< 1 Krönikeboken 12 >

1 Och dessa voro de som kommo till David i Siklag, medan han ännu höll sig undan för Saul, Kis' son; de hörde till de hjältar som bistodo honom under kriget.
Nawa anthu amene anabwera kwa Davide ali ku Zikilagi pamene iye anathamangitsidwa ndi Sauli mwana wa Kisi (iwowo anali mʼgulu la asilikali amene ankamuthandiza pa nkhondo.
2 De voro väpnade med båge och skickliga i att, både med höger och med vänster hand, slunga stenar och avskjuta pilar från bågen. Av Sauls stamfränder, benjaminiterna, kommo:
Iwo anali ndi mauta ndipo amadziwa kuponya mivi komanso miyala, ndipo amatha kuponyera dzanja lamanja kapena lamanzere. Iwo anali abale ake a Sauli ochokera ku fuko la Benjamini.
3 Ahieser, den förnämste, och Joas, gibeatiten Hassemaas söner; Jesuel och Pelet, Asmavets söner; Beraka; anatotiten Jehu;
Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri ndi Yowasi ana a Semaya wa ku Gibeya; Yezieli ndi Peleti ana a Azimaveti; Beraka, Yehu wa ku Anatoti,
4 gibeoniten Jismaja, en av de trettio hjältarna, anförare för de trettio; Jeremia; Jahasiel; Johanan; gederatiten Josabad;
ndi Isimaiya wa ku Gibiyoni, munthu wamphamvu mʼgulu la anthu makumi atatu aja, yemwenso anali mtsogoleri wawo; Yeremiya, Yahazieli, Yohanani, Yozabadi wa ku Gederi,
5 Eleusai; Jerimot; Bealja; Semarja; harufiten Sefatja;
Eluzai, Yerimoti, Bealiya, Semariya ndi Sefatiya Mharufi;
6 koraiterna Elkana, Jissia, Asarel, Joeser och Jasobeam;
Elikana, Isiya, Azareli, Yowezeri ndi Yasobeamu a ku banja la Kora;
7 Joela och Sebadja, söner till Jeroham, av strövskaran.
ndi Yowela ndi Zebadiya ana a Yerohamu wa ku Gedori.
8 Och av gaditerna avföllo några och gingo till David i bergfästet i öknen, tappra män, krigsmän skickliga att strida, rustade med sköld och spjut; de hade en uppsyn såsom lejon och voro snabba såsom gaseller på bergen:
Asilikali ena a fuko la Gadi anathawira kwa Davide ku linga lake ku chipululu. Iwo anali asilikali olimba mtima, okonzekera nkhondo ndipo amadziwa kugwiritsa ntchito chishango ndi mkondo. Iwowo anali woopsa ngati mikango ndipo anali aliwiro ngati ngoma zamʼmapiri.
9 Eser, den förnämste, Obadja, den andre, Eliab, den tredje,
Mtsogoleri wawo anali Ezeri, wotsatana naye anali Obadiya, wachitatu anali Eliabu,
10 Masmanna, den fjärde, Jeremia, den femte,
wachinayi anali Misimana, Yeremiya anali wachisanu,
11 Attai, den sjätte, Eliel, den sjunde,
wachisanu ndi chimodzi anali Atai, Elieli anali wachisanu ndi chiwiri,
12 Johanan, den åttonde, Elsabad, den nionde,
wachisanu ndi chitatu anali Yohanani, Elizabadi anali wachisanu ndi chinayi,
13 Jeremia, den tionde, Makbannai, den elfte.
wakhumi anali Yeremiya ndipo Makibanai anali wa 11.
14 Dessa hörde till Gads barn och till de förnämsta i hären; den ringaste av dem var ensam så god som hundra, men den ypperste så god som tusen.
Anthu a fuko la Gadi amenewa anali atsogoleri; angʼonoangʼono amalamulira anthu 100 pamene akuluakulu amalamulira anthu 1,000.
15 Dessa voro de som i första månaden gingo över Jordan, när den var full över alla sina bräddar, och som förjagade alla dem som bodde i dalarna, åt öster och åt väster.
Awa ndi amene anawoloka Yorodani mwezi woyamba pamene mtsinje unali utasefukira mbali zonse, ndipo anathamangitsa aliyense amene amakhala mʼchigwa, mbali ya kumadzulo ndi kummawa.
16 Av Benjamins och Juda barn kommo några män till David ända till bergfästet.
Anthu ena a fuko la Benjamini ndi ena ochokera ku Yuda anabweranso kwa Davide pamene anali ku linga lake.
17 Då gick David ut emot dem och tog till orda och sade till dem: "Om I kommen till mig i fredlig avsikt och viljen bistå mig, så är mitt hjärta redo till förening med eder; men om I kommen för att förråda mig åt mina ovänner, fastän ingen orätt är i mina händer, då må våra fäders Gud se därtill och straffa det."
Davide anapita kukakumana nawo ndipo anati, “Ngati mwabwera kwa ine mwamtendere, kuti mundithandize, ndakonzeka kugwirizana nanu. Koma ngati mwabwera kudzandipereka kwa adani anga, ngakhale kuti sindinalakwe, Mulungu wa makolo anthu aone izi ndipo akuweruzeni.”
18 Men Amasai, den förnämste bland de trettio, hade blivit beklädd med andekraft, och han sade: "Dina äro vi, David, och med dig stå vi, du Isais son. Frid vare med dig, frid, och frid vare med dem som bistå dig ty din Gud har bistått dig!" Och David tog emot dem och gav dem plats bland de förnämsta i sin skara.
Kenaka Mzimu anabwera pa Amasai, mtsogoleri wa anthu makumi atatu aja ndipo anati: “Inu Davide, ife ndife anu! Tili nanu limodzi, inu mwana wa Yese! Kupambana, Kupambana kwa inu, ndiponso kupambana kukhale kwa iwo amene akukuthandizani pakuti Mulungu wanu adzakuthandizani.” Kotero Davide anawalandira ndipo anawayika kukhala atsogoleri a magulu ake a ankhondo.
19 Från Manasse gingo några över till David, när han med filistéerna drog ut i strid mot Saul, dock fingo de icke bistå dessa; ty när filistéernas hövdingar hade rådplägat, skickade de bort honom, i det de sade: "Det gäller huvudet för oss, om han går över till sin herre Saul.
Anthu ena a fuko la Manase anathawira kwa Davide pamene anapita ndi Afilisti kukamenyana ndi Sauli. (Iye ndi anthu ake sanathandize Afilisti chifukwa, atsogoleri awo atakambirana, anamubweza Davide. Iwo anati, “Ife tidzawonongedwa ngati uyu adzabwerera kwa mbuye wake Sauli).”
20 När han då drog till Siklag, gingo dessa från Manasse över till honom: Adna, Josabad, Jediael, Mikael, Josabad, Elihu och Silletai, huvudmän för de ätter som tillhörde Manasse.
Davide atapita ku Zikilagi, anthu a fuko la Manase amene anathawira kwa iye anali awa: Adina, Yozabadi, Yediaeli, Mikayeli, Yozabadi, Elihu ndi Ziletai; atsogoleri a magulu a anthu 1,000 a ku Manase.
21 Dessa bistodo David mot strövskaran, ty de voro allasammans tappra stridsmän och blevo hövitsmän i hären.
Iwowa anathandiza Davide kulimbana ndi magulu achifwamba, pakuti onsewa anali asilikali olimba mtima ndipo anali atsogoleri mʼgulu lake la ankhondo.
22 Dag efter dag kommo nämligen allt flera till David för att bistå honom, så att hans läger blev övermåttan stort.
Tsiku ndi tsiku anthu amabwera kudzathandiza Davide, mpaka anakhala ndi gulu lalikulu la ankhondo, ngati gulu la ankhondo a Mulungu.
23 Detta är de tal som angiva summorna av det väpnade krigsfolk som kom till David i Hebron, för att efter HERRENS befallning flytta Sauls konungamakt över på honom:
Nachi chiwerengero cha magulu a anthu ankhondo amene anabwera kwa Davide ku Hebroni kudzapereka ufumu wa Sauli kwa iye, monga momwe ananenera Yehova:
24 Juda barn, som buro sköld och spjut, sex tusen åtta hundra, väpnade till strid;
Anthu a fuko la Yuda onyamula chishango ndi mkondo analipo 6,800;
25 av Simeons barn tappra krigsmän, sju tusen ett hundra;
Anthu a fuko la Simeoni, asilikali okonzekera nkhondo analipo 7,100;
26 av Levi barn fyra tusen sex hundra;
Anthu a fuko la Levi analipo 4,600,
27 därtill Jojada, fursten inom Arons släkt, och med honom tre tusen sju hundra;
mtsogoleri Yehoyada wa banja la Aaroni anabweranso ndi anthu 3,700,
28 så ock Sadok, en tapper yngling, med sin familj, tjugutvå hövitsmän;
ndi Zadoki, mnyamata wankhondo wolimba mtima, anabwera ndi akuluakulu 22 ochokera mʼbanja lake;
29 av Benjamins barn, Sauls stamfränder, tre tusen (ty ännu vid den tiden höllo de flesta av dem troget med Sauls hus);
Anthu a fuko la Benjamini, abale ake a Sauli analipo 3,000 ndipo ambiri anali ndi Sauli ku nyumba yake pa nthawiyi;
30 av Efraims barn tjugu tusen åtta hundra, tappra stridsmän, namnkunniga män i sina familjer;
Anthu a fuko la Efereimu, asilikali olimba mtima, otchuka pa mabanja awo analipo 20,800;
31 av ena hälften av Manasse stam aderton tusen namngivna män, som kommo för att göra David till konung;
Anthu a fuko latheka la Manase amene anawayitana kuti adzakhazikitse nawo ufumu wa Davide analipo 18,000;
32 av Isaskars barn kommo män som väl förstodo tidstecknen och insågo vad Israel borde göra, två hundra huvudmän, därtill alla deras stamfränder under deras befäl;
Anthu a fuko la Isakara amene ankazindikira nthawi ndipo amadziwa zimene Israeli ankayenera kuchita, analipo atsogoleri 200 pamodzi ndi abale awo onse amene amawatsogolera.
33 av Sebulon stridbara män, rustade till krig med alla slags vapen, femtio tusen, som samlades endräktigt;
Anthu a fuko la Zebuloni, analipo 5,000. Iwowa anali asilikali odziwa bwino nkhondo, okhala ndi zida za mtundu uliwonse, okonzekera kudzathandiza Davide ndi mtima umodzi.
34 av Naftali ett tusen hövitsmän, och med dem trettiosju tusen, väpnade med sköld och spjut;
Anthu a fuko la Nafutali, analipo atsogoleri 1,000 pamodzi ndi anthu 37,000 onyamula zishango ndi mikondo;
35 av daniterna krigsrustade män, tjuguåtta tusen sex hundra;
Anthu a fuko la Dani, okonzekera nkhondo analipo 28,600.
36 av Aser stridbara män, rustade till krig, fyrtio tusen;
Anthu a fuko la Aseri, asilikali odziwa bwino nkhondo, okonzekeradi nkhondo analipo 40,000;
37 och från andra sidan Jordan, av rubeniterna, gaditerna och andra hälften av Manasse stam, ett hundra tjugu tusen, väpnade med alla slags vapen som brukas vid krigföring.
Ndipo kuchokera kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase, amene anali ndi zida za mtundu uliwonse analipo 120,000.
38 Alla dessa krigsmän, ordnade till strid, kommo i sina hjärtans hängivenhet till Hebron för att göra David till konung över hela Israel. Också hela det övriga Israel var enigt i att göra David till konung.
Onsewa anali anthu odziwa kumenya nkhondo amene anadzipereka ku magulu awo. Iwo anabwera ku Hebroni ali otsimikiza kudzamuyika Davide kukhala mfumu ya Aisraeli. Aisraeli ena onse anali ndi mtima umodzinso womuyika Davide kukhala mfumu.
39 Och de voro där hos David i tre dagar och åto och drucko, ty deras bröder hade försett dem med livsmedel.
Anthuwa anakhala ndi Davide masiku atatu akudya ndi kumwa pakuti mabanja awo anawapatsa zakudya.
40 De som bodde närmast dem, ända upp till Isaskar, Sebulon och Naftali, tillförde dem ock på åsnor, kameler, mulåsnor och oxar livsmedel i myckenhet till föda: mjöl, fikonkakor och russinkakor, vin och olja, fäkreatur och småboskap; ty glädje rådde i Israel.
Komanso anthu oyandikana nawo ochokera ku Isakara, Zebuloni ndi Nafutali anabweretsa zakudya pa abulu, ngamira, nyulu ndi ngʼombe. Panali ufa wambiri, makeke ankhuyu, ntchintchi za mphesa, vinyo, mafuta, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi, popeza munali chimwemwe mu Israeli.

< 1 Krönikeboken 12 >