< Sakaria 8 >

1 Och Herrans ord skedde till mig, och sade:
Awa ndi mawu amene Yehova Wamphamvuzonse ananena.
2 Detta säger Herren Zebaoth: Jag hafver nit haft ganska svårliga om Zion, och hafver i stor vrede nit haft derom.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikuchitira nsanje yayikulu Ziyoni. Mtima wanga ukupweteka chifukwa cha nsanje pa iyeyo.”
3 Så säger Herren: Jag vänder mig åter till Zion, och vill bo i Jerusalem, så att Jerusalem skall kallas en sannfärdig stad, och Herrans Zebaoths berg ett heligt berg.
Yehova akuti, “Ndidzabwerera ku Ziyoni ndi kukakhala ku Yerusalemu. Pamenepo Yerusalemu adzatchedwa Mzinda wa Choonadi ndipo phiri la Yehova Wamphamvuzonse lidzatchedwa Phiri Lopatulika.”
4 Detta säger Herren Zebaoth: Der skola ännu härefter bo på Jerusalems gator gamle män och qvinnor, och de som med käpp gå af stor ålder.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Abambo ndi amayi okalamba adzakhalanso mʼmisewu ya mu Yerusalemu, aliyense ali ndi ndodo mʼmanja mwake chifukwa cha kuchuluka kwa masiku ake.
5 Och stadsens gator skola vara fulla med små piltar och pigor, som på gatomen leka.
Ndipo misewu ya mu mzindamo idzadzaza ndi anyamata ndi atsikana akusewera.”
6 Detta säger Herren Zebaoth: Tycker dem detta omöjeligit vara, för detta igenlefda folks ögon, i denna tid; skulle det ock fördenskull omöjeligit vara för min ögon? säger Herren Zebaoth.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati zikuoneka kuti nʼzosatheka kwa anthu otsala pa nthawi ino, kodi zidzakhala zosathekanso kwa Ine?” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
7 Detta säger Herren Zebaoth: Si, jag vill förlossa mitt folk ifrån österlandet och ifrå vesterlandet;
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani ndidzapulumutsa anthu anga kuchokera ku mayiko a kummawa ndi kumadzulo.
8 Och jag skall låta dem komma hit, till att bo i Jerusalem; och de skola vara mitt folk, och jag skall vara deras Gud, i sanning och rättfärdighet.
Ndidzawabweretsa kuti adzakhale mu Yerusalemu; adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, wokhulupirika ndi wolungama pakati pawo.”
9 Så säger Herren Zebaoth: Stärker edra händer, I som hören dessa orden, i denna tid, genom Propheternas mun, på den dagen då grunden lagd vardt på Herrans Zebaoths hus, att templet skulle bygdt varda.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Inu amene tsopano mukumva mawu awa amene akuyankhula aneneri amene analipo pamene ankayika maziko a nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, ‘limbani mtima kuti mumange Nyumba ya Yehova.’
10 Ty för dessa dagar var menniskors arbete förgäfves, och djurens arbete var omintet; och var ingen frid dem som ut och in foro för bedröfvelse; utan jag lät alla menniskor gå, hvar och en emot sin nästa.
Mpaka nthawi imeneyi panalibe munthu wolandira malipiro pa ntchito kapena ndalama zolipirira nyama zogwira ntchito. Panalibe munthu amene ankadzigwirira ntchito mwamtendere chifukwa choopa adani ake, pakuti Ine ndinkawayambanitsa.
11 Men nu vill jag icke göra, såsom i de förra dagar, med de öfverblefna af desso folke, säger Herren Zebaoth;
Koma tsopano sindidzachitira otsala mwa anthu awa zomwe ndinachita kale,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
12 Utan de skola vara fridsens säd; vin trät skall gifva sina frukt, och jorden gifva sin växt, och himmelen skall gifva sina dagg; och jag skall låta de öfverblefna af desso folke allt detta besitta.
“Pakuti mbewu zidzamera bwino, mpesa udzabala zipatso zake, nthaka idzatulutsa zomera zake, ndi thambo lidzagwetsa mame. Ndidzapereka zonse kukhala cholowa cha otsala mwa anthu awa.
13 Och det skall ske, lika som I af Juda hus, och af Israels hus, hafven varit en förbannelse ibland Hedningarna; så vill jag förlossa eder, att I skolen vara en välsignelse. Allenast frukter eder intet, och stärker edra händer.
Monga mwakhala muli chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu ina ya anthu, inu Yuda ndi Israeli, choncho ndidzakupulumutsani, ndipo mudzakhala dalitso. Musachite mantha, koma limbani mtima.”
14 Så säger Herren Zebaoth: Såsom jag tänkte att plåga eder, då edra fäder förtörnade mig, säger Herren Zebaoth, och det ångrade mig intet;
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Monga ndinatsimikiza mtima kubweretsa choyipa pa inu, komanso osakuchitirani chisoni pamene makolo anu anandikwiyitsa,” akutero Yehova,
15 Alltså tänker jag nu igen, i dessom dagom, göra väl emot Jerusalem och Juda hus. Allenast frukter eder intet.
“Choncho tsopano ndatsimikiza mtima kuchitiranso zabwino Yerusalemu ndi Yuda. Musachite mantha.
16 Men detta är det I göra skolen: Hvar och en tale sanningena med den andra; och dömer rätt, och skaffer frid i edrom portom;
Zinthu zoti muchite ndi izi: Muziwuzana zoona zokhazokha, muziweruza moona ndi mwachilungamo mʼmabwalo anu;
17 Och ingen tänke något ondt i sitt hjerta emot sin nästa, och älsker icke falska eder; ty allt sådant hatar jag, säger Herren.
musamachitire mnzanu chiwembu, musamakonde kulumbira zonama. Zonsezi Ine ndimadana nazo,” akutero Yehova.
18 Och Herrans Zebaoths ord skedde till mig, och sade:
Yehova Wamphamvuzonse anayankhulanso nane.
19 Så säger Herren Zebaoth: Fjerde, femte, sjunde, och tionde månadens fasta skall vara Jude huse till en fröjd och glädje, och till gladsamma årshögtider. Allenast älsker sanning och frid.
Ndipo ananena kuti, “Kusala zakudya kwa pa mwezi wachinayi, chisanu, chisanu ndi chiwiri ndi wakhumi, kudzakhala nthawi yachimwemwe, ya chisangalalo ndi nthawi ya madyerero chikondwerero kwa Yuda. Nʼchifukwa chake muzikonda choonadi ndi mtendere.”
20 Detta säger Herren Zebaoth: Framdeles skola ännu komma mycken folk, och många städers borgare.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a mitundu yambiri ndi anthu okhala mʼmizinda yambiri adzabwerabe,
21 Och borgarena af den ena staden skola gå till de andra, och säga; Låt oss gå bort till att bedja inför Herranom, och till att söka Herran Zebaoth; vi vilje gå med eder.
ndipo nzika za mzinda wina zidzapita ku mzinda wina, kukanena kuti, ‘Tiyeni mwamsanga tikapemphe madalitso kwa Yehova ndi kukapembedza Yehova Wamphamvuzonse. Inenso ndikupita kumeneko.’
22 Alltså skola mång folk och Hedningar hopetals komma till att söka Herran Zebaoth i Jerusalem, och bedja inför Herranom.
Anthu ambiri ndiponso a ku mayiko amphamvu adzabwera ku Yerusalemu kudzapembedza Yehova Wamphamvuzonse ndi kudzapempha madalitso.”
23 Så säger Herren Zebaoth: På den tiden skola tio män, af allahanda Hedningars mål, fatta en Judisk man i klädefliken, och sägs: Vi vilje gå med eder; ty vi höre, att Gud är med eder.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Masiku amenewo anthu khumi ochokera ku mitundu ya anthu a ziyankhulo zosiyana adzagwira mkanjo wa Myuda ndi kunena kuti, ‘Tipite nawo, chifukwa tamva kuti Mulungu ali nanu.’”

< Sakaria 8 >