< Psaltaren 17 >
1 En bön av David. Hör, o HERRE, en rättfärdig sak, akta på mitt rop, lyssna till min bön; den kommer icke ifrån falska läppar.
Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
2 Av dig må jag få min rätt; dina ögon må skåda vad rättvist är.
Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
3 Du prövar mitt hjärta, du utrannsakar mig, men du finner intet; ingen ond tanke går ut ur min mun.
Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
4 Efter dina läppars ord, och vad människor än må göra, tager jag mig till vara för våldsverkares stigar.
Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
5 Mina steg hålla sig stadigt på dina vägar, mina fötter vackla icke.
Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
6 Så åkallar jag nu dig, ty du, Gud, skall svara mig; böj ditt öra till mig, hör mitt tal.
Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
7 Bevisa din underbara nåd, du som frälsar undan motståndarna dem som taga sin tillflykt till din högra hand.
Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
8 Bevara mig såsom en ögonsten, beskärma mig under dina vingars skugga
Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
9 för de ogudaktiga, som vilja fördärva mig, för mina dödsfiender, som omringa mig.
kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
10 Sitt hjärta förstocka de; med sin mun tala de stora ord.
Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
11 Nu äro de omkring mig, var vi gå, deras ögon speja efter huru de skola böja mig till jorden.
Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
12 Ja, denne är lik ett lejon som längtar efter rov, lik ett ungt lejon som ligger i försåt.
Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
13 Stå upp, HERRE; träd emot honom, slå honom ned, rädda med ditt svärd min själ från den ogudaktige,
Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
14 ja, med din hand, från människorna, HERRE, från denna världens människor, som hava sin del i detta livet, och vilkas buk du fyller med dina håvor, som hava söner i mängd och lämna sitt överflöd åt sina barn.
Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
15 Men jag skall skåda ditt ansikte i rättfärdighet; när jag uppvaknar, vill jag mätta mig av din åsyn.
Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.