< 1 Timoteos 5 >
1 Yaşlı adama çıkışma, babanmış gibi yol göster. Genç erkeklere kardeşinmiş gibi, yaşlı kadınlara annenmiş gibi, genç kadınlara tam bir yürek temizliğiyle kızkardeşinmiş gibi yol göster.
Usadzudzule munthu wachikulire mokalipa, koma umuchenjeze ngati abambo ako. Achinyamata uwatenge ngati abale ako.
Amayi achikulire uwatenge ngati amayi ako ndipo amayi achitsikana uwatenge ngati alongo ako, nʼkuyera mtima konse.
3 Gerçekten kimsesiz dul kadınlara saygı göster.
Uziwachitira ulemu akazi amasiye amene ali okhaokha.
4 Ama dul kadının çocukları ya da torunları varsa, bunlar öncelikle kendi ev halkına yardım ederek Tanrı yolunda yürümeyi ve büyüklerine iyilik borcunu ödemeyi öğrensinler. Çünkü bu Tanrı'yı hoşnut eder.
Koma ngati mkazi wamasiye ali ndi ana ndi zidzukulu, anawo ayambe aphunzira kukwaniritsa udindo wawo pa banja lawo moopa Mulungu, potero akubweza zabwino kwa makolo awo ndi agogo awo. Pakuti zimenezi ndiye zimakondweretsa Mulungu.
5 Gerçekten kimsesiz, yalnız kalmış dul kadın umudunu Tanrı'ya bağlamıştır; gece gündüz O'na dilekte bulunmaya ve dua etmeye devam eder.
Mkazi wamasiye amene ali yekha ndi wopanda womuthandiza, ameneyo wayika chiyembekezo chake pa Mulungu, ndipo amapemphera kosalekeza usana ndi usiku kuti Mulungu azimuthandiza.
6 Kendini zevke veren dul kadınsa daha yaşarken ölmüştür.
Koma mkazi wamasiye amene amangokhalira kuchita zosangalatsa moyo wake, wafa kale ngakhale akanali ndi moyo.
7 Ayıplanacak duruma düşmemeleri için onları bu konularda uyar.
Pereka malangizo amenewa kwa anthu kuti akhale opanda zolakwa.
8 Kendi yakınlarına, özellikle de ev halkına bakmayan kişi imanı inkâr etmiş, imansızdan beter olmuştur.
Ngati wina sasamalira abale ake, makamaka a mʼbanja mwake mwenimweni, ameneyo wakana chikhulupiriro ndipo ndi woyipa kuposa wosakhulupirira.
9 Yaptığı iyiliklerle tanınmış, tek erkekle evlenmiş, en az altmış yaşında olan dul kadın, eğer çocuk büyütmüş, konuk ağırlamış, kutsalların ayaklarını yıkamış, sıkıntıda olanlara yardım etmiş, kendini her tür iyi işe adamışsa, adı dullar listesine yazılsın.
Mayi wamasiye aliyense amene sanakwanitse zaka 60 zakubadwa, asakhale mʼgulu la akazi amasiye. Akhale woti anakwatiwapo ndi mwamuna wake mmodzi yekha.
Akhale mayi woti amadziwika bwino pa ntchito zake zabwino monga kulera ana, kusamalira alendo, kusambitsa mapazi a anthu a Mulungu, kuthandiza amene ali pa mavuto ndi kudzipereka pa ntchito zonse zabwino.
11 Daha genç dulları listeye alma. Çünkü bedensel arzuları Mesih'e bağlılıklarına baskın çıkınca evlenmek isterler.
Akazi amasiye achitsikana, usawayike mʼgulu limeneli. Pakuti zilakolako zawo zikayamba kuwavutitsa nʼkuwalekanitsa ndi Khristu, amafuna kukwatiwanso.
12 Böylece verdikleri ilk sözü çiğneyerek hüküm giyerler.
Zikatero amadziweruza okha chifukwa aphwanya lonjezo lawo loyamba.
13 Aynı zamanda ev ev gezerek tembelliğe alışırlar. Yalnız tembelliğe alışmakla kalmazlar, üzerlerine düşmeyen sözler söyleyerek başkalarının işine karışan boşboğazlar olurlar.
Komanso amakhala ndi chizolowezi cha ulesi ndi kumangoyenda khomo ndi khomo. Ndipo sikungokhala aulesi kokha komanso kuchita miseche, kududukira za eni ake, kumangokamba zinthu zosayenera kukamba.
14 Bu nedenle, daha genç dulların evlenmelerini, çocuk yapmalarını, evlerini yönetmelerini, düşmana hiçbir iftira fırsatı vermemelerini isterim.
Kotero, ndikulangiza akazi amasiye achitsikana kuti akwatiwe, akhale ndi ana, asamalire makomo awo ndipo asamupatse mdani mpata wonyoza
15 Kimisi zaten sapmış, Şeytan'ın ardına düşmüştür.
Akazi amasiye ena apatuka kale nʼkumatsatira Satana.
16 İmanlı bir kadının dul yakınları varsa onlara yardım etsin. İnanlılar topluluğu yük altına girmesin ki, gerçekten kimsesiz olan dullara yardım edebilsin.
Ngati mayi aliyense wokhulupirira ali ndi akazi amasiye amene akuwasamalira, apitirizebe kuwasamalira ndipo asalemetse mpingo, kuti mpingo uthandize akazi amasiye amene ali okhaokha.
17 Topluluğu iyi yöneten ihtiyarlar, özellikle Tanrı sözünü duyurup öğretmeye emek verenler iki kat saygıya layık görülsün.
Akulu ampingo amene amayangʼanira bwino zochitika za mu mpingo, ndi oyenera ulemu wowirikiza, makamaka amene ntchito yawo ndi kulalikira ndi kuphunzitsa.
18 Çünkü Kutsal Yazı'da şöyle deniyor: “Harman döven öküzün ağzını bağlama” ve “İşçi ücretini hak eder.”
Pakuti Mawu a Mulungu amati, “Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu,” ndi “Wantchito ngoyenera kulandira malipiro ake.”
19 İki ya da üç tanık olmadıkça, bir ihtiyara yöneltilen suçlamayı kabul etme.
Usamamvere mawu oneneza akulu ampingo pokhapokha patakhala mboni ziwiri kapena zitatu.
20 Günah işleyenleri herkesin önünde azarla ki, öbürleri de korksun.
Akulu ampingo amene akuchimwa, uwadzudzule poyera kuti ena aphunzirepo.
21 Bu söylediklerimi yan tutmadan, kimseyi kayırmadan yerine getirmen için seni Tanrı'nın, Mesih İsa'nın ve seçilmiş meleklerin önünde uyarıyorum.
Ndikukulamulira pamaso pa Mulungu, pamaso pa Yesu Khristu ndi pamaso pa angelo osankhika, kuti usunge malangizowa mosachotsera ndipo usachite kalikonse mokondera.
22 Birinin üzerine ellerini koymakta aceleci davranma, başkalarının günahlarına ortak olma. Kendini temiz tut.
Usafulumire kusanjika manja munthu, ndipo usavomerezane ndi anthu ena pa machimo. Usunge bwino kuyera mtima kwako.
23 Artık yalnız su içmekten vazgeç; miden ve sık sık baş gösteren rahatsızlıkların için biraz da şarap iç.
Uleke kumangomwa madzi okha, koma uzimwako vinyo pangʼono chifukwa cha vuto lako la mʼmimba ndi kudwala kwako kwa pafupipafupi.
24 Bazı kişilerin günahları bellidir, kendilerinden önce yargı kürsüsüne ulaşır. Bazılarının günahlarıysa sonradan ortaya çıkar.
Anthu ena machimo awo amaonekeratu poyera, amakafika pa mpando wachiweruzo eni akewo asanakafike. Machimo a anthu ena amabwera mʼmbuyo mwawo.
25 Bunun gibi, iyi işler de bellidir; belli olmayanlar bile gizli kalamaz.
Momwemonso, ntchito zabwino zimaonekera poyera, ndipo ngakhale zipande kutero, sizingatheke kubisika.