< Psaltaren 116 >

1 Jag har HERREN kär, ty han hör min röst och mina böner.
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 Ja, han har böjt sitt öra till mig; i hela mitt liv skall jag åkalla honom.
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 Dödens band omvärvde mig, och dödsrikets ångest grep mig; jag kom i nöd och bedrövelse. (Sheol h7585)
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
4 Men jag åkallade HERRENS namn: »Ack HERRE, rädda min själ.»
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 HERREN är nådig och rättfärdig, vår Gud är barmhärtig.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 HERREN bevarar de enfaldiga; jag var i elände, och han frälste mig.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 Vänd nu åter till din ro, min själ, ty HERREN har gjort väl mot dig.
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 Ja, du har räddat min själ från döden, mitt öga från tårar, min fot ifrån fall;
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 jag skall få vandra inför HERREN i de levandes land.
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 Jag tror, ty därför talar jag, jag som var storligen plågad,
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 jag som måste säga i min ångest: »Alla människor äro lögnaktiga.»
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 Huru skall jag vedergälla HERREN alla hans välgärningar mot mig?
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 Jag vill taga frälsningens bägare och åkalla HERRENS namn.
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 Jag vill infria åt HERREN mina löften, ja, i hela hans folks åsyn.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 Dyrt aktad i HERRENS ögon är hans frommas död.
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 Ack HERRE, jag är ju din tjänare, jag är din tjänare, din tjänarinnas son; du har lossat mina band.
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 Dig vill jag offra lovets offer, och HERRENS namn vill jag åkalla.
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 Jag vill infria åt HERREN mina löften, ja, i hela hans folks åsyn,
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 i gårdarna till HERRENS hus, mitt i dig, Jerusalem. Halleluja!
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Psaltaren 116 >