< 2 Kungaboken 15 >

1 I Jerobeams, Israels konungs, tjugusjunde regeringsår blev Asarja, Amasjas son, konung i Juda.
Mʼchaka cha 27 cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Azariya mwana wa Amaziya mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 Han var sexton år gammal, när han blev konung, och han regerade femtiotvå år i Jerusalem. Hans moder hette Jekolja, från Jerusalem.
Iye anakhala mfumu ali ndi zaka 16 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 52. Amayi ake anali Yekoliya wa ku Yerusalemu.
3 Han gjorde vad rätt var i HERRENS ögon, alldeles såsom hans fader Amasja hade gjort.
Iyeyo anachita zabwino pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake.
4 Dock blevo offerhöjderna icke avskaffade, utan folket fortfor att frambära offer och tända offereld på höjderna.
Komabe malo opembedzerako mafano sanawachotse ndipo anthu anapitirizabe kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
5 Men HERREN hemsökte konungen, så att han blev spetälsk för hela sitt liv; och han bodde sedan i ett särskilt hus. Jotam, konungens son, förestod då hans hus och dömde folket i landet.
Ndipo Yehova analanga mfumu ndi nthenda ya khate mpaka tsiku limene inamwalira. Tsono mfumuyo inkakhala mʼnyumba yakeyake yapadera. Mwana wake Yotamu ndiye amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu ndiponso ndiye amene ankalamulira anthu mʼdzikomo.
6 Vad nu mer är att säga om Asarja och om allt vad han gjorde, det finnes upptecknat i Juda konungars krönika.
Ntchito zina za Azariya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
7 Och Asarja gick till vila hos sina fäder, och man begrov honom hos hans fäder i Davids stad. Och hans son Jotam blev konung efter honom.
Azariya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
8 I Asarjas, Juda konungs, trettioåttonde regeringsår blev Sakarja, Jerobeams son, konung över Israel i Samaria och regerade i sex månader.
Mʼchaka cha 38 cha Azariya mfumu ya Yuda, Zekariya mwana wa Yeroboamu anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya ndipo analamulira miyezi isanu ndi umodzi.
9 Han gjorde vad ont var i HERRENS ögon, såsom hans fäder hade gjort; han avstod icke från de Jerobeams, Nebats sons, synder genom vilka denne hade kommit Israel att synda.
Ndipo iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira makolo ake. Iye sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
10 Och Sallum, Jabes' son, anstiftade en sammansvärjning mot honom och slog honom till döds i folkets åsyn, och blev så konung i hans ställe
Salumu mwana wa Yabesi anachitira chiwembu Zekariya. Anamukantha anthu akuona, namupha, ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
11 Vad nu mer är att säga om Sakarja, det finnes upptecknat i Israels konungars krönika.
Ntchito zina za Zekariya, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
12 Så, uppfylldes det ord som HERREN, hade talat till Jehu, när han sade: "Dina söner till fjärde led skola sitta på Israels tron." Det skedde så.
Awa ndiwo mawu a Yehova amene anayankhula kwa Yehu kuti, “Ana ako adzalamulira Israeli mpaka mʼbado wachinayi.”
13 Sallum, Jabes' son, blev konung i Ussias, Juda konungs, trettionionde regeringsår, och han regerade en månads tid i Samaria.
Salumu mwana wa Yabesi anakhala mfumu mʼchaka cha 39 cha ulamuliro wa Uziya mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Samariya mwezi umodzi.
14 Men då drog Menahem, Gadis son, upp från Tirsa och kom till Samaria och slog Sallum, Jabes' son, till döds i Samaria, och blev så konung i hans ställe
Ndipo Menahemu mwana wa Gadi anachoka ku Tiriza napita ku Samariya nakantha Salumu mwana wa Yabesi ku Samariya, namupha ndipo iye analowa ufumu mʼmalo mwake.
15 Vad nu mer är att säga om Sallum och om den sammansvärjning han anstiftade, det finnes upptecknat i Israels konungars krönika.
Ntchito zina za Salumu ndiponso za chiwembu chimene anachita, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
16 Vid den tiden förhärjade Menahem Tifsa med allt vad därinne var, så ock hela dess område, från Tirsa; ty staden hade icke öppnat portarna, därför härjade han den, och alla dess havande kvinnor lät han upprista.
Nthawi imeneyo Menahemu, kuchokera ku Tiriza, anakathira nkhondo mzinda wa Tipisa ndi anthu onse amene anali mʼmenemo ndi dera lonse lozungulira chifukwa iwo anakana kutsekula zipata zawo. Iye anatenga katundu yense mu mzinda wa Tipisa ndi kutumbula akazi onse oyembekezera.
17 I Asarjas, Juda konungs, trettionionde regeringsår blev Menahem, Gadis son, konung över Israel och regerade i tio år, i Samaria.
Mʼchaka cha 39 cha Azariya mfumu ya Yuda, Menahemu mwana wa Gadi anakhala mfumu ya Israeli ndipo analamulira mu Samariya zaka khumi.
18 Han gjorde vad ont var i HERRENS ögon; han avstod icke, så länge han levde, från de Jerobeams Nebats sons, synder genom vilka denne hade kommit Israel att synda.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Nthawi yonse ya ulamuliro wake sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
19 Och Pul, konungen i Assyrien, föll in i landet; då gav Menahem åt Pul tusen talenter silver, för att han skulle understödja honom och befästa konungadömet i hans hand.
Tsono Puli mfumu ya ku Asiriya inadzathira nkhondo dzikolo ndipo Menahemu anapatsa Puliyo makilogalamu 34,000 a siliva kuti amuthandize ndi kulimbikitsa ufumu wake.
20 Och de penningar som Menahem skulle giva åt konungen i Assyrien tog han ut genom att lägga skatt på alla rika män i Israel, en skatt av femtio siklar silver på var och en. Så vände då konungen i Assyrien tillbaka och stannade icke där i landet.
Menahemu anapeza ndalamazo kudzera mu msonkho umene ankakhometsa Aisraeli. Munthu aliyense wachuma ankapereka masekeli a siliva makumi asanu kwa mfumu ya ku Asiriya. Choncho mfumu ya ku Asiriya inabwerera ndipo sinakhalenso mʼdzikomo.
21 Vad nu mer är att säga om Menahem och om allt vad han gjorde, det finnes upptecknat i Israels konungars krönika.
Ntchito zina za Menahemu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
22 Och Menahem gick till vila hos sina fäder. Och hans son Pekaja blev konung efter honom.
Menahemu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Pekahiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
23 I Asarjas, Juda konungs, femtionde regeringsår blev Pekaja, Menahems son, konung över Israel i Samaria och regerade i två år.
Mʼchaka cha makumi asanu a Azariya mfumu ya Yuda, Pekahiya mwana wa Menahemu anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya ndipo analamulira zaka ziwiri.
24 Han gjorde vad ont var i HERRENS ögon; han avstod icke från de Jerobeams, Nebats sons, synder genom vilka denne hade kommit Israel att synda.
Pekahiya anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Iye sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, omwe anachimwitsa nawo Israeli.
25 Och Peka, Remaljas son, hans livkämpe, anstiftade en sammansvärjning mot honom och dräpte honom i Samaria, i konungshusets palatsbyggnad, han tillika med Argob och Arje; därvid hade han med sig femtio gileaditer. Så dödade han honom och blev konung i hans ställe.
Ndipo Peka mwana wa Remaliya, mtsogoleri wake wa ankhondo, anamuchita chiwembu. Iye pamodzi ndi anthu makumi asanu a ku Giliyadi anapha Pekahiya pamodzi ndi Arigobu ndi Ariyeli mʼchipinda choteteza nyumba ya mfumu mu Samariya. Kotero Peka anapha Pekahiya ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
26 Vad nu mer är att säga om Pekaja och om allt vad han gjorde, det finnes upptecknat i Israels konungars krönika.
Ntchito zina za Pekahiya ndi zonse zimene anachita zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
27 I Asarjas, Juda konungs, femtioandra regeringsår blev Peka, Remaljas son, konung över Israel i Samaria och regerade i tjugu år.
Mʼchaka cha 52 cha Azariya mfumu ya Yuda, Peka mwana wa Remaliya anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya ndipo analamulira zaka makumi awiri.
28 Han gjorde vad ont var i HERRENS Ögon; han avstod icke från de Jerobeams; Nebats sons, synder genom vilka denne hade kommit Israel att synda.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
29 I Pekas, Israels konungs, tid kom Tiglat-Pileser, konungen i Assyrien, och intog Ijon, Abel-Bet-Maaka, Janoa, Kedes, Hasor, Gilead och Galileen, hela Naftali land, och förde folket bort till Assyrien.
Nthawi ya Peka mfumu ya Israeli, Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya anabwera ndi kudzalanda Iyoni, Abeli-Beti-Maaka, Yanowa, Kedesi ndi Hazori. Mfumu ya ku Asiriya inatenga Giliyadi ndi Galileya, kuphatikizanso madera onse a Nafutali ndipo anatumiza Aisraeli ku Asiriya.
30 Och Hosea, Elas son, anstiftade en sammansvärjning mot Peka, Remaljas son, och slog honom till döds och blev så konung i hans ställe, i Jotams, Ussias sons, tjugonde regeringsår.
Kenaka Hoseya mwana wa Ela anachitira chiwembu Peka mwana wa Remaliya. Anamukantha ndi kumupha ndipo anakhala mfumu mʼmalo mwake mʼchaka makumi awiri cha Yotamu mwana wa Uziya.
31 Vad nu mer är att säga om Peka och om allt vad han gjorde, det finnes upptecknat i Israels konungars krönika.
Ntchito zina za Peka ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
32 I Pekas, Remaljas sons, Israels konungs, andra regeringsår blev Jotam, Ussias son, konung i Juda.
Mʼchaka chachiwiri cha Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli, Yotamu mwana wa Uziya mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
33 Han var tjugufem år gammal, när han blev konung, och han regerade sexton år i Jerusalem. Hans moder hette Jerusa, Sadoks dotter.
Iye anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Amayi ake anali Yerusa mwana wa Zadoki.
34 Han gjorde vad rätt var i HERRENS ögon; han gjorde alldeles såsom hans fader Ussia hade gjort.
Iye anachita zabwino pamaso pa Yehova monga anachitira Uziya abambo ake.
35 Dock blevo offerhöjderna icke avskaffade, utan folket fortfor att frambära offer och tända offereld på höjderna. Han byggde Övre porten till HERRENS hus.
Komabe malo opembedzera mafano sanawachotse ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
36 Vad nu mer är att säga om Jotam, om vad han gjorde, det finnes upptecknat i Juda konungars krönika.
Ntchito zina za Yotamu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
37 Vid den tiden begynte HERREN att låta Juda hemsökas av Resin, konungen i Aram, och av Peka, Remaljas son.
(Nthawi imeneyo, Yehova anayamba kumatuma Rezini mfumu ya Aaramu ndi Peka mwana wa Remaliya kudzamenyana ndi Yuda).
38 Och Jotam gick till vila hos sina fäder och blev begraven hos sina fäder i sin fader Davids stad. Och hans son Ahas blev konung efter honom.
Yotamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Ahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Kungaboken 15 >