< 4 Mosebok 7 >

1 Då nu Mose hade satt upp tabernaklet och smort och helgat det, med alla dess tillbehör, och hade satt upp altaret med alla dess tillbehör, och smort och helgat detta,
Mose atamaliza kuyimika chihema chija, anachidzoza mafuta ndi kuchipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso guwa lansembe ndi kulipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse.
2 framburos offergåvor av Israels hövdingar, huvudmännen för stamfamiljerna, det är stamhövdingarna, som stodo i spetsen för de inmönstrade.
Kenaka atsogoleri a Aisraeli, akuluakulu a mabanja omwe ankayangʼanira mafuko a anthu omwe anawawerenga aja, anachita chopereka.
3 De förde fram såsom sin offergåva inför HERRENS ansikte sex övertäckta vagnar och tolv oxar: två hövdingar tillhopa en vagn och var hövding en oxe; dessa förde de fram inför tabernaklet.
Anabweretsa zopereka zawo pamaso pa Yehova: ngolo zophimbidwa zisanu ndi imodzi ndiponso ngʼombe zothena khumi ndi ziwiri. Mtsogoleri mmodzi ngʼombe yothena imodzi ndipo atsogoleri awiri ngolo imodzi. Izi anazipereka ku chihema.
4 Och HERREN sade till Mose:
Yehova anawuza Mose kuti,
5 "Tag emot detta av dem för att bruka det till uppenbarelsetältets tjänst; och lämna det åt leviterna, alltefter beskaffenheten av vars och ens tjänst."
“Ulandire zimenezi kwa iwo kuti zigwire ntchito ku tenti ya msonkhano. Uzipereke kwa Alevi, aliyense monga mwa ntchito yake.”
6 Och Mose tog emot vagnarna och oxarna och gav dem åt leviterna.
Choncho Mose anatenga ngolo ndi ngʼombe zothenazo nazipereka kwa Alevi.
7 Två vagnar och fyra oxar gav han åt Gersons barn, efter beskaffenheten av deras tjänst;
Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe zothena zinayi kwa Ageresoni monga mwantchito yawo
8 fyra vagnar och åtta oxar gav han åt Meraris barn, efter beskaffenheten av den tjänst de förrättade under ledning av Itamar, prästen Arons son;
ndiponso anapereka ngolo zinayi ndi ngʼombe zothena zisanu ndi zitatu kwa Amerari molingananso ndi ntchito yawo. Onsewa ankawayangʼanira anali Itamara mwana wa Aaroni wansembe.
9 men åt Kehats barn gav han icke något, ty dem ålåg att hava hand om de heliga föremålen, och dessa skulle bäras på axlarna.
Koma Mose sanapereke zimenezi kwa Akohati chifukwa zinthu zawo zopatulika zomwe ankayangʼanira zinali zoti azinyamula pa mapewa awo.
10 Och hövdingarna förde fram skänker till altarets invigning, när det smordes; hövdingarna förde fram dessa sina offergåvor inför altaret.
Guwa la nsembe litadzozedwa, atsogoleri anabweretsa zopereka zawo zopatulira guwa nazipereka paguwapo.
11 Och HERREN sade till Mose: "Låt hövdingarna, en i sänder, var och en på sin dag, föra fram sina offergåvor till altarets invigning."
Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, “Tsiku lililonse mtsogoleri mmodzi azibweretsa chopereka chake chopatulira guwa lansembe.”
12 Och den som på första dagen förde fram sin offergåva var Naheson, Amminadabs son, av Juda stam
Amene anabweretsa chopereka chake tsiku loyamba anali Naasoni mwana wa Aminadabu wa fuko la Yuda.
13 Hans offergåva var ett silverfat, ett hundra trettio siklar i vikt, och en silverskål om sjuttio siklar, efter helgedomssikelns vikt, båda fulla med fint mjöl, begjutet med olja, till spisoffer,
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, ndi beseni lasiliva limodzi lowazira, lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo wopatulika ndipo zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ngati chopereka chachakudya;
14 vidare en skål av guld om tio siklar, full med rökelse,
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
15 vidare en ungtjur, en vädur och ett årsgammalt lamm till brännoffer
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
16 och en bock till syndoffer,
mbuzi yayimuna imodzi, nsembe ya machimo;
17 samt till tackoffret två tjurar, fem vädurar, fem bockar och fem årsgamla lamm. Detta var Nahesons, Amminadabs sons, offergåva.
ndi ngʼombe zothena ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Naasoni mwana wa Aminadabu.
18 På andra dagen förde Netanel, Suars son, hövdingen för Isaskar, fram sin gåva;
Pa tsiku lachiwiri, Natanieli mwana wa Zuwara, mtsogoleri wa Isakara, anabweretsa chopereka chake.
19 han framförde såsom sin offergåva ett silverfat, ett hundra trettio siklar i vikt, och en silverskål om sjuttio siklar, efter helgedomssikelns vikt, båda fulla med fint mjöl, begjutet med olja, till spisoffer,
Chopereka chomwe anabwera nacho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, molingana ndi muyeso wa ku malo opatulika. Mbale zonse zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha chakudya.
20 vidare en skål av guld om tio siklar, full med rökelse,
Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110 yodzaza ndi lubani;
21 vidare en ungtjur, en vädur och ett årsgammalt lamm till brännoffer
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza:
22 och en bock till syndoffer,
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yotetezera machimo;
23 samt till tackoffret två tjurar, fem vädurar, fem bockar och fem årsgamla lamm. Detta var Netanels, Suars sons, offergåva.
ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi, nsembe ya chiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Netanieli mwana wa Zuwara.
24 På tredje dagen kom hövdingen för Sebulons barn, Eliab, Helons son;
Pa tsiku lachitatu, Eliabu mwana wa Heloni, mtsogoleri wa Azebuloni, anabweretsa chopereka chake.
25 hans offergåva var ett silverfat, ett hundra trettio siklar i vikt, och en silverskål om sjuttio siklar, efter helgedomssikelns vikt, båda fulla med fint mjöl, begjutet med olja, till spisoffer
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, mbale zonse zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka cha chakudya;
26 vidare en skål av guld om tio siklar, full med rökelse,
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
27 vidare en ungtjur, en vädur och ett årsgammalt lamm till brännoffer
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
28 och en bock till syndoffer,
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
29 samt till tackoffret två tjurar, fem vädurar, fem bockar och fem årsgamla lamm. Detta var Eliabs, Helons sons, offergåva.
ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliabu mwana wa Heloni.
30 På fjärde dagen kom hövdingen för Rubens barn, Elisur, Sedeurs son;
Tsiku lachinayi linali la Elizuri mwana wa Sedeuri, mtsogoleri wa fuko la Rubeni, anabweretsa chopereka chake.
31 hans offergåva var ett silverfat, ett hundra trettio siklar i vikt, och en silverskål om sjuttio siklar, efter helgedomssikelns vikt, båda fulla med fint mjöl, begjutet med olja, till spisoffer,
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka chachakudya.
32 vidare en skål av guld om tio siklar, full med rökelse,
Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
33 vidare en ungtjur, en vädur och ett årsgammalt lamm till brännoffer
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
34 och en bock till syndoffer,
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
35 samt till tackoffret två tjurar, fem vädurar, fem bockar och fem årsgamla lamm. Detta var Elisurs, Sedeurs sons, offergåva.
ndi ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elizuri mwana wa Sedeuri.
36 På femte dagen kom hövdingen för Simeons barn, Selumiel, Surisaddais son;
Pa tsiku lachisanu Selumieli mwana wa Zurisadai, mtsogoleri wa fuko la Simeoni, anabweretsa chopereka chake.
37 hans offergåva var ett silverfat, ett hundra trettio siklar i vikt, och en silverskål om sjuttio siklar, efter helgedomssikelns vikt, båda fulla med fint mjöl, begjutet med olja, till spisoffer,
Chopereka chake chinali mbale yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
38 vidare en skål av guld om tio siklar, full med rökelse,
mbale yagolide imodzi yolemera 110, yodzaza ndi lubani;
39 vidare en ungtjur, en vädur och ett årsgammalt lamm till brännoffer
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wamwamuna wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
40 och en bock till syndoffer,
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
41 samt till tackoffret två tjurar, fem vädurar, fem bockar och fem årsgamla lamm. Detta var Selumiels, Surisaddais sons, offergåva.
ngʼombe ziwiri, nkhosa zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Selumieli mwana wa Zurisadai.
42 På sjätte dagen kom hövdingen för Gads barn, Eljasaf, Deguels son;
Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, Eliyasafu mwana wa Deuweli, mtsogoleri wa fuko la Gadi, anabweretsa chopereka chake.
43 hans offergåva var ett silverfat, ett hundra trettio siklar i vikt, och en silverskål om sjuttio siklar, efter helgedomssikelns vikt, båda fulla med fint mjöl, begjutet med olja, till spisoffer,
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
44 vidare en skål av guld om tio siklar, full med rökelse,
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
45 vidare en ungtjur, en vädur och ett årsgammalt lamm till brännoffer
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, chopereka cha nsembe yopsereza:
46 och en bock till syndoffer,
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
47 samt till tackoffret två tjurar, fem vädurar, fem bockar och fem årsgamla lamm. Detta var Eljasafs, Deguels sons, offergåva.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliyasafu mwana wa Deuweli.
48 På sjunde dagen kom hövdingen för Efraims barn, Elisama, Ammihuds son;
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Elisama mwana wa Amihudi, mtsogoleri wa fuko la Efereimu, anabweretsa chopereka chake.
49 hans offergåva var ett silverfat, ett hundra trettio siklar i vikt, och en silverskål om sjuttio siklar, efter helgedomssikelns vikt, båda fulla med fint mjöl, begjutet med olja, till spisoffer,
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonsezi monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
50 vidare en skål av guld om tio siklar, full med rökelse,
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
51 vidare en ungtjur, en vädur och ett årsgammalt lamm till brännoffer
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
52 och en bock till syndoffer,
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
53 samt till tackoffret två tjurar, fem vädurar, fem bockar och fem årsgamla lamm. Detta var Elisamas, Ammihuds sons, offergåva.
ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elisama mwana wa Amihudi.
54 På åttonde dagen kom hövdingen för Manasse barn, Gamliel, Pedasurs son;
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Gamalieli mwana wa Pedazuri, mtsogoleri wa fuko Manase, anabweretsa chopereka chake.
55 hans offergåva var ett silverfat, ett hundra trettio siklar i vikt, och en silverskål om sjuttio siklar, efter helgedomssikelns vikt, båda fulla med fint mjöl, begjutet med olja, till spisoffer,
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
56 vidare en skål av guld om tio siklar, full med rökelse,
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani,
57 vidare en ungtjur en vädur och ett årsgammalt lamm till brännoffer
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
58 och en bock till syndoffer,
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
59 samt till tackoffret två tjurar, fem vädurar, fem bockar och fem årsgamla lamm. Detta var Gamliels Pedasurs sons, offergåva.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Gamalieli mwana wa Pedazuri.
60 På nionde dagen kom hövdingen för Benjamins barn, Abidan, Gideonis son;
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi Abidani mwana wa Gideoni mtsogoleri wa fuko la Benjamini, anabweretsa chopereka chake.
61 hans offergåva var ett silverfat, ett hundra trettio siklar i vikt, och en silverskål om sjuttio siklar, efter helgedomssikelns vikt, båda fulla med fint mjöl, begjutet med olja, till spisoffer,
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha zakudya;
62 vidare en skål av guld om tio siklar, full med rökelse,
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
63 vidare en ungtjur, en vädur och ett årsgammalt lamm till brännoffer
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
64 och en bock till syndoffer,
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
65 samt till tackoffret två tjurar, fem vädurar, fem bockar och fem årsgamla lamm. Detta var Abidans, Gideonis sons, offergåva.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Abidani mwana wa Gideoni.
66 På tionde dagen kom hövdingen för Dans barn, Ahieser, Ammisaddais son;
Pa tsiku lakhumi Ahiyezeri mwana wa Amisadai, mtsogoleri wa fuko la Dani anabweretsa chopereka chake.
67 hans offergåva var ett silverfat, ett hundra trettio siklar i vikt, och en silverskål om sjuttio siklar, efter helgedomssikelns vikt, båda fulla med fint mjöl, begjutet med olja, till spisoffer,
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
68 vidare en skål av guld om tio siklar, full med rökelse,
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
69 vidare en ungtjur, en vädur och ett årsgammalt lamm till brännoffer
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
70 och en bock till syndoffer,
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
71 samt till tackoffret två tjurar, fem vädurar, fem bockar och fem årsgamla lamm. Detta var Ahiesers, Ammisaddais sons, offergåva.
ndi ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
72 På elfte dagen kom hövdingen för Asers barn, Pagiel, Okrans son;
Pa tsiku la khumi ndi chimodzi, Pagieli mwana wa Okirani, mtsogoleri wa fuko la Aseri, anabweretsa chopereka chake.
73 hans offergåva var ett silverfat, ett hundra trettio siklar i vikt, och en silverskål om sjuttio siklar, efter helgedomssikelns vikt, båda fulla med fint mjöl, begjutet med olja, till spisoffer,
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
74 vidare en skål av guld om tio siklar, full med rökelse,
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
75 vidare en ungtjur, en vädur och ett årsgammalt lamm till brännoffer
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
76 och en bock till syndoffer,
mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo;
77 samt till tackoffret två tjurar, fem vädurar, fem bockar och fem årsgamla lamm. Detta var Pagiels, Okrans sons, offergåva.
ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Pagieli mwana wa Okirani.
78 På tolfte dagen kom hövdingen för Naftali barn, Ahira, Enans son;
Pa tsiku la khumi ndi chimodzi Ahira mwana wa Enani, mtsogoleri wa fuko la Nafutali, anabweretsa chopereka chake.
79 hans offergåva var ett silverfat, ett hundra trettio siklar i vikt, och en silverskål om sjuttio siklar, efter helgedomssikelns vikt, båda fulla med fint mjöl, begjutet med olja, till spisoffer,
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
80 vidare en skål av guld om tio siklar, full med rökelse,
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
81 vidare en ungtjur, en vädur och ett årsgammalt lamm till brännoffer
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
82 och en bock till syndoffer,
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
83 samt till tackoffret två tjurar, fem vädurar, fem bockar och fem årsgamla lamm. Detta var Ahiras, Enans sons, offergåva.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahira mwana wa Enani.
84 Detta var vad Israels hövdingar skänkte till altarets invigning, när det smordes: tolv silverfat, tolv silverskålar och tolv guldskålar.
Zopereka za atsogoleri a Israeli zopatulira guwa lansembe pamene linadzozedwa zinali izi: mbale khumi ndi ziwiri zasiliva, mabeseni owazira asiliva khumi ndi awiri ndi mbale zagolide khumi ndi ziwiri.
85 Vart fat kom på ett hundra trettio silversiklar och var skål på sjuttio siklar, så att silvret i dessa kärl sammanlagt utgjorde två tusen fyra hundra siklar, efter helgedomssikelns vikt.
Mbale iliyonse yasiliva inkalemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndipo beseni lililonse lowazira linkalemera magalamu 800. Pamodzi, mbale zonse zasiliva zinkalemera makilogalamu 27 monga mwa muyeso wa ku malo opatulika.
86 Av de tolv guldskålarna, som voro fulla med rökelse, vägde var och en tio siklar, efter helgedomssikelns vikt, så att guldet i skålarna sammanlagt utgjorde ett hundra tjugu siklar.
Mbale khumi ndi ziwiri zagolide zodzaza ndi lubanizo zinkalemera magalamu 110 iliyonse, monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Pamodzi, mbale zagolide zinkalemera kilogalamu imodzi ndi theka.
87 Brännoffers-fäkreaturen utgjorde tillsammans tolv tjurar, vartill kommo tolv vädurar, tolv årsgamla lamm, med tillhörande spisoffer, och tolv bockar till syndoffer.
Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yopsereza chinali motere: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, nkhosa zazimuna khumi ndi ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi awiri a chaka chimodzi pamodzi ndi chopereka chachakudya. Mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri zinali za nsembe yopepesera machimo.
88 Och tackoffers-fäkreaturen utgjorde tillsammans tjugufyra tjurar, vartill kommo sextio vädurar, sextio bockar och sextio årsgamla lamm. Detta var vad som skänktes till altarets invigning, sedan det hade blivit smort.
Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yachiyanjano chinali motere: ngʼombe zothena 24, nkhosa zazimuna 60, mbuzi zazimuna 60 ndi ana ankhosa aamuna a chaka chimodzi 60. Zimenezi ndi zimene zinali zopereka zopatulira guwa lansembe litadzozedwa.
89 Och när Mose gick in i uppenbarelsetältet för att tala med honom, hörde han rösten tala till sig från nådastolen ovanpå vittnesbördets ark, från platsen mellan de två keruberna; där talade rösten till honom.
Mose atalowa mu tenti ya msonkhano kukayankhula ndi Yehova, anamva mawu kuchokera pakati pa Akerubi awiri amene anali pamwamba pa chivundikiro cha bokosi la umboni. Ndipo anayankhula naye.

< 4 Mosebok 7 >