< Psaltaren 67 >

1 För sångmästaren, med strängaspel; en psalm, en sång. Gud vare oss nådig och välsigne oss, han låte sitt ansikte lysa och ledsaga oss, (Sela)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
2 för att man på jorden må känna din väg, bland alla hedningar din frälsning.
Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
3 Folken tacke dig, o Gud, alla folk tacke dig.
Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
4 Folkslagen glädje sig och juble, ty du dömer folken rätt, och du leder folkslagen på jorden. (Sela)
Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
5 Folken tacke dig, o Gud, alla folk tacke dig.
Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
6 Jorden har givit sin gröda. Gud, vår Gud, välsigne oss.
Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
7 Gud välsigne oss, och alla jordens ändar frukte honom.
Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.

< Psaltaren 67 >