< Sakaria 5 >

1 Och jag lyfte åter min ögon upp, och säg; och si, der var ett flygande bref.
Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona chikalata chimene chimawuluka.
2 Och han sade till mig: Hvad ser du? Och jag sade: Jag ser ett flygande bref, det är tjugu alnar långt, och tio alnar bredt.
Mngelo uja anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona chikalata chikuwuluka, mulitali mwake mamita asanu ndi anayi ndipo mulifupi mwake mamita anayi ndi theka.”
3 Och han sade till mig: Det är den förbannelsen, som utgår öfver hela landet; ty allo tjufvar varda efter detta bref fromme dömde, och alle menedare varda efter detta, bref fromme dömde.
Ndipo mngeloyo anandiwuza kuti, “Awa ndi matemberero amene akupita pa dziko lonse lapansi; potsata zimene zalembedwa mʼkati mwa chikalatamo, aliyense wakuba adzachotsedwa, ndipo potsata zomwe zalembedwa kunja kwake, aliyense wolumbira zabodza adzachotsedwanso.
4 Men jag vill hafvat fram, säger Herren Zebaoth, att det skall komma tjufvomen hem, och dem som falskeliga svärja vid mitt Namn; och skall blifva uti deras hus, och skall upptära det, med dess trä och stenar.
Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Temberero limeneli ndidzalitumiza, ndipo lidzalowa mʼnyumba ya munthu wakuba ndi munthu wolumbira zabodza mʼdzina langa. Lidzakhala mʼnyumbamo mpaka kuyiwonongeratu, matabwa ake ndi miyala yake yomwe.’”
5 Och Ängelen, som med mig talade, gick ut, och sade till mig: Lyft din ögon upp, och se, hvad går derut?
Kenaka mngelo amene amayankhula nane uja anabwera patsogolo panga ndipo anandiwuza kuti, “Kweza maso ako tsopano kuti uwone kuti ndi chiyani chikubwerachi.”
6 Och sade: Hvad är det? Men han sade: En skäppa går derut; och sade: Det är deras anseende i allo landena.
Ndinafunsa kuti, “Kodi chimenechi nʼchiyani?” Mngeloyo anayankha kuti, “Limeneli ndi dengu loyezera.” Ndipo anawonjezera kunena kuti, “Umenewu ndi uchimo wa anthu mʼdziko lonse.”
7 Och si, der for en centener bly, och der var en qvinna, hvilken i skäppone satt.
Pamenepo chovundikira chake chamtovu chinatukulidwa, ndipo mʼdengumo munali mutakhala mkazi.
8 Men han sade: Det är afguderit; och han kastade henne uti skäppona, och hof den blyklimpen der ofvanuppå.
Mngeloyo anati, “Chimenechi ndi choyipa,” ndipo anamukankhira mkaziyo mʼdengu muja, nabwezera chovundikira chamtovu chija pamwamba pake.
9 Och jag lyfte min ögon upp, och såg; och si, två qvinnor gingo ut, och hade vingar, de der drefvos af vädret; och det voro vingar, lika som storkars vingar; och de förde skäppona mellan jorden och himmelen.
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona akazi awiri akuwuluka kubwera kumene kunali ine; akuwuluzika ndi mphepo. Iwo anali ndi mapiko ngati a kakowa, ndipo ananyamula dengu lija, kupita nalo pakati pa mlengalenga ndi dziko lapansi.
10 Och jag sade till Ängelen, som med mig talade: Hvart föra de skäppona?
Ine ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Dengulo akupita nalo kuti?”
11 Men han sade till mig: Att henne skall ett hus bygdt och tillredt varda uti Sinears land och der satt varda på sin botten.
Iye anayankha kuti, “Ku dziko la Babuloni kuti akalimangire nyumba. Nyumbayo ikadzatha, adzayikamo dengulo.”

< Sakaria 5 >