< Qığeepç'iy 8 >
1 Rəbbee Mısayk'le eyhen: – Fironusqa hark'ın mang'uk'le eyhe: «Rəbbee inəxüdud eyhe: „Yizın millet g'aykke Zas ı'bəədat he'ecen!
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Ukamuwuze Farao kuti, Lolani anthu anga kuti apite, akandipembedze.
2 Vas g'avkas diviykıneene, Zı yiğna ölkavolle qı'rqı'mı't'er gyoğa'as.
Ndipo ngati simulola kuti apite Ine ndidzalanga dziko lonse la Igupto polidzaza ndi achule.
3 Nil qı'rqı'mı'teşika gyavts'u vuxhes. Dameençe manbı qığeeç'u yiğne sareeqa, g'ılexhane cigeeqa, tyuleeqa, yiğne insanaaşineyiy yiğne milletne xaybışeeqa, tandurbışeeqa, xamır ha'ane cigabışeeqa qales.
Mtsinje wa Nailo udzadzaza ndi achule. Achulewo adzatuluka ndi kukalowa mʼnyumba yaufumu, ku chipinda chogona ndi pa bedi lako, mʼnyumba za nduna zako ndi pa anthu ako ndi mophikira buledi ndiponso mopangira bulediyo.
4 Qı'rqı'mı't'er valqa, yiğne insanaaşilqa, yiğne milletılqa g'eek'valas“».
Achulewo adzakulumphira iwe ndi anthu ako ndiponso nduna zako.”
5 Rəbbee Mısayk'le meed eyhen: – Harunuk'le inəxüd eyhe: əsaa alyaat'u xıl damabışde, arxbışde, goleeşde ooqa hotkecen. Maadın qı'rqı'mı't'er Misirne ölkalqa salat'e'ecen.
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Loza ndodo yako ku mitsinje, ku ngalande ndi ku zithaphwi ndipo pakhale achule pa dziko lonse la Igupto.’”
6 Harunee əsaanan xıl Misirne xhyanbışilqa hotkumee, xhinençe qı'rqı'mı't'er ılqeeç'u ç'iyeyn aq'va aqqaqan.
Kotero Aaroni analoza dzanja lake pa madzi a ku Igupto, ndipo achule anatuluka nadzaza dziko lonse la Igupto.
7 Cadu ha'anbışissed cadubışika man kar ha'as əxən. Manbışissed Misirne ölkalqa qı'rqı'mı't'er salat'a'as əxənbı.
Koma amatsenga anachita zinthu zomwezo mʼmatsenga awo. Iwonso anatulutsa achule mʼdziko lonse la Igupto.
8 Fironee Mısayiy Harun qopt'ul eyhen: – Rəbbis düə he'e, zaked, yizde milletıked qı'rqı'mı't'er əq'əna qe'ecen. Manke zınad Rəbbis q'urban ablya'as millet g'aykkasın.
Kenaka, Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Pemphera kwa Yehova kuti achulewa achoke kwa ine ndi anthu anga, ndipo ine ndidzalola kuti anthu anu apite kukapereka nsembe kwa Yehova.”
9 Mısee fironuk'le eyhen: – Eyhe vas mısane ıkkan, zı val, yiğne insanaaşıl, yiğne milletil-alla düə hav'u? Mançile qiyğa qı'rqı'mı't'er vassed, yiğne saraybışissed əlyhəəsınbı. Manbı saccu Nilee axvas.
Mose anati kwa Farao, “Inu mungonditchulira nthawi imene mukufuna kuti ndikupempherereni, nduna zanu pamodzi ndi anthu anu kuti achule achoke mʼnyumba zanu ndi kuti atsale okhawo ali mu mtsinje wa Nailo.”
10 Fironee eyhen: – G'iyqa. Mısee alidghıniy qele: – Ğu eyhen xhinne ha'as, mançiked vak'le ats'axhxhesın yişde Allahık, Rəbbik akarna sacar deşda.
Farao anati, “Mawa.” Mose anamuyankha kuti, “Chabwino zidzakhala monga mwaneneramu, kuti mudzadziwe kuti palibe wina wofanana ndi Yehova Mulungu wathu.
11 Qı'rqı'mı't'er vassed, yiğne saraybışissed, yiğne insanaaşissed, yiğne milletıssed əq'əna qeetxhes. Qı'rqı'mı't'er saccu Nilee axvas.
Achule adzachoka mʼnyumba yanu, mʼnyumba za nduna zanu pamodzi ndi za anthu anu. Koma adzatsala mu mtsinje wa Nailo basi.”
12 Mısayiy Harun fironusse avayk'ananbı. Mısee Rəbbıke Vuce salat'ı'iyn qı'rqı'mı't'er ak'anı'iy heqqa.
Mose ndi Aaroni anachoka, ndipo Mose anapemphera kwa Yehova kuti achotse achule amene anatumiza kwa Farao.
13 Rəbbee Mısee Cuke heqqiyn ha'an. Xaybışeedın, məhlabışeedın, çolbuşeedın qı'rqı'mı't'er haat'anbı.
Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha. Achule amene anali mʼnyumba, mʼmabwalo ndi mʼminda anafa
14 Manbı anbarbışeeqa sa'a. Ç'iyeyke əq'ı'yn eva g'əə giyğal.
Aigupto anawunjika achulewo milumilu ndipo dziko linanunkha.
15 Fironuk'le işbı yəqqı'lqa gyatk'u sibık qexhe g'acumee, mana meer hı't'ilqa siyk'al. Rəbbee uvhuyn xhinne eyxhe, fironee Mısayliy Harunul k'ırı iliyxhe deş.
Koma Farao ataona kuti zinthu zinayambanso kukhala bwino, anawumitsanso mtima wake ndipo sanamverenso mawu a Mose ndi Aaroni, monga momwe Yehova ananenera.
16 Rəbbee Mısayk'le eyhen: – Harunuk'le eyhe, əsaa alyaat'u ç'iyelyne toozus ı'xecen. Misirvollete tooz huneeşilqa sak'alas.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti akweze ndodo yake ndi kumenya fumbi la pa nthaka, ndipo fumbilo lidzasanduka nsabwe pa dziko lonse la Igupto.”
17 Manbışe həməxüdud haa'an. Harunee xıle aqqıyn əsaa ulyot'ul ç'iyeleğana ulyosse. Mançe insanaaşilqad həyvanaşilqad huneer ileedaxva. Misirvollette gırgın tooz huneeşilqa siyk'al.
Iwo anachita momwemo, ndipo pamene Aaroni anakweza ndodo yake ndi kumenya fumbi, nsabwe zinafika pa munthu aliyense ndi pa ziweto. Fumbi lonse la mʼdziko la Igupto linasanduka nsabwe.
18 Cadu ha'anbışisıd caduyka insanaaşilqa huneer g'axiles ıkkiykan. Man manbışisse ha'as əxə deş. İnsanarab həyvanarad huneeşe gyats'enbı.
Koma amatsenga atayesa kupanga nsabwe mwa matsenga awo, analephera. Ndipo nsabwezo zinali pa munthu aliyense ndi pa ziweto zawo.
19 Cadu ha'anbışe fironuk'le eyhen: – İnçil Allahna xılib alivku. Meed Rəbbe uvhuyn xhinne eyxhe, firon hı't'ilqa siyk'al, mang'vee manbışil k'ırı iliyxhe deş.
Amatsenga anati kwa Farao, “Izi wachita ndi Mulungu.” Koma mtima wa Farao unali wowumabe ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananenera.
20 Rəbbee Mısayk'le eyhen: – G'iyqa miç'eer zara oza qıxha, firon damaysqa ı'qqəmee mang'usqa hark'ın eyhe: «Rəbbee invavud eyhe: „Yizın millet Zas ı'bəədat ha'as g'aykke!
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mmawa, upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso pamene azidzapita ku madzi ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Lola anthu anga kuti apite akandipembedze.
21 Ğu manbı g'ıdivkvee, Zı yiğne saraybışilqad, yiğne insanaaşilqad, yiğne milletılqad goganer veçebışiqa g'axıles. Gırgın ç'iyed, Misirbışin xaybıd goganeeşika gyatts'es.
Koma ngati suwalola anthu anga kuti apite, Ine ndidzatumiza pa iwe ntchentche zoluma ndi pa nduna zako ndi anthu ako ndi mʼnyumba zanu. Mʼnyumba za Aigupto mudzadzaza ntchentche zoluma. Ngakhale pa nthaka pamene akhalapo padzadzaza ndi ntchentche zoluma.’”
22 Zı həməxüd ha'as Yizın millet eyxhene Goşen eyhene cigee goganer ixhes deş. Məxüd vak'led ats'axhxhesın Zı ine cigaynar Rəbb ıxhay.
“Koma pa tsikulo ndidzapatula dera la Goseni, kumene kumakhala anthu anga, motero kuti sikudzakhala ntchentche zoluma. Choncho iwe udzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndikulamulira dziko lino.
23 Zı Yizın millet yiğne milletıke cura'asın. Man əlaamat g'iyqa ixhes“».
Ndidzasiyanitsa pakati pa anthu anga ndi anthu ako. Chizindikiro chozizwitsa ichi chidzachitika mawa.”
24 Rəbbee həməxüdud ha'an. Goganeeşin veçebı aledxu qadı ikkedaç'enbı fironne sareeqad, cune insanaaşine xaybışeeqad. Goganeeşe Misirne ölkalqa ver ablyav'u.
Ndipo Yehova anachita zimenezi: Ntchentche zoluma zochuluka zinalowa mʼnyumba yaufumu ya Farao ndi nyumba za nduna zake. Choncho ntchentche zolumazi zinawononga dziko lonse la Igupto.
25 Fironee Mısayiy Harun qopt'ul eyhen: – Şu vuşde Allahıs yişdecab ölkee q'urban ablee'e.
Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati, “Pitani kaperekeni nsembe kwa Mulungu wanu mʼdziko lomwe lino.”
26 Mıseemee eyhen: – Həməxüd ha'as ixhes deş, Misirbış həlyvətq'ıniy qales, şi yişde Allahıs, Rəbbis inyaa q'urban ablya'a g'avce. Manbışis həlyvətq'ıniy qalya'ana şi q'urban ablyav'ee, manbışe şi g'ayeyqqa hevles.
Koma Mose anati, “Sitingathe kutero pakuti nsembe zathu kwa Yehova Mulungu ndi zowayipira Aigupto. Ngati tipereke nsembe zowayipira Aigupto mʼmaso mwawo, adzatiponya miyala kuti tife.
27 De'eş, şi Rəbbis, yişde Allahıs q'urban ablya'asdemee xhebılle yiğna sahreeqa yəq əlyhəəs vukkan. Rəbbee şak'le məxüd uvhu.
Ife tiyenera kuyenda ulendo wa masiku atatu kupita ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wathu monga anatilamulira.”
28 Fironee eyhen: – Zı şu, vuşde Allahıs, Rəbbis q'urban ablyaa'as sahreeqa g'avkasınbı, saccu əq'ənaqa ımaak'an. Zal-allab düə hee'e.
Farao anati, “Ine ndikulolani kuti mupite ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wanu, koma musapite kutali kwambiri. Tsopano ndipempherereni.”
29 Mısee eyhen: – Zı vasse qığeç'umecar Rəbbis düə haa'as. G'iyqa goganer vassed, yiğne insanaaşissed, yiğne milletıssed aleetxu əlyhəəsınbı. Saccu ğu meed horbu hıma'a, millet Rəbbis q'urban ablyaa'as g'aykkasınva.
Mose anayankha kuti, “Ine ndikangochoka pano, ndikapemphera kwa Yehova ndipo mawa lomweli ntchentche zoluma zidzachoka kwa Farao, nduna zake pamodzi ndi anthu ake. Koma Farao, onetsetsani kuti musachitenso zachinyengo ndi kuwakaniza anthu kuti asakapereke nsembe kwa Yehova.”
30 Mısa fironusse ark'ın Rəbbis düə haa'a.
Choncho Mose anasiyana ndi Farao nakapemphera kwa Yehova.
31 Rəbbee Mısee Cuke heqqiyn ha'an. Firon vucur, cun insanarıb, cun milletıd goganeeşike g'attivxhan haa'anbı. Ma'ab sacab goganiy aaxva deş.
Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha: Ntchentche zoluma zinachoka kwa Farao ndi nduna zake ndiponso kwa anthu ake. Palibe ngakhale imodzi yomwe inatsala.
32 Firon meer hı't'ilqa siyk'al, mang'vee millet g'ekka deş.
Koma nthawi imeneyinso Farao anawumitsa mtima wake ndipo sanalole kuti anthu atuluke.