< Jesaja 36 >
1 Och i konung Hiskias fjortonde regeringsår hände sig, att Sanherib, konungen i Assyrien, drog upp och angrep alla befästa städer i Juda och intog dem.
Chaka cha khumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya ku Yuda, nayilanda.
2 Och konungen i Assyrien sände från Lakis åstad Rab-Sake med en stor här till Jerusalem mot konung Hiskia; och han stannade vid Övre dammens vattenledning, på vägen till Valkarfältet.
Kenaka mfumu ya ku Asiriya inatuma kazembe wake wankhondo pamodzi ndi gulu lalikulu lankhondo kuchokera ku Lakisi kupita kwa mfumu Hezekiya ku Yerusalemu. Tsono kazembeyo anayima pafupi ndi ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe lakumtunda pa msewu wopita ku malo a munda wa mmisiri wochapa zovala.
3 Då gingo överhovmästaren Eljakim, Hilkias son, och sekreteraren Sebna och kansleren Joa, Asafs son, ut till honom.
Panali anthu atatu. Woyamba anali Eliyakimu mwana wa Hilikiya komanso ndiye woyangʼanira nyumba ya mfumu. Wachiwiri anali Sebina amene anali mlembi wa bwalo; ndipo wachitatu anali Yowa mwana wa Asafu komanso anali wolemba zochitika. Anthu awa anatuluka kukakumana ndi kazembe wa ankhondo uja.
4 Och Rab-Sake sade till dem: "Sägen till Hiskia: Så säger den store konungen, konungen i Assyrien: Vad är det för en förtröstan, som du nu har hängivit dig åt?
Kazembe wa ankhondo anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti, “Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?
5 Jag säger: Det är allenast munväder, att du vet råd och har makt att föra kriget. På vem förtröstar du då, eftersom du har satt dig upp mot mig?
Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine?
6 Du förtröstar väl på den bräckta rörstaven Egypten, men se, när någon stöder sig på den, går den i i hans hand och genomborrar den. Ty sådan är Farao, konungen i Egypten, för alla som förtrösta på honom.
Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.
7 Eller säger du kanhända till mig: 'Vi förtrösta på HERREN, vår Gud?' Var det då icke hans offerhöjder och altaren Hiskia avskaffade, när han sade till Juda och Jerusalem: 'Inför detta altare skolen I tillbedja'?
Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, ‘Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu,’ kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake, Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe ili?’
8 Men ingå nu ett vad med min herre, konungen i Assyrien: jag vill giva dig två tusen hästar, om du kan skaffa dig ryttare till dem.
“Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: Ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo!
9 Huru skulle du då kunna slå tillbaka en enda ståthållare, en av min herres ringaste tjänare? Och du sätter din förtröstan till Egypten i hopp om att så få vagnar och ryttare!
Iwe ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo.
10 Menar du då att jag utan HERRENS vilja har dragit upp till detta land för att fördärva det? Nej, det är HERREN, som har sagt till mig: Drag upp mot detta land och fördärva det."
Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga dziko lino popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.”
11 Då sade Eljakim och Sebna och Joa till Rab-Sake: "Tala till dina tjänare på arameiska, ty vi förstå det språket, och tala icke till oss på judiska inför folket som står på muren."
Pamenepo Eliyakimu, Sebina ndi Yowa anawuza kazembeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”
12 Men Rab-Sake svarade: "Är det då till din herre och till dig, som min herre har sänt mig att tala dessa ord? Är det icke fastmer till de män som sitta på muren och som jämte eder skola nödgas äta sin egen träck och dricka sitt eget vatten?"
Koma kazembeyo anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”
13 Därefter trädde Rab-Sake närmare och ropade med hög röst på judiska och sade: "Hören den store konungens, den assyriske konungens, ord.
Tsono kazembeyo anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya!
14 Så säger konungen: Låten icke Hiskia bedraga eder, ty han förmår icke rädda eder.
Zimene mfumu ikunena ndi izi: Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni!
15 Och låten icke Hiskia förleda eder att förtrösta på HERREN, därmed att han säger: 'HERREN skall förvisso rädda oss; denna stad skall icke bliva given i den assyriske konungens hand.'
Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’
16 Hören icke på Hiskia. Ty så säger konungen i Assyrien: Gören upp i godo med mig och given eder åt mig, så skolen I få äta var och en av sitt vinträd och av sitt fikonträd och dricka var och en ur sin brunn,
“Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake,
17 till dess jag kommer och hämtar eder till ett land som är likt edert eget land, ett land med säd och vin, ett land med bröd och vingårdar.
mpaka mfumuyo itabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanulo, dziko limene lili ndi tirigu ndi vinyo watsopano, dziko loyenda mkaka ndi uchi.
18 Låten icke Hiskia förleda eder, när han säger: 'HERREN skall rädda oss.' Har väl någon av de andra folkens gudar räddat sitt land ur den assyriske konungens hand?
“Inu musalole kuti Hezekiya akusocheretseni pamene iye akuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’ Kodi alipo mulungu wa anthu a mtundu wina amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya?
19 Var äro Hamats och Arpads gudar? Var äro Sefarvaims gudar? Eller hava de räddat Samaria ur min hand?
Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa?
20 Vilken bland dessa länders alla gudar har väl räddat sitt land ur min hand, eftersom I menen, att HERREN skall rädda Jerusalem ur min hand?"
Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”
21 Men de tego och svarade honom icke ett ord, ty konungen hade så bjudit och sagt: "Svaren honom icke."
Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”
22 Och överhovmästaren Eljakim, Hilkias son, och sekreteraren Sebna och kansleren Joa, Asafs son, kommo till Hiskia med sönderrivna kläder och berättade för honom, vad Rab-Sake hade sagt.
Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu; Sebina mlembi wa bwalo; ndi Yowa, mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza zonse zimene anayankhula kazembe uja.