< Jesaja 66 >
1 Så säger HERREN: Himmelen är min tron, och jorden är min fotapall; vad för ett hus skullen I då kunna bygga åt mig, och vad för en plats skulle tjäna mig till vilostad?
Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
2 Min hand har ju gjort allt detta, och så har allt detta blivit till, säger HERREN. Men till den skådar jag ned, som är betryckt och har en förkrossad ande, och till den som fruktar för mitt ord.
Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
3 Den däremot, som slaktar sin offertjur, men ock är en mandråpare, den som offrar sitt lamm, men tillika krossar nacken på en hund, den som frambär ett spisoffer, men därvid frambär svinblod, den som offrar rökelse, men därunder hyllar en fåfänglig avgud -- likasom det lyster dessa att gå sina egna vägar och likasom deras själ har behag till deras styggelser,
Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
4 så lyster det ock mig att fara illa fram med dem och att låta förskräckelse komma över dem, eftersom ingen svarade, när jag kallade, och eftersom de icke hörde, när jag talade, utan gjorde, vad ont var i mina ögon, och hade sin lust i att göra, vad mig misshagligt var.
Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
5 Hören HERRENS ord, I som frukten för hans ord. Edra bröder, som hata eder och stöta eder bort för mitt namns skull, de säga: "Må HERREN förhärliga sig, så att vi få se eder glädje." Men de skola komma på skam.
Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
6 Hör, huru det larmar i staden, hör dånet i templet! Hör dånet, när HERREN vedergäller sina fiender, vad de hava gjort!
Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
7 Innan Sion har känt någon födslovånda, föder hon barnet; innan kval har kommit över henne, bliver hon förlöst med ett gossebarn.
“Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
8 Vem har hört något sådant, vem har sett något dylikt? Kan då ett land komma till liv på en enda dag, eller kan ett folk födas i ett ögonblick, eftersom Sion födde fram sina barn, just då våndan begynte?
Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
9 Ja, ty skulle jag väl låta fostret bliva fullgånget, men icke giva kraft att föda fram det? säger HERREN. Eller skulle jag giva kraft att föda, men sedan hålla fostret tillbaka? säger din Gud.
Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
10 Glädjens med Jerusalem och fröjden eder över henne, alla I som haven henne kär; jublen högt med henne, alla I som haven sörjt över henne.
“Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
11 Så skolen I få dia eder mätta vid hennes hugsvalelses bröst; så skolen I få suga med lust av hennes rika barm.
Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
12 Ty så säger HERREN: Se, jag vill låta frid komma över henne såsom en ström och folkens rikedomar såsom en översvämmande flod, och I skolen så få dia, I skolen bliva burna på armen och skolen få sitta i knäet och bliva smekta.
Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
13 Såsom en moder tröstar sin son, så skall jag trösta eder; ja, i Jerusalem skolen I få tröst.
Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
14 Och edra hjärtan skola glädja sig, när I fån se detta, och benen i edra kroppar skola hava livskraft såsom spirande gräs; och man skall förnimma, att HERRENS hand är med hans tjänare och att ogunst kommer över hans fiender.
Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
15 Ty se, HERREN skall komma i eld, och hans vagnar skola vara såsom en stormvind; och han skall låta sin vrede drabba med hetta och sin näpst med eldslågor.
Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
16 Ty HERREN skall hålla dom med eld, och med sitt svärd skall han slå allt kött, och många skola de vara, som bliva slagna av HERREN.
Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
17 De som låta inviga sig och rena sig till gudstjänst i lustgårdar, anförda av en som står där i mitten, de som äta svinkött och annan styggelse, ja, också möss, de skola allasammans förgås, säger HERREN.
Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
18 Jag känner deras gärningar och tankar. Den tid kommer, då jag skall församla alla folk och tungomål; och de skola komma och se min härlighet.
“Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
19 Och jag skall göra ett tecken bland dem; och några av dem som bliva räddade skall jag sända såsom budbärare till hednafolken, till Tarsis, till Pul och Lud, bågskyttfolken, till Tubal och Javan, till havsländerna i fjärran, som icke hava hört något om mig eller sett min härlighet; och de skola förkunna min härlighet bland folken.
“Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
20 Och på hästar och i vagnar och bärstolar och på mulåsnor och dromedarer skola de från alla folk föra alla edra bröder fram till mitt heliga berg i Jerusalem såsom ett spisoffer åt HERREN, säger HERREN, likasom Israels barn i rena kärl föra fram spisoffer till HERRENS hus.
Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
21 Och jämväl sådana skall jag taga till mina präster, till mina leviter, säger HERREN.
Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
22 Ty likasom de nya himlar och den nya jord, som jag vill göra, bliva beståndande inför mig, säger HERREN, så skall det ock vara med edra barn och med edert namn.
“Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
23 Och nymånadsdag efter nymånadsdag och sabbatsdag efter sabbatsdag skall det ske, att allt kött kommer och tillbeder inför mig, säger HERREN.
“Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
24 Och man skall gå ut och se med lust, huru de människor, som avföllo från mig, nu ligga där döda; ty deras mask skall icke dö, och deras eld skall icke utsläckas, och de skola vara till vämjelse för allt kött.
“Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”