< 1 Kungaboken 4 >

1 Konung Salomo var nu konung över hela Israel.
Ndipo Mfumu Solomoni inakhala mfumu ya Aisraeli onse.
2 Och dessa voro hans förnämsta män: Asarja, Sadoks son, var präst;
Nduna zake zikuluzikulu zinali izi: Azariya mwana wa Zadoki anali wansembe;
3 Elihoref och Ahia, Sisas söner, voro sekreterare; Josafat, Ahiluds son, var kansler;
Elihorefe ndi Ahiya, ana a Sisa, anali alembi; Yehosafati mwana wa Ahiludi, anali mlembi wa zochitika;
4 Benaja, Jojadas son, var överbefälhavare; Sadok och Ebjatar voro präster;
Benaya mwana wa Yehoyada, anali mtsogoleri wa ankhondo; Zadoki ndi Abiatara, anali ansembe;
5 Asarja, Natans son, var överfogde; Sabud, Natans son, en präst, var konungens vän;
Azariya mwana wa Natani, anali woyangʼanira nduna za mʼzigawo; Zabudi mwana wa Natani, anali wansembe ndi bwenzi la mfumu;
6 Ahisar var överhovmästare; Adoniram, Abdas son, hade uppsikten över de allmänna arbetena.
Ahisara, anali mkulu woyangʼanira nyumba ya mfumu; Adoniramu mwana wa Abida, anali mkulu woyangʼanira ntchito za thangata.
7 Och Salomo hade satt över hela Israel tolv fogdar, som skulle sörja för vad konungen och hans hus behövde; var och en hade årligen sin månad, då han skulle sörja för dessa behov.
Solomoni analinso ndi abwanamkubwa khumi ndi awiri amene ankayangʼanira zigawo zonse za dziko la Israeli. Iwo ankapereka chakudya kwa mfumu ndiponso ku banja laufumu. Bwanamkubwa aliyense ankapereka chakudya mwezi umodzi pa chaka.
8 Och följande voro deras namn: Ben-Hur i Efraims bergsbygd;
Mayina awo ndi awa: Beni-Huri, wa ku dziko la mapiri la Efereimu;
9 Ben-Deker i Makas, Saalbim, Bet-Semes, Elon, Bet-Hanan;
Beni-Dekeri, woyangʼanira mizinda ya Makazi, Saalibimu, Beti-Semesi ndi Eloni Beti-Hanani;
10 Ben-Hesed i Arubbot, vilken hade Soko och hela Heferlandet;
Beni-Hesedi, woyangʼanira mizinda ya Aruboti (Soko ndi dziko lonse la Heferi);
11 Ben-Abinadab i hela Nafat-Dor -- denne fick Salomos dotter Tafat till hustru --;
Beni-Abinadabu, woyangʼanira Nafoti Dori (iye anakwatira Tafati mwana wa Solomoni);
12 Baana, Ahiluds son, i Taanak och Megiddo och i hela den del av Bet-Sean, som ligger på sidan om Saretan, nedanför Jisreel, från Bet-Sean ända till Abel-Mehola och bortom Jokmeam;
Baana mwana wa Ahiludi, anali woyangʼanira Taanaki ndi Megido, ndi ku Beti Sani konse, kufupi ndi ku Zaretani kumunsi kwa Yezireeli, kuyambira ku Beti-Seani mpaka ku Abeli-Mehola kukafika mpaka ku Yokineamu;
13 Ben-Geber i Ramot i Gilead; han hade Manasses son Jairs byar, som ligga i Gilead; han hade ock landsträckan Argob, som ligger i Basan, sextio stora städer med murar och kopparbommar;
Beni-Geberi, anali woyangʼanira Ramoti Giliyadi (midzi ya Yairi inali ya mwana wa Manase ku Giliyadi, pamodzinso ndi chigawo cha Arigobu ku Basani ndiponso mizinda yake yayikulu makumi asanu ndi umodzi yokhala ndi malinga ndi mipiringidzo yamkuwa).
14 Ahinadab, Iddos son, i Mahanaim;
Ahinadabu mwana wa Ido, anali woyangʼanira Mahanaimu;
15 Ahimaas i Naftali; också han hade tagit en dotter av Salomo, Basemat, till hustru;
Ahimaazi anali woyangʼanira Nafutali (iyeyu anakwatira Basemati mwana wa Solomoni);
16 Baana, Husais son, i Aser och Alot;
Baana mwana wa Husai, anali woyangʼanira Aseri ndi Bealoti;
17 Josafat, Paruas son, i Isaskar;
Yehosafati mwana wa Paruwa, anali woyangʼanira Isakara;
18 Simei, Elas son, i Benjamin;
Simei mwana wa Ela, anali woyangʼanira Benjamini;
19 Geber, Uris son, i Gileads land, det land som hade tillhört Sihon, amoréernas konung, och Og, konungen i Basan; ty allenast en enda fogde fanns i det landet.
Geberi mwana wa Uri, anali woyangʼanira Giliyadi (dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi mfumu ya Basani). Iye ankayangʼanira chigawo chonsechi yekha.
20 Juda och Israel voro då talrika, så talrika som sanden vid havet; och man åt och drack och var glad.
Anthu a ku Yuda ndi ku Israeli anali ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Ankadya ndi kumwa ndipo ankasangalala.
21 Så var nu Salomo herre över alla riken ifrån floden till filistéernas land och ända ned till Egyptens gräns; de förde skänker till Salomo och voro honom underdåniga, så länge han levde.
Ndipo Solomoni analamulira mayiko onse kuyambira ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku dziko la Afilisti, kukafika mpaka ku malire a dziko la Igupto. Mayikowa ankabweretsa mphatso ndipo anali pansi pa ulamuliro wa Solomoni moyo wake wonse.
22 Och vad Salomo för var dag behövde av livsmedel var: trettio korer fint mjöl och sextio korer vanligt mjöl,
Chakudya cha tsiku ndi tsiku cha Solomoni chinali madengu 150 a ufa wosalala ndi madengu 300 a mgayiwa,
23 tio gödda oxar, tjugu valloxar och hundra far, förutom hjortar, gaseller, dovhjortar och gödda fåglar.
ngʼombe khumi zonenepa zodyetsera mʼkhola, ngʼombe za ku busa makumi awiri, ndiponso nkhosa ndi mbuzi 100, pamodzinso ndi mbawala, agwape, mphoyo ndi mbalame zoweta zonona.
24 Ty han rådde över hela landet på andra sidan floden, ifrån Tifsa ända till Gasa, över alla konungar på andra sidan floden; och han hade fred på alla sidor, runt omkring,
Pakuti ankalamulira dziko lonse la kumadzulo kwa mtsinje wa Yufurate kuyambira ku Tifisa mpaka ku Gaza, mafumu onse a kumadzulo kwa Mtsinje, ndipo anali pa mtendere ndi mayiko onse ozungulira.
25 Så att Juda och Israel sutto i trygghet, var och en under sitt vinträd och sitt fikonträd, ifrån Dan ända till Beer-Seba, så länge Salomo levde.
Pa nthawi ya Solomoni, Yuda ndi Israeli anali pa mtendere, kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba. Munthu aliyense ankangodzikhalira pansi pa mpesa wake ndi mtengo wake wa mkuyu.
26 Och Salomo hade fyrtio tusen spann vagnshästar och tolv tusen ridhästar.
Solomoni anali ndi zipinda 4,000 zodyeramo akavalo okoka magaleta ake ndi anthu 12,000 oyendetsa magaleta.
27 Och de nämnda fogdarna sörjde var sin månad för konung Salomos behov, och för allas som hade tillträde till konung Salomos bord; de läto intet fattas.
Abwanamkubwa a zigawo aja, aliyense pa mwezi wake, ankapereka chakudya cha Mfumu Solomoni ndi cha anthu onse amene ankadya naye. Iwo ankaonetsetsa kuti pasasowe kalikonse.
28 Och kornet och halmen för hästarna och travarna förde de, var och en i sin ordning, till det ställe där han uppehöll sig.
Ankabweretsanso ku malo ake ofunikira muyeso wawo wa barele ndi udzu wa akavalo okoka magaleta ndiponso akavalo ena.
29 Och Gud gav Salomo vishet och förstånd i mycket rikt mått och så mycken insikt, att den kunde liknas vid sanden på havets strand,
Mulungu anamupatsa Solomoni nzeru ndi luntha losaneneka ndipo nzeru zake zinali zochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
30 så att Salomos vishet var större än alla österlänningars vishet och all Egyptens vishet.
Nzeru za Solomoni zinali zoposa nzeru za anthu onse a Kummawa ndiponso nzeru zonse za ku Igupto.
31 Han var visare än alla andra människor, visare än esraiten Etan och Heman och Kalkol och Darda, Mahols söner; och ryktet om honom gick ut bland alla folk runt omkring.
Iye anali wanzeru kuposa munthu wina aliyense, kuposa ngakhale Etani wa banja la Ezara, Hemani, Kalikoli ndi Darida, ana a Maholi. Ndipo mbiri yake inamveka kwa mitundu yonse ya anthu ozungulira.
32 Han diktade tre tusen ordspråk, och hans sånger voro ett tusen fem.
Solomoni anapeka miyambi 3,000 ndi kulemba nyimbo 1,005.
33 Han talade om träden, från cedern på Libanon ända till isopen, som växer fram ur väggen. Han talade ock om fyrfotadjuren, om fåglarna, om kräldjuren och om fiskarna.
Iye ankaphunzitsa za mitengo, kuyambira mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni mpaka kachitsamba ka hisope khomera pa khoma. Iye ankaphunzitsanso za nyama ndi mbalame, zinthu zokwawa pansi ndiponso za nsomba.
34 Och från alla folk kom man för att höra Salomos visdom, från alla konungar på jorden, som hade hört talas om hans visdom.
Anthu a mitundu yonse ankabwera kudzamva nzeru za Solomoni. Anthu amenewa ankatumizidwa ndi mafumu onse a dziko lapansi amene anamvapo za nzeru zakezo.

< 1 Kungaboken 4 >