< 2 Tarihler 15 >
1 Tanrı'nın Ruhu Odet oğlu Azarya'nın üzerine indi.
Mzimu wa Mulungu unabwera pa Azariya mwana wa Odedi.
2 Azarya, Kral Asa'ya gidip şöyle dedi: “Ey Asa, ey Yahuda ve Benyamin halkı, beni dinleyin! RAB'le birlikte olduğunuz sürece, O da sizinle olacaktır. O'nu ararsanız bulursunuz. Ama O'nu bırakırsanız, O da sizi bırakır.
Iye anapita kukakumana ndi Asa ndipo anati kwa iye, “Tandimverani, inu Asa ndi Ayuda onse ndi Benjamini. Yehova ali ndi inu, inunso mukakhala naye. Ngati inu mumufunafuna Iye mudzamupeza, koma ngati mumusiya, Iye adzakusiyani.
3 İsrail halkı uzun süre gerçek Tanrı'dan, eğitici kâhinlerden ve yasadan uzak yaşadı.
Kwa nthawi yayitali Israeli anali wopanda Mulungu weniweni, wopanda wansembe wophunzitsa ndi wopanda malamulo.
4 Ama sıkıntıya düştüklerinde İsrail'in Tanrısı RAB'be döndüler, O'nu arayıp buldular.
Koma pamene anali pa mavuto anatembenukira kwa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi kufunafuna Iye, ndipo anamupeza.
5 O günlerde yolcuların güvenliği yoktu. Çünkü çevre ülkelerde yaşayanların tümü büyük kargaşa içindeydi.
Masiku amenewo sikunali kwabwino kuyenda ulendo, pakuti anthu onse okhala mʼdziko anali pa mavuto aakulu.
6 Ulus ulusu, kent kenti ezmeye çalışıyordu. Çünkü Tanrı onları çeşitli sıkıntılarla tedirgin ediyordu.
Mtundu umodzi umakanthidwa ndi mtundu wina ndipo mzinda wina umakanthidwa ndi mzinda wina, pakuti Mulungu amawasautsa ndi mazunzo a mtundu uliwonse.
7 Ama siz güçlü olun, cesaretinizi yitirmeyin. Yaptıklarınızın karşılığını alacaksınız.”
Koma inu, khalani amphamvu ndipo musataye mtima, pakuti mudzalandira mphotho ya ntchito yanu.”
8 Asa bu sözleri, Peygamber Odet'in oğlu Azarya'nın peygamberliğini duyunca, cesaret buldu. Yahuda ve Benyamin topraklarından, Efrayim'in dağlık bölgesinde ele geçirdiği kentlerden iğrenç putları kaldırdı. RAB'bin Tapınağı'nın eyvanının önündeki RAB'bin sunağını onardı.
Asa atamva mawu awa ndiponso uneneri wa Azariya mwana wa Odedi, analimba mtima. Iye anachotsa mafano onse onyansa mʼdziko lonse la Yuda ndi Benjamini ndi mʼmizinda yonse imene analanda a ku mapiri a Efereimu. Iye anakonzetsa guwa lansembe la Yehova limene linali kutsogolo kwa khonde la Nyumba ya Mulungu.
9 Efrayim'den, Manaşşe'den, Şimon'dan gelen birçok İsrailli, Tanrısı RAB'bin Asa'yla birlikte olduğunu görünce onun tarafına geçti. Asa bu gelenlerle Yahuda ve Benyamin halkını bir araya topladı.
Kenaka anasonkhanitsa anthu onse a ku Yuda ndi Benjamini ndiponso anthu ochokera ku Efereimu, Manase ndi Simeoni amene ankakhala pakati pawo, pakuti gulu lalikulu linabwera kwa iye kuchokera ku Israeli litaona kuti anali ndi Yehova Mulungu wake.
10 Asa'nın krallığının on beşinci yılının üçüncü ayında Yeruşalim'de toplandılar.
Iwo anasonkhana mu Yerusalemu mwezi wachitatu wa chaka cha 15 cha ulamuliro wa Asa.
11 Yağmalamış oldukları hayvanlardan yedi yüz sığırla yedi bin davarı o gün RAB'be kurban ettiler.
Pa nthawi imeneyi anapereka nsembe kwa Yehova, ngʼombe 700 ndiponso nkhosa ndi mbuzi 7,000 zochokera pa zolanda ku nkhondo zimene anabweretsa.
12 Bütün yürekleriyle, bütün canlarıyla atalarının Tanrısı RAB'be yönelmek için antlaşma yaptılar.
Iwo anachita pangano loti azifunafuna Yehova, Mulungu wa makolo awo, ndi mtima ndi moyo wawo wonse.
13 Büyük küçük, kadın erkek, kim İsrail'in Tanrısı RAB'be yönelmezse öldürülecekti.
Aliyense wosafunafuna Yehova Mulungu wa Israeli aziphedwa, kaya ndi wamngʼono kapena wamkulu, mwamuna kapena mkazi.
14 Yüksek sesle bağırarak, borazan ve boru çalarak RAB'bin önünde ant içtiler.
Iwo analumbira kwa Yehova, mokweza mawu, akuyimba malipenga ndi mbetete.
15 Yahudalılar bütün yürekleriyle içtikleri ant için sevindiler. RAB'bi istekle arayıp buldular. O da onları her yandan esenlikle kuşattı.
Anthu onse a ku Yuda anakondwera pa kulumbirako chifukwa analumbira ndi mtima wawo wonse. Iwo anafunafuna Mulungu mwachidwi, ndipo anamupeza Iye. Kotero Yehova anawapatsa mpumulo mbali zonse.
16 Kral Asa annesi Maaka'nın kraliçeliğini elinden aldı. Çünkü o Aşera için iğrenç bir put yaptırmıştı. Asa bu iğrenç putu kesip parçaladıktan sonra Kidron Vadisi'nde yaktı.
Mfumu Asa anachotsanso Maaka agogo ake pa udindo wa amayi a mfumu chifukwa anapanga fano lonyansa la Asera. Asa anagwetsa fanolo, naliswa ndipo kenaka anakaliwotcha ku chigwa cha Kidroni.
17 Ancak İsrail'den puta tapılan yerleri kaldırmadı. Ama yaşamı boyunca yüreğini RAB'be adadı.
Ngakhale kuti sanachotse malo opembedzerako mafano mu Israeli, mtima wa Asa unali wodzipereka kwathunthu kwa Yehova, masiku onse a moyo wake.
18 Babasının ve kendisinin adadığı altını, gümüşü ve eşyaları Tanrı'nın Tapınağı'na getirdi.
Iye anabweretsanso mʼNyumba ya Mulungu zipangizo zasiliva, golide ndi ziwiya zina zimene iyeyo ndi abambo ake anazipatula.
19 Asa'nın krallığının otuz beşinci yılına kadar savaş olmadı.
Panalibenso nkhondo mpaka chaka cha 35 cha ufumu wa Asa.