakhala mu Yerusalemu.
9 Yehoşafat onlara şu buyrukları verdi: “Görevinizi RAB korkusuyla, bağlılıkla, bütün yüreğinizle yapmalısınız.
Iye anawalamula kuti, “Inu mutumikire mokhulupirika ndi mtima wanu wonse moopa Yehova.
10 Kentlerde yaşayan kardeşlerinizden gelen her davada –kan davası, Kutsal Yasa, buyruklar, kurallar ya da ilkelerle ilgili her konuda– onları RAB'be karşı suç işlememeleri için uyarın; öyle ki RAB size de kardeşlerinize de öfkelenmesin. Böyle yaparsanız suç işlememiş olursunuz.
Pa mlandu uliwonse wobwera kwa inu kuchokera kwa abale anu amene amakhala mʼmizinda, mlandu wokhetsa magazi kapena mlandu wosamvera malamulo kapena malangizo kapena ziphunzitso zina, inu muziwachenjeza kuti asachimwire Yehova pakuti mukapanda kutero mkwiyo wake udzakhala pa inu ndi abale anu. Chitani zimenezi ndipo simudzachimwa.
11 “RAB'be ilişkin her konuda Başkâhin Amarya, krala ilişkin her konuda ise Yahuda oymağının önderi İsmail oğlu Zevadya size başkanlık edecek. Levililer de görevli olarak size yardımcı olacaklar. Yürekli olun, bu buyrukları uygulayın. RAB doğru kişiyle olsun!”
“Amariya, mkulu wa ansembe adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza Yehova, ndipo Zebadiya mwana wa Ismaeli, mtsogoleri wa fuko la Yuda, adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza mfumu ndipo Alevi adzatumikira ngati okuyangʼanirani. Muchite molimba mtima ndipo Yehova akhale ndi iwo amene adzachita bwino.”