< 1 Krallar 20 >
1 Aram Kralı Ben-Hadat bütün ordusunu topladı. Atları, savaş arabaları ve kendisini destekleyen otuz iki kralla birlikte Samiriye'nin üzerine yürüyerek kenti kuşattı.
Tsono Beni-Hadadi mfumu ya ku Aramu inasonkhanitsa magulu ake onse a ankhondo. Iye pamodzi ndi mafumu 32, akavalo awo ndi magaleta awo, anapita kukawuzungulira mzinda wa Samariya ndi kuwuthira nkhondo.
2 Ben-Hadat, kentte bulunan İsrail Kralı Ahav'a haberciler göndererek şöyle buyruk verdi:
Iye anatuma amithenga ake mu mzindamo kwa Ahabu mfumu ya Israeli, kukanena kuti,
3 “Ben-Hadat diyor ki, ‘Altınını, gümüşünü, karılarını ve en gürbüz çocuklarını bana teslim et.’”
“Beni-Hadadi akuti, ‘Siliva wako ndi golide wako ndi wanga, ndipo akazi ako okongola ndi ana ako ndi anganso.’”
4 İsrail Kralı, “Efendim kralın dediklerini kabul ediyorum” diye karşılık verdi, “Beni ve sahip olduğum her şeyi alabilirsin.”
Mfumu ya Israeli inayankha kuti, “Monga mmene mwanenera, mbuye wanga mfumu, ine pamodzi ndi zonse zomwe ndili nazo ndi zanu.”
5 Haberciler yine gelip Ahav'a şöyle dediler: “Ben-Hadat diyor ki, ‘Sana altınını, gümüşünü, karılarını ve çocuklarını bana vereceksin diye haber göndermiştim.
Amithenga aja anabwereranso kwa Ahabu ndipo anamuwuza kuti, “Beni-Hadadi akuti, ‘Ine ndinakulamula kuti undipatse siliva wako ndi golide wako, akazi ako ndi ana ako.
6 Ayrıca yarın bu saatlerde sarayında ve görevlilerinin evlerinde arama yapmak üzere kendi görevlilerimi göndereceğim. Değerli olan her şeyini alıp getirecekler.’”
Koma mawa nthawi ngati yomwe ino ndidzatuma atumiki anga kudzafufuza mʼnyumba yako yaufumu ndi nyumba za akuluakulu ako. Iwo adzatenga chilichonse chimene umachidalira ndi kupita nacho.’”
7 İsrail Kralı ülkenin bütün ileri gelenlerini toplayarak, “Bakın, bu adam nasıl bela arıyor!” dedi, “Bana haber gönderip altınımı, gümüşümü, karılarımı, çocuklarımı istedi, reddetmedim.”
Pamenepo mfumu ya Israeli inayitanitsa akuluakulu a mʼdzikomo niwawuza kuti, “Taonani momwe munthuyu akufunira kutibweretsera mavuto! Atatumiza mawu oti ndimupatse akazi anga ndi ana anga, siliva wanga ndi golide wanga, ine sindinamukanize.”
8 Bütün ileri gelenler ve halk, “Onu dinleme, isteklerini de kabul etme” diye karşılık verdiler.
Akuluakulu onse ndi anthu onse anayankha kuti, “Musamumvere kapena kuvomereza zofuna zake.”
9 Böylece Ahav, Ben-Hadat'ın habercilerine, “Efendimiz krala ilk isteklerinin hepsini kabul edeceğimi, ama ikincisini kabul edemeyeceğimi söyleyin” dedi. Haberciler gidip Ben-Hadat'a durumu bildirdiler.
Tsono Ahabu anayankha amithenga a Beni-Hadadi kuti, “Kamuwuzeni mbuye wanga mfumu kuti, ‘Mtumiki wanu adzachita zonse zimene munazifuna nthawi yoyamba ija, koma izi mwazifunazi sindingazikwanitse.’” Iwo anachoka nakapereka yankho kwa Beni-Hadadi.
10 O zaman Ben-Hadat Ahav'a başka bir haber gönderdi: “O kadar çok adamla senin üstüne yürüyeceğim ki, Samiriye'yi yerle bir edeceğim. Kentin tozları askerlerimin avuçlarını bile dolduramayacak. Eğer bunu yapmazsam, ilahlar bana aynısını, hatta daha kötüsünü yapsın!”
Pamenepo Beni-Hadadi anatumizanso uthenga wina kwa Ahabu kuti, “Milungu indilange koopsa, ngati mu Samariya mudzakhale fumbi loti nʼkudzaza dzanja la aliyense wa anthu anga.”
11 İsrail Kralı şöyle karşılık verdi: “Kralınıza deyin ki, ‘Zırhını kuşanmadan önce değil, kuşandıktan sonra övünsün.’”
Mfumu ya Israeli inayankha kuti, “Kamuwuzeni kuti, ‘Mwamuna mnzako nʼpachulu, nʼkulinga utakwerapo.’”
12 Ben-Hadat bunu duyduğunda, kendisini destekleyen krallarla birlikte çadırda içki içiyordu. Hemen adamlarına buyruk verdi: “Saldırıya hazırlanın.” Böylece Samiriye'ye karşı saldırı hazırlıklarına giriştiler.
Beni-Hadadi anamva uthenga umenewu pamene iye ankamwa ndi mafumu anzake mʼmatenti awo, ndipo analamula anthu ake kuti, “Konzekerani kukathira nkhondo.” Choncho anakonzekera kukathira nkhondo mzindawo.
13 O sırada bir peygamber gelip İsrail Kralı Ahav'a şöyle dedi: “RAB diyor ki, ‘Bu büyük orduyu görüyor musun? Onları bugün senin eline teslim edeceğim. O zaman benim RAB olduğumu anlayacaksın.’”
Ndipo taonani, mneneri wina anabwera kwa Ahabu mfumu ya Israeli nadzalengeza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi ukuchiona chigulu chachikulu cha ankhondochi? Taona, ndikuchipereka chimenechi lero mʼdzanja lako, ndipo pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
14 Ahav, “Kimin aracılığıyla olacak bu?” diye sordu. Peygamber şu karşılığı verdi: “RAB diyor ki, ‘İlçe komutanlarının genç askerleri bunu başaracak.’” Ahav, “Savaşa kim başlayacak?” diye sordu. Peygamber, “Sen başlayacaksın” dedi.
Ahabu anafunsa kuti, “Koma ndani adzachita zimenezi?” Mneneri anayankha kuti, “Yehova akuti, ‘Adzachita zimenezi ndi asilikali a nduna za mʼzigawo.’” Ndipo iye anafunsa kuti, “Kodi ndani adzayambe nkhondoyi?” Mneneriyo anayankha kuti, “Ndinu.”
15 Ahav ilçe komutanlarının genç askerlerini çağırıp saydı. İki yüz otuz iki kişiydiler. Sonra bütün İsrail ordusunu toplayıp saydı, onlar da yedi bin kişiydiler.
Choncho Ahabu anawerenga asilikali achinyamata a nduna za mʼzigawo ndipo onse analipo 232. Ndipo anawerenganso ankhondo a ku Israeli ndipo onse analipo 7,000.
16 Öğleyin Ben-Hadat ile kendisini destekleyen otuz iki kral çadırlarda içip sarhoş olmuşken İsrail saldırısı başladı.
Iwo ananyamuka nthawi yamasana pamene Beni-Hadadi ndi mafumu 32 othandizana naye ankamwa mpaka kuledzera mʼmatenti awo.
17 Önce genç askerler saldırıya geçti. Ben-Hadat'ın gönderdiği gözcüler, “Samiriyeliler geliyor” diye ona haber getirdiler.
Asilikali achinyamata a nduna za mʼzigawo ndiwo amene anayamba kupita ku nkhondo. Nthawi imeneyi Beni-Hadadi nʼkuti atatumiza anthu oti akazonde, amene anadzafotokoza kuti, “Anthu ankhondo akubwera kuchokera ku Samariya.”
18 Ben-Hadat, “İster barış, ister savaş için gelsinler, onları canlı yakalayın” dedi.
Iye anati, “Kaya akubwera mwamtendere kapena mwankhondo, muwagwire amoyo.”
19 Genç askerler arkalarındaki İsrail ordusuyla birlikte kentten çıkıp saldırıya geçtiler.
Choncho asilikali achinyamata a nduna za mʼzigawo anatuluka mu mzinda, gulu lankhondo lili pambuyo pawo.
20 Herkes önüne geleni öldürdü. Aramlılar kaçmaya başlayınca, İsrailliler peşlerine düştü. Ama Aram Kralı Ben-Hadat, atına binerek atlılarla birlikte kaçıp kurtuldu.
Ndipo aliyense wa iwo anapha munthu wake. Ataona izi, Aaramu anathawa Aisraeli ali pambuyo pawo kuwapirikitsa. Koma Beni-Hadadi mfumu ya ku Aaramu anathawa atakwera pa kavalo pamodzi ndi ankhondo ena okweranso pa akavalo.
21 İsrail Kralı atlarla savaş arabalarına büyük zararlar vererek Aramlılar'ı ağır bir yenilgiye uğrattı.
Mfumu ya Israeli inapita chitsogolo ndi kugwira akavalo ndi magaleta ndipo Aaramu ambiri anaphedwa.
22 Daha sonra peygamber gelip İsrail Kralı'na, “Git, gücünü pekiştir ve neler yapman gerektiğini iyi düşün” dedi, “Çünkü önümüzdeki ilkbaharda Aram Kralı sana yine saldıracak.”
Zitachitika izi, mneneri wina anabwera kwa mfumu ya Israeli ndipo anati, “Mulimbike ndipo muganize bwino zoti mudzachite, chifukwa chaka chikudzachi mfumu ya Aramu idzakuthiraninso nkhondo.”
23 Bu arada görevlileri Aram Kralı'nın kendisine, “İsrail'in ilahı dağ ilahıdır” dediler, “Bu nedenle bizden güçlü çıktılar. Ama ovada savaşırsak, onları kesinlikle yeneriz.
Nthawi imeneyi, akuluakulu a mfumu ya Aramu anamulangiza kuti, “Milungu ya anthu a ku Israeli ndi milungu ya mʼmapiri. Nʼchifukwa chake anali ndi mphamvu zotipambana ife. Koma ngati tidzamenyana nawo ku chigwa, ndithudi ife tidzakhala ndi mphamvu kuposa iwo.
24 Şimdi bütün kralları görevlerinden al, onların yerine yeni komutanlar ata.
Inu chitani izi: chotsani mafumu onse pa maudindo awo ndipo mʼmalo mwawo muyikemo atsogoleri a ankhondo.
25 Kaybettiğin kadar at ve savaş arabası toplayarak kendine yeni bir ordu kur. İsrailliler'le ovada savaşalım. O zaman onları kesinlikle yeneriz.” Aram Kralı Ben-Hadat bütün söylenenleri kabul edip yerine getirdi.
Musonkhanitsenso gulu lankhondo lofanana ndi lomwe linaphedwa lija, akavalo monga omwe anaphedwa aja, ndi magaleta monga omwe anawonongedwa aja, kuti tikamenyane ndi Israeli ku chigwa. Pamenepo, ife tidzapambana iwowo.” Beni-Hadadi anagwirizana nawo ndipo anachita momwemo.
26 İlkbaharda Aramlılar'ı toplayıp İsrailliler'le savaşmak üzere Afek Kenti'ne gitti.
Chaka chinacho Beni-Hadadi anasonkhanitsa Aaramu, napita ku Afeki kukamenyana ndi Israeli.
27 İsrail halkı da toplanıp yiyeceğini hazırladı. Aramlılar'la savaşmak üzere yola çıkıp onların karşısına ordugah kurdu. Ülkeyi dolduran Aramlılar'ın karşısında İsrailliler iki küçük oğlak sürüsü gibi kalıyordu.
Aisraeli atasonkhananso, napatsidwa zakudya zawo anapita kukakumana nawo. Aisraeli anamanga misasa yawo moyangʼanana ndi Aaramu ndipo ankaoneka ngati timagulu tiwiri ta mbuzi, pomwe Aaramu anali atakuta dera lonselo.
28 Bir Tanrı adamı gidip İsrail Kralı Ahav'a şöyle dedi: “RAB diyor ki, ‘Aramlılar, RAB dağların Tanrısı'dır, ovaların değil, dedikleri için bu güçlü ordunun tümünü senin eline teslim edeceğim. O zaman benim RAB olduğumu anlayacaksın.’”
Munthu wa Mulungu anabwera, nawuza mfumu ya Israeli kuti, “Yehova akuti, ‘Popeza Aaramu akuganiza kuti Yehova ndi mulungu wa ku mapiri, osati wa ku zigwa, Ine ndidzapereka chigulu chonsechi kwa iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
29 Birbirlerine karşı ordugah kuran Aramlılar'la İsrailliler yedi gün beklediler. Yedinci gün savaş başladı. İsrailliler bir gün içinde yüz bin Aramlı yaya asker öldürdü.
Kwa masiku asanu ndi awiri anakhala moyangʼanana mʼmisasa yawo, ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri nkhondo inayambika. Aisraeli anapha Aaramu okwana 100,000 tsiku limodzi lokha.
30 Sağ kalanlar Afek Kenti'ne kaçtılar. Orada da yirmi yedi bin kişinin üstüne surlar yıkıldı. Ben-Hadat kentin içine kaçıp bir iç odaya saklandı.
Ena onse otsala anathawira ku Afeki, kumene khoma linagwera anthu 27,000. Ndipo Beni-Hadadi anathawira mu mzinda, nakabisala mʼchipinda chamʼkati.
31 Görevlileri Ben-Hadat'a şöyle dediler: “Duyduğumuza göre, İsrail kralları iyi yürekli krallarmış. Haydi bellerimize çul kuşanıp başlarımıza ip saralım ve İsrail Kralı'nın huzuruna çıkalım. Belki senin canını bağışlar.”
Atumiki ake anamuwuza kuti, “Taonani, ife tamva kuti mafumu a fuko la Israeli ndi achifundo. Tiyeni tipite kwa mfumu ya ku Israeli titavala ziguduli mʼchiwuno mwathu ndi kumanga zingwe mʼmakosi mwathu. Mwina iye sakakuphani.”
32 Bellerine çul kuşanıp başlarına da ip bağladılar ve İsrail Kralı'nın huzuruna çıkarak, “Kulun Ben-Hadat ‘Canımı bağışla’ diye yalvarıyor” dediler. Ahav, “Ben-Hadat hâlâ yaşıyor mu? O benim kardeşim sayılır” diye karşılık verdi.
Atavala ziguduli mʼchiwuno mwawo ndi kumanga zingwe mʼmakosi mwawo, anapita kwa mfumu ya ku Israeli ndipo anayiwuza kuti, “Mtumiki wanu Beni-Hadadi akunena kuti, ‘Chonde loleni kuti ndikhale moyo.’” Mfumu inayankha kuti, “Kodi iye akanali ndi moyo? Iye ujatu ndi mʼbale wanga.”
33 Adamlar bunu olumlu bir belirti sayarak hemen sözü ağzından aldılar ve, “Evet, Ben-Hadat kardeşin sayılır!” dediler. Kral, “Gidin, onu getirin” diye buyruk verdi. Ben-Hadat gelince, Ahav onu kendi savaş arabasına aldı.
Anthuwo ankaganiza kuti mawuwo anali abwino ndipo anavomereza mawuwa mofulumira. Iwo anati, “Inde, Beni-Hadadi ndi mʼbale wanu!” Mfumu inati, “Pitani kamutengeni.” Beni-Hadadi atatuluka, Ahabu anamukweza mʼgaleta lake.
34 Ben-Hadat, “Babamın babandan almış olduğu kentleri geri vereceğim” dedi, “Babam nasıl Samiriye'de çarşılar kurduysa, sen de Şam'da çarşılar kurabilirsin.” Bunun üzerine Ahav, “Ben de bu şartlara dayanarak sana özgürlüğünü veriyorum” dedi. Böylece onunla bir antlaşma yaparak gitmesine izin verdi.
Beni-Hadadi anawuza Ahabu kuti, “Ndidzabweza mizinda imene abambo anga analanda abambo anu. Ndipo mutha kumanga nyumba zanu zamalonda mu Damasiko, monga anachitira abambo anga ku Samariya.” Ahabu anati, “Chifukwa cha mgwirizano umenewu, ine ndidzakumasula.” Choncho anachita naye mgwirizano, ndipo anamulola kuti apite.
35 Peygamberlerden biri, RAB'bin sözüne uyarak arkadaşına, “Lütfen, beni vur!” dedi. Ama arkadaşı onu vurmak istemedi.
Molamulidwa ndi Yehova, mmodzi mwa ana a aneneri anawuza mnzake kuti, “Chonde, menye ndi chida chako,” koma mnzakeyo anakana.
36 O zaman peygamber arkadaşına şöyle dedi: “Sen RAB'bin buyruğunu dinlemediğin için, yanımdan ayrılır ayrılmaz bir aslan seni öldürecek.” Adam oradan ayrıldıktan sonra aslan onu yakalayıp öldürdü.
Choncho mneneriyo anati, “Chifukwa sunamvere Yehova, ukangochoka pano, mkango ukupha.” Ndipo munthuyo atangochoka pamenepo, mkango unamupeza ndi kumupha.
37 Bunun üzerine aynı peygamber, başka bir adama giderek, “Lütfen beni vur!” dedi. Adam da onu vurup yaraladı.
Mneneriyo anapeza munthu wina ndipo anamuwuza kuti, “Chonde, menye.” Choncho munthuyo anamumenya ndi kumuvulaza.
38 Peygamber gitti, kılığını değiştirmek için gözlerini bağladı. Yol kenarında kralın geçmesini beklemeye başladı.
Pamenepo mneneriyo anapita nakayima pa msewu kudikirira mfumu. Iye anadzibisa nakulunga nsalu nkhope yake.
39 Kral oradan geçerken, peygamber ona şöyle seslendi: “Ben kulun, tam savaşın içindeyken, askerin biri bana bir tutsak getirip, ‘Bu adamı iyi koru’ dedi, ‘Kaçacak olursa, karşılığını ya canınla, ya da bir talant gümüşle ödersin.’
Mmene mfumu inkadutsa pamenepo, mneneriyo anafuwula kwa mfumuyo kuti, “Ine mtumiki wanu ndinalowa pakati pa nkhondo, ndipo munthu wina anabwera kwa ine atatenga mmodzi mwa anthu ogwidwa pa nkhondo, nandiwuza kuti, ‘Sunga munthu uyu. Ngati asowa, ndiye kuti ndidzakupha, kapena udzalipira ndalama 3,000 za siliva.’
40 Ama ben oraya buraya bakarken, adam kayboldu.” İsrail Kralı, “Sen kendini yargılamış oldun” diye karşılık verdi, “Cezanı çekeceksin.”
Pamene ine mtumiki wanu ndinali wotanganidwa apa ndi apa, munthuyo anasowa.” Mfumu ya Israeli inati, “Chimenechi ndiye chilango chako. Iwe wadziweruza wekha.”
41 Peygamber, hemen gözlerindeki sargıyı çıkardı. O zaman İsrail Kralı onun bir peygamber olduğunu anladı.
Pamenepo mneneriyo anachotsa msangamsanga nsalu yomwe anakulunga pa nkhope yake, ndipo mfumu ya Israeli inamuzindikira kuti ndi mmodzi mwa aneneri.
42 Bunun üzerine peygamber krala şöyle dedi: “RAB diyor ki, ‘Ölüme mahkûm ettiğim adamı salıverdiğin için onun yerine sen öleceksin. Onun halkının başına gelecekler senin halkının başına gelecek.’”
Iye anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chakuti mwamasula munthu amene Ine ndinati ndi woyenera kuphedwa, inuyo ndi amene mudzaphedwe mʼmalo mwa iyeyo, anthu anu mʼmalo mwa anthu ake.’”
43 Keyfi kaçan İsrail Kralı öfkeyle Samiriye'deki sarayına döndü.
Mwachisoni ndi mokwiya, mfumu ya Israeli inapita ku nyumba yake yaufumu ku Samariya.