< 2 Tarihler 13 >

1 İsrail Kralı Yarovam'ın krallığının on sekizinci yılında Aviya Yahuda Kralı oldu.
Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu, Abiya analowa ufumu wa Yuda,
2 Yeruşalim'de üç yıl krallık yaptı. Annesi Givalı Uriel'in kızı Mikaya'ydı. Aviya'yla Yarovam arasında savaş vardı.
ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka zitatu. Dzina la amayi ake linali Maaka mwana wa Urieli wa ku Gibeya. Koma panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu.
3 Aviya seçme yiğit askerlerden oluşan dört yüz bin kişilik bir orduyla savaşa çıktı. Yarovam da sekiz yüz bin seçme yiğit savaşçıdan oluşan bir orduyla ona karşı savaş düzenine girdi.
Abiya anapita ku nkhondo ndi asilikali odziwa bwino nkhondo 400,000, ndipo Yeroboamu anandandalitsa ankhondo, asilikali 800,000 odziwa bwino nkhondo, osankhidwa ndi amphamvu, woti amenyane naye.
4 Aviya Efrayim dağlık bölgesindeki Semarayim Dağı'na çıkıp şöyle seslendi: “Ey Yarovam ve bütün İsrailliler, beni dinleyin!
Abiya anayima pa phiri la Zemaraimu, mʼdziko lamapiri la Efereimu, ndipo anati, “Yeroboamu ndi Aisraeli onse, tandimverani!
5 İsrail'in Tanrısı RAB'bin bozulmaz bir antlaşmayla İsrail Krallığı'nı sonsuza dek Davut'a ve soyuna verdiğini bilmiyor musunuz?
Kodi inu simukudziwa kuti Yehova, Mulungu wa Israeli, wapereka ufumu wa Israeli kwa Davide ndi zidzukulu zake mpaka muyaya ndiponso pangano la mchere?
6 Nevat oğlu Yarovam efendisi Davut oğlu Süleyman'a başkaldırdı.
Komabe Yeroboamu mwana wa Nebati, mtumiki wa Solomoni mwana wa Davide, anawukira mbuye wake.
7 Bir takım işe yaramaz kötü kişiler çevresinde toplanıp Süleyman oğlu Rehavam'a baskı yaptılar. O sırada Rehavam onlara karşı koyamayacak kadar genç ve deneyimsizdi.
Ndipo anthu ena achabechabe anasonkhana kwa iye ndipo anatsutsana ndi Rehobowamu mwana wa Solomoni pamene anali wamngʼono ndi wosalimba mtima ndi wopanda mphamvu kuti athe kulimbana nawo.
8 “Şimdi de siz Davut soyunun elindeki RAB'bin Krallığı'na karşı gelmeyi tasarlıyorsunuz. Büyük bir ordusunuz. Üstelik Yarovam'ın ilahlarınız olsun diye yaptırdığı altın buzağılar da yanınızda.
“Ndipo tsopano inu mwakonzekera kutsutsana ndi ufumu wa Yehova, umene uli mʼmanja mwa zidzukulu za Davide. Inu ndithu mulipo ankhondo ambirimbiri ndipo muli ndi ana angʼombe agolide amene Yeroboamu anapanga kuti akhale milungu yanu.
9 RAB'bin kâhinlerini, Harunoğulları'yla Levililer'i kovmadınız mı? Onların yerine öbür halklar gibi kendinize kâhinler atamadınız mı? Atanmak için bir boğa ve yedi koçla gelen herkes, tanrı olmayanlara kâhin olabiliyor.
Koma kodi inu simunathamangitse ansembe a Yehova, ana a Aaroni ndiponso Alevi ndi kudzisankhira ansembe anuanu monga anthu ena amachitira? Aliyense amene amabwera kuti adzipatule atatenga mwana wangʼombe wamwamuna ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri amakhala wansembe wa zinthu zimene sizili milungu.
10 “Ama bizim Tanrımız RAB'dir, O'nu bırakmadık. RAB'be hizmet eden kâhinler Harun soyundandır. Levililer de onlara yardımcıdır.
“Koma kunena za ife, Yehova ndiye Mulungu wathu, ndipo sitinamusiye. Ansembe amene amatumikira Yehova ndi ana a Aaroni ndipo amathandizidwa ndi Alevi.
11 Onlar her sabah, her akşam RAB'be yakmalık sunular sunar, hoş kokulu buhur yakar, dinsel açıdan temiz masanın üzerine adak ekmeklerini dizerler. Her akşam altın kandilliğin kandillerini yakarlar. Biz Tanrımız RAB'bin buyruklarını yerine getiriyoruz. Oysa siz O'na sırt çevirdiniz.
Mmawa uliwonse ndi madzulo aliwonse amapereka nsembe zopsereza ndi kufukiza lubani kwa Yehova. Iwo amayika buledi pa tebulo loyeretsedwa monga mwa mwambo ndipo amayatsa nyale pa zoyikapo nyale zagolide madzulo aliwonse. Ife timachita zofuna za Yehova Mulungu wathu. Koma inu mwamusiya.
12 Tanrı bizimledir, O önderimizdir. O'nun kâhinleri borazanlarla size karşı savaş çağrısı yapacaklar. Ey İsrail halkı, atalarınızın Tanrısı RAB'be karşı savaşmayın; çünkü başaramazsınız.”
Mulungu ali nafe pakuti ndiye mtsogoleri wathu. Ansembe ake atanyamula malipenga, adzayimba mfuwu wankhondo kulimbana nanu. Inu Aisraeli musalimbane ndi Yehova, Mulungu wa makolo anu, pakuti simungathe kupambana.”
13 Yarovam askerlerinin bir bölümüyle Yahudalılar'ı önden karşılarken, öbür bölümünü arkalarında pusu kurmaya göndermişti.
Tsono Yeroboamu anali atatumiza asilikali kumbuyo mowazungulira, kotero kuti iye ali kutsogolo kwa anthu a ku Yuda, anthu owabisalira anali kumbuyo kwawo.
14 Yahudalılar önden, arkadan kuşatıldıklarını görünce, RAB'be yakardılar. Kâhinler borazanlarını çaldı.
Asilikali a Yuda anatembenuka ndipo anaona kuti nkhondo imachitikira kutsogolo ndi kumbuyo. Ndipo iwo anafuwulira Yehova. Ansembe anayimba malipenga awo
15 Yahudalılar savaş çığlıkları attığı anda, Tanrı Yarovam'la İsrailliler'i Aviya'yla Yahudalılar'ın önünde yenilgiye uğrattı.
ndipo asilikali a Yuda anafuwula mawu ankhondo. Atafuwula mawu ankhondowo, Mulungu anagonjetsa Yeroboamu pamodzi ndi Aisraeli onse pamaso pa Abiya ndi Yuda.
16 İsrailliler Yahudalılar'ın önünden kaçtı. Tanrı onları Yahudalılar'ın eline teslim etti.
Aisraeli anathawa Ayuda. Ndipo Mulungu anawapereka mʼmanja mwawo.
17 Aviya'yla ordusu İsrailliler'i bozguna uğrattı. İsrailliler'den beş yüz bin seçme asker öldürüldü.
Abiya pamodzi ndi anthu ake anapha anthu ambiri, kotero kuti Aisraeli 500,000 odziwa bwino nkhondo anaphedwa.
18 Böylece İsrailliler yenilgiye uğradı, Yahudalılar'sa zafer kazandı. Çünkü Yahudalılar atalarının Tanrısı RAB'be güvenmişlerdi.
Ankhondo a Israeli anagonjetsedwa pa nthawi imeneyi, ndipo ankhondo a Yuda anapambana chifukwa anadalira Yehova, Mulungu wa makolo awo.
19 Aviya Yarovam'ı kovaladı. Yarovam'a ait Beytel, Yeşana, Efron kentleriyle çevrelerindeki köyleri ele geçirdi.
Abiya anathamangitsa Yeroboamu ndipo anamulanda mizinda ya Beteli, Yesana, ndi Efroni pamodzi ndi midzi yawo yozungulira.
20 Aviya'nın krallığı döneminde Yarovam bir daha eski gücünü toparlayamadı. Sonunda RAB onu cezalandırdı, Yarovam öldü.
Yeroboamu sanapezenso mphamvu nthawi ya Abiya. Ndipo Yehova anamukantha nafa.
21 Aviya ise gitgide krallığını güçlendirdi. On dört kadınla evlenip yirmi iki erkek, on altı kız babası oldu.
Koma Abiya mphamvu zake zinakula. Iye anakwatira akazi 14 ndipo anali ndi ana aamuna 22 ndi ana aakazi 16.
22 Aviya'nın yaptığı öbür işler, uygulamaları ve söyledikleri, Peygamber İddo'nun yorumunda yazılıdır.
Zina ndi zina zokhudza Abiya, zimene anachita ndi zimene anayankhula, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mneneri Ido.

< 2 Tarihler 13 >