< Psaltaren 96 >

1 Sjungen till HERRENS ära en ny sång, sjungen till HERRENS ära, alla länder.
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
2 Sjungen till HERRENS ära, loven hans namn. Båden glädje var dag, förkunnen hans frälsning.
Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
3 Förtäljen bland hedningarna hans ära, bland alla folk hans under.
Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
4 Ty stor är HERREN och högt lovad, fruktansvärd är han mer än alla gudar.
Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
5 Ty folkens alla gudar äro avgudar, men HERREN är den som har gjort himmelen.
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
6 Majestät och härlighet äro inför hans ansikte, makt och glans i hans helgedom.
Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
7 Given åt HERREN, I folkens släkter, given åt HERREN ära och makt;
Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
8 given åt HERREN hans namns ära, bären fram skänker, och kommen i hans gårdar.
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
9 Tillbedjen HERREN i helig skrud, bäven för hans ansikte, alla länder.
Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
10 Sägen bland hedningarna: "HERREN är nu konung! Därför står jordkretsen fast och vacklar icke; han dömer folken med rättvisa."
Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
11 Himmelen vare glad, och jorden fröjde sig; havet bruse och allt vad däri är.
Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
12 Marken glädje sig och allt som är därpå, ja, då juble alla skogens träd.
minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
13 inför HERREN, ty han kommer, ty han kommer för att döma jorden. Han skall döma jordens krets med rättfärdighet och folken med sin trofasthet.
idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.

< Psaltaren 96 >