< 1 Tarihler 19 >

1 Bir süre sonra Ammon Kralı Nahaş öldü, yerine oğlu kral oldu.
Patapita nthawi Nahasi mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
2 Davut, “Babası bana iyilik ettiği için ben de Nahaş oğlu Hanun'a iyilik edeceğim” diye düşünerek, babasının ölümünden dolayı baş sağlığı dilemek için Hanun'a ulaklar gönderdi. Davut'un ulakları Hanun'a baş sağlığı dilemek için Ammonlular'ın ülkesine varınca,
Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake. Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni kudzamupepesa,
3 Ammon önderleri Hanun'a şöyle dediler: “Davut sana baş sağlığı dileyen bu adamları gönderdi diye babana saygı duyduğunu mu sanıyorsun? Bu ulaklar ülkeyi araştırmak, casusluk etmek, yıkmak için buraya geldiler.”
atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi anthuwa sanawatumize kuti adzaone dziko lathu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?”
4 Bunun üzerine Hanun Davut'un ulaklarını yakalattı. Sakallarını tıraş edip giysilerinin kalçayı kapatan kesimini ortadan kesti ve onları öylece gönderdi.
Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anawameta ndi kudula zovala zawo pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera ndipo anawabweza kwawo.
5 Davut bunu duyunca, ulakları karşılamak üzere adamlar gönderdi. Çünkü ulaklar çok utanıyorlardı. Kral, “Sakalınız uzayıncaya dek Eriha'da kalın, sonra dönün” diye buyruk verdi.
Munthu wina atafika ndi kufotokozera Davide za anthuwo, iye anatuma amithenga kukakumana nawo, chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”
6 Ammonlular Davut'un nefretini kazandıklarını anlayınca, Hanun'la Ammonlular Aram-Naharayim, Aram-Maaka ve Sova'dan savaş arabalarıyla atlılar kiralamak için bin talant gümüş gönderdiler.
Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, Hanuni ndi Aamoni anatumiza siliva wolemera makilogalamu 34,000 kuti akalipirire magaleta ndi okwerapo ake a ku Mesopotamiya; Aramu-Maaka ndi Zoba.
7 Otuz iki bin savaş arabası ve Maaka Kralı'yla askerlerini kiraladılar. Maaka Kralı'yla askerleri gelip Medeva'nın yakınında ordugah kurdular. Ammonlular da savaşmak üzere kentlerinden çıkıp bir araya geldiler.
Iwo analipira magaleta okwanira 32,000, pamodzi ndi mfumu ya ku Maaka ndi ankhondo ake. Amenewa anabwera ndi kudzamanga misasa yawo pafupi ndi Medeba. Nawonso Aamoni anabwera kuchokera ku mizinda yawo ndipo anapita kukachita nkhondo.
8 Davut bunu duyunca, Yoav'ı ve güçlü adamlardan oluşan bütün ordusunu onlara karşı gönderdi.
Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu.
9 Ammonlular çıkıp kent kapısında savaş düzeni aldılar. Yardıma gelen krallar da kırda savaş düzenine girdiler.
Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene mafumu amene anabwera nawo anali kwa wokha, ku malo wopanda mitengo.
10 Önde, arkada düşman birliklerini gören Yoav, İsrail'in en iyi askerlerinden bazılarını seçerek Aramlılar'ın karşısına yerleştirdi.
Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake; iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu.
11 Geri kalan birlikleri de kardeşi Avişay'ın komutasına vererek Ammonlular'a karşı yerleştirdi.
Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni.
12 Yoav, “Aramlılar benden güçlü çıkarsa, yardımıma gelirsin” dedi, “Ama Ammonlular senden güçlü çıkarsa, ben sana yardıma gelirim.
Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse; koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa.
13 Güçlü ol! Halkımızın ve Tanrımız'ın kentleri uğruna yürekli olalım! RAB gözünde iyi olanı yapsın.”
Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”
14 Yoav'la yanındakiler Aramlılar'a karşı savaşmak için ileri atılınca, Aramlılar onlardan kaçtı.
Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake.
15 Aramlılar'ın kaçıştığını gören Ammonlular da Yoav'ın kardeşi Avişay'dan kaçarak kente girdiler. Yoav ise Yeruşalim'e döndü.
Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai mʼbale wake ndi kulowa mu mzinda. Motero Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.
16 İsrailliler'in önünde bozguna uğradıklarını gören Aramlılar, ulaklar gönderip Fırat Irmağı'nın karşı yakasında, Hadadezer'in ordu komutanı Şofak'ın komutasındaki Aramlılar'ı çağırdılar.
Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, pamodzi ndi mtsogoleri wa ankhondo wa Hadadezeri, Sofaki akuwatsogolera.
17 Davut bunu duyunca, bütün İsrail ordusunu topladı. Şeria Irmağı'ndan geçerek onlara doğru ilerleyip karşılarında savaş düzeni aldı. Davut savaşmak için düzen alınca, Aramlılar onunla savaştılar.
Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani. Iyeyo anapita kukakumana nawo ndipo anakhala mʼmizere yankhondo moyangʼanana ndipo iwo anamenyana naye.
18 Ne var ki, Aramlılar İsrailliler'in önünden kaçtılar. Davut onlardan yedi bin savaş arabası sürücüsü ile kırk bin yaya asker öldürdü. Ordu komutanı Şofak'ı da öldürdü.
Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 7,000 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Iye anaphanso Sofaki, mtsogoleri wawo wankhondo.
19 Hadadezer'in buyruğundaki krallar İsrailliler'in önünde bozguna uğradıklarını görünce, Davut'la barış yaparak ona boyun eğdiler. Aramlılar bundan böyle Ammonlular'a yardım etmekten kaçındılar.
Mafumu amene ali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anachita mtendere ndi Davide ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.

< 1 Tarihler 19 >