< 1 Samuel 4 >
1 Samuel'in sözü bütün İsrail'de yayıldı. İsrailliler Filistliler'le savaşmak üzere yola çıktılar. İsrailliler Even-Ezer'de, Filistliler de Afek'te ordugah kurdu.
Ndipo mawu a Samueli anafika kwa Aisraeli onse. Aisraeli anapita kukamenya nkhondo ndi Afilisti. Aisraeli anamanga misasa yawo ku Ebenezeri, ndipo Afilisti anamanga ku Afeki.
2 Filistliler İsrail'e karşı savaş düzenine girdiler. Savaş her yere yayılınca, Filistliler İsrailliler'i bozguna uğrattı. Savaş alanında dört bine yakın İsrailli'yi öldürdüler.
Afilisti anandanda kuyangʼana Aisraeli nayamba kumenyana. Nkhondo inakula ndipo Afilisti anagonjetsa Aisraeli napha anthu 4,000 pa malo a nkhondopo.
3 Askerler ordugaha dönünce, İsrail'in ileri gelenleri, “Neden bugün RAB bizi Filistliler'in önünde bozguna uğrattı?” diye sordular, “RAB'bin Antlaşma Sandığı'nı Şilo'dan buraya getirelim ki, aramıza geldiğinde bizi düşmanlarımızın elinden kurtarsın.”
Asilikali atabwerera ku misasa, akuluakulu a Israeli anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Yehova walola kuti tigonjetsedwe lero pamaso pa Afilisti? Tiyeni tikatenge Bokosi la Chipangano cha Yehova ku Silo kuti Yehovayo abwere kukhala pakati pathu ndi kutipulumutsa mʼmanja mwa adani athu.”
4 Halk Şilo'ya adamlar gönderdi. Keruvlar arasında taht kurmuş, Her Şeye Egemen RAB'bin Antlaşma Sandığı'nı oradan getirdiler. Eli'nin iki oğlu, Hofni ile Pinehas da Tanrı'nın Antlaşma Sandığı'nın yanındaydılar.
Choncho anatuma anthu ku Silo ndipo anakatenga Bokosi la Chipangano cha Yehova Wamphamvuzonse amene amakhala pa akerubi. Ndipo ana awiri a Eli, Hofini ndi Finehasi anatsagana nalo Bokosi la Chipangano cha Mulungu.
5 RAB'bin Antlaşma Sandığı ordugaha varınca, bütün İsrailliler öyle yüksek sesle bağırdılar ki, yer yerinden oynadı.
Bokosi la Chipangano cha Yehova litafika ku msasa, Aisraeli onse anafuwula kwambiri mpaka nthaka inagwedezeka.
6 Filistliler bağrışmaları duyunca, “İbraniler'in ordugahındaki bu yüksek bağrışmaların anlamı ne?” diye sordular. RAB'bin Sandığı'nın ordugaha getirildiğini öğrenince,
Atamva kufuwulaku, Afilisti anafunsa, “Kodi kufuwula kwakukulu kumeneku ku misasa ya Ahebri ndi kwachiyani?” Atamva kuti Bokosi la Yehova lafika ku msasako,
7 korkarak, “Tanrılar ordugaha gelmiş” dediler, “Vay başımıza! Daha önce buna benzer bir olay olmamıştı.
Afilisti anachita mantha pakuti iwo ankanena kuti, “Milungu yafika ku msasa. Iwo anati, ‘Tili pamavuto. Chinthu choterechi sichinachitikepo nʼkale lomwe.
8 Vay başımıza! Bu güçlü tanrıların elinden bizi kim kurtarabilir? Çölde Mısırlılar'ı her tür belaya çarptıran tanrılar bunlar.
Atsoka ife! Adzatipulumutsa ndani mʼmanja mwa milungu yamphamvuyi? Iyi ndi milungu imene inakantha Aigupto ndi miliri yosiyanasiyana mʼchipululu.
9 Güçlü olun, ey Filistliler! Yiğitçe davranın! Yoksa, İbraniler size nasıl boyun eğdiyse, siz de onlara öyle boyun eğeceksiniz. Bu yüzden yiğitçe davranın ve savaşın!”
Limbani mtima Afilisti! Chitani chamuna, kuti mungakhale akapolo a Ahebri monga iwowa alili akapolo anu. Chitani chamuna ndipo menyani nkhondo!’”
10 Böylece Filistliler savaşıp İsrailliler'i bozguna uğrattılar. İsrailliler'in hepsi evlerine kaçtı. Yenilgi öyle büyüktü ki, İsrailliler otuz bin yaya asker yitirdi,
Choncho Afilisti anamenya nkhondo, ndipo anagonjetsa Aisraeli. Iwo anathawa aliyense kwawo. Ankhondo a Aisraeli oyenda pansi okwanira 30,000 anaphedwa.
11 Tanrı'nın Sandığı alındı, Eli'nin iki oğlu, Hofni ile Pinehas öldü.
Ndipo Bokosi la Chipangano la Yehova linalandidwa, ndiponso ana awiri Eli, Hofini ndi Finehasi anaphedwa.
12 Benyaminli bir adam savaş alanından koşarak aynı gün Şilo'ya ulaştı. Giysileri yırtılmış, başı toz toprak içindeydi.
Tsiku lomwelo munthu wina wa fuko la Benjamini anathawa ku nkhondo ndipo anafika ku Silo. Iyeyu zovala zake zinali zongʼamba ndipo anadzithira dothi kumutu kuonetsa chisoni.
13 Adam Şilo'ya vardığında, Tanrı'nın Sandığı için yüreği titreyen Eli, yol kenarında bir sandalyeye oturmuş, kaygıyla bekliyordu. Adam kente girip olup bitenleri anlatınca, kenttekilerin tümü haykırdı.
Atafika, anapeza Eli atakhala pa mpando wake mʼmbali mwa msewu, akungoyangʼana, pakuti ankadera nkhawa Bokosi la Mulungu. Munthuyo atalowa mu mzindamo ndi kufotokoza zimene zinachitika ku nkhondo, anthu onse a mu mzindamo anayamba kulira.
14 Eli haykırışları duyunca, “Bu gürültünün anlamı ne?” diye sordu. Adam olanları Eli'ye bildirmek için hemen onun yanına geldi.
Eli atamva kulirako anafunsa kuti, “Kodi phokosoli likutanthauza chiyani?” Tsono munthu wa fuko la Benjamini uja anapita msanga kwa Eli kukamufotokozera.
15 O sırada Eli doksan sekiz yaşındaydı. Gözleri zayıflamış, göremiyordu.
Nthawiyo nʼkuti Eli ali wa zaka 98 ndipo maso ake anali atachita khungu kotero kuti samatha kuona.
16 Adam Eli'ye, “Ben savaş alanından geliyorum” dedi, “Savaş alanından bugün kaçtım.” Eli, “Ne oldu, oğlum?” diye sordu.
Munthuyo anamuwuza Eli kuti, “Ine ndabwera kuchokera ku nkhondo, ndathawako lero lomwe lino.” Eli anafunsa, “Nanga nkhondo yayenda bwanji mwana wanga?”
17 Haber getiren adam şöyle yanıtladı: “İsrailliler Filistliler'in önünden kaçtı. Askerler büyük bir yenilgiye uğradı. İki oğlun, Hofni'yle Pinehas öldü. Tanrı'nın Sandığı da ele geçirildi.”
Iye anayankha kuti, “Aisraeli athawa pamaso pa Afilisti. Anthu ambirimbiri aphedwa. Ana anunso Hofini ndi Finehasi aphedwa. Bokosi la Mulungu nalonso lalandidwa.”
18 Adam Tanrı'nın Sandığı'ndan söz edince, Eli sandalyeden geriye, kapının yanına düştü. Yaşlı ve şişman olduğundan boynu kırılıp öldü. İsrail halkını kırk yıl süreyle yönetmişti.
Atangotchula Bokosi la Yehova, Eli anagwa chagada, kuchoka pa mpando wake umene unali mʼmbali mwa chitseko cha mpanda. Khosi lake linathyoka ndipo anafa, pakuti anali okalamba ndi onenepa kwambiri. Iye anatsogolera Israeli zaka makumi anayi.
19 Eli'nin gelini –Pinehas'ın karısı– gebeydi, doğurmak üzereydi. Tanrı'nın Sandığı'nın ele geçirildiğini, kayınbabasıyla kocasının öldüğünü duyunca birden sancıları tuttu, yere çömelip doğurdu.
Nthawiyo, mpongozi wa Eli, mkazi wa Finehasi anali woyembekezera ndipo anali pafupi kuchira. Atamva kuti Bokosi la Mulungu lalandidwa ndi kuti mpongozi wake Eli ndi mwamuna wake amwalira, ululu wa pobereka mwana unamufikira modzidzimutsa ndipo anabereka mwana.
20 Ölmek üzereyken ona yardım eden kadınlar, “Korkma, bir oğlun oldu” dediler. Ama o aldırmadı, karşılık da vermedi.
Popeza mkaziyo anali pafupi kumwalira, akazi amene amamuthandiza anati, “Usaope, wabereka mwana wamwamuna” Koma iye sanayankhe kapena kulabadirako.
21 Tanrı'nın Sandığı ele geçirilmiş, kayınbabasıyla kocası ölmüştü. Bu yüzden, “Yücelik İsrail'den ayrıldı!” diyerek çocuğa İkavot adını verdi.
Tsono iye anatcha mwanayo dzina loti Ikabodi kutanthauza kuti, “Ulemerero wachoka mu Israeli,” chifukwa cha kulandidwa Bokosi la Mulungu ndi imfa ya mpongozi wake Eli ndi mwamuna wake.
22 “Yücelik İsrail'den ayrıldı!” dedi, “Çünkü Tanrı'nın Sandığı ele geçirildi.”
Ananena momwemo kuti, “Ulemerero wachoka mu Israeli, pakuti Bokosi la Mulungu lalandidwa.”