< 2 Tarihler 18 >

1 Büyük bir zenginlik ve onura kavuşan Yehoşafat, evlilik bağıyla Ahav'a akraba oldu.
Tsono Yehosafati anali ndi chuma chambiri ndi ulemu, ndipo iye anachita mgwirizano wa ukwati ndi Ahabu.
2 Birkaç yıl sonra Samiriye Kenti'nde yaşayan Ahav'ı görmeye gitti. Ahav onun ve yanındakilerin onuruna birçok davar, sığır keserek Ramot-Gilat'a saldırmak için onu kışkırttı.
Patapita zaka zina, iye anapita kukacheza kwa Ahabu mu Samariya. Ahabu anaphera iye pamodzi ndi anthu amene anali naye, nkhosa zambiri ndi ngʼombe ndipo anamuwumiriza kuti akathire nawo nkhondo Ramoti Giliyadi
3 İsrail Kralı Ahav, Yahuda Kralı Yehoşafat'a, “Ramot-Gilat'a karşı benimle birlikte savaşır mısın?” diye sordu. Yehoşafat, “Beni kendin, halkımı halkın say. Savaşta sana eşlik edeceğiz” diye yanıtladı,
Ahabu mfumu ya Israeli anafunsa Yehosafati mfumu ya Yuda kuti, “Kodi mudzapita nane kukalimbana ndi Ramoti Giliyadi?” Yehosafati anayankha kuti, “Ine ndili ngati inu nomwe, ndi anthu anga ngati anthu anu. Ife tikhala nanu limodzi pa nkhondoyi.”
4 “Ama önce RAB'be danışalım” diye ekledi.
Koma Yehosafati anatinso kwa mfumu ya Israeli, “Choyamba mupemphe nzeru kwa Yehova.”
5 İsrail Kralı Ahav dört yüz peygamber toplayıp, “Ramot-Gilat'a karşı savaşalım mı, yoksa vaz mı geçeyim?” diye sordu. Peygamberler, “Savaş, çünkü Tanrı kenti senin eline teslim edecek” diye yanıtladılar.
Tsono mfumu ya Israeli inasonkhanitsa aneneri 400 ndipo inawafunsa kuti, “Kodi tipite kukalimbana ndi Ramoti Giliyadi kapena tileke?” Iwo anayankha kuti, “Pitani, pakuti Mulungu adzawupereka mʼdzanja la mfumu.”
6 Ama Yehoşafat, “Burada danışabileceğimiz RAB'bin başka peygamberi yok mu?” diye sordu.
Koma Yehosafati anafunsanso kuti, “Kodi kuno kulibe mneneri wina wa Yehova amene ife tingafunsireko?”
7 İsrail Kralı, “Yimla oğlu Mikaya adında biri daha var” diye yanıtladı, “Onun aracılığıyla RAB'be danışabiliriz. Ama ben ondan nefret ederim. Çünkü benimle ilgili hiç iyi peygamberlik etmez, hep kötü şeyler söyler.” Yehoşafat, “Böyle konuşmaman gerekir, ey kral!” dedi.
Mfumu ya Israeli inayankha Yehosafati kuti, “Alipo munthu mmodzi amene ife kudzera mwa iye titha kufunsira kwa Yehova, koma ndimadana naye chifukwa sandilosera zabwino koma zoyipa nthawi zonse. Iyeyu ndi Mikaya mwana wa Imula.” Yehosafati anayankha kuti, “Mfumu isanene motero.”
8 İsrail Kralı bir görevli çağırıp, “Hemen Yimla oğlu Mikaya'yı getir!” diye buyurdu.
Choncho mfumu ya Israeli inayitana mmodzi mwa akuluakulu ake ndipo inati, “Kamutengeni Mikaya mwana wa Imula, abwere msanga.”
9 İsrail Kralı Ahav ile Yahuda Kralı Yehoşafat kral giysileriyle Samiriye Kapısı'nın girişinde, harman yerine konan tahtlarında oturuyorlardı. Bütün peygamberler de onların önünde peygamberlik ediyordu.
Mfumu ya Israeli ndi Yehosafati mfumu ya Yuda, atavala mikanjo yawo yaufumu anali atakhala pa mipando yawo yaufumu pabwalo lopunthira tirigu pa khomo la chipata cha Samariya, pamodzi ndi aneneri onse akunenera pamaso pawo.
10 Kenaana oğlu Sidkiya, yaptığı demir boynuzları göstererek şöyle dedi: “RAB diyor ki, ‘Aramlılar'ı yok edinceye dek onları bu boynuzlarla vuracaksın.’”
Tsono Zedekiya mwana wa Kenaana anapanga nyanga zachitsulo ndipo analengeza kuti, “Yehova akuti, ‘Ndi nyanga izi udzagunda Aaramu mpaka atawonongedwa!’”
11 Öteki peygamberlerin hepsi de aynı şeyi söylediler: “Ramot– Gilat'a saldır, kazanacaksın! Çünkü RAB onları senin eline teslim edecek.”
Aneneri ena onse amanenera chimodzimodzi kuti, “Kathireni nkhondo Ramoti Giliyadi ndipo kapambaneni, pakuti Mulungu adzamupereka mʼdzanja la mfumu.”
12 Mikaya'yı çağırmaya giden görevli ona, “Bak! Peygamberler bir ağızdan kral için olumlu şeyler söylüyorlar” dedi, “Rica ederim, senin sözün de onlarınkine uygun olsun; olumlu bir şey söyle.”
Wauthenga amene anapita kukayitana Mikaya anati kwa iye, “Taonani aneneri ena onse ngati munthu mmodzi akulosera za chipambano cha mfumu. Mawu anunso agwirizane ndi awo ndipo muyankhule zabwino.”
13 Mikaya, “Yaşayan RAB'bin hakkı için, Tanrım ne derse onu söyleyeceğim” diye karşılık verdi.
Koma Mikaya anati, “Pali Yehova wamoyo, ine ndidzanena zimene Mulungu wanga andiwuze.”
14 Mikaya gelince kral, “Mikaya, Ramot-Gilat'a karşı savaşa gidelim mi, yoksa vaz mı geçeyim?” diye sordu. Mikaya, “Saldırın, kazanacaksınız! Çünkü onlar sizin elinize teslim edilecek” diye yanıtladı.
Iye atafika mfumu inamufunsa kuti, “Mikaya, kodi tipite ku nkhondo kukalimbana ndi Ramoti Giliyadi kapena tileke?” Iye anayankha kuti, “Kathireni nkhondo ndipo kapambaneni, pakuti mzindawo udzaperekedwa mʼdzanja lanu.”
15 Bunun üzerine kral, “RAB'bin adına bana gerçeğin dışında bir şey söylemeyeceğine ilişkin sana kaç kez ant içireyim?” diye sordu.
Mfumu inati kwa iye, “Kodi ndikuwuze kangati kuti ulumbire kuti usandiwuze chilichonse koma zoonadi mʼdzina la Yehova?”
16 Mikaya şöyle karşılık verdi: “İsrailliler'i dağlara dağılmış çobansız koyunlar gibi gördüm. RAB, ‘Bunların sahibi yok. Herkes güvenlik içinde evine dönsün’ dedi.”
Ndipo Mikaya anayankha kuti, “Ine ndinaona Aisraeli atabalalika mʼmapiri monga nkhosa zopanda mʼbusa, ndipo Yehova anati, ‘Anthu awa alibe mbuye wawo. Aliyense apite kwawo mu mtendere!’”
17 İsrail Kralı Ahav Yehoşafat'a, “Benimle ilgili iyi peygamberlik etmez, hep kötü şeyler söyler dememiş miydim?” dedi.
Mfumu ya Israeli inati kwa Yehosafati, “Kodi ine sindinakuwuzeni kuti sandinenera zabwino koma zoyipa zokhazokha?”
18 Mikaya konuşmasını sürdürdü: “Öyleyse RAB'bin sözünü dinleyin! Gördüm ki, RAB tahtında oturuyor, bütün göksel varlıklar da sağında, solunda duruyordu.
Mikaya anapitiriza ndi kunena kuti, “Imvani tsono mawu a Yehova: Ine ndinaona Yehova atakhala pa mpando wake waufumu ndi gulu lonse lakumwamba litayima ku dzanja lake lamanja ndi lamanzere.
19 RAB sordu: ‘Ramot-Gilat'a saldırıp ölsün diye İsrail Kralı Ahav'ı kim kandıracak?’ “Kimi şöyle, kimi böyle derken,
Ndipo Yehova anati, ‘Ndani amene adzamunyengerere Ahabu mfumu ya Israeli kuti akathire nkhondo Ramoti Giliyadi ndi kukafera komweko?’ “Wina ananena zina, winanso ananena zina.”
20 bir ruh çıkıp RAB'bin önünde durdu ve, ‘Ben onu kandıracağım’ dedi. “RAB, ‘Nasıl?’ diye sordu.
Pomaliza mzimu wina unatuluka ndi kuyima pamaso pa Yehova ndipo unati, “Ine ndikamunyengerera!” Yehova anafunsa kuti, “Ukagwiritsa ntchito njira yanji?”
21 “Ruh, ‘Aldatıcı ruh olarak gidip Ahav'ın bütün peygamberlerine yalan söyleteceğim’ diye karşılık verdi. “RAB, ‘Onu kandırmayı başaracaksın’ dedi, ‘Git, dediğini yap.’
Mzimuwo unati, “Ine ndidzapita ndi kukhala mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri ake onse!” Yehova anati, “‘Iwe ukamunyengadi iyeyo. Pita kachite zimenezo.’
22 “İşte RAB bu peygamberlerinin ağzına aldatıcı bir ruh koydu. Çünkü sana kötülük etmeye karar verdi.”
“Choncho Yehova wayika mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri anuwa. Yehova waneneratu kuti inu mukaona tsoka.”
23 Kenaana oğlu Sidkiya yaklaşıp Mikaya'nın yüzüne bir tokat attı. “RAB'bin Ruhu nasıl benden çıkıp da seninle konuştu?” dedi.
Ndipo Zedekiya mwana wa Kenaana anapita pafupi ndi kumenya khofi Mikaya. Zedekiya anafunsa kuti, “Kodi mzimu wochokera kwa Yehova unadzera njira iti pamene unachoka kwa ine kupita kwa iwe?”
24 Mikaya, “Gizlenmek için bir iç odaya girdiğin gün göreceksin” diye yanıtladı.
Mikaya anayankha kuti, “Udzadziwa pa tsiku limene uzikalowa mʼchipinda chamʼkati kuti ukabisale.”
25 Bunun üzerine İsrail Kralı, “Mikaya'yı kentin yöneticisi Amon'a ve kralın oğlu Yoaş'a götürün” dedi,
Pamenepo mfumu ya Israeli inalamula kuti, “Tengani Mikaya ndipo mupite naye kwa Amoni, wolamulira mzindawo ndi kwa Yowasi mwana wa mfumu,
26 “Ben güvenlik içinde dönünceye dek bu adamı cezaevinde tutmalarını, ona su ve ekmekten başka bir şey vermemelerini söyleyin!”
ndipo mukanene kuti, ‘Chimene mfumu ikunena ndi ichi; Muyike munthu uyu mʼndende ndipo musamupatse kanthu kalikonse koma buledi ndi madzi pangʼono mpaka nditabwera mwamtendere.’”
27 Mikaya, “Eğer sen güvenlik içinde dönersen, RAB benim aracılığımla konuşmamış demektir” dedi ve, “Herkes bunu duysun!” diye ekledi.
Mikaya anayankhula kuti, “Ngati inu mukabwera mwamtendere, Yehova sanayankhule kudzera mwa ine.” Ndipo anawonjeza kuti, “Anthu nonsenu, mumve zimene ndanenazi.”
28 İsrail Kralı Ahav'la Yahuda Kralı Yehoşafat Ramot-Gilat'a saldırmak için yola çıktılar.
Choncho mfumu ya Israeli ndi Yehosafati mfumu ya Yuda anapita ku Ramoti Giliyadi.
29 İsrail Kralı, Yehoşafat'a, “Ben kılık değiştirip savaşa öyle gireceğim, ama sen kral giysilerini giy” dedi. Böylece İsrail Kralı kılığını değiştirdi, sonra savaşa girdiler.
Mfumu ya Israeli inati kwa Yehosafati, “Ine ndipita ku nkhondo modzibisa koma iwe uvale mikanjo yaufumu.” Kotero mfumu ya Israeli inadzibisa ndipo inapita ku nkhondoko.
30 Aram Kralı, savaş arabalarının komutanlarına, “İsrail Kralı dışında, büyük küçük hiç kimseye saldırmayın!” diye buyruk vermişti.
Tsono mfumu ya Aramu inalamulira olamulira magaleta kuti, “Musamenyane ndi wina aliyense, wamngʼono kapena wamkulu koma mfumu ya Israeli yokha.”
31 Savaş arabalarının komutanları Yehoşafat'ı görünce, İsrail Kralı sanıp saldırmak için ona döndüler. Yehoşafat yakarmaya başladı. RAB Tanrı ona yardım edip saldıranların yönünü değiştirdi.
Olamulira magaleta ataona Yehosafati, iwo anaganiza kuti, “Mfumu ya Israeli ndi iyi.” Kotero anatembenuka kukamenyana naye koma Yehosafati anafuwula, ndipo Yehova anamuthandiza. Mulungu anawabweza mʼmbuyo,
32 Komutanlar onun İsrail Kralı olmadığını anlayınca peşini bıraktılar.
pakuti olamulira magaleta ataona kuti sanali mfumu ya Israeli, anasiya kumuthamangitsa.
33 O sırada bir asker rasgele attığı bir okla İsrail Kralı'nı zırhının parçalarının birleştiği yerden vurdu. Kral arabacısına, “Dönüp beni savaş alanından çıkar, yaralandım” dedi.
Koma munthu wina anaponya muvi wake mwachiponyeponye ndipo analasa mfumu ya Israeli pakati polumikizira malaya achitsulo. Mfumu inawuza oyendetsa galeta kuti, “Bwerera, undichotse pa nkhondo pano. Ndavulazidwa.”
34 Savaş o gün şiddetlendi. Arabasında Aramlılar'a karşı akşama kadar dayanan İsrail Kralı gün batımında öldü.
Nkhondo inakula kwambiri tsiku lonse, ndipo mfumu ya Israeli inakhala tsonga mʼgaleta lake kuyangʼanana ndi Aaramu mpaka madzulo. Ndipo pamene dzuwa linkalowa inamwalira.

< 2 Tarihler 18 >