< Qığeepç'iy 1 >

1 İzrailyne (Yaaq'ubne) xizanbışika sacigee cuka Misirqa qabıyne dixbışin dobı inbı vod:
Awa ndi mayina a ana a Israeli amene anapita ku Igupto pamodzi ndi Yakobo abambo awo, aliyense ndi banja lake:
2 Ruven, Şimon, Levi, Yahud,
Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda;
3 İssaxar, Zevulun, Benyamin,
Isakara, Zebuloni, Benjamini;
4 Dan, Naftali, Qad, Aşer.
Dani, Nafutali; Gadi ndi Aseri.
5 Yaaq'ubıke g'arına yights'al insan ıxha. Yusuf manke Misirniy vor.
Anthu onse obadwa mwa Yakobo analipo 70. Yosefe nʼkuti ali kale ku Igupto.
6 Ooğançe geed gahbı ılğeeç'umee, Yusufur cun çocarıb coka vooxhen cone gahın insanarıb habat'anbı.
Tsono Yosefe ndi abale ake onse ndiponso mʼbado wawo wonse anamwalira.
7 İzrailybımee geeb barakatnanbı vuxha, g'abı hexxebaxhenbı. Manbı geeb qeepxha bıkırna ölka gyavts'aa'ana.
Koma Aisraeli anaberekana ndi kuchuluka kwambiri nakhala amphamvu kwambiri, kotero kuti anadzaza dzikolo.
8 Xılece gahbı ılğeeç'umee, Misirıs xəbvalla Yusuf dyats'ane sa paççahee haa'a.
Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
9 Mang'vee cune xalq'ık'le eyhen: – İlyaakende, İzrailybı şale geeb qepxha, şaleb gucuka vob.
Iyo inati kwa anthu ake, “Taonani, Aisraeli achuluka ndipo ndi amphamvu kwambiri kuposa ife.
10 Qudoora ək'elikan sa kar ha'as, deşxheene manbı sık'ılbab geeb qeepxhes. Dəv'ə gibğılee, manbı yişde duşmanaaşika sapçi şalqa ables. Qiyğale xhineyib yişde ölkeençe qığeepç'ı əlyhəəsınbı.
Tiyeni tiwachenjerere. Tikapanda kutero adzachuluka kuposa ife, ndipo ngati kutakhala nkhondo, adzadziphatika kwa adani athu nadzamenyana nafe, kenaka nʼkudzachoka mʼdziko muno.”
11 Misirbışe İzrailybışda ı'mı'r dağam qa'asva manbışike nukarar hav'u, manbışil ooqa con insanar giviyxhe. Mane cone insanaaşeb manbışis yı'q' haqvara'asda xhinnena iş hoole. Məxüd ıxha İzrailybışe fironus Pitomiy Ramses donan şaharbı ali'ı. Mane şaharbışee manbışin anbarbı eyxhe.
Kotero anayika akapitawo kuti aziwazunza ndi kuwagwiritsa ntchito yolemetsa mokakamiza. Iwo anamangira Farao mizinda ya Pitomu ndi Ramesesi kumene ankasungirako chakudya.
12 İzrailybı nimee hopç'un-g'opç'uneyib manbı sa hamanimegab geeb qeebaxhe vuxha. Mançile Misirbı qəpq'ı'n İzrailybı
Koma pamene ankawazunza kwambiri, Aisraeli ndiye ankachulukirachulukira mpaka kubalalikira mʼdziko lonse. Kotero Aigupto anayamba kuopa Aisraeliwo
13 qidviykkın işlemişepxhes ulyooka.
ndipo anawagwiritsa ntchito mwankhanza kwambiri.
14 Misirbışe İzrailybışisqa nyaq'uke karpıçbı ha'as, cigabı alya'as, çoleedın yı'q'ı'n işbı g'acesniy ulyookanbı. Məxüb manbışe İzrailbışda ı'mı'r dağam qav'u. İzrailybı qidvikkın gırgın yı'q'ı'n işbı manbışisqa ha'as ilekka ıxha.
Aigupto anachititsa moyo wa Aisraeli kukhala owawa kwambiri powagwiritsa ntchito yakalavulagaga yowumba njerwa ndi kuponda dothi lomangira, pamodzi ndi ntchito zina zosiyanasiyana zamʼminda. Iwo anakakamiza Aisraeli mwankhanza kuti agwire ntchito yowawayi.
15 Misirne paççahee cühüt'yaaşis ebaçer (uşax uxoxang'a kumag ha'ane) Şifrayiy Pua donane yadaaşik'le eyhen:
Mfumu ya Igupto inati kwa azamba a Chihebri omwe mayina awo anali Sifira ndi Puwa,
16 – Cühüt'yaaşine xhunaşşeeşis uşaxar vooxheng'a yugba ilyaake, gade ixheene gik'e, içiy yixheene g'alerçe.
“Mukamathandiza amayi a Chihebri pa mwala wochirira, muzionetsetsa kuti akabadwa mwana wamwamuna muzipha, koma akakhala wamkazi muzimuleka akhale ndi moyo.”
17 Ebaçer Allahıle qəvəyq'ənanbı vooxhee, manbışe paççahe uvhuyn ha'a deş. Manbışe gadebı üç'übba g'alyaa'a vuxha.
Koma azambawo ankaopa Mulungu ndipo sanachite zimene mfumu ya Igupto inawawuza kuti achite. Iwo analeka ana aamuna kuti akhale ndi moyo.
18 Paççahee ebaçer cusqa qopt'ul qiyghanan: – Nya'a şu məxüd ha'a? Nya'a gadebı üç'übba g'alyaa'a?
Kenaka mfumu ya Igupto inayitanitsa azamba aja ndi kuwafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwachita zimenezi? Bwanji mwasiya ana aamuna kuti akhale ndi moyo?”
19 Ebaçerşe eyhen: – Cühüt'yaaşin yedar misirbışin yedar xhinne deşub, manbı taq'atıkavub, şi hivxharassecad uxoxa vod.
Azambawo anamuyankha Farao kuti, “Amayi a Chihebri sali ngati amayi a Chiigupto; Iwo ndi amphamvu ndipo amachira azamba asanafike.”
20 Mançil-allar Allah ebaçeeşiqa yugra eyxhe. Məxüd milletıd geed qexhe, çina gucub hexxooxhena.
Kotero Mulungu anawakomera mtima azambawo, ndipo Aisraeli anapitirirabe kuchulukana nakhala amphamvu kwambiri.
21 Ebaçer Allahıle qəvəyq'ənva, Allahee manbı xizanınbı, uşaxınbı haa'a.
Pakuti azambawo ankaopa Mulungu, Iye anawapatsa mabanja awoawo.
22 Fironee cune milletılqa əmr haa'a: – Cühüt'yaaşis vuxuyn gırgın gadebı Nil eyhene dameeqa dağee'e! Vuxhayne içeeşikme simoot'a, üç'übba g'alee'e.
Pamenepo Farao analamulira anthu ake onse kuti, “Mwana wamwamuna aliyense akabadwa, mukamuponye mu mtsinje wa Nailo, koma wamkazi mulekeni akhale ndi moyo.”

< Qığeepç'iy 1 >