< Sakaria 2 >

1 Och jag hof min ögon upp, och si, en man hade ett mätesnöre i handene.
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona munthu atanyamula chingwe choyezera mʼmanja mwake.
2 Och jag sade: Hvart går du? Men han sade till mig: Till att mäta Jerusalem, och se huru bredt och långt det vara skall.
Ndipo ndinafunsa kuti, “Kodi ukupita kuti?” Anandiyankha kuti, “Akukayeza Yerusalemu kuti ndidziwe mulifupi mwake ndi mulitali mwake.”
3 Och si, Ängelen, som med mig talade, gick ut; och en annar Ängel gick ut emot honom;
Taonani, mngelo amene amayankhula nane uja akuchoka, mngelo wina anabwera kudzakumana naye
4 Och sade till honom: Löp bort, och tala till den unga mannen, och säg: Jerusalem skall besuttet varda utan murar, för mycket folks och fäs skull, som derinne vara skall.
ndipo anamuwuza kuti, “Thamanga, kamuwuze mnyamatayo kuti, ‘Yerusalemu udzakhala mzinda wopanda malinga chifukwa mudzakhala anthu ambiri ndiponso ziweto zochuluka.
5 Och jag vill, säger Herren, vara en eldsmur deromkring; och skall vara der inne, och bevisa mig härliga derinne.
Ndipo Ine mwini ndidzakhala linga lamoto kuteteza mzindawo,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakhala ulemerero mʼkati mwake.’
6 O, o, flyr utu nordlandet, säger Herren; ty jag hafver förstrött eder uti fyra väder under himmelen, säger Herren.
“Tulukani! Tulukani! Thawaniko ku dziko la kumpoto,” akutero Yehova, “pakuti ndinakumwazirani ku mphepo zinayi zamlengalenga,” akutero Yehova.
7 O, Zion, du som bor när dottrene Babel, fly.
“Tuluka, iwe Ziyoni! Thawa, iwe amene umakhala mʼdziko la mwana wamkazi wa Babuloni!”
8 Ty så säger Herren Zebaoth: Han hafve sändt mig till Hedningarna, som eder beröfvat hafva; deras magt hafver en ända i den eder rörer, han rörer hans ögnasten.
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Atatha kundilemekeza wanditumiza kwa anthu a mitundu ina amene anakufunkhani; pakuti aliyense wokhudza inu wakhudza mwanadiso wanga.
9 Ty si, jag vill upphäfva mina hand öfver dem, att de skola varda dem ett rof, som dem tjent hafva; att I skolen förnimma att Herren Zebaoth mig sändt hafver.
Ndithu Ine ndidzawamenya anthuwo ndi dzanja langa ndipo amene anali akapolo awo ndiye adzawalande zinthu. Pamenepo mudzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye wandituma.
10 Fröjda dig, och var glad, du dotter Zion; ty si, jag kommer, och vill bo när dig, säger Herren.
“Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, fuwula ndipo sangalala. Pakuti taona ndikubwera, ndipo ndidzakhala pakati pako,” akutero Yehova.
11 Och på den tiden skola månge Hedningar gifva sig intill Herran, och skola vara mitt folk; och jag skall bo när dig, att du skall förnimma, att Herren Zebaoth mig till dig sändt hafver.
“Nthawi imeneyo anthu a mitundu yambiri adzabwera kwa Yehova ndipo adzasanduka anthu anga. Ndidzakhala pakati pako ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe.
12 Och Herren skall ärfva Juda för sin del, uti de helga landena; och skall åter utvälja Jerusalem.
Yehova adzachititsa kuti Yuda akhale chuma chake mʼdziko lopatulika ndipo adzasankhanso Yerusalemu.
13 Allt kött vare stilla för Herranom; ty han är uppstånden ifrå sitt helga rum.
Khalani chete pamaso pa Yehova anthu nonse, chifukwa Iye wavumbuluka kuchoka ku malo ake opatulika.”

< Sakaria 2 >