< Sakaria 8 >
1 Vidare kom HERREN Sebaots ord; han sade:
Awa ndi mawu amene Yehova Wamphamvuzonse ananena.
2 Så säger HERREN Sebaot: Jag har stor nitälskan för Sion, ja, med stor vrede nitälskar jag för henne.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikuchitira nsanje yayikulu Ziyoni. Mtima wanga ukupweteka chifukwa cha nsanje pa iyeyo.”
3 Så säger HERREN: Jag vill vända: åter till Sion och taga min boning i Jerusalem; och Jerusalem skall kallas »den trogna staden», och HERREN Sebaots berg »det heliga berget».
Yehova akuti, “Ndidzabwerera ku Ziyoni ndi kukakhala ku Yerusalemu. Pamenepo Yerusalemu adzatchedwa Mzinda wa Choonadi ndipo phiri la Yehova Wamphamvuzonse lidzatchedwa Phiri Lopatulika.”
4 Så säger HERREN Sebaot: Ännu en gång skola gamla män och gamla kvinnor vara att finna på gatorna i Jerusalem, var och en med sin stav i handen, för hög ålders skull.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Abambo ndi amayi okalamba adzakhalanso mʼmisewu ya mu Yerusalemu, aliyense ali ndi ndodo mʼmanja mwake chifukwa cha kuchuluka kwa masiku ake.
5 Och stadens gator skola vara fulla av gossar och flickor, som leka där på gatorna,
Ndipo misewu ya mu mzindamo idzadzaza ndi anyamata ndi atsikana akusewera.”
6 Så säger HERREN Sebaot. Om än sådant på den tiden kan komma att synas alltför underbart för kvarlevan av detta folk, icke måste det väl därför synas alltför underbart också för mig? säger HERREN Sebaot.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati zikuoneka kuti nʼzosatheka kwa anthu otsala pa nthawi ino, kodi zidzakhala zosathekanso kwa Ine?” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
7 Så säger HERREN Sebaot: Se, jag skall frälsa mitt folk ut ur både österland och västerland
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani ndidzapulumutsa anthu anga kuchokera ku mayiko a kummawa ndi kumadzulo.
8 och låta dem komma och bosätta sig i Jerusalem; och de skola vara mitt folk, och jag skall vara deras Gud, i sanning och rättfärdighet.
Ndidzawabweretsa kuti adzakhale mu Yerusalemu; adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, wokhulupirika ndi wolungama pakati pawo.”
9 Så säger HERREN Sebaot: Fatten mod, I som i denna tid hören dessa ord av samma profeters mun, som talade på den tid då grunden lades till HERREN Sebaots hus, templet som skulle byggas upp.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Inu amene tsopano mukumva mawu awa amene akuyankhula aneneri amene analipo pamene ankayika maziko a nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, ‘limbani mtima kuti mumange Nyumba ya Yehova.’
10 Ty före den tiden var människornas arbete lönlöst och djurens arbete fåfängt; ingen hade någon ro för sina ovänner, vare sig han gick ut eller in, ty jag eggade alla människor mot varandra.
Mpaka nthawi imeneyi panalibe munthu wolandira malipiro pa ntchito kapena ndalama zolipirira nyama zogwira ntchito. Panalibe munthu amene ankadzigwirira ntchito mwamtendere chifukwa choopa adani ake, pakuti Ine ndinkawayambanitsa.
11 Men nu är jag icke mer så sinnad mot kvarlevan av detta folk som jag var i forna dagar, säger HERREN Sebaot.
Koma tsopano sindidzachitira otsala mwa anthu awa zomwe ndinachita kale,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
12 Ty nu skall friden skaffa utsäde, vinträdet skall giva sin frukt, jorden skall giva sin gröda, och himmelen skall giva sin dagg; och jag skall låta kvarlevan av detta folk få allt detta till sin arvedel.
“Pakuti mbewu zidzamera bwino, mpesa udzabala zipatso zake, nthaka idzatulutsa zomera zake, ndi thambo lidzagwetsa mame. Ndidzapereka zonse kukhala cholowa cha otsala mwa anthu awa.
13 Och det skall ske, att likasom I, både Juda hus och Israels hus, haven varit ett exempel som man har nämnt, när man förbannade bland hedningarna, så skolen I nu, då jag har frälsat eder, tvärtom bliva nämnda, när man välsignar. Frukten icke, utan fatten mod.
Monga mwakhala muli chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu ina ya anthu, inu Yuda ndi Israeli, choncho ndidzakupulumutsani, ndipo mudzakhala dalitso. Musachite mantha, koma limbani mtima.”
14 Ty så säger HERREN Sebaot: Likasom jag, när edra fäder förtörnade mig, beslöt att göra eder ont, säger HERREN Sebaot, och icke sedan ångrade det,
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Monga ndinatsimikiza mtima kubweretsa choyipa pa inu, komanso osakuchitirani chisoni pamene makolo anu anandikwiyitsa,” akutero Yehova,
15 så har jag tvärtom i denna tid beslutit att göra gott mot Jerusalem och Juda hus; frukten icke.
“Choncho tsopano ndatsimikiza mtima kuchitiranso zabwino Yerusalemu ndi Yuda. Musachite mantha.
16 Men detta är vad I skolen göra: Talen sanning med varandra; domen rätta och fridsamma domar i edra portar.
Zinthu zoti muchite ndi izi: Muziwuzana zoona zokhazokha, muziweruza moona ndi mwachilungamo mʼmabwalo anu;
17 Tänken icke i edra hjärtan ut ont mot varandra, och älsken icke falska eder; ty allt sådant hatar jag, säger HERREN.
musamachitire mnzanu chiwembu, musamakonde kulumbira zonama. Zonsezi Ine ndimadana nazo,” akutero Yehova.
18 Och HERREN Sebaots ord kom till mig; han sade:
Yehova Wamphamvuzonse anayankhulanso nane.
19 Så säger HERREN Sebaot: Fastedagarna i fjärde, femte, sjunde och tionde månaden skola för Juda hus bliva till fröjd och glädje och till sköna högtider. Men älsken sanning och frid.
Ndipo ananena kuti, “Kusala zakudya kwa pa mwezi wachinayi, chisanu, chisanu ndi chiwiri ndi wakhumi, kudzakhala nthawi yachimwemwe, ya chisangalalo ndi nthawi ya madyerero chikondwerero kwa Yuda. Nʼchifukwa chake muzikonda choonadi ndi mtendere.”
20 Så säger HERREN Sebaot: Ännu en gång skall det ske att folk skola komma hit och många städers invånare;
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a mitundu yambiri ndi anthu okhala mʼmizinda yambiri adzabwerabe,
21 och invånarna i den ena staden skola gå till den andra och säga: »Upp, låtom oss gå åstad och bönfalla inför HERREN och söka HERREN Sebaot; jag själv vill ock gå åstad.»
ndipo nzika za mzinda wina zidzapita ku mzinda wina, kukanena kuti, ‘Tiyeni mwamsanga tikapemphe madalitso kwa Yehova ndi kukapembedza Yehova Wamphamvuzonse. Inenso ndikupita kumeneko.’
22 Ja, många folk och mäktiga hednafolk skola komma och söka HERREN Sebaot i Jerusalem och bönfalla inför HERREN,
Anthu ambiri ndiponso a ku mayiko amphamvu adzabwera ku Yerusalemu kudzapembedza Yehova Wamphamvuzonse ndi kudzapempha madalitso.”
23 Så säger HERREN Sebaot: På den tiden skall det ske att tio män av allahanda tungomål som talas bland hednafolken skola fatta en judisk man i mantelfliken och säga: »Låt oss gå med eder, ty vi hava hört att Gud är med eder.»
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Masiku amenewo anthu khumi ochokera ku mitundu ya anthu a ziyankhulo zosiyana adzagwira mkanjo wa Myuda ndi kunena kuti, ‘Tipite nawo, chifukwa tamva kuti Mulungu ali nanu.’”