< 4 Mosebok 29 >

1 Och i sjunde månaden, på första dagen i månaden, skolen I hålla en helig sammankomst; ingen arbetssyssla skolen I då göra. En basunklangens dag skall den vara för eder.
“‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
2 Såsom brännoffer till en välbehaglig lukt för HERREN skolen I då offra en ungtjur, en vädur, sju årsgamla felfria lamm,
Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
3 och såsom spisoffer därtill fint mjöl, begjutet med olja: tre tiondedels efa till tjuren, två tiondedels efa till väduren
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
4 och en tiondedels efa till vart och ett av de sju lammen;
Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
5 tillika skolen I offra en bock såsom syndoffer, till att bringa försoning för eder --
Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
6 detta förutom nymånadsbrännoffret med tillhörande spisoffer, och förutom det dagliga brännoffret med tillhörande spisoffer, och förutom de drickoffer som på föreskrivet sätt skola offras till båda: allt till en välbehaglig lukt, ett eldsoffer åt HERREN.
Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
7 På tionde dagen i samma sjunde månad skolen I ock hålla en helig sammankomst, och I skolen då späka eder; intet arbete skolen I då göra.
“‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
8 Och såsom brännoffer till en välbehaglig lukt för HERREN skolen I då offra en ungtjur, en vädur, sju årsgamla lamm -- felfria skola de vara --
Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
9 och såsom spisoffer därtill fint mjöl, begjutet med olja: tre tiondedels efa till tjuren, två tiondedels efa till väduren,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
10 en tiondedels efa till vart och ett av de sju lammen;
kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
11 tillika skolen I offra en bock såsom syndoffer -- detta förutom försoningssyndoffret och det dagliga brännoffret med tillhörande spisoffer, och förutom de drickoffer som höra till båda.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
12 På femtonde dagen i sjunde månaden skolen I ock hålla en helig sammankomst; ingen arbetssyssla skolen I då göra. Då skolen I fira en HERRENS högtid, i sju dagar.
“‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
13 Och såsom brännoffer, såsom eldsoffer, skolen I då offra till en välbehaglig lukt för HERREN tretton ungtjurar, två vädurar, fjorton årsgamla lamm -- felfria skola de vara --
Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
14 och såsom spisoffer därtill fint mjöl, begjutet med olja: tre tiondedels efa till var och en av de tretton tjurarna, två tiondedels efa till var och en av de två vädurarna,
Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
15 en tiondedels efa till vart och ett av de fjorton lammen;
Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
16 tillika skolen I offra en bock såsom syndoffer -- detta förutom det dagliga brännoffret med tillhörande spisoffer och drickoffer.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
17 Och på den andra dagen: tolv ungtjurar, två vädurar, fjorton årsgamla felfria lamm,
“‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
18 med det spisoffer och de drickoffer som skola offras till dem, till tjurarna, vädurarna och lammen, efter deras antal, på föreskrivet sätt,
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
19 tillika också en bock såsom syndoffer -- detta förutom det dagliga brännoffret med tillhörande spisoffer och det drickoffer som hör till dem.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
20 Och på den tredje dagen: elva tjurar, två vädurar, fjorton årsgamla felfria lamm,
“‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
21 med det spisoffer och de drickoffer som skola offras till dem, till tjurarna, vädurarna och lammen, efter deras antal, på föreskrivet sätt,
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
22 tillika också en syndoffersbock -- detta förutom det dagliga brännoffret med tillhörande spisoffer och drickoffer.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
23 Och på den fjärde dagen; tio tjurar, två vädurar, fjorton årsgamla felfria lamm,
“‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
24 med det spisoffer och de drickoffer som skola offras till dem, till tjurarna, vädurarna och lammen, efter deras antal, på föreskrivet satt,
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
25 tillika också en bock såsom syndoffer -- detta förutom det dagliga brännoffret med tillhörande spisoffer och drickoffer.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
26 Och på den femte dagen: nio tjurar, två vädurar, fjorton årsgamla felfria lamm,
“‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
27 med det spisoffer och de drickoffer som skola offras till dem, till tjurarna, vädurarna och lammen, efter deras antal, på föreskrivet sätt,
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
28 tillika också en syndoffersbock -- detta förutom det dagliga brännoffret med tillhörande spisoffer och drickoffer.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
29 Och på den sjätte dagen: åtta tjurar, två vädurar, fjorton årsgamla felfria lamm,
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
30 med det spisoffer och de drickoffer som skola offras till dem, till tjurarna, vädurarna och lammen, efter deras antal, på föreskrivet sätt,
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
31 tillika också en syndoffersbock -- detta förutom det dagliga brännoffret med tillhörande spisoffer och drickoffer.
Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
32 Och på den sjunde dagen: sju tjurar, två vädurar, fjorton årsgamla felfria lamm,
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
33 med det spisoffer och de drickoffer som skola offras till dem, till tjurarna, vädurarna och lammen, efter deras antal, på föreskrivet sätt,
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
34 tillika också en syndoffersbock -- detta förutom det dagliga brännoffret med tillhörande spisoffer och drickoffer.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
35 På den åttonde dagen skolen I hålla en högtidsförsamling; ingen arbetssyssla skolen I då göra.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
36 Och såsom brännoffer, såsom eldsoffer, skolen I då offra till en välbehaglig lukt för HERREN en tjur, en vädur, sju årsgamla felfria lamm,
Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
37 med det spisoffer och de drickoffer som skola offras till dem, till tjuren, väduren och lammen, efter deras antal, på föreskrivet sätt,
Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
38 tillika också en syndoffersbock -- detta förutom det dagliga brännoffret med tillhörande spisoffer och drickoffer.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
39 Dessa offer skolen I offra åt HERREN vid edra högtider, förutom edra löftesoffer och frivilliga offer, dessa må nu vara brännoffer eller spisoffer eller drickoffer eller tackoffer.
“‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
40 Och Mose sade detta till Israels barn, alldeles såsom HERREN hade bjudit honom.
Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.

< 4 Mosebok 29 >