< Sakaria 7 >

1 Och det skedde i fjerde lirena Konungs Darios, att Herrans ord skedde till ZacharIa, på fjerde dagen af nionde månadenom, den Chislev heter;
Pa chaka chachinayi cha Mfumu Dariyo, pa tsiku lachinayi la Kisilevi, mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi Zekariya.
2 Då SarEzer och RegemMelech, samt med deras män, sände till BethEl, till att bedja inför Herranom;
Anthu a ku Beteli anali atatuma Sarezeri ndi Regemu-Meleki pamodzi ndi anthu awo, kuti akapemphe chifundo kwa Yehova
3 Och läto säga Prestomen, som voro omkring Herrans Zebaoths hus, och till Propheterna: Skall jag ock ännu gråta i femte månadenom, och tvinga mig, såsom jag nu i några år gjort hafver?
pokafunsa kwa ansembe a ku Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse ndi aneneri kuti, “Kodi ine ndizilira ndi kusala zakudya pa mwezi wachisanu, monga mmene ndakhala ndikuchitira pa zaka zambiri?”
4 Och Herrans Zebaoths ord skedde till mig, och sade:
Pamenepo Yehova Wamphamvuzonse anayankhula nane kuti,
5 Tala till allt folket i landena, och till Presterna, och säg: Då I fastaden, och jämraden eder, i femte och sjunde månadenom, i dessa sjutio år. Hafven I då fastat mig?
“Funsa anthu onse a mʼdziko ndi ansembe kuti, ‘Pamene munkasala zakudya pa mwezi wachisanu ndi wachisanu ndi chiwiri pa zaka 70 zapitazi, kodi munkasala chifukwa cha Ine?
6 Eller då I åten och drucken, hafven I icke ätit och druckit för eder sjelf?
Ndipo pamene munkadya ndi kumwa, kodi simunkachita zimenezi podzisangalatsa nokha?
7 Är icke detta, som Herren predika lät genom de förra Propheter; då Jerusalem ännu besuttet var, och hade nog, samt med sina städer omkring, och då der folk bodde, både söderut och i dalomen?
Kodi awa si mawu amene Yehova ankanena kudzera mwa aneneri oyamba aja pamene Yerusalemu ndi mizinda yake yozungulira anali pa mtendere ndi pa ulemerero, ndi pamene Negevi ndi ku madera akumadzulo a mʼmbali mwa phiri munali anthu?’”
8 Och Herrans ord skedde till ZacharIa och sade:
Ndipo Yehova anayankhulanso ndi Zekariya kuti,
9 Så säger Herren Zebaoth: Dömer rätt och hvar och en bevise godhet och barmhertighet uppå sin broder.
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Muziweruza molungama; muzichitirana chifundo ndi kumverana chisoni.
10 Och görer icke enkom, faderlösom, främlingom och fattigom, orätt; och ingen tänke något ondt emot sin broder i sitt hjerta.
Musamazunze akazi amasiye kapena ana amasiye, alendo kapena osauka. Musamaganizirane zoyipa mʼmitima mwanu.’
11 Men de ville intet akta deruppå och vände ryggen till mig, och förstockade sin öron, att de icke höra skulle;
“Koma makolo anu anakana kumvera uthenga umenewu; anawumitsa mtima nandifulatira, natseka makutu awo kuti asamve.
12 Och gjorde sin hjerta lika som en diamant, att de icke skulle höra lagen och orden, som Herren Zebaoth, i sinom Anda, sände genom de förra Propheter; derföre sådana stor vrede af Herranom Zebaoth kommen är;
Anawumitsa mitima yawo ngati mwala wa sangalabwi ndipo sanamvere lamulo kapena mawu amene Yehova Wamphamvuzonse anawatumiza mwa Mzimu wake kudzera mwa aneneri oyamba aja. Kotero Yehova Wamphamvuzonse anakwiya kwambiri.
13 Och det år så skedt, som predikadt vardt, och de ville intet hörat; så ville jag ock intet hörat, då de ropade, säger Herren Zebaoth.
“‘Pamene ndinawayitana, iwo sanamvere; choncho pamene iwo anandiyitana, Ine sindinamverenso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
14 Alltså hafver jag förstrött dem ibland alla Hedningar, hvilka de intet känna; och landet är efter dem öde blifvet, så att der ingen uti vandrar eller bor; och det ädla landet är till ett öde gjordt.
‘Ndinawamwaza ndi kamvuluvulu pakati pa mitundu yonse ya anthu, kumene anali alendo. Dziko lawo linatsala litasakazidwa kwambiri kotero kuti palibe amene amabwera kapena kupitamo. Umu ndi mmene anasandutsira dziko labwino kukhala chipululu.’”

< Sakaria 7 >